Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yohane 15:27 - Buku Lopatulika

27 Ndipo inunso muchita umboni, pakuti muli ndi Ine kuyambira chiyambi.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

27 Ndipo inunso muchita umboni, pakuti muli ndi Ine kuyambira chiyambi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

27 Inunso mudzandichitira umboni, popeza kuti mwakhala nane kuyambira pa chiyambi.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

27 Inunso mudzandichitira umboni Ine, popeza mwakhala nane kuchokera pachiyambi.”

Onani mutuwo Koperani




Yohane 15:27
21 Mawu Ofanana  

Chiyambi chake cha Uthenga Wabwino wa Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu.


Inu ndinu mboni za izi.


Ndipo iye amene anaona, wachita umboni, ndi umboni wake uli woona; ndipo iyeyu adziwa kuti anena zoona, kuti inunso mukakhulupirire.


Yemweyu ndiye wophunzira wakuchita umboni za izi, ndipo analembera izi; ndipo tidziwa kuti umboni wake ndi woona.


Komatu mudzalandira mphamvu, Mzimu Woyera atadza pa inu: ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ndi mu Yudeya monse, ndi mu Samariya, ndi kufikira malekezero ake a dziko.


ndipo anaonekera masiku ambiri ndi iwo amene anamperekeza Iye pokwera ku Yerusalemu kuchokera ku Galileya, amenewo ndiwo akumchitira umboni tsopano kwa anthu.


Koma pamene Silasi ndi Timoteo anadza potsika ku Masedoniya, Paulo anapsinjidwa ndi mau, nachitira umboni kwa Ayuda kuti Yesu ndiye Khristu.


Ndipo usiku wake Ambuye anaimirira pa iye, nati, Limbika mtima; pakuti monga wandichitira umboni ku Yerusalemu, koteronso uyenera kundichitira umboni ku Roma.


ndipo munamupha Mkulu wa moyo; amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa; za ichi ife tili mboni.


pakuti sitingathe ife kuleka kulankhula zimene tinaziona ndi kuzimva.


Ndipo atumwi anachita umboni ndi mphamvu yaikulu za kuuka kwa Ambuye Yesu; ndipo panali chisomo chachikulu pa iwo onse.


Akulu tsono mwa inu ndiwadandaulira, ine mkulu mnzanu ndi mboni ya zowawa za Khristu, ndinenso wolawana nao ulemerero udzavumbulutsikawo:


Mwa Silivano, mbale wathu wokhulupirika monga ndimayesa, ndalembera kwa inu mwachidule, ndi kudandaulira, ndi kuchita umboni, kuti chisomo choona cha Mulungu ndi ichi; m'chimenechi muimemo.


Ndipo ife tapenyera, ndipo tichita umboni kuti Atate anatuma Mwana akhale Mpulumutsi wa dziko lapansi.


amene anachita umboni za mau a Mulungu, ndi za umboni wa Yesu Khristu, zonse zimene adaziona.


Ine Yohane, mbale wanu ndi woyanjana nanu m'chisautso ndi ufumu ndi chipiriro zokhala mwa Yesu, ndinakhala pa chisumbu chotchedwa Patimosi, chifukwa cha mau a Mulungu ndi umboni wa Yesu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa