Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


149 Mau a Mulungu Odziwa Zonse

149 Mau a Mulungu Odziwa Zonse


Masalimo 139:1-4

Munandisanthula, Yehova, nimundidziwa. kungakhale komweko dzanja lanu lidzanditsogolera, nilidzandigwira dzanja lanu lamanja. Ndipo ndikati, Koma mdima undiphimbe, ndi kuunika kondizinga kukhale usiku. Ungakhale mdima sudetsa pamaso panu, koma usiku uwala ngati usana; mdima ukunga kuunika. Pakuti Inu munalenga impso zanga; munandiumba ndisanabadwe ine. Ndikuyamikani chifukwa kuti chipangidwe changa nchoopsa ndi chodabwitsa; ntchito zanu nzodabwitsa; moyo wanga uchidziwa ichi bwino ndithu. Thupi langa silinabisikire Inu popangidwa ine mobisika, poombedwa ine monga m'munsi mwake mwa dziko lapansi. Ndisanaumbidwe ine maso anu anandipenya, ziwalo zanga zonse zinalembedwa m'buku mwanu, masiku akuti ziumbidwe, pakalibe chimodzi cha izo. Potero, Mulungu, ndiziyesa zolingalira zanu za mtengo wake ndithu! Mawerengedwe ake ndi ambirimbiri! Ndikaziwerenga zichuluka koposa mchenga: Ndikauka ndikhalanso nanu. Indedi, mudzaomba woipa, Mulungu: Ndipo amuna inu okhumba mwazi, chokani kwa ine. Inu mudziwa kukhala kwanga ndi kuuka kwanga, muzindikira lingaliro langa muli kutali. Popeza anena za Inu moipa, ndi adani anu atchula dzina lanu mwachabe. Kodi sindidana nao iwo akudana ndi Inu, Yehova? Ndipo kodi sindimva nao chisoni iwo akuukira Inu? Ndidana nao ndi udani weniweni, ndiwayesa adani. Mundisanthule, Mulungu, nimudziwe mtima wanga; mundiyese nimudziwe zolingalira zanga. Ndipo mupenye ngati ndili nao mayendedwe oipa, nimunditsogolere panjira yosatha. Muyesa popita ine ndi pogona ine, ndi njira zanga zonse muzolowerana nazo. Pakuti asanafike mau pa lilime langa, taonani, Yehova, muwadziwa onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 4:13

Ndipo palibe cholembedwa chosaonekera pamaso pake, koma zonse zikhala za pambalambanda ndi zovundukuka pamaso pake pa Iye amene tichita naye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:20

m'mene monse mtima wathu utitsutsa; chifukwa Mulungu ali wamkulu woposa mitima yathu, nazindikira zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:28

Kodi iwe sunadziwe? Kodi sunamve? Mulungu wachikhalire, Yehova, Mlengi wa malekezero a dziko lapansi, salefuka konse, salema; nzeru zake sizisanthulika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:3

Maso a Yehova ali ponseponse, nayang'anira oipa ndi abwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:5

Ambuye wathu ndi wamkulu ndi wa mphamvu zambiri; nzeru yake njosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 11:33-34

Ha! Kuya kwake kwa kulemera ndi kwa nzeru ndi kwa kudziwa kwake kwa Mulungu! Osasanthulikadi maweruzo ake, ndi njira zake nzosalondoleka! Pakuti anadziwitsa ndani mtima wake wa Ambuye? Kapena anakhala phungu wake ndani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 1:5

Ndisanakulenge iwe m'mimba ndinakudziwa, ndipo usanabadwe ndinakupatula iwe; ndinakuika kuti ukhale mneneri wa mitundu ya anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 37:16

Kodi mudziwa madendekeredwe ake a mitambo, zodabwitsa za Iye wakudziwa mwangwiro?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 5:21

Pakuti njira za munthu zili pamaso pa Yehova, asinkhasinkha za mayendedwe ake onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 10:30

komatu inu, matsitsi onse a m'mutu mwanu awerengedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 28:9

Ndipo iwe Solomoni mwana wanga, umdziwe Mulungu wa atate wako, umtumikire ndi mtima wangwiro ndi moyo waufulu; pakuti Yehova asanthula mitima yonse, nazindikira zolingirira zonse za maganizo; ukamfunafuna Iye udzampeza, koma ukamsiya Iye adzakusiya kosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:11

Yehova adziwa zolingalira za munthu, kuti zili zachabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 23:24

Kodi munthu angathe kubisala mobisika kuti ndisamuone iye? Ati Yehova. Kodi Ine sindidzala kumwamba ndi dziko lapansi? Ati Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 34:21

Pakuti maso ake ali panjira ya munthu aliyense, napenya moponda mwake monse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 33:13-15

Yehova apenyerera m'mwamba; aona ana onse a anthu. M'malo akhalamo Iye, amapenya pansi pa onse akukhala m'dziko lapansi. Iye amene akonza mitima ya iwo onse, amene azindikira zochita zao zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 2:10-11

Koma kwa ife Mulungu anationetsera izi mwa Mzimu; pakuti Mzimu asanthula zonse, zakuya za Mulungu zomwe. Pakuti ndani wa anthu adziwa za munthu, koma mzimu wa munthuyu uli mwa iye? Momwemonso za Mulungu palibe wina azidziwa, koma Mzimu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:16

Ndisanaumbidwe ine maso anu anandipenya, ziwalo zanga zonse zinalembedwa m'buku mwanu, masiku akuti ziumbidwe, pakalibe chimodzi cha izo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:2

Njira zonse za munthu zilungama pamaso pake; koma Yehova ayesa mitima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 55:8-9

Pakuti maganizo anga sali maganizo anu, ngakhale njira zanu sizili njira zanga, ati Yehova. Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, momwemo njira zanga zili zazitali kupambana njira zanu, ndi maganizo anga kupambana maganizo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 44:21

Mulungu sakadasanthula ichi kodi? Pakuti adziwa zinsinsi za mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:27

ndipo Iye amene asanthula m'mitima adziwa chimene achisamalira Mzimu, chifukwa apempherera oyera mtima monga mwa chifuniro cha Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 17:10

Ine Yehova ndisanthula mtima, ndiyesa impso, kuti ndimpatse munthu yense monga mwa njira zake, monga zipatso za ntchito zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:2

Inu mudziwa kukhala kwanga ndi kuuka kwanga, muzindikira lingaliro langa muli kutali.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:4

Awerenga nyenyezi momwe zili; azitcha maina zonsezi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:8

Chifukwa chake inu musafanane nao: pakuti Atate wanu adziwa zomwe muzisowa, inu musanayambe kupempha Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Danieli 2:22

Iye avumbulutsa zinthu zakuya ndi zinsinsi; adziwa zokhala mumdima, ndi kuunika kumakhala kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 21:22

Ngati pali munthu wakumphunzitsa Mulungu nzeru? Popeza Iye aweruza mlandu iwo okwezeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 2:24-25

Koma Yesu sanakhulupirire iwo kuti akhale nao, chifukwa Iye anadziwa anthu onse, ndipo sanasowe wina achite umboni za munthu; pakuti anadziwa Iye yekha chimene chinali mwa munthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 3:20

ndiponso Ambuye azindikira zolingirira za anzeru, kuti zili zopanda pake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 4:12-13

Pakuti mau a Mulungu ali amoyo, ndi ochitachita, ndi akuthwa koposa lupanga lakuthwa konsekonse, napyoza kufikira kugawira moyo ndi mzimu, ndi zimfundo ndi mafuta a m'mafupa, nazindikiritsa zolingirira ndi zitsimikizo za mtima. Ndipo palibe cholembedwa chosaonekera pamaso pake, koma zonse zikhala za pambalambanda ndi zovundukuka pamaso pake pa Iye amene tichita naye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:12

Ungakhale mdima sudetsa pamaso panu, koma usiku uwala ngati usana; mdima ukunga kuunika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:13-14

Ndani anapangira mzimu wa Yehova, kapena kukhala phungu lake, ndi kumphunzitsa Iye? Iye anakhala upo ndi yani, ndipo ndani analangiza Iye ndi kumphunzitsa m'njira ya chiweruzo, ndi kumphunzitsa nzeru ndi kumuonetsa njira ya luntha?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mafumu 19:27

Koma ndidziwa kukhala pansi kwako, ndi kutuluka kwako, ndi kulowa kwako, ndi kundizazira kwako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 28:24

Pakuti apenyerera malekezero a dziko lapansi, naona pansi pa thambo ponse;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 11:5

Pamenepo mzimu wa Yehova unandigwera, ndipo anati kwa ine, Nena, Atero Yehova, Mwatero nyumba ya Israele, pakuti ndidziwa zimene zimalowa m'mtima mwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:12

Ukanena, Taonani, sitinadziwe chimenechi; kodi woyesa mitima sachizindikira ichi? Ndi wosunga moyo wako kodi sachidziwa? Ndipo kodi sabwezera munthu yense monga mwa machitidwe ake?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 16:17

Pakuti maso anga ali panjira zao zonse, sabisika pa nkhope yanga, mphulupulu yao siibisika pamaso panga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:6

Kudziwa ichi kundiposa ndi kundidabwitsa: Kundikhalira patali, sindifikirako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 90:8

Munaika mphulupulu zathu pamaso panu, ndi zoipa zathu zobisika pounikira nkhope yanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:19-20

Yehova anakhazika dziko ndi nzeru; naika zamwamba ndi luntha. pakuti adzakuonjezera masiku ambiri, ndi zaka za moyo ndi mtendere. Zakuya zinang'ambika ndi kudziwa kwake; thambo ligwetsa mame.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 2:3

Musalankhulenso modzikuza kwambiri motero; m'kamwa mwanu musatuluke zolulutsa; chifukwa Yehova ndi Mulungu wanzeru, ndipo Iye ayesa zochita anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 11:36

Chifukwa zinthu zonse zichokera kwa Iye, zichitika mwa Iye, ndi kufikira kwa Iye. Kwa Iyeyo ukhale ulemerero kunthawi zonse. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 50:11

Ndidziwa mbalame zonse za m'mapiri, ndipo nyama zakuthengo zili ndi Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 16:11-12

Funsirani kwa Yehova ndi mphamvu yake; funani nkhope yake nthawi zonse. Kumbukirani zodabwitsa zake adazichita, zizindikiro zake, ndi maweruzo a pakamwa pake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 34:22

Palibe mdima kapena mthunzi wa imfa, kuti ochita zopanda pake abisaleko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 12:2

Koma kulibe kanthu kovundikiridwa kamene sikadzaululidwa; ndi kobisika kamene sikadzadziwika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 29:15

Tsoka kwa iwo amene afunitsa kubisira Yehova uphungu wao, ndi ntchito zao zili mumdima, ndipo amati ndani ationa ife? Ndani atidziwa ife?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:7

Ndidzapita kuti kuzembera mzimu wanu? Kapena ndidzathawira kuti kuzembera nkhope yanu?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mafumu 8:39

pamenepo mverani Inu mu Mwamba mokhala Inu, ndi kukhululukira, ndi kuchita, ndi kubwezera munthu yense monga njira zake zonse, amene Inu mumdziwa mtima wake, popeza Inu, Inu nokha, mudziwa mitima ya ana onse a anthu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 16:9

Pakuti maso a Yehova ayang'ana uko ndi uko m'dziko lonse lapansi, kudzionetsera wamphamvu kwa iwo amene mtima wao uli wangwiro ndi Iye. Mwachita chopusa m'menemo; pakuti kuyambira tsopano mudzaona nkhondo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 1:2

monga mwa kudziwiratu kwa Mulungu Atate, m'chiyeretso cha Mzimu, chochitira chimvero, ndi kuwaza kwa mwazi wa Yesu Khristu: Chisomo, ndi mtendere zichulukire inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:15

Atumiza lamulo lake kudziko lapansi; mau ake athamanga liwiro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 15:18

ati Ambuye, amene azidziwitsa zinthu zonsezo chiyambire dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:168

Ndinasamalira malangizo anu ndi mboni zanu; popeza njira zanga zonse zili pamaso panu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 66:18

Pakuti Ine ndidziwa ntchito zao ndi maganizo ao; nthawi ikudza yakudzasonkhanitsa Ine a mitundu yonse ndi zinenedwe zonse, ndipo adzafika nadzaona ulemerero wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 21:17

Ananena naye kachitatu, Simoni mwana wa Yona, kodi undikonda Ine? Petro anamva chisoni kuti anati kwa iye kachitatu, Kodi undikonda Ine? Ndipo anati kwa iye, Ambuye, mudziwa Inu zonse; muzindikira kuti ndikukondani Inu. Yesu ananena naye, Dyetsa nkhosa zanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 48:6

Iwe wachimva; taona zonsezi; ndipo inu kodi inu simudzachinena? Ndakusonyeza iwe zinthu zatsopano kuchokera nthawi ino, ngakhale zinthu zobisika, zimene iwe sunazidziwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:24

Yehova alongosola mayendedwe a mwamuna; munthu tsono angazindikire bwanji njira yake?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 23:10

Koma adziwa njira ndilowayi; atandiyesa ndidzatuluka ngati golide.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:9

Kodi Iye wakupanga khutu ngwosamva? Kodi Iye wakuumba diso ngwosapenya?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:1

Munandisanthula, Yehova, nimundidziwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:13

m'menemo tizindikira kuti tikhala mwa Iye, ndi Iye mwa ife, chifukwa anatipatsako Mzimu wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:3

Muyesa popita ine ndi pogona ine, ndi njira zanga zonse muzolowerana nazo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mafumu 8:27

Kodi Mulungu adzakhala ndithu padziko lapansi? Taonani, thambo ndi mu Mwambamwamba zichepa kukulandirani, koposa kotani nanga nyumba iyi ndaimangayi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 2:19

Koma ndithu maziko a Mulungu aimika pokhazikika, ndi kukhala nacho chizindikiro ichi, Ambuye azindikira iwo amene ali ake; ndipo, Adzipatule kwa chosalungama yense wakutchula dzina la Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 17:26-27

ndipo ndi mmodzi analenga mitundu yonse ya anthu, kuti akhale ponse pa nkhope ya dziko lapansi, atapangiratu nyengo zao, ndi malekezero a pokhala pao; kuti afunefune Mulungu, kapena akamfufuze ndi kumpeza, ngakhale sakhala patali ndi yense wa ife;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:2-3

Yehova amanga Yerusalemu; asokolotsa otayika a Israele. Sanatero nao anthu a mtundu wina; ndipo za maweruzo ake, sanawadziwe. Aleluya. Achiritsa osweka mtima, namanga mabala ao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 3:20

Ndipo kwa Iye amene angathe kuchita koposaposatu zonse zimene tizipempha, kapena tiziganiza, monga mwa mphamvu ya kuchita mwa ife,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 11:2

Ndipo mzimu wa Yehova udzambalira iye mzimu wanzeru ndi wakuzindikira, mzimu wa uphungu ndi mphamvu, mzimu wakudziwa ndi wakuopa Yehova;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 16:27

kwa Mulungu wanzeru yekhayo, mwa Yesu Khristu, kwa yemweyo ukhale ulemerero kunthawi zonse. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 44:20-21

Tikadaiwala dzina la Mulungu wathu, ndi kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo; Mulungu sakadasanthula ichi kodi? Pakuti adziwa zinsinsi za mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:11

Kumanda ndi kuchionongeko kuli pamaso pa Yehova; koposa kotani nanga mitima ya ana a anthu?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 45:21

Nenani inu, tulutsani mlandu wanu; inde, achite uphungu pamodzi; ndani waonetsa ichi chiyambire nthawi yakale? Ndani wanena ichi kale? Kodi si ndine Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina popanda Ine; Mulungu wolungama, ndi Mpulumutsi; palibenso wina popanda Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Danieli 2:20-22

Daniele anayankha, nati, Lilemekezedwe dzina la Mulungu kunthawi za nthawi, pakuti nzeru ndi mphamvu zili zake; pakuti amasanduliza nthawi ndi nyengo, achotsa mafumu, nalonga mafumu, apatsa anzeru nzeru, ndi chidziwitso kwa iwo okhoza kuzindikira. Iye avumbulutsa zinthu zakuya ndi zinsinsi; adziwa zokhala mumdima, ndi kuunika kumakhala kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 1:8-9

chimene anatichulukitsira ife m'nzeru zonse, ndi chisamaliro. Anatizindikiritsa ife chinsinsi cha chifuniro chake, monga kunamkomera ndi monga anatsimikiza mtima kale mwa Iye,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 18:30

Mulungu ndiye wangwiro m'njira zake; mau a Yehova ngoyengeka; ndiye chikopa cha onse okhulupirira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Samueli 22:31

Kunena za Mulungu, njira yake ili yangwiro; mau a Yehova anayesedwa; Iye ndiye chikopa kwa onse akukhulupirira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:66

Mundiphunzitse chisiyanitso ndi nzeru; pakuti ndinakhulupirira malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 38:4-5

Unali kuti muja ndinaika maziko a dziko lapansi? Fotokoza ngati udziwa kuzindikira. pamene ibwatama m'ngaka mwao, nikhala mobisala kulaliramo? Amkonzeratu khwangwala chakudya chake ndani, pamenepo ana ake afuulira kwa Mulungu, naulukauluka osowa chakudya? Analemba malire ake ndani, popeza udziwa? Anayesapo chingwe chake ndani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:15

Thupi langa silinabisikire Inu popangidwa ine mobisika, poombedwa ine monga m'munsi mwake mwa dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:26

Kwezani maso anu kumwamba, muone amene analenga izo, amene atulutsa khamu lao ndi kuziwerenga; azitcha zonse maina ao, ndi mphamvu zake zazikulu, ndi popeza ali wolimba mphamvu, palibe imodzi isoweka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 3:12

Pakuti maso a Ambuye ali pa olungama, ndi makutu ake akumva pembedzo lao; koma nkhope ya Ambuye ili pa ochita zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 9:4

Ndipo Yesu, pozindikira maganizo ao, anati, Chifukwa chanji mulinkuganizira zoipa m'mitima yanu?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:1

Aleluya; Pakuti kuimbira zomlemekeza Mulungu wathu nkokoma; pakuti chikondweretsa ichi, chilemekezo chiyenera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 1:25

Chifukwa kuti chopusa cha Mulungu chiposa anthu ndi nzeru zao; ndipo chofooka cha Mulungu chiposa anthu ndi mphamvu yao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:14

Iye anakhala upo ndi yani, ndipo ndani analangiza Iye ndi kumphunzitsa m'njira ya chiweruzo, ndi kumphunzitsa nzeru ndi kumuonetsa njira ya luntha?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:7

Adzabukitsa chikumbukiro cha ubwino wanu waukulu, nadzaimbira chilungamo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 3:9

ndi kuwalitsira onse adziwe makonzedwe a chinsinsicho, chimene chinabisika kuyambira kalekale mwa Mulungu wolenga zonse;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 2:3

amene zolemera zonse za nzeru ndi chidziwitso zibisika mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 12:13

Kwa Iye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi luntha ali nazo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:24

Ntchito zanu zichulukadi, Yehova! Munazichita zonse mwanzeru; dziko lapansi lidzala nacho chuma chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 55:9

Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, momwemo njira zanga zili zazitali kupambana njira zanu, ndi maganizo anga kupambana maganizo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 38:1-2

Pamenepo Yehova anayankha Yobu m'kamvulumvulu, nati, ndi kuilembera malire anga, ndi kuika mipikizo ndi zitseko, ndi kuti, Ufike mpaka apa, osapitirirapo; apa adzaletseka mafunde ako odzikuza? Kodi walamulira m'mawa chiyambire masiku ako, ndi kudziwitsa mbandakucha malo ake; kuti agwire malekezero a dziko lapansi, nakutumule oipa achokeko? Lisandulika ngati dothi lonyata pansi pa chosindikiza, ndi zonse zibuka ngati chovala; ndi kuunika kwa oipa kuletsedwa kuti asakuone, ndi dzanja losamulidwa lithyoledwa. Kodi unalowa magwero a nyanja? Kodi unayendayenda pozama penipeni? Kodi zipata za imfa zinavumbulukira iwe? Kapena kodi unaona zipata za mthunzi wa imfa? Kodi unazindikira chitando cha dziko lapansi? Fotokozera, ngati uchidziwa chonse. Ili kuti njira yomukira pokhala kuunika? Ndi mdima, pokhala pake pali kuti, Ndani uyu adetsa uphungu, ndi mau opanda nzeru?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 103:14

Popeza adziwa mapangidwe athu; akumbukira kuti ife ndife fumbi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 8:17

Pakuti palibe chinthu chobisika, chimene sichidzakhala choonekera; kapena chinsinsi chimene sichidzadziwika ndi kuvumbuluka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 46:10

ndilalikira za chimaliziro kuyambira pachiyambi, ndi kuyambira nthawi zakale ndinena zinthu zimene zisanachitidwe; ndi kunena, Uphungu wanga udzakhala, ndipo ndidzachita zofuna zanga zonse;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 77:14

Inu ndinu Mulungu wakuchita chodabwitsa; munazindikiritsa mphamvu yanu mwa mitundu ya anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 11:33

Ha! Kuya kwake kwa kulemera ndi kwa nzeru ndi kwa kudziwa kwake kwa Mulungu! Osasanthulikadi maweruzo ake, ndi njira zake nzosalondoleka!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 29:11-12

Ukulu, ndi mphamvu, ndi ulemerero, ndi chipambano, ndi chifumu ndi zanu, Yehova; pakuti zonse zam'mwamba ndi padziko lapansi ndi zanu; ufumu ndi wanu, Yehova; ndipo mwakwezeka mutu wa pa zonse. Zolemera ndi ulemu zifuma kwanu, ndipo muchita ufumu pa zonse, ndi m'dzanja mwanu muli mphamvu yaikulu; kukuza ndi kupatsa onse mphamvu kuli m'dzanja lanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 9:10

Chiyambi cha nzeru ndicho kuopa Yehova; kudziwa Woyerayo ndiko luntha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:142

Chilungamo chanu ndicho chilungamo chosatha; ndi chilamulo chanu ndicho choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 50:4

Ambuye Yehova wandipatsa Ine lilime la ophunzira, kuti ndidziwe kunena mau akuchirikiza iye amene ali wolema. Iye andigalamutsa m'mawa ndi m'mawa, nagalamutsa khutu langa kuti limve monga ophunzira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 42:9

Taona, zinthu zakale zaoneka, ndipo zatsopano Ine ndizitchula; zisanabuke ndidzakumvetsani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:26

ndiwo chinsinsicho chinabisika kuyambira pa nthawizo, ndi kuyambira pa mibadwoyo; koma anachionetsa tsopano kwa oyera mtima ake,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 26:14

Taonani, awa ndi malekezero a njira zake; ndi chimene tikumva za Iye ndi chinong'onezo chaching'ono; koma kugunda kwa mphamvu yake akuzindikiritsa ndani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 11:3

ndipo adzakondwera nako kumuopa Yehova, ndipo sadzaweruza monga apenya maso, sadzadzudzula mwamphekesera:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:29

Chifukwa kuti iwo amene Iye anawadziwiratu, iwowa anawalamuliratu afanizidwe ndi chifaniziro cha Mwana wake, kuti Iye akakhale mwana woyamba wa abale ambiri;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:3

Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu; ndi ukulu wake ngwosasanthulika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 1:17

Ndipo kwa Mfumu yosatha, yosavunda, yosaoneka, Mulungu wa yekha, ukhale ulemu ndi ulemerero, kufikira nthawi za nthawi. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 29:29

Zinsinsi nza Yehova Mulungu wathu; koma zovumbuluka nza ife ndi ana athu kosatha, kuti tichite mau onse a chilamulo ichi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 111:10

Kumuopa Yehova ndiko chiyambi cha nzeru; onse akuchita chotero ali nacho chidziwitso chokoma; chilemekezo chake chikhalitsa kosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 4:15

Pakuti sitili naye mkulu wa ansembe wosatha kumva chifundo ndi zofooka zathu; koma wayesedwa m'zonse monga momwe ife, koma wopanda uchimo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:12

Ndani wayesa madzi m'dzanja lake, nayesa thambo ndi chikhato, ndi kudzaza fumbi la nthaka m'nsengwa, ndi kuyesa mapiri m'mbale zoyesera, ndi zitunda m'mulingo?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 11:7-9

Kodi ukhoza kupeza Mulungu mwa mufunafuna? Ukhoza kupeza Wamphamvuyonse motsindika? Kumpeza kutalika ngati kumwamba, ungachitenji? Kuzama ngati kumanda, ungadziwenji? Muyeso wake utalikira utali wake wa dziko lapansi, chitando chake chiposa cha nyanja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 8:2-3

Ngati wina ayesa kuti adziwa kanthu sanayambe kudziwa monga ayenera kudziwa. Koma ngati wina akonda Mulungu, yemweyu adziwika ndi Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:73

Manja anu anandilenga nandiumba; mundizindikiritse, kuti ndiphunzire malemba anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 38:16

Kodi unalowa magwero a nyanja? Kodi unayendayenda pozama penipeni?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:1

Malongosoledwe a mtima nga munthu; koma mayankhidwe a lilime achokera kwa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 42:8-9

Ine ndine Yehova; dzina langa ndi lomweli; ndipo ulemerero wanga Ine sindidzapereka kwa wina, ngakhale kunditamanda kwa mafano osemedwa. Taona, zinthu zakale zaoneka, ndipo zatsopano Ine ndizitchula; zisanabuke ndidzakumvetsani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 2:6-7

Koma tilankhula nzeru mwa angwiro; koma si nzeru ya nthawi ino ya pansi pano, kapena ya akulu a nthawi ino ya pansi pano, amene alinkuthedwa; koma tilankhula nzeru ya Mulungu m'chinsinsi, yobisikayo, imene Mulungu anaikiratu, pasanakhale nyengo za pansi pano, ku ulemerero wathu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 32:8

Ine ndidzakulangiza ndi kuphunzitsa iwe za njira ukayendayo; ndidzakupangira ndi diso langa lakuyang'ana iwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:26-27

Ndipo momwemonso Mzimu athandiza kufooka kwathu; pakuti chimene tizipempha monga chiyenera, sitidziwa; koma Mzimu mwini atipempherera ndi zobuula zosatheka kuneneka; ndipo Iye amene asanthula m'mitima adziwa chimene achisamalira Mzimu, chifukwa apempherera oyera mtima monga mwa chifuniro cha Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 13:12

Pakuti tsopano tipenya m'kalirole, ngati chimbuuzi; koma pomwepo maso ndi maso. Tsopano ndizindikira mderamdera; koma pomwepo ndidzazindikiratu, monganso ndazindikiridwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 66:1-2

