Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 115 - Buku Lopatulika


Mulungu ndi wa ulemerero, mafano ndiwo achabe

1 Kwa ife ai, Yehova, kwa ife ai, koma kwa dzina lanu patsani ulemerero, chifukwa cha chifundo chanu, ndi choonadi chanu.

2 Aneneranji amitundu, Ali kuti Mulungu wao?

3 Koma Mulungu wathu ndiye ali m'mwamba; achita chilichonse chimkonda.

4 Mafano ao ndiwo a siliva ndi golide, ntchito za manja a anthu.

5 Pakamwa ali napo, koma osalankhula; maso ali nao, koma osapenya;

6 makutu ali nao, koma osamva; mphuno ali nazo, koma osanunkhiza;

7 manja ali nao, koma osagwira; mapazi ali nao, koma osayenda; kapena sanena pammero pao.

8 Adzafanana nao iwo akuwapanga; ndi onse akuwakhulupirira.

9 Israele, khulupirira Yehova: Ndiye mthandizi wao ndi chikopa chao.

10 Nyumba ya Aroni, khulupirira Yehova: Ndiye mthandizi wao, ndi chikopa chao.

11 Inu akuopa Yehova, khulupirirani Yehova; ndiye mthandizi wao ndi chikopa chao.

12 Yehova watikumbukira; adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israele; adzadalitsa nyumba ya Aroni.

13 Adzadalitsa iwo akuopa Yehova, aang'ono ndi aakulu.

14 Yehova akuonjezereni dalitso, inu ndi ana anu.

15 Odalitsika inu a kwa Yehova, wakulenga kumwamba ndi dziko lapansi.

16 Kunena za kumwamba, kumwamba ndiko kwa Yehova; koma dziko lapansi analipereka kwa ana a anthu.

17 Akufa salemekeza Yehova, kapena aliyense wakutsikira kuli chete:

18 Koma ife tidzalemekeza Yehova kuyambira tsopano kufikira nthawi yonse. Aleluya.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa