Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 100 - Buku Lopatulika


Olengedwa ndi Mulungu amlemekeze
Salimo la Chiyamiko.

1 Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi.

2 Tumikirani Yehova ndi chikondwerero: Idzani pamaso pake ndi kumuimbira mokondwera.

3 Dziwani kuti Yehova ndiye Mulungu; Iyeyu anatilenga, ndipo ife ndife ake; ndife anthu ake ndi nkhosa zapabusa pake.

4 Lowani kuzipata zake ndi chiyamiko, ndi kumabwalo ake ndi chilemekezo: Myamikeni; lilemekezeni dzina lake.

5 Pakuti Yehova ndiye wabwino; chifundo chake chimanka muyaya; ndi chikhulupiriko chake ku mibadwomibadwo.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa