Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


MAVESI Odziwika

MAVESI Odziwika

Mawu a Mulungu ndi amphamvu ndipo amasintha moyo wanga. Pali mavesi ambiri amene timawamva kawirikawiri ndipo ali ndi mphamvu yosintha miyoyo yathu. Angasinthe maganizo athu, moyo wathu wonse. Mavesi amenewa timaphunzira nthawi zonse kuti tiwagwiritse ntchito pa moyo wathu watsiku ndi tsiku.

"Ndingathe kuchita zonse mwa Khristu amene amandipatsa mphamvu." (Afilipi 4:13) Uwu ndi umodzi mwa mavesi amene timaphunzira nthawi zonse, ndipo timaugwiritsa ntchito nthawi imene tikutaya mtima.

"Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapereka Mwana wake wobadwa yekha, kuti yense wakukhulupirira Iye asatayike, koma akhale nawo moyo wosatha." (Yohane 3:16) Uwu ndi umodzi mwa mavesi ofunika kwambiri, ndipo nthawi zambiri ndi umodzi mwa mavesi oyamba kumva ukayamba kumudziwa Ambuye Yesu. Pali mavesi ambiri ofunika, ndipo apa mutha kuwapeza.




Miyambo 1:7

Kuopa Yehova ndiko chiyambi cha kudziwa; opusa anyoza nzeru ndi mwambo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:5-6

Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako; umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:7

Nzeru ipambana, tatenga nzeru; m'kutenga kwako konseko utenge luntha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 9:10

Chiyambi cha nzeru ndicho kuopa Yehova; kudziwa Woyerayo ndiko luntha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:5

Koma wina wa inu ikamsowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, amene apatsa kwa onse modzala manja, niwosatonza; ndipo adzampatsa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 2:6

Pakuti Yehova apatsa nzeru; kudziwa ndi kuzindikira kutuluka m'kamwa mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:2

Pakudza kudzikuza padzanso manyazi; koma nzeru ili ndi odzichepetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:16

Kodi kulandira nzeru sikupambana ndi golide, kulandira luntha ndi kusankhika koposa siliva?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:20

Tamvera uphungu, nulandire mwambo, kuti ukhale wanzeru pa chimaliziro chako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:15

Njira ya chitsiru njolungama pamaso pakepake; koma wanzeru amamvera uphungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:33

Kuopa Yehova ndiko mwambo wanzeru; ndipo chifatso chitsogolera ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:10

Kudzikuza kupikisanitsa; koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:29

Wosakwiya msanga apambana kumvetsa; koma wansontho akuza utsiru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:8

Wolandira nzeru akonda moyo wake; wosunga luntha adzapeza zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:1

Mayankhidwe ofatsa abweza mkwiyo; koma mau owawitsa aputa msunamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:19

Pochuluka mau zolakwa sizisoweka; koma wokhala chete achita mwanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:27

Wopanda chikamwakamwa apambana kudziwa; ndipo wofatsa mtima ali wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:11

Chitsiru chivumbulutsa mkwiyo wake wonse; koma wanzeru auletsa nautontholetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:3

Wochenjera aona zoipa, nabisala; koma achibwana angopitirira, nalipitsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:13-14

Wodala ndi wopeza nzeru, ndi woona luntha; pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva, phindu lake liposa golide woyengeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 8:11

Pakuti nzeru iposa ngale, ndi zonse tizifunitsa sizilingana nayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:22

Zolingalira zizimidwa popanda upo; koma pochuluka aphungu zikhazikika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:1

Wokonda mwambo akonda kudziwa; koma wakuda chidzudzulo apulukira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:3-4

Nzeru imangitsa nyumba; luntha liikhazikitsa. Ndinapita pamunda wa waulesi, polima mphesa munthu wosowa nzeru. Taonani, ponsepo panamera minga, ndi kuwirirapo khwisa; tchinga lake lamiyala ndi kupasuka. Pamenepo ndinayang'ana ndi kuganizira, ndinaona ndi kulandira mwambo. Tulo tapang'ono, kungoodzera pang'ono, kungomanga manja pang'ono m'kugona, ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala; ndi kusauka kwako ngati munthu wachikopa. Kudziwa kudzaza zipinda zake ndi chuma chonse chofunika cha mtengo wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:12

Pakuti nzeru itchinjiriza monga ndalama zitchinjiriza; koma kudziwa kupambana, chifukwa nzeru isunga moyo wa eni ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:23

Masewero a chitsiru ndiwo kuchita zoipa; koma masewero a wozindikira ndiwo nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:15

Mtima wa wozindikira umaphunzira; khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:11

Kulingalira kwa munthu kuchedwetsa mkwiyo; ulemerero wake uli wakuti akhululukire cholakwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:23

Chinjiriza mtima wako koposa zonse uzisunga; pakuti magwero a moyo atulukamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:8

Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo; koma chitsiru cholongolola chidzagwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:16

Wanzeru amaopa nasiya zoipa; koma wopusa amanyada osatekeseka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:14

Nyumba ndi chuma ndizo cholowa cha atate; koma mkazi wanzeru achokera kwa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:15

Alipo golide ndi ngale zambiri; koma milomo yodziwa ndiyo chokometsera cha mtengo wapatali.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:5

Zoganizira za wakhama zichulukitsadi katundu; koma yense wansontho angopeza umphawi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:30

Kulibe nzeru ngakhale luntha ngakhale uphungu wotsutsana ndi Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:17

Tchera makutu ako, numvere mau a anzeru, nulozetse mtima wako kukadziwa zanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:5

Mwamuna wanzeru ngwamphamvu; munthu wodziwa ankabe nalimba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:7

Usadziyese wekha wanzeru; opa Yehova, nupatuke pazoipa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:1-2

Mwananga, usaiwale malamulo anga, mtima wako usunge malangizo anga; motero nkhokwe zako zidzangoti thee, mbiya zako zidzasefuka vinyo. Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova, ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwake; pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda; monga atate mwana amene akondwera naye. Wodala ndi wopeza nzeru, ndi woona luntha; pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva, phindu lake liposa golide woyengeka. Mtengo wake uposa ngale; ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye. Masiku ambiri ali m'dzanja lamanja lake; chuma ndi ulemu m'dzanja lake lamanzere. Njira zake zili zokondweretsa, mayendedwe ake onse ndiwo mtendere. Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira; wakuiumirira ngwodala. Yehova anakhazika dziko ndi nzeru; naika zamwamba ndi luntha. pakuti adzakuonjezera masiku ambiri, ndi zaka za moyo ndi mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 9:9

Ukachenjeza wanzeru adzakulitsa nzeru yake; ukaphunzitsa wolungama adzaonjezera kuphunzira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:1

Mwana wanzeru akondweretsa atate; koma mwana wopusa amvetsa amake chisoni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:30

Chipatso cha wolungama ndi mtengo wa moyo; ndipo wokola mtima ali wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:20

Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru: koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:1

Mkazi yense wanzeru amanga banja lake; koma wopusa alipasula ndi manja ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:8

Nzeru ya wochenjera ndiyo yakuti azindikire njira yake; koma utsiru wa opusa ndiwo chinyengo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:12

Ilipo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka; koma matsiriziro ake ndi njira za imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:14

Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa; koma m'kamwa mwa opusa mudya utsiru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:31

Khutu lomvera chidzudzulo cha moyo lidzakhalabe mwa anzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:20

Wolabadira mau adzapeza bwino; ndipo wokhulupirira Yehova adala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:24

Nzeru ili pamaso pa wozindikira; koma maso a wopusa ali m'malekezero a dziko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:4

Mau a m'kamwa mwa munthu ndiwo madzi akuya; kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wodzala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:6-7

Milomo ya wopusa ifikitsa makangano; ndipo m'kamwa mwake muputa kukwapulidwa. M'kamwa mwa wopusa mumuononga, milomo yake ikhala msampha wa moyo wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:2

Kukhumba kosadziwa sikuli kwabwino; ndipo wofulumira ndi mapazi ake amachimwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:1

Vinyo achita chiphwete, chakumwa chaukali chisokosa; wosochera nazo alibe nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:1

Mbiri yabwino ifunika kopambana chuma chambiri; kukukomera mtima anzako kuposa siliva ndi golide.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 23:23

Gula ntheradi, osaigulitsa; nzeru, ndi mwambo, ndi luntha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:6

Pakuti udzaponya nkhondo yako ndi upo, ndi kupulumuka pochuluka aphungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 25:12

Monga mphete yagolide ndi chipini chagolide woyengeka, momwemo wanzeru wodzudzula pa khutu lomvera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 26:12

Kodi uona munthu wodziyesa wanzeru? Ngakhale chitsiru chidzachenjera koma ameneyo ai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:26

Wokhulupirira mtima wakewake ali wopusa; koma woyenda mwanzeru adzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:16

Zapang'ono, ulikuopa Yehova, zipambana ndi katundu wambiri pokhala phokoso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:5-6

Tenga nzeru, tenga luntha; usaiwale, usapatuke pa mau a m'kamwa mwanga; usasiye nzeru, ndipo idzakusunga; uikonde, idzakutchinjiriza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:21-22

Mwananga, zisachokere kumaso ako; sunga nzeru yeniyeni ndi kulingalira; ndipo mtima wako udzatengapo moyo, ndi khosi lako chisomo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:3

Pereka zochita zako kwa Yehova, ndipo zolingalira zako zidzakhazikika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:14

Popanda upo wanzeru anthu amagwa; koma pochuluka aphungu pali chipulumutso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:10

Chidzudzulo chilowa m'kati mwa wozindikira, kopambana ndi kukwapula wopusa kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:32

Wosakwiya msanga aposa wamphamvu; wolamulira mtima wake naposa wolanda mzinda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:1

Woipa athawa palibe momthamangitsa; koma olungama alimba mtima ngati mkango.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:18

Uphungu utsimikiza zolingalira, ponya nkhondo utapanga upo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:10

Ukalefuka tsiku la tsoka mphamvu yako ichepa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:4

Mkazi wodekha ndiye korona wa mwamuna wake; koma wochititsa manyazi akunga chovunditsa mafupa a mwamunayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:12

Chiyembekezo chozengereza chidwalitsa mtima; koma pakufika chifunirocho ndicho mtengo wa moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:9

Wobisa cholakwa afunitsa chikondano; koma wobwerezabwereza mau afetsa ubwenzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:2

Wopusa sakondwera ndi kuzindikira; koma kungovumbulutsa za m'mtima mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:21

Lilime lili ndi mphamvu pa imfa ndi moyo; wolikonda adzadya zipatso zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:6

Anthu ambiri abukitsa yense kukoma mtima kwake; koma ndani angapeze munthu wokhulupirika?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 25:28

Wosalamulira mtima wake akunga mzinda wopasuka wopanda linga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 26:20

Posowa nkhuni moto ungozima; ndi popanda kazitape makangano angoleka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:20

Kodi uona munthu wansontho m'mau ake? Ngakhale chitsiru chidzachenjera, koma ameneyo ai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 2:26

Pakuti yemwe Mulungu amuyesa wabwino ampatsa nzeru ndi chidziwitso ndi chimwemwe; koma wochimwa amlawitsa vuto la kusonkhanitsa ndi kukundika, kuti aperekere yemwe Mulungu amuyesa wabwino. Ichinso ndi chabe ndi kungosautsa mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:5

Kumva chidzudzulo cha anzeru kupambana kumva nyimbo ya zitsiru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:9

Mtima wa munthu ulingalira njira yake; koma Yehova ayendetsa mapazi ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:13

Gwira mwambo, osauleka; uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:1

Usanyadire zamawa, popeza sudziwa tsiku lina lidzabala chiyani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:16

Mkwiyo wa chitsiru udziwika posachedwa; koma wanzeru amabisa manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:25

Nkhawa iweramitsa mtima wa munthu; koma mau abwino aukondweretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:4

Kuchiza lilime ndiko mtengo wa moyo; koma likakhota liswa moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:17

Bwenzi limakonda nthawi zonse; ndipo mbale anabadwira kuti akuthandize pooneka tsoka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:6

Phunzitsa mwana poyamba njira yake; ndipo angakhale atakalamba sadzachokamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:12

Udani upikisanitsa; koma chikondi chikwirira zolakwa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:13

Kazitape woyendayenda amawanditsa zinsinsi; koma wokhulupirika mtima abisa mau.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:20

Chinyengo chili m'mitima ya oganizira zoipa; koma aphungu a mtendere amakondwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:21

Wonyoza anzake achimwa; koma wochitira osauka chifundo adala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:24

Mau okoma ndiwo chisa cha uchi, otsekemera m'moyo ndi olamitsa mafupa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:24

Woyanjana ndi ambiri angodziononga; koma lilipo bwenzi lipambana ndi mbale kuumirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:24-25

Usayanjane ndi munthu wokwiya msanga; ngakhale kupita ndi mwamuna waukali; kuti ungaphunzire mayendedwe ake, ndi kutengera moyo wako msampha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 23:15-16

Mwananga, mtima wako ukakhala wanzeru, mtima wanga wa inedi udzakondwa. Imso zanga zidzasangalala, polankhula milomo yako zoongoka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 25:11

Mau oyenera a pa nthawi yake akunga zipatso zagolide m'nsengwa zasiliva.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 26:27

Wokumba dzenje adzagwamo, wogubuduza mwala, udzabweranso pa iye mwini.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:17

Chitsulo chinola chitsulo; chomwecho munthu anola nkhope ya mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 10:10

Chitsulo chikakhala chosathwa, ndipo ukaleka kunola, uzipambana kulimbikira; koma nzeru ipindulira pochenjeza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:13

Wobisa machimo ake sadzaona mwai; koma wakuwavomereza, nawasiya adzachitidwa chifundo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:23

Kuopa Yehova kupatsa moyo; wokhala nako adzakhala wokhuta; zoipa sizidzamgwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:17

Wosunga mwambo ali m'njira ya moyo; koma wosiya chidzudzulo asochera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:25

Ilipo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka, koma matsiriziro ake ndi njira za imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:23

Wosunga m'kamwa mwake ndi lilime lake asunga moyo wake kumavuto.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:12

Wochenjera aona zoipa, nabisala; koma achibwana angopitirira, nalipitsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:13

Mtima wokondwa usekeretsa nkhope; koma moyo umasweka ndi zowawa za m'mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:35

Anzeru adzalandira ulemu cholowa chao; koma opusa adzakweza manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:1

Muyeso wonyenga unyansa Yehova; koma mulingo wamphumphu umsekeretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 6:16-19

Zilipo zinthu zisanu ndi chimodzi Yehova azida; ngakhale zisanu ndi ziwiri zimnyansa: Maso akunyada, lilime lonama, ndi manja akupha anthu osachimwa; mtima woganizira ziwembu zoipa, mapazi akuthamangira mphulupulu m'mangum'mangu; mboni yonama yonong'ona mabodza, ndi wopikisanitsa abale.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:27

Mzimu wa munthu ndiwo nyali ya Yehova; usanthula m'kati monse mwa mimba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:25

Kuopa anthu kutchera msampha; koma wokhulupirira Yehova adzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:3

Wogwira pakamwa pake asunga moyo wake; koma woyasamula milomo yake adzaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:24

Wolekerera mwanake osammenya amuda; koma womkonda amyambize kumlanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 23:12

Lozetsa mtima wako kumwambo, ndi makutu ako ku mau anzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:23

M'ntchito zonse muli phindu; koma kulankhulalankhula kungopatsa umphawi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:18

Kunyada kutsogolera kuonongeka; mtima wodzikuza ndi kutsogolera kuphunthwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:7

Wolemera alamulira osauka; ndipo wokongola ndiye kapolo wa womkongoletsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:10

Dzina la Yehova ndilo nsanja yolimba; wolungama athamangiramo napulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:20

Munthu wokhulupirika ali ndi madalitso ambiri; koma wokangaza kulemera sadzapulumuka chilango.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:4

Mphotho ya chifatso ndi kuopa Yehova ndiye chuma, ndi ulemu, ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:11

Zakudya zikwanira wolima minda yake; koma wotsata anthu opanda pake asowa nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:4

Moyo wa waulesi ukhumba osalandira kanthu; koma moyo wa akhama udzalemera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:15

Wachibwana akhulupirira mau onse; koma wochenjera asamalira mayendedwe ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:29

Kodi upenya munthu wofulumiza ntchito zake? Adzaima pamaso pa mafumu, osaima pamaso pa anthu achabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:2

Njira zonse za munthu zilungama pamaso pake; koma Yehova ayesa mitima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:18

Wosunga mkuyu adzadya zipatso zake; wosamalira ambuyake adzalemekezedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:25

Mtima wa mataya udzalemera; wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:17

Wochitira waumphawi chifundo abwereka Yehova; adzambwezera chokoma chakecho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:5

Oipa samvetsetsa chiweruzo; koma omwe afuna Yehova amvetsetsa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:22

Madalitso a Yehova alemeretsa, saonjezerapo chisoni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:13

Wotseka makutu ake polira waumphawi, nayenso adzalira koma osamvedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:27

Kuopa Yehova ndiko kasupe wa moyo, kupatutsa kumisampha ya imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:9

Mwini diso lamataya adzadala; pakuti apatsa osauka zakudya zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:27-28

Oyenera kulandira zabwino usawamane; pokhoza dzanja lako kuwachitira zabwino. Usanene kwa mnzako, Ukabwerenso, ndipo mawa ndidzakupatsa; pokhala uli nako kanthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:29

Yehova atalikira oipa; koma pemphero la olungama alimvera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:18-19

Koma mayendedwe a olungama akunga kuunika kwa mbandakucha, kunkabe kuwala kufikira usana woti mbee. Njira ya oipa ikunga mdima; sadziwa chimene chiwaphunthwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:3

Maso a Yehova ali ponseponse, nayang'anira oipa ndi abwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:17

Wokonda zoseketsa adzasauka; wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 23:17-18

Mtima wako usachitire nsanje akuchimwawo; koma opabe Yehova tsiku lonse. Pakutitu padzakhala mphotho; ndipo chiyembekezo chako sichidzalephereka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:23

Udziwitsitse zoweta zako zili bwanji, samalira magulu ako;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:11

Mwini muyeso ndi mulingo wolungama ndiye Yehova; ndiyenso anapanga miyala yonse yoyesera ya m'thumba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:19-20

Yehova anakhazika dziko ndi nzeru; naika zamwamba ndi luntha. pakuti adzakuonjezera masiku ambiri, ndi zaka za moyo ndi mtendere. Zakuya zinang'ambika ndi kudziwa kwake; thambo ligwetsa mame.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:5

Mboni yonama sidzakhala yosalangidwa; wolankhula mabodza sadzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:3-4

Chifundo ndi choonadi zisakusiye; uzimange pakhosi pako; uzilembe pamtima pako; Usakangane ndi munthu chabe, ngati sanakuchitire choipa. Usachitire nsanje munthu wachiwawa; usasankhe njira yake iliyonse. Pakuti wamphulupulu anyansa Yehova; koma chinsinsi chake chili ndi oongoka. Yehova atemberera za m'nyumba ya woipa; koma adalitsa mokhalamo olungama. Anyozadi akunyoza, koma apatsa akufatsa chisomo. Anzeru adzalandira ulemu cholowa chao; koma opusa adzakweza manyazi. motero udzapeza chisomo ndi nzeru yabwino, pamaso pa Mulungu ndi anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Zikomo Ambuye, inu ndinu wochiritsa wanga, wopereka wanga, ndi mlonda wanga. Inu ndiye mumamenya nkhondo zanga, ndipo munditsogolera kuchoka ulemerero kupita ku ulemerero. Mu dzina lamphamvu la Yesu, zikomo chifukwa cha mawu anu, ndi chakudya changa chabwino, ndipo mmenemo muli kukula kwanga kwauzimu. Ndiwo amaunikira njira yanga ndi kunditeteza kuti ndisagwe. Mundipatse nzeru zanu kuti ndikudziweni ndi kukumvetsani kudzera mwa iwo. Inu ndiye mundichirikiza ndi kundiuza kuti, "Usachite mantha, ndikuthandizani." Lero ndikupemphani kuti mukhalitse ufumu wanu m'moyo wanga ndi m'banja langa. Zikomo chifukwa mawu anu amati, "Inu ndinu pothawirapo panga ndi mphamvu yanga; thandizo langa m'masautso." Pa nthawi yovutayi ndikudziwa kuti mumandiyang'anira, ndipo ndikulengeza kuti ngakhale nditayenda m'chigwa cha mthunzi wa imfa, sindidzaopa choipa chilichonse. Muzimitse mdima wonse, ndipo muwalitse kuwala kwa Khristu m'moyo wanga ndi m'nyumba mwanga. M'dzina la Yesu. Amene.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa