Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 122:1 - Buku Lopatulika

1 Ndinakondwera m'mene ananena nane, Tiyeni kunyumba ya Yehova.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Ndinakondwera m'mene ananena nane, Tiyeni kunyumba ya Yehova.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Ndidasangalala pamene adandiwuza kuti, “Tiyeni tipite ku Nyumba ya Chauta.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 122:1
27 Mawu Ofanana  

Ndinalandira mboni zanu zikhale cholandira chosatha; pakuti ndizo zokondweretsa mtima wanga.


Ndinafuulira kwa Yehova mu msauko wanga, ndipo anandivomereza.


Ndikweza maso anga kumapiri: Thandizo langa lidzera kuti?


Ndikweza maso anga kwa Inu, kwa Inu wakukhala kumwamba.


Akadapanda kukhala nafe Yehova, anene tsono Israele;


Iwo akukhulupirira Yehova akunga phiri la Ziyoni, losasunthika, likhazikika kosatha.


Pobweza Yehova ukapolo wa Ziyoni, tinakhala ngati anthu akulota.


Akapanda kumanga nyumba Yehova, akuimanga agwiritsa ntchito chabe; akapanda kusunga mzinda Yehova, mlonda adikira chabe.


Wodala yense wakuopa Yehova, wakuyenda m'njira zake.


Anandisautsa kawirikawiri kuyambira ubwana wanga, anene tsono Israele;


M'mozamamo ndinakufuulirani, Yehova.


Yehova, mtima wanga sunadzikuze ndi maso anga sanakwezeke; ndipo sindinatsate zazikulu, kapena zodabwitsa zondiposa.


Yehova, kumbukirani Davide kuzunzika kwake konse.


Onani, nkokoma ndi kokondweretsa ndithu kuti abale akhale pamodzi!


Taonani, lemekezani Yehova, atumiki a Yehova inu nonse, akuimirira m'nyumba ya Yehova usiku.


Yehova, ndikonda chikhalidwe cha nyumba yanu, ndi malo akukhalamo ulemerero wanu.


Ndidzikumbukira izi ndipo nditsanulira moyo wanga m'kati mwa ine, pakuti ndinkapita ndi unyinji wa anthu, ndinawatsogolera kunyumba ya Mulungu, ndi mau akuimbitsa ndi kuyamika, ndi unyinji wakusunga dzuwa lokondwera.


Tinapangirana upo wokoma, tinaperekeza khamu la anthu popita kunyumba ya Mulungu.


Pakuti tsiku limodzi m'mabwalo anu likoma koposa masiku ambirimbiri akukhala pena. Kukhala ine wapakhomo m'nyumba ya Mulungu wanga, kundikonda ine koposa kugonera m'mahema a choipa.


Ndipo anthu ambiri adzanka, nati, Tiyeni tikwere kunka kuphiri la Yehova, kunyumba ya Mulungu wa Yakobo; ndipo Iye adzatiphunzitsa za njira zake, ndipo tidzayenda m'mayendedwe ake; chifukwa mu Ziyoni mudzatuluka chilamulo, ndi mau a Yehova kuchokera mu Yerusalemu.


Pakuti lidzafika tsiku, limene alonda a pa mapiri a Efuremu adzafuula, Ukani inu, tikwere ku Ziyoni kwa Yehova Mulungu wathu.


Kalongayo tsono, polowa iwo alowe pakati pao, ndipo potuluka iwo atulukire pamodzi.


Ndipo amitundu ambiri adzamuka, nadzati, Tiyeni, tikwere kuphiri la Yehova, ndi kunyumba ya Mulungu wa Yakobo; kuti Iye atiphunzitse njira zake, ndipo tidzayenda m'mabande ake; pakuti ku Ziyoni kudzatuluka chilamulo, ndi ku Yerusalemu mau a Yehova.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa