Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 122 - Buku Lopatulika


Apempherera mtendere wa Yerusalemu
Nyimbo yokwerera; ya Davide.

1 Ndinakondwera m'mene ananena nane, Tiyeni kunyumba ya Yehova.

2 Mapazi athu alinkuima m'zipata zanu, Yerusalemu

3 Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda woundana bwino:

4 Kumene akwerako mafuko, ndiwo mafuko a Yehova; akhale mboni ya kwa Israele, Ayamike dzina la Yehova.

5 Pakuti pamenepo anaika mipando ya chiweruzo, mipando ya nyumba ya Davide.

6 Mupempherere mtendere wa Yerusalemu; akukonda inu adzaona phindu.

7 M'linga mwako mukhale mtendere, m'nyumba za mafumu mukhale phindu.

8 Chifukwa cha abale anga ndi mabwenzi anga, ndidzanena tsopano, Mukhale mtendere mwa inu.

9 Chifukwa cha nyumba ya Yehova Mulungu wathu ndidzakufunira zokoma.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa