Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -



NDIME ZA ZOCHITIKA ZAPADERA

NDIME ZA ZOCHITIKA ZAPADERA

Timatamanda Mulungu chifukwa cha tsiku lililonse lapadera limene timakumana nalo, ndi masiku osangalala ndi kukondwerera. Mulungu amasangalala tikamayenda mu mtendere ndi chimwemwe. Muzimutamanda Yehova m'masiku amenewa ndipo musaiwale kuti ndi Mulungu amene amakuchititsani kukhala ndi nthawi zapadera.

Masalimo 30:11-12 amati, “Munasintha kulira kwanga kukhala kuvina; Munandichotsa chiguduli, n’kundiveka chokondwerera; kuti moyo wanga uziyimba nyimbo zotamanda Inu, osakhala chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzakutamandani nthawi zonse.” M’Baibulo muli mavesi ambiri okhudza zochitika zapadera.




Hoseya 9:5

Mudzachitanji tsiku la misonkhano yoikika, ndi tsiku la chikondwerero cha Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 30:23

Ndipo msonkhano wonse unapangana kuchita masiku asanu ndi awiri ena, nachita masiku asanu ndi ena ndi chimwemwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 34:18

Uzisunga chikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa. Uzidya mkate wopanda chotupitsa masiku asanu ndi awiri, monga ndakuuza pa nthawi yonenedwa, m'mwezi wa Abibu; pakuti mwezi wa Abibu unatuluka mu Ejipito.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 23:15

Uzisunga chikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa; masiku asanu ndi awiri uzidya mkate wopanda chotupitsa, monga ndinakuuza, nyengo yoikika, mwezi wa Abibu, pakuti m'menemo unatuluka mu Ejipito; koma asaoneke munthu pamaso panga opanda kanthu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 31:16

Chifukwa chake ana a Israele azisunga Sabata, kuchita Sabata mwa mibadwo yao, likhale pangano losatha;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:24

Tsiku ili ndilo adaliika Yehova; tidzasekera ndi kukondwera m'mwemo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nehemiya 8:14-15

Napeza munalembedwa m'chilamulo kuti Yehova analamulira ndi Mose, kuti ana a Israele azikhala m'misasa pa chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri, ndi kuti azilalikira ndi kumveketsa m'midzi mwao monse ndi mu Yerusalemu, ndi kuti, Muzitulukira kuphiri, ndi kutengako nthambi za azitona, ndi nthambi za mitengo yamafuta, ndi nthambi za mitengo yamchisu, ndi zinkhwamba za migwalangwa, ndi nthambi za mitengo zothonana, kumanga nazo misasa monga munalembedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Hoseya 2:11

Ndidzaleketsanso kusekerera kwake konse, zikondwerero zake, pokhala mwezi pake, ndi masabata ake, ndi misonkhano yake yonse yoikika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 1:13-14

Musadze nazonso, nsembe zachabechabe; nsembe zofukiza zindinyansa; tsiku lokhala mwezi ndi Sabata, kumema misonkhano, sindingalole mphulupulu ndi misonkhano. Masiku anu okhala mwezi ndi nthawi ya zikondwerero zanu mtima wanga uzida; zindivuta Ine; ndalema ndi kupirira nazo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 32:5

Pakuchiona Aroni, anamanga guwa la nsembe patsogolo pake; ndipo Aroni anafuula nati, Mawa aliko madyerero a Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 66:23

Ndipo kudzakhala kuti kuyambira pa mwezi wokhala kufikira ku unzake, ndi kuyambira pa Sabata lina kufikira kulinzake, anthu onse adzafika kudzapembedzera pamaso pa Ine, ati Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 15:3

ndipo mukakonzera Yehova nsembe yamoto, nsembe yopsereza, kapena yophera, pochita chowinda cha padera, kapena nsembe yaufulu, kapena nsembe ya pa nyengo zanu zoikika, kumchitira Yehova fungo lokoma, la ng'ombe kapena nkhosa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 31:10-11

Ndipo Mose anawauza, ndi kuti, Pakutha pake pa zaka zisanu ndi ziwiri, pa nyengo yoikika ya m'chaka chakulekerera, pa chikondwerero cha Misasa; pakufika Israele wonse kuoneka pamaso pa Yehova Mulungu wanu, m'malo amene adzasankha, muzilalikira chilamulo ichi pamaso pa Israele wonse, m'makutu mwao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 23:18

Usapereka mwazi wa nsembe yanga pamodzi ndi mkate wa chotupitsa; ndi mafuta a madyerero anga asagonamo kufikira m'mawa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 14:22-23

Muzipereka ndithu limodzi la magawo khumi la zipatso zonse za mbeu zanu, zofuma kumunda, chaka ndi chaka. Ndipo muzidye pamaso pa Yehova Mulungu wanu, m'malo m'mene asankhamo Iye, kukhalitsamo dzina lake; limodzi la magawo khumi la tirigu wanu, la vinyo wanu, ndi la mafuta anu, ndi oyamba kubadwa a ng'ombe zanu ndi a nkhosa ndi mbuzi zanu; kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu masiku onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Amosi 8:10

Ndipo ndidzasanduliza zikondwerero zanu zikhale maliro, ndi nyimbo zanu zikhale za maliro, ndi kufikitsa ziguduli m'chuuno monse, ndi mpala pamutu uliwonse; nadzakhala ngati maliro a mwana mmodzi yekha, ndi chitsiriziro chake ngati tsiku lowawa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 25:8-9

Ndipo uziwerengera masabata a zaka asanu ndi awiri, zaka zisanu ndi ziwiri kasanu ndi kawiri; kotero kuti zaka za masabata a zaka asanu ndi awiri, zifikire zaka makumi anai kudza zisanu ndi zinai. Pamenepo uzitumizira lipenga lomveka m'mwezi wachisanu ndi chiwiri, tsiku lakhumi la mweziwo; tsiku la chitetezero mutumizire lipenga lifikire m'dziko lanu lonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:6

Ndipo tsiku lakhumi ndi chisanu la mwezi womwewo ndilo chikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa a Yehova; masiku asanu ndi awiri muzidya mkate wopanda chotupitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 45:25

Mwezi wachisanu ndi chiwiri, tsiku lakhumi ndi chisanu la mwezi, pachikondwerero, achite momwemo masiku asanu ndi awiri, monga mwa nsembe yauchimo, monga mwa nsembe yopsereza, ndi monga mwa nsembe yaufa, ndi monga mwa mafuta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 45:21

Mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi chinai la mwezi, muzichita Paska, chikondwerero cha masiku asanu ndi awiri; audye mkate wopanda chotupitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezara 3:4

Nachita chikondwerero cha Misasa monga kwalembedwa, napereka nsembe yopsereza tsiku ndi tsiku mawerengedwe ake, monga mwa lamulo lake la tsiku lake pa tsiku lake;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 30:21

Ndipo ana a Israele opezeka mu Yerusalemu anachita chikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa masiku asanu ndi awiri ndi chimwemwe chachikulu; ndi Alevi ndi ansembe analemekeza Yehova tsiku ndi tsiku ndi zoimbira zakuliritsa kwa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 8:13

monga momwe mudayenera, tsiku ndi tsiku; napereka monga momwe adauza Mose pamasabata, pokhala mwezi, ndi pa zikondwerero zoikika, katatu m'chaka: pa chikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa, ndi pa chikondwerero cha Masabata, ndi pa chikondwerero cha Misasa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 16:16

Amuna onse azioneka pamaso pa Yehova Mulungu wanu m'malo amene Iye adzasankha, katatu m'chaka; pa chikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa, pa chikondwerero cha masabata, ndi pa chikondwerero cha Misasa; ndipo asaoneke pamaso pa Yehova opanda kanthu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 28:16

Ndipo mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi chinai la mwezi pali Paska wa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 9:2-3

Ana a Israele achite Paska pa nyengo yoikidwa. Ndipo pokhala mtambo pamwamba pa chihema masiku pang'ono; pamenepo anakhala m'chigono monga awauza Yehova, nayendanso ulendo monga anauza Yehova. Koma mtambo ukakhala kuyambira madzulo kufikira m'mawa; pokwera mtambo m'mawa, ayenda ulendo. Ngakhale masiku awiri, kapena mwezi, kapena masiku ambiri, pokhalitsa mtambo pamwamba pa chihema ndi kukhalapo, ana a Israele anakhala m'chigono, osayenda ulendo; koma pakukwera uwu, anayenda ulendo. Powauza Yehova amanga mahema, powauza Yehova ayenda ulendo; anasunga udikiro wa Yehova powauza Yehova mwa dzanja la Mose. Tsiku lakhumi ndi chinai la mweziwo, madzulo, muziuchita, pa nyengo yake yoikidwa; muuchite monga mwa malemba ake onse, ndi maweruzo ake onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:39

Koma tsiku lakhumi ndi chisanu la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutatuta zipatso za m'dziko, muzisunga chikondwerero cha Yehova masiku asanu ndi awiri; tsiku loyamba mupumule, ndi tsiku lachisanu ndi chitatu mupumule.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:34

Nena ndi ana a Israele, kuti, Tsiku lakhumi ndi chisanu la mwezi uno wachisanu ndi chiwiri pali chikondwerero cha Misasa ya Yehova, masiku asanu ndi awiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:27

Komatu, tsiku lakhumi la mwezi uwu wachisanu ndi chiwiri, ndilo tsiku la chitetezero; mukhale nao msonkhano wopatulika, ndipo mudzichepetse; ndi kubwera nayo nsembe yamoto kwa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:24

Nena ndi ana a Israele, ndi kuti, Mwezi wachisanu ndi chiwiri, tsiku loyamba la mweziwo, muzipumula, ndiko chikumbutso cha kuliza malipenga, msonkhano wopatulika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:15-16

Ndipo mudziwerengere kuyambira tsiku lotsata Sabata, kuyambira tsikuli mudadza nao mtolo wansembe yoweyula; pakhale masabata asanu ndi awiri amphumphu; muwerenge masiku makumi asanu kufikira tsiku lotsata sabata lachisanu ndi chiwiri; pamenepo mubwere nayo kwa Yehova nsembe ya ufa watsopano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:10-11

Nena ndi ana a Israele, nuti nao, Mutakalowa m'dziko limene ndikupatsani, ndi kucheka dzinthu zake, pamenepo muzidza nao mtolo wa zipatso zoyamba za masika anu kwa wansembe; ndipo iye aweyule mtolowo pamaso pa Yehova, ulandirikire inu, tsiku lotsata Sabata wansembe aweyule.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:5

Mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi chinai la mweziwo, madzulo, pali Paska wa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:4

Izi ndi nyengo zoikika za Yehova, misonkhano yopatulika, zimene muzilalikira pa nyengo zoikika zao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:2

Nena ndi ana a Israele, nuti nao, Nyengo zoikika za Yehova zimene muzilalikira zikhale misonkhano yopatulika, ndizo nyengo zanga zoikika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 13:10

Chifukwa chake uzikasunga lemba ili pa nyengo yake chaka ndi chaka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 12:24-27

Ndipo muzisunga chinthu ichi chikhale lemba la kwa inu, ndi kwa ana anu ku nthawi zonse. Ndipo kudzakhala, pamene mulowa m'dziko limene Yehova adzakupatsani, monga analankhula, muzisunga kutumikira kumeneku. Ndipo kudzakhala, pamene ana anu adzanena ndi inu, Kutumikiraku muli nako nkutani? Mudzati, Ndiko nsembe ya Paska wa Yehova, amene anapitirira nyumba za ana a Israele mu Ejipito, pamene anakantha Aejipito, napulumutsa nyumba zathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 28:17-18

Ndipo tsiku lakhumi ndi chisanu la mwezi uwu pali zikondwerero; masiku asanu ndi awiri azidya mkate wopanda chotupitsa. Tsiku loyamba pali kusonkhana kopatulika; musamachita ntchito ya masiku ena;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 29:1

Ndipo mwezi wachisanu ndi chiwiri, tsiku loyamba la mweziwo, muzikhala nako kusonkhana kopatulika; musamachita ntchito ya masiku ena; likukhalireni inu tsiku lakuliza malipenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 12:14

Ndipo tsiku lino lidzakhala kwa inu chikumbutso, muzilisunga la chikondwerero cha Yehova; ku mibadwo yanu muzilisunga la chikondwerero, likhale lemba losatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 16:1

Samalirani mwezi wa Abibu, kuti muzichitira Yehova Mulungu wanu Paska; popeza m'mwezi wa Abibu Yehova Mulungu wanu anakutulutsani m'dziko la Ejipito usiku.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 34:22

Ndipo uzichita chikondwerero cha Masabata, ndicho chikondwerero cha Zipatso zoyamba za Masika a tirigu, ndi chikondwerero cha Kututa pakutha pa chaka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 23:14-16

Muzindichitira Ine madyerero katatu m'chaka. Uzisunga chikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa; masiku asanu ndi awiri uzidya mkate wopanda chotupitsa, monga ndinakuuza, nyengo yoikika, mwezi wa Abibu, pakuti m'menemo unatuluka mu Ejipito; koma asaoneke munthu pamaso panga opanda kanthu; ndi chikondwerero cha Masika, zipatso zoyamba za ntchito zako, zimene udazibzala m'munda; ndi chikondwerero cha Kututa, pakutha chaka, pamene ututa ntchito zako za m'munda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 16:13-14

Mudzichitire chikondwerero cha Misasa masiku asanu ndi awiri, mutasunga za padwale ndi za mopondera mphesa; nimukondwere m'madyerero mwanu, inu, ndi ana anu aamuna, ndi ana anu aakazi, ndi antchito anu aamuna, ndi antchito anu aakazi, ndi Mlevi, ndi mlendo, ndi mwana wamasiye, ndi mkazi wamasiye okhala m'mudzi mwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 16:10

Ndipo muchitire Yehova Mulungu wanu chikondwerero cha Masabata, ndiwo msonkho waufulu wa dzanja lanu, umene mupereke monga Yehova Mulungu wanu akudalitsani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 14:16

Ndipo kudzachitika kuti otsala onse a amitundu onse anadzawo kulimbana ndi Yerusalemu, adzakwera chaka ndi chaka kulambira mfumu Yehova wa makamu, ndi kusunga chikondwerero cha Misasa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 7:2

Koma chikondwerero cha Ayuda cha Misasa, linayandikira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 2:13

Ndipo Paska wa Ayuda unayandikira, ndipo Yesu anakwera kunka ku Yerusalemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 6:4

Ndipo Paska, chikondwerero cha Ayuda, anayandikira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 2:1

Ndipo pakufika tsiku la Pentekoste, anali onse pamodzi pamalo amodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 12:3-4

Ndipo pakuona kuti kudakondweretsa Ayuda, anaonjezapo nagwiranso Petro. Ndipo awo ndi masiku a mkate wopanda chotupitsa. Ndipo m'mene adamgwira, anamuika m'ndende, nampereka kwa magulu anai a alonda, lonse anaianai, amdikire iye; ndipo anafuna kumtulutsa kudza naye kwa anthu atapita Paska.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 25:10

Ndipo muchipatule chaka cha makumi asanu, ndi kulalikira kwa onse okhala m'dzikomo kuti akhale aufulu; muchiyese chaka choliza lipenga; ndipo mubwerere munthu aliyense ku zakezake, ndipo mubwerere yense ku banja lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 33:20

Tayang'ana pa Ziyoni, mzinda wa zikondwerero zathu; maso ako adzaona, Yerusalemu malo a phee, chihema chimene sichidzasunthidwa, zichiri zake sizidzazulidwa konse, zingwe zake sizidzadulidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 11:55

Koma Paska wa Ayuda anali pafupi; ndipo ambiri anakwera kunka ku Yerusalemu kuchoka kuminda, asanafike Paska, kukadziyeretsa iwo okha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:44

Ndipo Mose anafotokozera ana a Israele nyengo zoikika za Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 29:12

Ndipo tsiku lakhumi ndi chisanu la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzikhala nako kusonkhana kopatulika; musamachita ntchito ya masiku ena, koma muchitire Yehova madyerero masiku asanu ndi awiri;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezara 6:22

nasunga chikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa masiku asanu ndi awiri ndi chimwemwe; pakuti Yehova adawakondweretsa, nawatembenuzira mtima wa mfumu ya Asiriya, kulimbitsa manja ao mu ntchito ya nyumba ya Mulungu, Mulungu wa Israele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 10:22

Koma kunali phwando la kukonzetsanso mu Yerusalemu; nyengoyo ndi yachisanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 10:10

Momwemo tsiku lakukondwera inu, ndi nyengo zoikidwa zanu, ndi poyamba miyezi yanu, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza, ndi pa nsembe zanu zoyamika; ndipo akhale kwa inu chikumbutso pamaso pa Mulungu wanu; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 29:7

Ndipo tsiku la khumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri uwu muzikhala nako kusonkhana kopatulika; pamenepo mudzichepetse, musamagwira ntchito;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 35:2

Masiku asanu ndi limodzi azigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri muliyese lopatulika, Sabata lakupuma la Yehova: aliyense agwira ntchito pamenepo, aphedwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 20:6

Ndipo tinapita m'ngalawa kuchokera ku Filipi, atapita masiku a mkate wopanda chotupitsa, ndipo popita masiku asanu tinawapeza ku Troasi; pamenepo tinatsotsa masiku asanu ndi awiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mafumu 23:21

Ndipo mfumu inalamulira anthu onse, kuti, Mchitireni Yehova Mulungu wanu Paska, monga mulembedwa m'buku ili la chipangano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Estere 9:22

ndiwo masiku amene Ayuda anapumula pa adani ao; ndi mwezi wachisoni unawasandulikira wakukondwera, ndi wamaliro ukhale tsiku lokoma, awayese masiku amadyerero ndi akukondwera, akutumizirana magawo, ndi akupatsa zaufulu kwa osauka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:32

Likhale ndi inu Sabata lakupumula; ndipo mudzichepetse; tsiku lachisanu ndi chinai madzulo, kuyambira madzulo kufikira madzulo musunge Sabata lanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 12:17

Ndipo muzisunga chikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa; pakuti tsiku lomwe lino ndinatulutsa makamu anu m'dziko la Ejipito; chifukwa chake muzisunga tsiku lino m'mibadwo yanu, lemba losatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 7:37

Koma tsiku lomaliza, lalikululo la chikondwerero, Yesu anaimirira nafuula, ndi kunena, Ngati pali munthu akumva ludzu, adze kwa Ine, namwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 8:19

Atero Yehova wa makamu: Kusala kwa mwezi wachinai, ndi kusala kwa mwezi wachisanu, ndi kusala kwa mwezi wachisanu ndi chiwiri, ndi kusala kwa mwezi wakhumi kukhale kwa nyumba ya Yuda chimwemwe ndi chikondwerero, ndi nyengo zoikika zosekerera; chifukwa chake kondani choonadi ndi mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 9:13

Munthu akakhala woyera, wosakhala paulendo, koma akaleka kuchita Paska, amsadze munthuyo kwa anthu a mtundu wake; popeza sanabwere nacho chopereka cha Yehova pa nyengo yake yoikidwa, munthuyu asenze kuchimwa kwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 35:17

Ndipo ana a Israele okhalako anachita Paska nthawi yomweyo, ndi chikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa masiku asanu ndi awiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 25:6

Ndipo m'phiri limeneli Yehova wa makamu adzakonzera anthu ake onse phwando la zinthu zonona, phwando la vinyo wa pamitsokwe, la zinthu zonona za mafuta okhaokha, la vinyo wansenga wokuntha bwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 30:29

Inu mudzakhala ndi nyimbo, monga usiku, podya phwando lopatulika; ndi mtima wokondwa, monga pomuka wina ndi chitoliro, kufikira kuphiri la Yehova, kuthanthwe la Israele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 30:26

Momwemo munali chimwemwe chachikulu mu Yerusalemu; pakuti kuyambira masiku a Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israele simunachitike chotero mu Yerusalemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 122:1

Ndinakondwera m'mene ananena nane, Tiyeni kunyumba ya Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 42:4

Ndidzikumbukira izi ndipo nditsanulira moyo wanga m'kati mwa ine, pakuti ndinkapita ndi unyinji wa anthu, ndinawatsogolera kunyumba ya Mulungu, ndi mau akuimbitsa ndi kuyamika, ndi unyinji wakusunga dzuwa lokondwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 27:9

Ndipo itapita nthawi yambiri, ndipo unayambokhala woopsa ulendowo, popezanso nyengo ya kusala chakudya idapita kale, Paulo anawachenjeza,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 7:8

Kwerani inu kunka kuphwando; sindikwera Ine kuphwando ili tsopano apa; pakuti nthawi yanga siinakwanire.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:5

Koma ananena iwo, pa nthawi ya chikondwerero iai, kuti pasakhale phokoso la anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:1

Zitapita izi panali chikondwerero cha Ayuda; ndipo Yesu anakwera kunka ku Yerusalemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 46:9

Koma pofika anthu a m'dziko pamaso pa Yehova m'zikondwerero zoikika, iye amene alowera njira ya kuchipata cha kumpoto kudzalambira, atulukire njira ya kuchipata cha kumwera; ndi iye amene alowera njira ya kuchipata cha kumwera, atulukire njira ya kuchipata cha kumpoto; asabwerere njira ya chipata anadzeracho, koma atulukire m'tsogolo mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:37

Izi ndi nyengo zoikika za Yehova, zimene muzilalikira zikhale misonkhano yopatulika, kukabwera nayo nsembe yamoto kwa Yehova, nsembe yopsereza, ndi nsembe yaufa, nsembe yophera, ndi nsembe yothira, yonse pa tsiku lakelake;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 81:3

Ombani lipenga, pokhala mwezi, utakula mwezi, tsiku la phwando lathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nehemiya 8:18

Anawerenganso m'buku la chilamulo cha Mulungu tsiku ndi tsiku, kuyambira tsiku loyamba kufikira tsiku lotsiriza. Nachita chikondwerero masiku asanu ndi awiri; ndi tsiku lachisanu ndi chitatu ndilo msonkhano woletsa, monga mwa malemba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Estere 9:27-28

Ayuda anakhazikitsa ichi, nadzilonjezetsa okha, ndi mbeu yao, ndi onse akuphatikana nao, chingalekeke, kuti adzasunga masiku awa awiri monga mwalembedwa, ndi monga mwa nyengo yao yoikika, chaka ndi chaka; ndi kuti masikuwa adzakumbukika ndi kusungika mwa mibadwo yonse, banja lililonse, dziko lililonse, ndi mzinda uliwonse; ndi kuti masiku awa sadzalekeka mwa Ayuda, kapena kusiyidwa chikumbukiro chao mwa mbeu yao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 25:11

Muchiyese chaka cha makumi asanucho choliza lipenga, musamabzala, kapena kucheka zophuka zokha m'mwemo; kapena kucheka mphesa zake za mipesa yosadzombola.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 10:2

Dzipangire malipenga awiri asiliva; uwasule mapangidwe ake; uchite nao poitana khamu, ndi poyendetsa a m'zigono.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mafumu 12:32

Ndipo Yerobowamu anaika madyerero mwezi wachisanu ndi chitatu, tsiku lakhumi ndi chisanu la mwezi olingana ndi madyerero aja a ku Yuda, napereka nsembe paguwa la nsembe; anatero mu Betele, nawaphera nsembe anaang'ombe aja anawapanga, naika mu Betele ansembe a misanje imene anaimanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 45:17

Ndipo udindo wa kalonga ndiwo kupereka nsembe zopsereza, ndi nsembe zaufa, ndi nsembe zothira, pachikondwerero, ndi pokhala mwezi, ndi pa masabata; pa zikondwerero zonse zoikika a nyumba ya Israele; ndipo apereke nsembe yauchimo, ndi nsembe yaufa, ndi nsembe yopsereza, ndi nsembe zamtendere, kuchitira chotetezera nyumba ya Israele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yoweli 2:15

Ombani lipenga mu Ziyoni, patulani tsiku losala, lalikirani msonkhano woletsa,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 25:12

Popeza ndicho chaka choliza lipenga; muchiyese chopatulika, mudye zipatso zake kunja kwa munda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 14:12

Ndipo tsiku loyamba la mikate yopanda chotupitsa, pamene amapha Paska, ophunzira ananena naye, Mufuna tinke kuti, tikakonze mkadyereko Paska?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 22:7

Ndipo tsiku la mikate yopanda chotupitsa linafika, limene inayenera kuphedwa nsembe ya Paska.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 22:1

Ndipo chikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa chinayandikira, ndicho chotchedwa Paska.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:17

Ndipo tsiku loyamba la mkate wopanda chotupitsa, ophunzira anadza kwa Yesu, nati, Mufuna tikakonzere kuti Paska, kuti mukadye?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga Wamuyaya, Wamkulu ndi Wamphamvu, Inu nokha ndinu Woyenera ulemerero ndi ulemu wonse! Pa tsiku lapaderali kwa ambiri a ife omwe tiri pano, ndikukuthokozani chifukwa cha thanzi ndi mtendere umene mutipatse kuti tisangalale ndi anansi ndi abale. Dalitsani onse omwe tidzakhala m'msonkhano uno, kuti tidziwane kumverana, kumvana, kukambirana, ndi kulemekezana maganizo, kuti ntchito iyi ikhale yaulemerero wanu ndipo Mzimu Woyera wanu udzioneke m'mitima mwathu ndipo tilandire kuchokera m'dzanja lanu chimene mukufuna kuti tikhale nacho. Mawu anu amati: "Taona, ndikulamula kuti ulimbike mtima ndi kukhala wolimba; usachite mantha kapena kuzengereza, pakuti Yehova Mulungu wako adzakhala nawe kulikonse kumene upita." Titumizireni, Ambuye, chisomo ndi mphamvu zanu kuti chikondi chanu chitsogolere mapazi athu onse; kuti tithe kuyika luso lathu kukutumikirani Inu. Bwerani, Ambuye, ndipo mutenge ulamuliro wa miyoyo yathu ndi maluso athu. Dalitsani ndi kubwezeretsa mphamvu za omwe adachita nawo pakukonzekera msonkhano uno, sungani mitima yawo ndi kuwapatsa chitukuko. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa