Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


MAVESI A MPHAMVU

MAVESI A MPHAMVU

Ndimakondwa kwambiri kudziwa kuti ngakhale mavuto amene tingakumane nawo pa moyo wathu, tili ndi mphamvu ya Mulungu mwa ife. Ana a Mulungu sitimakhala tokha pa vuto lililonse, Mulungu nthawi zonse amakhala nafe. Ambuye amatitsogolera, akumenyera nkhondo zanu ndi kukudzazitsani ndi mphamvu Yake kuti mupambane pa vuto limene mukukumanalo.

Mu 2 Akorinto 12:9-10, Mulungu akutiuza kuti chisomo Chake chikwanira chifukwa mphamvu Yake imaonekera bwino mu kufooka kwathu. Ndi chinthu chokondweretsa kudziwa kuti pakati pa mavuto amene mukulimbana nawo, kufooka kwanu, Mulungu ali pomwepo akutsimikizira mphamvu Yake mwa inu.

Mulungu amatipatsa mphamvu Yake. Mu Luka 24:49, akuti, “Ndipo onani, Ine ndikutumizirani lonjezo la Atate wanga; koma inu khalani mumzinda wa Yerusalemu kufikira mutavala mphamvu yochokera kumwamba.”

Tili ndi Mulungu Wamphamvuyonse, palibe chomwe chingamulephere, angathe kuchita chilichonse. Mukhulupirire Iye ndipo adzagwira ntchito m'moyo wanu.




Chivumbulutso 12:11

Ndipo iwo anampambana iye chifukwa cha mwazi wa Mwanawankhosa, ndi chifukwa cha mau a umboni wao; ndipo sanakonde moyo wao kungakhale kufikira imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:46

Ndidzalankhulanso za umboni wanu pamaso pa mafumu, osachitapo manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 4:20

pakuti sitingathe ife kuleka kulankhula zimene tinaziona ndi kuzimva.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 43:10

Inu ndinu mboni zanga, ati Yehova, ndi mtumiki wanga, amene ndakusankha; kuti mundidziwe, ndi kundikhulupirira Ine, ndi kuzindikira, kuti Ine ndine; ndisanakhale Ine, panalibe Mulungu wolengedwa, ngakhale pambuyo panga sipadzakhala wina.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 11:4

Ndi chikhulupiriro Abele anapereka kwa Mulungu nsembe yoposa ija ya Kaini, imene anachitidwa umboni nayo kuti anali wolungama; nachitapo umboni Mulungu pa mitulo yake; ndipo momwemo iye, angakhale adafa alankhulabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:16

Pakuti Uthenga Wabwino sundichititsa manyazi; pakuti uli mphamvu ya Mulungu yakupulumutsa munthu aliyense wakukhulupirira; kuyambira Myuda, ndiponso Mgriki.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 22:15

Ndipo udzamkhalira Iye mboni kwa anthu onse, za izo udaziona ndi kuzimva.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 4:12

Munthu asapeputse ubwana wako; komatu khala chitsanzo kwa iwo okhulupirira, m'mau, m'mayendedwe, m'chikondi, m'chikhulupiriro, m'kuyera mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 22:22

Ndidzalalikira dzina lanu kwa abale anga, pakati pa msonkhano ndidzakulemekezani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 28:19

Chifukwa chake mukani, phunzitsani anthu a mitundu yonse, ndi kuwabatiza iwo m'dzina la Atate, ndi la Mwana, ndi la Mzimu Woyera:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:10

Iye amene amkhulupirira Mwana wa Mulungu ali nao umboni mwa iye; iye wosakhulupirira Mulungu anamuyesa Iye wonama; chifukwa sanakhulupirire umboni wa Mulungu anauchita wa Mwana wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 15:27

Ndipo inunso muchita umboni, pakuti muli ndi Ine kuyambira chiyambi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 3:15

koma mumpatulikitse Ambuye Khristu m'mitima yanu; okonzeka nthawi zonse kuchita chodzikanira pa yense wakukufunsani chifukwa cha chiyembekezo chili mwa inu, komatu ndi chifatso ndi mantha;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 71:15-16

Pakamwa panga padzafotokozera chilungamo chanu, ndi chipulumutso chanu tsiku lonse; pakuti sindidziwa mawerengedwe ake. Ndidzamuka mu mphamvu ya Ambuye Yehova; ndidzatchula chilungamo chanu, inde chanu chokha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 1:8

Komatu mudzalandira mphamvu, Mzimu Woyera atadza pa inu: ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ndi mu Yudeya monse, ndi mu Samariya, ndi kufikira malekezero ake a dziko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:16

Chomwecho muwalitse inu kuunika kwanu pamaso pa anthu, kuti pakuona ntchito zanu zabwino, alemekeze Atate wanu wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 1:8

Potero usachite manyazi pa umboni wa Ambuye wathu, kapena pa ine wandende wake; komatu umve masautso ndi Uthenga Wabwino, monga mwa mphamvu ya Mulungu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 10:32

Chifukwa chake yense amene adzavomereza Ine pamaso pa anthu, Inenso ndidzamvomereza iye pamaso pa Atate wanga wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 16:15

Ndipo ananena nao, Mukani kudziko lonse lapansi, lalikirani Uthenga Wabwino kwa olengedwa onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 66:16

Idzani, imvani, inu nonse akuopa Mulungu, ndipo ndidzafotokozera zonse anazichitira moyo wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 14:3

Chifukwa chake anakhala nthawi yaikulu nanenetsa zolimba mtima mwa Ambuye, amene anachitira umboni mau a chisomo chake, napatsa zizindikiro ndi zozizwa kuti zichitidwe ndi manja ao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:13

ndipo musapereke ziwalo zanu kuuchimo, zikhale zida za chosalungama; koma mudzipereke inu nokha kwa Mulungu, monga amoyo atatuluka mwa akufa, ndi ziwalo zanu kwa Mulungu zikhale zida za chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 15:58

Chifukwa chake, abale anga okondedwa, khalani okhazikika, osasunthika, akuchuluka mu ntchito ya Ambuye, nthawi zonse, podziwa kuti kuchititsa kwanu sikuli chabe mwa Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:1

Akulu tsono mwa inu ndiwadandaulira, ine mkulu mnzanu ndi mboni ya zowawa za Khristu, ndinenso wolawana nao ulemerero udzavumbulutsikawo:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 6:19

ndi ine ndemwe, kuti andipatse mau m'kunditsegulira m'kamwa molimbika, kuti ndizindikiritse anthu chinsinsicho cha Uthenga Wabwino,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 55:11

momwemo adzakhala mau anga amene atuluka m'kamwa mwanga, sadzabwerera kwa Ine chabe, koma adzachita chimene ndifuna, ndipo adzakula m'mene ndinawatumizira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 8:18

Ine ndine wakuchita umboni wa Ine ndekha, ndipo Atate amene anandituma Ine achita umboni wa Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 17:6

Pamene sanawapeze anakokera Yasoni ndi abale ena pamaso pa akulu a mzinda, nafuula kuti, Omwe aja asanduliza dziko lokhalamo anthu, afika kunonso;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 2:13

Ndipo mwa ichinso ife tiyamika Mulungu kosalekeza, kuti, pakulandira mau a Uthenga wa Mulungu, simunawalandire monga mau a anthu, komatu monga momwe ali ndithu, mau a Mulungu, amenenso achita mwa inu okhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:39

Musanthula m'malembo, popeza muyesa kuti momwemo muli nao moyo wosatha; ndipo akundichitira Ine umboni ndi iwo omwewo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:4

Mbadwo wina udzalemekezera ntchito zanu mbadwo unzake, ndipo udzalalikira zamphamvu zanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 3:33

Iye amene analandira umboni wake anaikapo chizindikiro chake kuti Mulungu ali woona.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 10:42

Ndipo anatilamulira ife tilalikire kwa anthu, ndipo tichite umboni kuti Uyu ndiye amene aikidwa ndi Mulungu akhale woweruza amoyo ndi akufa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:11

Ndipo uwu ndi umboniwo, kuti Mulungu anatipatsa ife moyo wosatha, ndipo moyo umene uli mwa Mwana wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 24:48

Inu ndinu mboni za izi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 1:9

Ine Yohane, mbale wanu ndi woyanjana nanu m'chisautso ndi ufumu ndi chipiriro zokhala mwa Yesu, ndinakhala pa chisumbu chotchedwa Patimosi, chifukwa cha mau a Mulungu ndi umboni wa Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 1:12

Chifukwa cha ichicho ndinamva zowawa izi; komatu sindichita manyazi; pakuti ndimdziwa Iye amene ndamkhulupirira, ndipo ndikopeka mtima kuti ali wa mphamvu ya kudikira chosungitsa changacho kufikira tsiku lijalo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:111

Ndinalandira mboni zanu zikhale cholandira chosatha; pakuti ndizo zokondweretsa mtima wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 9:16

Pakuti ngati ndilalikira Uthenga Wabwino ndilibe kanthu kakudzitamandira; pakuti chondikakamiza ndigwidwa nacho; pakuti tsoka ine ngati sindilalikira Uthenga Wabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 2:32

Yesu ameneyo, Mulungu anamuukitsa; za ichi tili mboni ife tonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 3:7-8

Komatu zonse zimene zinandipindulira, zomwezo ndinaziyesa chitayiko chifukwa cha Khristu. Komatu zenizeninso ndiyesa zonse zikhale chitayiko chifukwa cha mapambanidwe a chizindikiritso cha Khristu Yesu Ambuye wanga, chifukwa cha Iyeyu ndinatayikitsa zinthu zonse, ndipo ndiziyesa zapadzala, kuti ndikadzionjezere Khristu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 26:16

Komatu uka, imirira pa mapazi ako; pakuti chifukwa cha ichi ndinaonekera kwa iwe, kukuika iwe ukhale mtumiki ndi mboni ya izi wandionamo Ine, ndiponso ya izi ndidzakuonekeramo iwe;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 4:16

koma akamva zowawa ngati Mkhristu asachite manyazi; koma alemekeze Mulungu m'dzina ili.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 16:31

Ndipo iwo anati, Ukhulupirire Ambuye Yesu, ndipo udzapulumuka, iwe ndi apabanja ako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 22:20

Iye wakuchitira umboni izi, anena, Indetu; ndidza msanga. Amen; idzani, Ambuye Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 34:3

Bukitsani pamodzi ndine ukulu wa Yehova, ndipo tikweze dzina lake pamodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 3:8

Kwa ine wochepa ndi wochepetsa wa onse oyera mtima anandipatsa chisomo ichi ndilalikire kwa amitundu chuma chosalondoleka cha Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 52:7

Ha, akongolatu pamapiri mapazi a iye amene adza ndi uthenga wabwino, amene abukitsa mtendere, amene adza ndi uthenga wabwino wa zinthu zabwino, amene abukitsa chipulumutso; amene ati kwa Ziyoni, Mulungu wako ndi mfumu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 1:2

(ndipo moyowo unaonekera, ndipo tidaona, ndipo tichita umboni, ndipo tikulalikirani moyo wosathawo, umene unali kwa Atate, nuonekera kwa ife);

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 10:18

ndiponso adzamuka nanu kwa akazembe ndi mafumu chifukwa cha Ine, kukhala mboni ya kwa iwo, ndi kwa anthu akunja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:2

Odala iwo akusunga mboni zake, akumfuna ndi mtima wonse;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 17:18

Monga momwe munandituma Ine kudziko lapansi, Inenso ndinatuma iwo kudziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:12

Kudziwitsa ana a anthu zamphamvu zake, ndi ulemerero waukulu wa ufumu wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 5:29

Ndipo anayankha Petro ndi atumwi, nati, Tiyenera kumvera Mulungu koposa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 6:68-69

Simoni Petro anamyankha Iye, Ambuye, tidzamuka kwa yani? Inu muli nao mau a moyo wosatha. Ndipo ife tikhulupirira, ndipo tidziwa kuti Inu ndinu Woyera wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 1:24

Si kuti tichita ufumu pa chikhulupiriro chanu, koma tikhala othandizana nacho chimwemwe chanu; pakuti ndi chikhulupiriro muimadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 8:4

Pamenepo ndipo iwo akubalalitsidwa anapitapita nalalikira mauwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 11:28

Koma Iye anati, Inde, koma odala iwo akumva mau a Mulungu, nawasunga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 10:17

Chomwecho chikhulupiriro chidza ndi mbiri, ndi mbiri idza mwa mau a Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 12:1

Chifukwa chake ifenso, popeza tizingidwa nao mtambo waukulu wotere wa mboni, titaye cholemetsa chilichonse, ndi tchimoli limangotizinga, ndipo tithamange mwachipiriro makaniwo adatiikira, ndi kupenyerera woyambira ndi womaliza wa chikhulupiriro chathu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 1:8

Pakuti kutuluka kwa inu kudamveka mau a Ambuye, osati mu Masedoniya ndi Akaya mokha, komatu m'malo monse chikhulupiriro chanu cha kwa Mulungu chidatuluka; kotero kuti sikufunika kwa ife kulankhula kanthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 8:39

Pita kunyumba kwako, nufotokozere zazikuluzo anakuchitira iwe Mulungu. Ndipo iye anachoka, nalalikira kumzinda wonse zazikuluzo Yesu anamchitira iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:16

Mzimu yekha achita umboni pamodzi ndi mzimu wathu, kuti tili ana a Mulungu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:9

Koma inu ndinu mbadwa yosankhika, ansembe achifumu, mtundu woyera mtima, anthu a mwini wake, kotero kuti mukalalikire zoposazo za Iye amene anakuitanani mutuluke mumdima, mulowe kuunika kwake kodabwitsa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:14

Ndipo ife tapenyera, ndipo tichita umboni kuti Atate anatuma Mwana akhale Mpulumutsi wa dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 13:47

Pakuti kotero anatilamula Ambuye ndi kuti, Ndakuika iwe kuunika kwa amitundu, kuti udzakhala iwe chipulumutso kufikira malekezero a dziko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 96:3

Fotokozerani ulemerero wake mwa amitundu; zodabwitsa zake mwa mitundu yonse ya anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 1:27

Chokhachi, mayendedwe anu ayenere Uthenga Wabwino wa Khristu: kuti, ndingakhale nditi ndilinkudza ndi kuona inu, ndingakhale nditi ndili kwina, ndikamva za kwa inu, kuti muchilimika mu mzimu umodzi, ndi kugwirira pamodzi ndi moyo umodzi chikhulupiriro cha Uthenga Wabwino;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 5:20

Chifukwa chake tili atumiki m'malo mwa Khristu, monga ngati Mulungu alikudandaulira mwa ife; tiumiriza inu m'malo mwa Khristu, yanjanitsidwani ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 4:39

Ndipo m'mzinda muja anthu Asamariya ambiri anamkhulupirira Iye chifukwa cha mau a mkazi, wochita umboniyo, kuti, Anandiuza ine zinthu zilizonse ndinazichita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:7

Iyeyu anadza mwa umboni kudzachita umboni za kuunikaku, kuti onse akakhulupirire mwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 3:3

popeza mwaonetsedwa kuti muli kalata ya Khristu, wakumtumikira ndi ife, wosalembedwa ndi kapezi iai, koma ndi Mzimu wa Mulungu wamoyo; wosati m'magome amiyala, koma m'magome a mitima yathupi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 1:3

chimene tidachiona, ndipo tidachimva, tikulalikirani inunso, kuti inunso mukayanjane pamodzi ndi ife; ndipo chiyanjano chathu chilinso ndi Atate, ndipo ndi Mwana wake Yesu Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:26

Koma Nkhosweyo, Mzimu Woyera, amene Atate adzamtuma m'dzina langa, Iyeyo adzaphunzitsa inu zonse, nadzakumbutsa inu zinthu zonse zimene ndinanena kwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 1:6

monga umboni wa Khristu unakhazikika mwa inu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 5:32

Ndipo ife ndife mboni za zinthu izi; Mzimu Woyeranso, amene Mulungu anapatsa kwa iwo akumvera Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 40:10

Chilungamo chanu sindinachibise m'kati mwamtima mwanga; chikhulupiriko chanu ndi chipulumutso chanu ndinachinena; chifundo chanu ndi choonadi chanu sindinachibisire msonkhano waukulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 2:1-2

Ndipo ine, abale, m'mene ndinadza kwa inu, sindinadze ndi kuposa kwa mau, kapena kwa nzeru, polalikira kwa inu chinsinsi cha Mulungu. Koma kwa ife Mulungu anationetsera izi mwa Mzimu; pakuti Mzimu asanthula zonse, zakuya za Mulungu zomwe. Pakuti ndani wa anthu adziwa za munthu, koma mzimu wa munthuyu uli mwa iye? Momwemonso za Mulungu palibe wina azidziwa, koma Mzimu wa Mulungu. Koma sitinalandira ife mzimu wa dziko lapansi, koma Mzimu wa kwa Mulungu, kuti tikadziwe zimene zipatsidwa kwa ife ndi Mulungu kwaufulu. Zimenenso tilankhula, si ndi mau ophunzitsidwa ndi nzeru za munthu, koma ophunzitsidwa ndi Mzimu; ndi kulinganiza zamzimu ndi zamzimu. Koma munthu wa chibadwidwe cha umunthu salandira za Mzimu wa Mulungu: pakuti aziyesa zopusa; ndipo sangathe kuzizindikira, chifukwa ziyesedwa mwauzimu. Koma iye amene ali wauzimu ayesa zonse, koma iye yekha sayesedwa ndi mmodzi yense. Pakuti wadziwa ndani mtima wa Ambuye, kuti akamlangize Iye? Koma ife tili nao mtima wa Khristu. Pakuti ndinatsimikiza mtima kuti ndisadziwe kanthu mwa inu, koma Yesu Khristu, ndi Iye wopachikidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 3:11

Indetu, indetu, ndinena kwa iwe, Tilankhula chimene tichidziwa, ndipo tichita umboni za chimene tachiona; ndipo umboni wathu simuulandira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 12:4

Tsiku lomwelo mudzati, Muyamikire Yehova, bukitsani dzina lake, mulalikire machitidwe ake mwa mitundu ya anthu, munene kuti dzina lake lakwezedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:17

Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo, ndipo ndidzafotokozera ntchito za Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 1:12

Pakuti kudzitamandira kwathu ndiko umboni wa chikumbumtima chathu, kuti m'chiyero ndi kuona mtima kwa Mulungu, si m'nzeru ya thupi, koma m'chisomo cha Mulungu tinadzisunga m'dziko lapansi, koma koposa kwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 9:26

Pakuti aliyense amene adzachita manyazi chifukwa cha Ine ndi mau anga, Mwana wa Munthu adzachita manyazi chifukwa cha iye, pamene adzafika ndi ulemerero wake ndi wa Atate, ndi wa angelo oyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:15

Yohane achita umboni za Iye, nafuula nati, Uyu ndiye amene ndinanena za Iye, Wakudzayo pambuyo panga analipo ndisanabadwe ine; chifukwa anakhala woyamba wa ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 2:4

komatu monga Mulungu anativomereza kutiikiza Uthenga Wabwino, kotero tilankhula; osati monga okondweretsa anthu, koma Mulungu; amene ayesa mitima yathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:15

kuti mukakhale osalakwa ndi oona, ana a Mulungu opanda chilema pakati pa mbadwo wokhotakhota ndi wopotoka, mwa iwo amene muonekera monga mauniko m'dziko lapansi,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:15

Potero mwa Iye tipereke chiperekere nsembe yakuyamika Mulungu, ndiyo chipatso cha milomo yovomereza dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:8

pakuti kale munali mdima, koma tsopano muli kuunika mwa Ambuye; yendani monga ana a kuunika,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 3:16

ndi kukhala nacho chikumbumtima chabwino, kuti umo akunenerani, iwo akunenera konama mayendedwe anu abwino mu Khristu akachitidwe manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 107:2

Atere oomboledwa a Yehova, amene anawaombola m'dzanja la wosautsa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:1

Ndikudandaulirani inu tsono, ine wandende mwa Ambuye, muyende koyenera maitanidwe amene munaitanidwa nao,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 12:8

Ndipo ndinena kwa inu, Amene aliyense akavomereza Ine pamaso pa anthu, inde, Mwana wa Munthu adzamvomereza iye pamaso pa angelo a Mulungu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 20:24

Komatu sindiuyesa kanthu moyo wanga, kuti uli wa mtengo wake kwa ine ndekha; kotero kuti ndikatsirize njira yanga, ndi utumiki ndinaulandira kwa Ambuye Yesu, kuchitira umboni Uthenga Wabwino wa chisomo cha Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:7-8

Pakuti palibe mmodzi wa ife adzikhalira ndi moyo yekha, ndipo palibe mmodzi adzifera yekha. Pakuti tingakhale tili ndi moyo, tikhalira Ambuye moyo; kapena tikafa, tifera Ambuye; chifukwa chake tingakhale tili ndi moyo, kapena tikafa, tikhala ake a Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:88

Mundipatse moyo monga mwa chifundo chanu; ndipo ndidzasamalira mboni ya pakamwa panu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 24:14

Ndipo Uthenga uwu Wabwino wa Ufumu udzalalikidwa padziko lonse lapansi, ukhale mboni kwa anthu a mitundu yonse; ndipo pomwepo chidzafika chimaliziro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 4:2

lalikira mau; chita nao pa nthawi yake, popanda nthawi yake; tsutsa, dzudzula, chenjeza, ndi kuleza mtima konse ndi chiphunzitso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:38-39

Pakuti ndakopeka mtima kuti ngakhale imfa, ngakhale moyo, ngakhale angelo, ngakhale maufumu, ngakhale zinthu zilipo, ngakhale zinthu zilinkudza, ngakhale zimphamvu, ngakhale utali, ngakhale kuya, ngakhale cholengedwa china chilichonse, sichingadzakhoze kutisiyanitsa ife ndi chikondi cha Mulungu, chimene chili mwa Khristu Yesu Ambuye wathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Zikomo Ambuye, ndinu wochiritsa wanga, wopereka wanga, ndi mlonda wanga. Ndinu amene mumalungamira nkhondo zanga, ndi kunditsogolera kuchokera ku ulemerero kupita ku ulemerero. M'dzina lamphamvu la Yesu, ndikubwera kwa Inu, ndikukuthokozani chifukwa pemphero ndi chida champhamvu kwambiri chothetsera mavuto aliwonse, ndiye chinsinsi chotsegulira zitseko zonse. Ambuye, mwatiitana kukhala mchere wa dziko lapansi ndi kuunika kwa dziko, kuti tionetse ulemerero wanu ndi mphamvu zanu kulikonse kumene tingapite. Mu mau anu mukuti, "Ndipo ndakuyika iwe kuti ndionetse mphamvu yanga mwa iwe, ndi kuti dzina langa lidzalalikidwe pa dziko lonse lapansi." Ambuye Yesu, ndithandizeni kukhala wokhazikika ndi kupemphera nthawi zonse ndi pemphero lililonse ndi pembedzero mwa Mzimu, mundiphunzitse kukhala maso ndi kudzuka ngati wopempherera, ndikuteteza banja langa, mtundu wanga, ndi abale anga m'chikhulupiriro. M'dzina la Yesu, Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa