Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 119:2 - Buku Lopatulika

2 Odala iwo akusunga mboni zake, akumfuna ndi mtima wonse;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

2 Odala iwo akusunga mboni zake, akumfuna ndi mtima wonse;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

2 Ngodala amene amasunga malamulo a Chauta, amene amafunafuna Chauta ndi mtima wao wonse,

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 119:2
24 Mawu Ofanana  

nusunge chilangizo cha Yehova Mulungu wako, kuyenda m'njira zake, kusunga malemba ndi malamulo ndi maweruzo ndi umboni wake, monga mulembedwa m'chilamulo cha Mose, kuti ukachite mwa nzeru m'zonse ukachitazo, ndi kumene konse ukatembenukirako;


Perekani tsono mtima ndi moyo wanu kufunafuna Yehova Mulungu wanu; ndipo nyamukani ndi kumanga malo opatulika a Yehova Mulungu, kuti abwere nalo likasa la chipangano la Yehova, ndi zipangizo zopatulika za Mulungu, kunyumba imene idzamangidwira dzina la Yehova.


Ndipo m'ntchito iliyonse anaiyamba mu utumiki wa nyumba ya Mulungu, ndi m'chilamulo, ndi m'mauzo, kufuna Mulungu wake, anachita ndi mtima wake wonse, nalemerera nayo.


Kuti asamalire malemba ake, nasunge malamulo ake. Aleluya.


Ndinakufunani ndi mtima wanga wonse; ndisasokere kusiyana nao malamulo anu.


Ndinaletsa mapazi anga njira iliyonse yaoipa, kuti ndisamalire mau anu.


Mundichokere ochita zoipa inu; kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga.


Ndinaitanira Inu; ndipulumutseni, ndipo ndidzasamalira mboni zanu.


Muchitire chokoma mtumiki wanu kuti ndikhale ndi moyo; ndipo ndidzasamalira mau anu.


Mundichotsere chotonza, ndi chimpepulo; pakuti ndinasunga mboni zanu.


Mundiphunzitse, Yehova, njira ya malemba anu; ndidzaisunga kufikira kutha kwake.


Mundizindikiritse, ndipo ndidzasunga malamulo anu; ndidzawasamalira ndi mtima wanga wonse.


Yehova ndiye gawo langa: Ndinati ndidzasunga mau anu.


Odzikuza anandipangira bodza: Ndidzasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.


Mundipatse moyo monga mwa chifundo chanu; ndipo ndidzasamalira mboni ya pakamwa panu.


Mayendedwe onse a Yehova ndiwo chifundo ndi choonadi, kwa iwo akusunga pangano lake ndi mboni zake.


Mwananga, undipatse mtima wako, maso ako akondwere ndi njira zanga.


Ndipo mudzandifuna Ine, ndi kundipeza, pamene mundifuna ndi mtima wanu wonse.


Ndipo ndidzaika mzimu wanga m'kati mwanu, ndi kukuyendetsani m'malemba anga; ndipo mudzasunga maweruzo anga ndi kuwachita.


Yesu anayankha nati kwa iye, Ngati wina akonda Ine, adzasunga mau anga; ndipo Atate wanga adzamkonda, ndipo tidzadza kwa iye, ndipo tidzayesa kwa iye mokhalamo.


Koma mukafuna Yehova Mulungu wanu kumeneko, mudzampeza, ngati mumfunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.


Muzisunga mwachangu malamulo a Yehova Mulungu wanu, ndi mboni zake, ndi malemba ake, amene anakulamulirani.


ndipo muzikonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse, ndi mphamvu yanu yonse.


m'mene monse mtima wathu utitsutsa; chifukwa Mulungu ali wamkulu woposa mitima yathu, nazindikira zonse.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa