Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 34:3 - Buku Lopatulika

3 Bukitsani pamodzi ndine ukulu wa Yehova, ndipo tikweze dzina lake pamodzi.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

3 Bukitsani pamodzi ndine ukulu wa Yehova, ndipo tikweze dzina lake pamodzi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

3 Lalikani pamodzi nane ukulu wa Chauta, tiyeni limodzi tiyamike dzina lake.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 34:3
18 Mawu Ofanana  

Mudzitamandire ndi dzina lake lopatulika; mitima yao ya iwo ofuna Yehova ikondwere.


Ndipo Davide anati kwa khamu lonse, Mulemekeze tsono Yehova Mulungu wanu. Ndi khamu lonse linalemekeza Yehova Mulungu wa makolo ao, nawerama, nalambira Yehova, ndi mfumu.


Hezekiya mfumu ndi akalonga nauzanso Alevi aimbire Yehova zomlemekeza ndi mau a Davide ndi a Asafu mlauli. Ndipo anaimbira zomlemekeza mokondwera, nawerama mitu yao, nalambira.


Afuule mokondwera nasangalale iwo akukondwera nacho chilungamo changa, ndipo anene kosalekeza, Abuke Yehova, amene akondwera ndi mtendere wa mtumiki wake.


Asekerere nakondwerere mwa Inu onse akufuna Inu; iwo akukonda chipulumutso chanu asaleke kunena, Abuke Yehova.


Lemekezani Mulungu wathu, mitundu ya anthu inu, ndipo mumveketse liu la chilemekezo chake.


Ndidzalemekeza dzina la Mulungu ndi kuliimbira, ndipo ndidzambukitsa ndi kumyamika.


Pakuti Yehova amvera aumphawi, ndipo sapeputsa am'ndende ake.


Atero Yehova, wanzeru asadzitamandire m'nzeru zake, wamphamvu asadzitamandire m'mphamvu yake, wachuma asadzitamandire m'chuma chake;


koma wakudzitamandira adzitamandire adzikweze umo, kuti ali wakuzindikira, ndi kundidziwa Ine, kuti ndine Yehova wakuchita zokoma mtima, chiweruziro, ndi chilungamo m'dziko lapansi, pakuti m'menemo ndikondwerera, ati Yehova.


Ndipo Maria anati, Moyo wanga ulemekeza Ambuye,


Zimenezo zidamveka kwa onse, Ayuda ndi Agriki, amene anakhala ku Efeso; ndipo mantha anagwera onsewo, ndipo dzina la Ambuye Yesu linakuzika.


monga mwa kulingiriritsa ndi chiyembekezo changa, kuti palibe chinthu chidzandichititsa manyazi, komatu mwa kulimbika mtima konse, monga nthawi yonse, tsopanonso Khristu adzakuzidwa m'thupi langa, kapena mwa moyo, kapena mwa imfa.


ndi kunena ndi mau aakulu, Opani Mulungu, mpatseni ulemerero; pakuti yafika nthawi ya chiweruziro chake; ndipo mlambireni Iye amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi ndi nyanja ndi akasupe amadzi.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa