Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yohane 3:33 - Buku Lopatulika

33 Iye amene analandira umboni wake anaikapo chizindikiro chake kuti Mulungu ali woona.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

33 Iye amene analandira umboni wake anaikapo chizindikiro chake kuti Mulungu ali woona.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

33 Koma munthu akakhulupirira mau akeŵo, pamenepo amatsimikiza kuti Mulungu sanama.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

33 Munthu amene amawulandira akutsimikizira kuti Mulungu ndi woona.

Onani mutuwo Koperani




Yohane 3:33
17 Mawu Ofanana  

Gwirani ntchito si chifukwa cha chakudya chimene chitayika koma cha chakudya chimene chitsalira kumoyo wosatha, chimene Mwana wa Munthu adzakupatsani inu; pakuti ameneyo Atate, ndiye Mulungu, adamlembera chizindikiro.


Ndili nazo zambiri zakulankhula ndi zakuweruza za inu; koma wondituma Ine ali woona; ndipo zimene ndazimva kwa Iye, zomwezo ndilankhula kwa dziko lapansi.


Koma pamene ndikatsiriza ichi, ndi kuwasindikizira iwo chipatso ichi, ndidzapyola kwanu kupita ku Spaniya.


iye ndipo analandira chizindikiro cha mdulidwe, ndicho chosindikiza chilungamo cha chikhulupiriro, chomwe iye anali nacho asanadulidwe; kuti kotero iye akhale kholo la onse akukhulupirira, angakhale iwo sanadulidwe, kuti chilungamo chiwerengedwe kwa iwonso;


Ngati sindili mtumwi kwa ena, komatu ndili kwa inu; pakuti chizindikiro cha utumwi wanga ndi inu mwa Ambuye.


Koma Mulungu ali wokhulupirika, kuti mau athu a kwa inu sanakhale eya ndi iai.


amenenso anatisindikiza chizindikiro, natipatsa chikole cha Mzimu mu mitima yathu.


Mwa Iyeyo inunso, mutamva mau a choonadi, Uthenga Wabwino wa chipulumutso chanu, ndi kumkhulupirira Iye, munasindikizidwa chizindikiro ndi Mzimu Woyera wa lonjezano,


Ndipo musamvetse chisoni Mzimu Woyera wa Mulungu, amene munasindikizidwa chizindikiro mwa Iye, kufikira tsiku la maomboledwe.


Koma ndithu maziko a Mulungu aimika pokhazikika, ndi kukhala nacho chizindikiro ichi, Ambuye azindikira iwo amene ali ake; ndipo, Adzipatule kwa chosalungama yense wakutchula dzina la Ambuye.


Momwemo Mulungu, pofuna kuonetsera mochulukira kwa olowa a lonjezano kuti chifuniro chake sichisinthika, analowa pakati ndi lumbiro;


Tikanena kuti sitidachimwe, timuyesa Iye wonama, ndipo mau ake sakhala mwa ife.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa