Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 146 - Buku Lopatulika


Chifooko cha munthu, chikhulupiriko cha Mulungu

1 Aleluya; Ulemekeze Yehova, moyo wanga.

2 Ndidzalemekeza Yehova m'moyo mwanga; ndidzaimbira zomlemekeza Mulungu wanga pokhala ndi moyo ine.

3 Musamakhulupirira zinduna, kapena mwana wa munthu, amene mulibe chipulumutso mwa iye.

4 Mpweya wake uchoka, abwerera kunka kunthaka yake; tsiku lomwelo zotsimikiza mtima zake zitayika.

5 Wodala munthu amene akhala naye Mulungu wa Yakobo kuti amthandize, chiyembekezo chake chili pa Yehova, Mulungu wake.

6 Amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili m'mwemo. Ndiye wakusunga choonadi kosatha,

7 ndiye wakuchitira chiweruzo osautsika; ndiye wakupatsa anjala chakudya; Yehova amasula akaidi.

8 Yehova apenyetsa osaona; Yehova aongoletsa onse owerama; Yehova akonda olungama.

9 Yehova asunga alendo; agwiriziza mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye; koma akhotetsa njira ya oipa.

10 Yehova adzachita ufumu kosatha, Mulungu wako, Ziyoni, ku mibadwomibadwo. Aleluya.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa