Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Miyambo 3 - Buku Lopatulika


Malangizo a kuopa, kukhulupirira, ndi kumvera Yehova

1 Mwananga, usaiwale malamulo anga, mtima wako usunge malangizo anga;

2 pakuti adzakuonjezera masiku ambiri, ndi zaka za moyo ndi mtendere.

3 Chifundo ndi choonadi zisakusiye; uzimange pakhosi pako; uzilembe pamtima pako;

4 motero udzapeza chisomo ndi nzeru yabwino, pamaso pa Mulungu ndi anthu.

5 Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako;

6 umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

7 Usadziyese wekha wanzeru; opa Yehova, nupatuke pazoipa;

8 mitsempha yako idzalandirapo moyo, ndi mafupa ako uwisi.

9 Lemekeza Yehova ndi chuma chako, ndi zinthu zako zonse zoyambirira kucha;

10 motero nkhokwe zako zidzangoti thee, mbiya zako zidzasefuka vinyo.

11 Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova, ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwake;

12 pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda; monga atate mwana amene akondwera naye.


Phindu la Nzeru

13 Wodala ndi wopeza nzeru, ndi woona luntha;

14 pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva, phindu lake liposa golide woyengeka.

15 Mtengo wake uposa ngale; ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye.

16 Masiku ambiri ali m'dzanja lamanja lake; chuma ndi ulemu m'dzanja lake lamanzere.

17 Njira zake zili zokondweretsa, mayendedwe ake onse ndiwo mtendere.

18 Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira; wakuiumirira ngwodala.

19 Yehova anakhazika dziko ndi nzeru; naika zamwamba ndi luntha.

20 Zakuya zinang'ambika ndi kudziwa kwake; thambo ligwetsa mame.

21 Mwananga, zisachokere kumaso ako; sunga nzeru yeniyeni ndi kulingalira;

22 ndipo mtima wako udzatengapo moyo, ndi khosi lako chisomo.

23 Pompo udzayenda m'njira yako osaopa, osaphunthwa phazi lako.

24 Ukagona, sudzachita mantha; udzagona tulo tokondweretsa.

25 Usaope zoopsa zodzidzimutsa, ngakhale zikadza zopasula oipa;

26 pakuti Yehova adzalimbitsa mtima wako, nadzasunga phazi lako lingakodwe.


Malangizo ena osiyana

27 Oyenera kulandira zabwino usawamane; pokhoza dzanja lako kuwachitira zabwino.

28 Usanene kwa mnzako, Ukabwerenso, ndipo mawa ndidzakupatsa; pokhala uli nako kanthu.

29 Usapangire mnzako chiwembu; popeza akhala nawe pafupi osatekeseka.

30 Usakangane ndi munthu chabe, ngati sanakuchitire choipa.

31 Usachitire nsanje munthu wachiwawa; usasankhe njira yake iliyonse.

32 Pakuti wamphulupulu anyansa Yehova; koma chinsinsi chake chili ndi oongoka.

33 Yehova atemberera za m'nyumba ya woipa; koma adalitsa mokhalamo olungama.

34 Anyozadi akunyoza, koma apatsa akufatsa chisomo.

35 Anzeru adzalandira ulemu cholowa chao; koma opusa adzakweza manyazi.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa