Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 16 - Buku Lopatulika


Munthu wokhulupirira Mulungu akhazikika mtima, osaopa kutayika
Mikitamu wa Davide.

1 Ndisungeni ine, Mulungu: pakuti ndakhulupirira Inu.

2 Ndinati kwa Yehova, Inu ndinu Ambuye wanga, ndilibe chabwino china choposa Inu.

3 Za oyera mtima okhala padziko lapansi, iwo ndiwo omveka mbiri, mwa iwowo muli chikondwero changa chonse.

4 Zidzachuluka zisoni zao za iwo otsata Mulungu wina. Sindidzathira nsembe zao zamwazi, ndipo sindidzatchula maina ao pakamwa panga.

5 Yehova ndiye gawo la cholowa changa ndi chikho changa, ndinu wondigwirira cholandira changa.

6 Zingwe zandigwera mondikondweretsa; inde cholowa chokoma ndili nacho.

7 Ndidzadalitsa Yehova, amene anandichitira uphungu, usikunso impso zanga zindilangiza.

8 Ndaika Yehova patsogolo panga nthawi zonse; popeza ali padzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.

9 Chifukwa chake wasekera mtima wanga, nukondwera ulemu wanga; mnofu wanganso udzakhala mokhazikika.

10 Pakuti simudzasiya moyo wanga kumanda; simudzalola wokondedwa wanu avunde.

11 Mudzandidziwitsa njira ya moyo, pankhope panu pali chimwemwe chokwanira; m'dzanja lanu lamanja muli zokondweretsa zomka muyaya.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa