Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 138 - Buku Lopatulika


Davide ayamika Mulungu pa kukhulupirika kwake, naneneratu kuti mafumu onse adzatero
Salimo la Davide.

1 Ndidzakuyamikani ndi mtima wanga wonse; ndidzaimba zakukulemekezani patsogolo pa milungu.

2 Ndidzagwadira kuloza ku Kachisi wanu woyera, ndi kuyamika dzina lanu, chifukwa cha chifundo chanu ndi choonadi chanu; popeza munakuzitsa mau anu koposa dzina lanu lonse.

3 Tsiku loitana ine, munandiyankha, munandilimbitsa ndi mphamvu m'moyo mwanga.

4 Mafumu onse a padziko lapansi adzakuyamikani, Yehova, popeza adamva mau a pakamwa panu.

5 Ndipo adzaimbira njira za Yehova; pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.

6 Angakhale Yehova ngwokwezeka, apenyanso wopepukayo; koma wodzikuza amdziwira kutali.

7 Ndingakhale ndiyenda pakati pa nsautso, mudzandipatsa moyo; mudzatambasula dzanja lanu pa mkwiyo wa adani anu, ndipo dzanja lanu lamanja lidzandipulumutsa.

8 Yehova adzanditsirizira za kwa ine: Chifundo chanu, Yehova, chifikira kunthawi zonse: Musasiye ntchito za manja anu.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa