Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Miyambo 3:1 - Buku Lopatulika

1 Mwananga, usaiwale malamulo anga, mtima wako usunge malangizo anga;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Mwananga, usaiwale malamulo anga, mtima wako usunge malangizo anga;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Mwana wanga, usaiŵale malangizo angaŵa, koma mtima wako usunge malamulo anga.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.

Onani mutuwo Koperani




Miyambo 3:1
31 Mawu Ofanana  

Ndinawabisa mau anu mumtima mwanga, kuti ndisalakwire Inu.


Penyani kuzunzika kwanga, nimundilanditse; pakuti sindiiwala chilamulo chanu.


Ndidzadzikondweretsa nao malemba anu; sindidzaiwala mau anu.


Ndinasochera ngati nkhosa yotayika; funani mtumiki wanu; pakuti sindiiwala malamulo anu.


Mundizindikiritse, ndipo ndidzasunga malamulo anu; ndidzawasamalira ndi mtima wanga wonse.


Anandikulunga nazo zingwe za oipa; koma sindinaiwale chilamulo chanu.


Sindidzaiwala malangizo anu nthawi zonse; popeza munandipatsa nao moyo.


Ndidzamkhutitsa ndi masiku ambiri, ndi kumuonetsera chipulumutso changa.


ndi kuwachitira chifundo anthu zikwizikwi a iwo amene akondana ndi Ine, nasunga malamulo anga.


Mwananga, tamva mwambo wa atate wako, ndi kusasiya chilangizo cha amai ako;


Imvi ndiyo korona wa ulemu, idzapezedwa m'njira ya chilungamo.


Mwananga, ukalandira mau anga, ndi kusunga malamulo anga;


Mwananga, undipatse mtima wako, maso ako akondwere ndi njira zanga.


Kuti angamwe, naiwale malamulo, naweruze mokhota anthu onse osautsidwa.


pakuti ndikuphunzitsani zabwino; musasiye chilangizo changa.


Asachoke kumaso ako; uwasunge m'kati mwa mtima wako.


Tenga nzeru, tenga luntha; usaiwale, usapatuke pa mau a m'kamwa mwanga;


Kodi nzeru siitana, luntha ndi kukweza mau ake?


Nzeru yamanga nyumba yake, yasema zoimiritsa zake zisanu ndi ziwiri;


Galamuka, galamuka, imirira Yerusalemu amene unamwa m'dzanja la Yehova chikho cha ukali wake; iwe wamwa mbale ya chikho chonjenjemeretsa ndi kuchigugudiza.


Koma ili ndi pangano limene ndidzapangana ndi nyumba ya Israele atapita masiku aja, ati Yehova; ndidzaika chilamulo changa m'kati mwao, ndipo m'mtima mwao ndidzachilemba; ndipo ndidzakhala Mulungu wao, nadzakhala iwo anthu anga;


Anthu anga aonongeka chifukwa cha kusadziwa; popeza unakana kudziwa, Inenso ndikukaniza, kuti usakhale wansembe wanga; popeza waiwala chilamulo cha Mulungu wako, Inenso ndidzaiwala ana ako.


Dzichenjerani, mungaiwale chipangano cha Yehova Mulungu wanu, chimene anapangana nanu, ndi kuti mungadzipangire fano losema, chifaniziro cha kanthu kalikonse Yehova Mulungu wanu anakuletsani.


Chokhachi, dzichenjerani nokha, ndi kusunga moyo wanu mwachangu, kuti mungaiwale zinthuzi adaziona maso anu, ndi kuti zisachoke kumtima kwanu masiku onse a moyo wanu; koma muzidziwitsa ana anu ndi zidzukulu zanu.


Lemekeza atate wako ndi amai ako, monga Yehova Mulungu wako anakulamulira; kuti masiku ako achuluke, ndi kuti chikukomere, m'dziko limene Yehova Mulungu wako akupatsa iwe.


Muziyenda m'njira yonse imene Yehova Mulungu wanu anakulamulirani, kuti mukakhale ndi moyo, ndi kuti chikukomereni, ndi kuti masiku anu achuluke m'dziko limene mudzakhala nalo lanulanu.


Muzisamalira kuchita malamulo onse amene ndikuuzani lero lino, kuti mukhale ndi moyo, ndi kuchuluka, ndi kulowa, ndi kulandira dziko limene Yehova analumbirira makolo anu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa