Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 135 - Buku Lopatulika


Mulungu alemekezedwa pa ukulu wake. Mafano ndi achabe

1 Aleluya; Lemekezani dzina la Yehova! Lemekezani inu atumiki a Yehova.

2 Inu akuimirira m'nyumba ya Yehova, m'mabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.

3 Lemekezani Yehova; pakuti Yehova ndiye wabwino; muimbire zolemekeza dzina lake; pakuti nkokondweretsa kutero.

4 Pakuti Yehova anadzisankhira Yakobo, Israele, akhale chuma chake chenicheni.

5 Pakuti ndidziwa kuti Yehova ndi wamkulu, ndi Ambuye wathu aposa milungu yonse.

6 Chilichonse chimkonda Yehova achichita, kumwamba ndi padziko lapansi, m'nyanja ndi mozama monse.

7 Akweza mitambo ichokere ku malekezero a dziko lapansi; ang'animitsa mphezi zidzetse mvula; atulutsa mphepo mosungira mwake.

8 Anapanda oyamba a Ejipito, kuyambira munthu kufikira zoweta.

9 Anatumiza zizindikiro ndi zodabwitsa pakati pako, Ejipito iwe, pa Farao ndi pa omtumikira onse.

10 Ndiye amene anapanda amitundu ambiri, napha mafumu amphamvu;

11 Sihoni mfumu ya Aamori, ndi Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a Kanani:

12 Ndipo anapereka dziko lao likhale cholowa, cholowa cha kwa Israele anthu ake.

13 Dzina lanu, Yehova, likhala kosatha; chikumbukiro chanu, Yehova, kufikira mibadwomibadwo.

14 Pakuti Yehova adzaweruza anthu ake, koma adzaleka atumiki ake.

15 Mafano a amitundu ndiwo siliva ndi golide, ntchito ya manja a anthu.

16 Pakamwa ali napo koma osalankhula; maso ali nao, koma osapenya;

17 makutu ali nao, koma osamva; inde, pakamwa pao palibe mpweya.

18 Akuwapanga adzafanana nao; inde, onse akuwakhulupirira.

19 A nyumba ya Israele inu, lemekezani Yehova: A nyumba ya Aroni inu, lemekezani Yehova:

20 A nyumba ya Levi inu, lemekezani Yehova: Inu akuopa Yehova, lemekezani Yehova.

21 Alemekezedwe Yehova kuchokera mu Ziyoni, amene akhala mu Yerusalemu. Aleluya.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa