Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

143 Mau a Mulungu Okhudza Ubwino Wake


Masalimo 100:5

Pakuti Yehova ndiye wabwino; chifundo chake chimanka muyaya; ndi chikhulupiriko chake ku mibadwomibadwo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:8

Talawani, ndipo onani kuti Yehova ndiye wabwino; wodala munthuyo wakukhulupirira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 23:6

Inde ukoma ndi chifundo zidzanditsata masiku onse a moyo wanga, ndipo ndidzakhala m'nyumba ya Yehova masiku onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 2:4

Kapena upeputsa kodi kulemera kwa ubwino wake, ndi chilekerero ndi chipiriro chake, wosadziwa kuti ubwino wa Mulungu ukubwezera kuti ulape?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:9

Yehova achitira chokoma onse; ndi nsoni zokoma zake zigwera ntchito zake zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Maliro 3:22-23

Chifukwa chakusathedwa ife ndicho chifundo cha Yehova, pakuti chisoni chake sichileka,

chioneka chatsopano m'mawa ndi m'mawa; mukhulupirika ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 86:5

Pakuti Inu, Ambuye, ndinu wabwino, ndi wokhululukira, ndi wa chifundo chochulukira onse akuitana Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 1:31

Ndipo anaziona Mulungu zonse zimene adazipanga, ndipo, taonani, zinali zabwino ndithu. Ndipo panali madzulo ndipo panali m'mawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:68

Inu ndinu wabwino, ndi wakuchita zabwino; mundiphunzitse malemba anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 136:1

Yamikani Yehova pakuti ndiye wabwino; pakuti chifundo chake nchosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 107:1

Yamikani Yehova pakuti Iye ndiye wabwino; pakuti chifundo chake nchosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:11

Chomwecho, ngati inu, muli oipa, mudziwa kupatsa ana anu mphatso zabwino, kopambana kotani nanga Atate wanu wa Kumwamba adzapatsa zinthu zabwino kwa iwo akumpempha Iye?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 118:1

Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino; pakuti chifundo chake nchosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 25:8

Yehova ndiye wabwino ndi wolunjika mtima, chifukwa chake adzaphunzitsa olakwa za njira.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 34:6

Ndipo Yehova anapita pamaso pake, nafuula, Yehova, Yehova, Mulungu wachifundo ndi wachisomo, wolekereza, ndi wa ukoma mtima wochuluka, ndi wachoonadi;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:15-16

Maso a onse ayembekeza Inu; ndipo muwapatsa chakudya chao m'nyengo zao.

Muolowetsa dzanja lanu, nimukwaniritsira zamoyo zonse chokhumba chao.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:76

Chifundo chanu chikhaletu chakunditonthoza, ndikupemphani, monga mwa mau anu kwa mtumiki wanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Tito 3:4-5

Koma pamene kukoma mtima, ndi chikondi cha pa anthu, cha Mpulumutsi wathu Mulungu zidanoneka,

zosati zochokera m'ntchito za m'chilungamo, zimene tidazichita ife, komatu monga mwa chifundo chake anatipulumutsa ife, mwa kutsuka kwa kubadwanso ndi makonzedwe a Mzimu Woyera,

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:28

Ndipo tidziwa kuti amene akonda Mulungu zinthu zonse zithandizana kuwachitira ubwino, ndiwo amene aitanidwa monga mwa kutsimikiza kwa mtima wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 146:9

Yehova asunga alendo; agwiriziza mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye; koma akhotetsa njira ya oipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:3-4

Khulupirira Yehova, ndipo chita chokoma; khala m'dziko, ndipo tsata choonadi.

Pakamwa pa wolungama palankhula zanzeru, ndi lilime lake linena chiweruzo.

Malamulo a Mulungu wake ali mumtima mwake; pakuyenda pake sadzaterereka.

Woipa aunguza wolungama, nafuna kumupha.

Yehova sadzamsiya m'dzanja lake; ndipo sadzamtsutsa poweruzidwa iye.

Yembekeza Yehova, nusunge njira yake, ndipo Iye adzakukweza kuti ulandire dziko. Pakudulidwa oipa udzapenya.

Ndapenya woipa, alikuopsa, natasa monga mtengo wauwisi wanzika.

Koma anapita ndipo taona, kwati zii; ndipo ndinampwaira osampeza.

Tapenya wangwiro, ndipo taona woongoka mtima! Pakuti ku matsiriziro ake a munthuyo kuli mtendere.

Koma olakwa adzaonongeka pamodzi; matsiriziro a oipa adzadulidwa.

Koma chipulumutso cha olungama chidzera kwa Yehova, Iye ndiye mphamvu yao m'nyengo ya nsautso.

Udzikondweretsenso mwa Yehova; ndipo Iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 54:10

Pakuti mapiri adzachoka, ndi zitunda zidzasunthika; koma kukoma mtima kwanga sikudzakuchokera iwe, kapena kusunthika chipangano changa cha mtendere, ati Yehova amene wakuchitira iwe chifundo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:14

Ndikuyamikani chifukwa kuti chipangidwe changa nchoopsa ndi chodabwitsa; ntchito zanu nzodabwitsa; moyo wanga uchidziwa ichi bwino ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 23:1-3

Yehova ndiye mbusa wanga; sindidzasowa.

Andigonetsa kubusa lamsipu, anditsogolera kumadzi odikha.

Atsitsimutsa moyo wanga; anditsogolera m'mabande a chilungamo, chifukwa cha dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 31:19

Ha! Kukoma kwanu ndiko kwakukulu nanga, kumene munasungira iwo akuopa Inu, kumene munachitira iwo akukhulupirira Inu, pamaso pa ana a anthu!

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 111:4-5

Anachita chokumbukitsa zodabwitsa zake; Yehova ndiye wachisomo ndi nsoni zokoma.

Anapatsa akumuopa Iye chakudya; adzakumbukira chipangano chake kosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 16:2

Ndinati kwa Yehova, Inu ndinu Ambuye wanga, ndilibe chabwino china choposa Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 78:38

Koma Iye pokhala ngwa chifundo, anakhululukira choipa, osawaononga; nabweza mkwiyo wake kawirikawiri, sanautse ukali wake wonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:17

Yehova ali wolungama m'njira zake zonse, ndi wachifundo m'ntchito zake zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 19:17

Ndipo Iye anati kwa iye, Undifunsiranji za chinthu chabwino? Alipo Mmodzi ndiye wabwino: koma ngati ufuna kulowa m'moyo, sunga malamulo.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 5:8

Koma Mulungu atsimikiza kwa ife chikondi chake cha mwini yekha m'menemo, kuti pokhala ife chikhalire ochimwa, Khristu adatifera ife.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:8

Yehova ndiye wa nsoni zokoma ndi wachisomo, wosakwiya msanga, ndi wa chifundo chochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 86:15

Koma Inu, Ambuye, ndinu Mulungu wansoni ndi wachisomo, wopatsa mtima msanga, ndi wochulukira chifundo ndi choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 33:5

Ndipo anatukula maso ake nawaona akazi ndi ana; nati, Ndani awa ali ndi iwe? Ndipo iye anati, Ndiwo ana amene Mulungu anakomera mtima kumpatsa kapolo wanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 147:7-9

Yamikani Yehova ndi kuthira mang'ombe; muimbireni Mulungu wathu zomlemekeza pazeze:

Amene aphimba thambo ndi mitambo, amene akonzera mvula nthaka, amene aphukitsa msipu pamapiri.

Amene apatsa zoweta chakudya chao, ana a khwangwala alikulira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 68:19

Wolemekeza Ambuye, tsiku ndi tsiku atisenzera katundu, ndiye Mulungu wa chipulumutso chathu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 100:4

Lowani kuzipata zake ndi chiyamiko, ndi kumabwalo ake ndi chilemekezo: Myamikeni; lilemekezeni dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 63:7

Ndidzatchula zachifundo chake cha Yehova, ndi matamando a Yehova, monga mwa zonse zimene Yehova wapereka kwa ife; ndi ubwino wake waukulu kwa banja la Israele, umene Iye wapereka kwa iwo, monga mwa chifundo chake, ndi monga mwa ntchito zochuluka za chikondi chake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:8-9

Yehova ndiye wachisomo, ndi wachifundo; osakwiya msanga, ndi wa chifundo chachikulu.

Yehova achitira chokoma onse; ndi nsoni zokoma zake zigwera ntchito zake zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:20

Pakuti chilengedwere dziko lapansi zaoneka bwino zosaoneka zake ndizo mphamvu yake yosatha ndi umulungu wake; popeza zazindikirika ndi zinthu zolengedwa, kuti iwo adzakhale opanda mau akuwiringula;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 16:5

Yehova ndiye gawo la cholowa changa ndi chikho changa, ndinu wondigwirira cholandira changa.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 49:25

Ndi Mulungu wa atate wako amene adzakuthangata iwe, ndi Wamphamvuyonse, amene adzakudalitsa iwe. Ndi madalitso a Kumwamba, madalitso a madzi akuya akukhala pansi, madalitso a mawere, ndi a mimba.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 33:5

Iye ndiye wakukonda chilungamo ndi chiweruzo, dziko lapansi ladzala ndi chifundo cha Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 9:10

ndipo iwo akudziwa dzina lanu adzakhulupirira Inu; pakuti, Inu Yehova, simunawasiye iwo akufuna Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 136:2

Yamikani Mulungu wa milungu; pakuti chifundo chake nchosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 33:19

Ndipo Iye anati, Ndidzapititsa ukoma wanga wonse pamaso pako, ndipo ndidzatchula dzina la Yehova pamaso pako; ndipo ndidzachitira ufulu amene ndidzamchitira ufulu; ndi kuchitira chifundo amene ndidzamchitira chifundo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 115:1-3

Kwa ife ai, Yehova, kwa ife ai, koma kwa dzina lanu patsani ulemerero, chifukwa cha chifundo chanu, ndi choonadi chanu.

Nyumba ya Aroni, khulupirira Yehova: Ndiye mthandizi wao, ndi chikopa chao.

Inu akuopa Yehova, khulupirirani Yehova; ndiye mthandizi wao ndi chikopa chao.

Yehova watikumbukira; adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israele; adzadalitsa nyumba ya Aroni.

Adzadalitsa iwo akuopa Yehova, aang'ono ndi aakulu.

Yehova akuonjezereni dalitso, inu ndi ana anu.

Odalitsika inu a kwa Yehova, wakulenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Kunena za kumwamba, kumwamba ndiko kwa Yehova; koma dziko lapansi analipereka kwa ana a anthu.

Akufa salemekeza Yehova, kapena aliyense wakutsikira kuli chete:

Koma ife tidzalemekeza Yehova kuyambira tsopano kufikira nthawi yonse. Aleluya.

Aneneranji amitundu, Ali kuti Mulungu wao?

Koma Mulungu wathu ndiye ali m'mwamba; achita chilichonse chimkonda.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:12

pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda; monga atate mwana amene akondwera naye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 84:11

Pakuti Yehova Mulungu ndiye dzuwa ndi chikopa; Yehova adzapatsa chifundo ndi ulemerero; sadzakaniza chokoma iwo akuyenda angwiro.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 121:5

Yehova ndiye wakukusunga; Yehova ndiye mthunzi wako wa kudzanja lako lamanja.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 25:10

Mayendedwe onse a Yehova ndiwo chifundo ndi choonadi, kwa iwo akusunga pangano lake ndi mboni zake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:18

Yehova ali pafupi ndi iwo a mtima wosweka, apulumutsa iwo a mzimu wolapadi.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 63:9

M'mazunzo ao onse Iye anazunzidwa, ndipo mthenga wakuimirira pamaso pake anawapulumutsa; m'kukonda kwake ndi m'chisoni chake Iye anawaombola, nawabereka nawanyamula masiku onse akale.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 73:1

Indedi Mulungu achitira Israele zabwino, iwo a mtima wa mbee.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:13

Ndipo Mulungu wa chiyembekezo adzaze inu ndi chimwemwe chonse ndi mtendere m'kukhulupirira, kuti mukachuluke ndi chiyembekezo, mu mphamvu ya Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:8

Yehova ndiye wachisomo, ndi wachifundo; osakwiya msanga, ndi wa chifundo chachikulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:1-5

Lemekeza Yehova, moyo wanga; ndi zonse za m'kati mwanga zilemekeze dzina lake loyera.

Sanatichitira monga mwa zolakwa zathu, kapena kutibwezera monga mwa mphulupulu zathu.

Pakuti monga m'mwamba mutalikira ndi dziko lapansi, motero chifundo chake chikulira iwo akumuopa Iye.

Monga kum'mawa kutanimpha ndi kumadzulo, momwemo anatisiyanitsira kutali zolakwa zathu.

Monga atate achitira ana ake chifundo, Yehova achitira chifundo iwo akumuopa Iye.

Popeza adziwa mapangidwe athu; akumbukira kuti ife ndife fumbi.

Koma munthu, masiku ake akunga udzu; aphuka monga duwa lakuthengo.

Pakuti mphepo ikapitapo pakhala palibe: Ndi malo ake salidziwanso.

Koma chifundo cha Yehova ndicho choyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha kwa iwo akumuopa Iye, ndi chilungamo chake kufikira kwa ana a ana;

kwa iwo akusunga chipangano chake, ndi kwa iwo akukumbukira malangizo ake kuwachita.

Yehova anakhazika mpando wachifumu wake Kumwamba; ndi ufumu wake uchita mphamvu ponsepo.

Lemekeza Yehova, moyo wanga, ndi kusaiwala zokoma zake zonse atichitirazi:

Lemekezani Yehova, inu angelo ake; a mphamvu zolimba, akuchita mau ake, akumvera liu la mau ake.

Lemekezani Yehova, inu makamu ake onse; inu atumiki ake akuchita chomkondweretsa Iye.

Lemekezani Yehova, inu, ntchito zake zonse, ponseponse pali ufumu wake: Lemekeza Yehova, moyo wanga iwe.

Amene akhululukira mphulupulu zako zonse; nachiritsa nthenda zako zonse;

amene aombola moyo wako ungaonongeke; nakuveka korona wa chifundo ndi nsoni zokoma:

Amene akhutitsa m'kamwa mwako ndi zabwino; nabweza ubwana wako unge mphungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:25

Ndinali mwana ndipo ndakalamba; ndipo sindinapenye wolungama atasiyidwa, kapena mbumba zake zilinkupempha chakudya.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:17-18

Koma chifundo cha Yehova ndicho choyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha kwa iwo akumuopa Iye, ndi chilungamo chake kufikira kwa ana a ana;

kwa iwo akusunga chipangano chake, ndi kwa iwo akukumbukira malangizo ake kuwachita.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 107:8-9

Ayamike Yehova chifukwa cha chifundo chake, ndi zodabwitsa zake za kwa ana a anthu!

Pakuti akhutitsa mtima wolakalaka, nadzaza mtima wanjala ndi zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 147:3

Achiritsa osweka mtima, namanga mabala ao.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 31:19-20

Ha! Kukoma kwanu ndiko kwakukulu nanga, kumene munasungira iwo akuopa Inu, kumene munachitira iwo akukhulupirira Inu, pamaso pa ana a anthu!

Munditcherere khutu lanu; ndipulumutseni msanga. Mundikhalire ine thanthwe lolimba, nyumba yamalinga yakundisunga.

Pobisalira pamaso panu mudzawabisa kwa chiwembu cha munthu, mudzawabisa iwo mumsasa kuti muwalanditse pa kutetana kwa malilime.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:17

Wochitira waumphawi chifundo abwereka Yehova; adzambwezera chokoma chakecho.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:4

amene aombola moyo wako ungaonongeke; nakuveka korona wa chifundo ndi nsoni zokoma:

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 30:5

Pakuti mkwiyo wake ukhala kanthawi kokha; koma kuyanja kwake moyo wonse. Kulira kuchezera, koma mamawa kuli kufuula kokondwera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:116

Mundichirikize monga mwa mau anu, kuti ndikhale ndi moyo; ndipo ndisachite manyazi pa chiyembekezo changa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:32

Ndidzathamangira njira ya malamulo anu, mutakulitsa mtima wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 38:5

Mabala anga anunkha, adaola, chifukwa cha kupusa kwanga.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:3

ngati mwalawa kuti Ambuye ali wokoma mtima;

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:45

kotero kuti mukakhale ana a Atate wanu wa Kumwamba; chifukwa Iye amakwezera dzuwa lake pa oipa ndi pa abwino, namavumbitsira mvula pa olungama ndi pa osalungama.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 31:21

Wolemekezeka Yehova, pakuti anandichitira chifundo chake chodabwitsa m'mzinda walinga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 136:26

Yamikani Mulungu wa Kumwamba, pakuti chifundo chake nchosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 54:8

M'kukwiya kwa kusefukira ndinakubisira nkhope yanga kamphindi; koma ndi kukoma mtima kwa chikhalire ndidzakuchitira chifundo, ati Yehova Mombolo wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:65

Munachitira mtumiki wanu chokoma, Yehova, monga mwa mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 68:4

Imbirani Mulungu, liimbireni nyimbo dzina lake; undirani mseu Iye woberekekayo kuchidikha; dzina lake ndiye Yehova; ndipo tumphani ndi chimwemwe pamaso pake.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:22

Koma chipatso cha Mzimu ndicho chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, chikhulupiriro,

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 2:6-7

amene adzabwezera munthu aliyense kolingana ndi ntchito zake;

kwa iwo amene afunafuna ulemerero ndi ulemu ndi chisaonongeko, mwa kupirira pa ntchito zabwino, adzabwezera moyo wosatha;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 62:5

Moyo wanga, ukhalire chete Mulungu yekha; pakuti chiyembekezo changa chifuma kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 78:39

Ndipo anakumbukira kuti iwo ndiwo anthu; mphepo yopita yosabweranso.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:16

Ndisanaumbidwe ine maso anu anandipenya, ziwalo zanga zonse zinalembedwa m'buku mwanu, masiku akuti ziumbidwe, pakalibe chimodzi cha izo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:47

Ndipo ndidzadzikondweretsa nao malamulo anu, amene ndiwakonda.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:70

Mtima wao unona ngati mafuta; koma ine ndikondwera nacho chilamulo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:16

Muolowetsa dzanja lanu, nimukwaniritsira zamoyo zonse chokhumba chao.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 18:30

Mulungu ndiye wangwiro m'njira zake; mau a Yehova ngoyengeka; ndiye chikopa cha onse okhulupirira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 89:1-2

Ndidzaimbira zachifundo za Yehova nthawi yonse, pakamwa panga ndidzadziwitsira chikhulupiriko chanu ku mibadwomibadwo.

Mudathyola Rahabu, monga munthu wophedwa; munabalalitsa adani anu ndi mkono wa mphamvu yanu.

Kumwamba ndi kwanu, dziko lapansi lomwe ndi lanu; munakhazika dziko lokhalamo anthu ndi kudzala kwake.

Munalenga kumpoto ndi kumwera; Tabori ndi Heremoni afuula mokondwera m'dzina lanu.

Muli nao mkono wanu wolimba; m'dzanja mwanu muli mphamvu, dzanja lamanja lanu nlokwezeka.

Chilungamo ndi chiweruzo ndiwo maziko a mpando wanu wachifumu; chifundo ndi choonadi zitsogolera pankhope panu.

Odala anthu odziwa liu la lipenga; ayenda m'kuunika kwa nkhope yanu, Yehova.

Akondwera m'dzina lanu tsiku lonse; ndipo akwezeka m'chilungamo chanu.

Popeza Inu ndinu ulemerero wa mphamvu yao; ndipo potivomereza Inu nyanga yathu idzakwezeka.

Pakuti chikopa chathu chifuma kwa Yehova; ndi mfumu yathu kwa Woyera wa Israele.

Pamenepo munalankhula m'masomphenya ndi okondedwa anu, ndipo mudati, Ndasenza thandizo pa chiphona; ndakweza wina wosankhika mwa anthu.

Pakuti ndinati, Chifundo adzachimanga kosaleka; mudzakhazika chikhulupiriko chanu mu Mwamba mwenimweni.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 23:5

Mundiyalikira gome pamaso panga m'kuona kwa adani anga; mwandidzoza mutu wanga mafuta; chikho changa chisefuka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:18-19

Yehova adziwa masiku a anthu angwiro; ndipo cholowa chao chidzakhala chosatha.

Sadzachita manyazi m'nyengo yoipa, ndipo m'masiku a njala adzakhuta.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:13

Ufumu wanu ndiwo ufumu womka muyaya, ndi kuweruza kwanu kufikira mibadwo yonseyonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 5:12

Pakuti Inu, Yehova, mudzadalitsa wolungamayo; mudzamtchinjiriza nacho chivomerezo ngati chikopa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:48

Chifukwa chake inu mukhale angwiro, monga Atate wanu wa Kumwamba ali wangwiro.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 106:1

Aleluya. Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino: Pakuti chifundo chake nchosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 136:25

Ndiye wakupatsa nyama zonse chakudya; pakuti chifundo chake nchosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 146:7

ndiye wakuchitira chiweruzo osautsika; ndiye wakupatsa anjala chakudya; Yehova amasula akaidi.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 4:4

Pakuti cholengedwa chonse cha Mulungu nchabwino, ndipo palibe kanthu kayenera kutayika, ngati kalandiridwa ndi chiyamiko;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:17

Koma chifundo cha Yehova ndicho choyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha kwa iwo akumuopa Iye, ndi chilungamo chake kufikira kwa ana a ana;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 116:1

Ndimkonda, popeza Yehova amamva mau anga ndi kupemba kwanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 138:8

Yehova adzanditsirizira za kwa ine: Chifundo chanu, Yehova, chifikira kunthawi zonse: Musasiye ntchito za manja anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 25:4

Chifukwa Inu mwakhala linga la aumphawi, linga la osowa m'kuvutidwa kwake, pobisalira chimphepo, mthunzi wa pa dzuwa, pamene kuomba kwa akuopsa kufanana ndi chimphepo chakuomba tchemba.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:3

Ndiyamika Mulungu wanga pokumbukira inu ponse;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:142

Chilungamo chanu ndicho chilungamo chosatha; ndi chilamulo chanu ndicho choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:20

Yehova asunga onse akukondana naye; koma oipa onse adzawaononga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:64

Dziko lapansi lidzala nacho chifundo chanu, Yehova; mundiphunzitse malemba anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 36:5-6

Yehova, m'mwamba muli chifundo chanu; choonadi chanu chifikira kuthambo.

Chilungamo chanu chikunga mapiri a Mulungu; maweruzo anu akunga chozama chachikulu, Yehova, musunga munthu ndi nyama.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:16

Ndipo ife tazindikira, ndipo takhulupirira chikondicho Mulungu ali nacho pa ife. Mulungu ndiye chikondi, ndipo iye amene akhala m'chikondi akhala mwa Mulungu, ndipo Mulungu akhala mwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:31

Ndipo tidzatani ndi zinthu izi? Ngati Mulungu ali ndi ife, adzatikaniza ndani?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 33:18-19

Taonani, diso la Yehova lili pa iwo akumuopa Iye, pa iwo akuyembekeza chifundo chake.

Kupulumutsa moyo wao kwa imfa, ndi kuwasunga ndi moyo m'nyengo ya njala.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 6:10

pakuti Mulungu sali wosalungama kuti adzaiwala ntchito yanu, ndi chikondicho mudachionetsera kudzina lake, umo mudatumikira oyera mtima ndi kuwatumikirabe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 32:10

Zisoni zambiri zigwera woipa; koma chifundo chidzamzinga iye wakukhulupirira Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 135:5

Pakuti ndidziwa kuti Yehova ndi wamkulu, ndi Ambuye wathu aposa milungu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 86:12

Ndidzakuyamikani, Ambuye, Mulungu wanga, ndi mtima wanga wonse; ndipo ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:7

Pemphani, ndipo chidzapatsidwa kwa inu; funani, ndipo mudzapeza; gogodani, ndipo chidzatsegulidwa kwa inu;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:136

Maso anga atsitsa mitsinje ya madzi, popeza sasamalira chilamulo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 66:20

Wolemekezeka Mulungu, amene sanandipatutsire ine pemphero langa, kapena chifundo chake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 116:5

Yehova ngwa chifundo ndi wolungama; ndi Mulungu wathu ngwa nsoni.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:29

Mundichotsere njira ya chinyengo; nimundipatse mwachifundo chilamulo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:6

Mphulupulu iomboledwa ndi chifundo ndi ntheradi; apatuka pa zoipa poopa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 77:11-12

Ndidzakumbukira zimene adazichita Yehova; inde, ndidzakumbukira zodabwitsa zanu zoyambira kale.

Ndipo ndidzalingalira ntchito yanu yonse, ndi kulingalirabe zimene munazichita Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 94:18-19

Pamene ndinati, Literereka phazi langa, chifundo chanu, Yehova, chinandichirikiza.

Pondichulukira zolingalira zanga m'kati mwanga, zotonthoza zanu zikondweretsa moyo wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 6:9

Koma tisaleme pakuchita zabwino; pakuti pa nyengo yake tidzatuta tikapanda kufooka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 31:14-15

Koma ine ndakhulupirira Inu, Yehova, ndinati, Inu ndinu Mulungu wanga.

Nyengo zanga zili m'manja mwanu, mundilanditse m'manja a adani anga, ndi kwa iwo akundilondola ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 84:5

Wodala munthu amene mphamvu yake ili mwa Inu; mumtima mwake muli makwalala a ku Ziyoni.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:62

Pakati pa usiku ndidzauka kukuyamikani chifukwa cha maweruzo anu olungama.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 91:2

Ndidzati kwa Yehova, Pothawirapo panga ndi linga langa; Mulungu wanga, amene ndimkhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:11

Iye adzadyetsa zoweta zake ngati mbusa, nadzasonkhanitsa anaankhosa m'manja mwake, nadzawatengera pa chifuwa chake, ndipo adzatsogolera bwinobwino zimene ziyamwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 40:5

Inu, Yehova, Mulungu wanga, zodabwitsa zanu mudazichita nzambiri, ndipo zolingirira zanu za pa ife; palibe wina wozifotokozera Inu; ndikazisimba ndi kuzitchula, zindichulukira kuziwerenga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:6

Yehova achitira onse osautsidwa chilungamo ndi chiweruzo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 138:2

Ndidzagwadira kuloza ku Kachisi wanu woyera, ndi kuyamika dzina lanu, chifukwa cha chifundo chanu ndi choonadi chanu; popeza munakuzitsa mau anu koposa dzina lanu lonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:10

Misona ya mkango isowa nimva njala, koma iwo akufuna Yehova sadzasowa kanthu kabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:87

Akadandithera padziko lapansi; koma ine sindinasiye malangizo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:26

Tsiku lonse achitira chifundo, nakongoletsa; ndipo mbumba zake zidalitsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:5-7

Ndidzalingalira ulemerero waukulu wa ulemu wanu, ndi ntchito zanu zodabwitsa.

Ndipo adzanenera mphamvu za ntchito zanu zoopsa; ndi ukulu wanu ndidzaufotokozera.

Adzabukitsa chikumbukiro cha ubwino wanu waukulu, nadzaimbira chilungamo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:7

Khala chete mwa Yehova, numlindirire Iye; usavutike mtima chifukwa cha iye wolemerera m'njira yake, chifukwa cha munthu wakuchita chiwembu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 12:1

Tsiku lomwelo udzati, Ndikuyamikani inu Yehova; pakuti ngakhale munandikwiyira, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mutonthoza mtima wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 5:1-2

Popeza tsono tayesedwa olungama ndi chikhulupiriro, tikhala ndi mtendere ndi Mulungu mwa Ambuye wathu Yesu Khristu;

Pakuti ngati, pokhala ife adani ake, tinayanjanitsidwa ndi Mulungu mwa imfa ya Mwana wake, makamaka ndithu, popeza ife tayanjanitsidwa, tidzapulumuka ndi moyo wake.

Ndipo si chotero chokha, koma ife tikondwera ndi Mulungu mwa Ambuye wathu Yesu Khristu, amene talandira naye tsopano chiyanjanitso.

Chifukwa chake, monga uchimo unalowa m'dziko lapansi mwa munthu mmodzi, ndi imfa mwa uchimo; chotero imfa inafikira anthu onse, chifukwa kuti onse anachimwa.

Pakuti kufikira nthawi ya lamulo uchimo unali m'dziko lapansi; koma uchimo suwerengedwa popanda lamulo.

Komatu imfa inachita ufumu kuyambira kwa Adamu kufikira kwa Mose, ngakhale pa iwonso amene sanachimwe monga machimwidwe ake a Adamu, ndiye fanizo la wakudzayo.

Koma mphatso yaulere siilingana ndi kulakwa. Pakuti ngati ambiriwo anafa chifukwa cha kulakwa kwa mmodziyo, makamaka ndithu chisomo cha Mulungu, ndi mphatso yaulere zakuchokera ndi munthu mmodziyo Yesu Khristu, zinachulukira anthu ambiri.

Ndipo mphatso siinadze monga mwa mmodzi wakuchimwa, pakuti mlandu ndithu unachokera kwa munthu mmodzi kufikira kutitsutsa, koma mphatso yaulere ichokera ku zolakwa zambiri kufikira kutiyesa olungama.

Pakuti ngati, ndi kulakwa kwa mmodzi, imfa inachita ufumu mwa mmodziyo; makamaka ndithu amene akulandira kuchuluka kwake kwa chisomo ndi kwa mphatso ya chilungamo, adzachita ufumu m'moyo mwa mmodzi, ndiye Yesu Khristu.

Chifukwa chake, monga mwa kulakwa kumodzi kutsutsa kunafikira anthu onse; chomwechonso mwa chilungamitso chimodzi chilungamo cha moyo chinafikira anthu onse.

Pakuti monga ndi kusamvera kwa munthu mmodzi ambiri anayesedwa ochimwa, chomwecho ndi kumvera kwa mmodzi ambiri adzayesedwa olungama.

amene ife tikhoza kulowa naye ndi chikhulupiriro m'chisomo ichi m'mene tilikuimamo; ndipo tikondwera m'chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 33:22

Yehova, chifundo chanu chikhale pa ife, monga takuyembekezani Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 126:3

Yehova anatichitira ife zazikulu; potero tikhala okondwera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 128:1-2

Wodala yense wakuopa Yehova, wakuyenda m'njira zake.

Pakuti udzadya za ntchito ya manja ako; wodala iwe, ndipo kudzakukomera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 29:11

Yehova adzapatsa anthu ake mphamvu, Yehova adzadalitsa anthu ake ndi mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:151

Inu muli pafupi, Yehova; ndipo malamulo anu onse ndiwo choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:32

Iye amene sanatimane Mwana wake wa Iye yekha, koma anampereka chifukwa cha ife tonse, adzalekeranji kutipatsanso ife zinthu zonse kwaulere pamodzi ndi Iye?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 30:2

Yehova, Mulungu wanga, ndinafuulira kwa Inu, ndipo munandichiritsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 51:1

Mundichitire ine chifundo, Mulungu, monga mwa kukoma mtima kwanu; monga mwa unyinji wa nsoni zanu zokoma mufafanize machimo anga.

Mutu    |  Mabaibulo