Atero Yehova, Kumwamba ndi mpando wanga wachifumu, ndi dziko lapansi ndi choikapo mapazi anga; mudzandimangira Ine nyumba yotani? Ndi malo ondiyenera kupumamo ali kuti? Sangalalani inu pamodzi ndi Yerusalemu, ndipo kondwani chifukwa cha iye, inu nonse amene mumkonda; sangalalani kokondwa pamodzi ndi iye, inu nonse akumlira maliro; kuti mukayamwe ndi kukhuta ndi mawere a zitonthozo zake; kuti mukafinye mkaka ndi kukondwerera ndi unyinji wa ulemerero wake. Pakuti atero Yehova, Taonani ndidzamfikitsira mtendere ngati mtsinje, ndi ulemerero wa amitundu ngati mtsinje wosefukira. Inu mudzayamwa, ndi kunyamulidwa pambali, ndi kululuzidwa pa maondo. Monga munthu amene amake amtonthoza mtima, momwemo ndidzatonthoza mtima wanu; ndipo mudzatonthozedwa mtima mu Yerusalemu. Ndipo mudzachiona, ndipo mtima wanu udzasangalala, ndipo mafupa anu adzakula ngati msipu; ndipo dzanja la Yehova lidzadziwika ndi atumiki ake, ndipo adzakwiyira adani ake. Pakuti taonani, Yehova adzafika m'moto, ndi magaleta ake adzafanana ndi kamvulumvulu; kubwezera mkwiyo wake ndi ukali, ndi kudzudzula ndi malawi amoto. Pakuti Yehova adzatsutsana ndi moto, ndi lupanga lake, ndi anthu onse; ndi ophedwa a Yehova adzakhala ambiri. Iwo amene adzipatulitsa nadziyeretsa, kuti amuke kuminda tsatanetsatane, ndi kudya nyama ya nkhumba, ndi chonyansa, ndi mbewa, adzathedwa pamodzi, ati Yehova. Pakuti Ine ndidziwa ntchito zao ndi maganizo ao; nthawi ikudza yakudzasonkhanitsa Ine a mitundu yonse ndi zinenedwe zonse, ndipo adzafika nadzaona ulemerero wanga. Ndipo ndidzaika chizindikiro pakati pao, ndipo ndidzatumiza onse amene apulumuka mwa iwo kwa amitundu, kwa Tarisisi, kwa Puti ndi kwa Aludi, okoka uta kwa Tubala ndi Yavani, kuzisumbu zakutali, amene sanamve mbiri yanga, ngakhale kuona ulemerero wanga; ndipo adzabukitsa ulemerero wanga pakati pa amitundu. Pakuti zonsezi mkono wanga wazilenga, momwemo zonsezi zinaoneka, ati Yehova; koma ndidzayang'anira munthu uyu amene ali waumphawi, ndi wa mzimu wosweka, nanthunthumira ndi mau anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 12:10

M'dzanja mwake muli mpweya wa zamoyo zonse, ndi mzimu wa munthu aliyense.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 1:18

ndiko kunena kuti maso a mitima yanu awalitsike, kuti mukadziwe inu chiyembekezo cha kuitana kwake nchiyani; chiyaninso chuma cha ulemerero wa cholowa chake mwa oyera mtima,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 56:8

Muwerenga kuthawathawa kwanga, sungani misozi yanga m'nsupa yanu; kodi siikhala m'buku mwanu?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 16:7

Koma Yehova ananena ndi Samuele, Usayang'ane nkhope yake, kapena kutalika kwa msinkhu wake, popeza Ine ndinamkana iye; pakuti Yehova saona monga aona munthu; pakuti munthu ayang'ana chooneka ndi maso, koma Yehova ayang'ana mumtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 5:3

Yehova Inu, maso anu sali pachoonadi kodi? Munawapanda iwo, koma sanaphwetekedwe mtima; munawatha iwo, koma akana kudzudzulidwa; alimbitsa nkhope zao koposa mwala; akana kubwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:9

Mtima wa munthu ulingalira njira yake; koma Yehova ayendetsa mapazi ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 11:3

Ndi chikhulupiriro tizindikira kuti maiko ndi a m'mwamba omwe anakonzedwa ndi mau a Mulungu, kotero kuti zinthu zopenyeka sizinapangidwe kuchokera mu zoonekazo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 28:29

Ichinso chifumira kwa Yehova wa makamu, uphungu wake uzizwitsa ndi nzeru yake impambana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 12:22

Avumbulutsa zozama mumdima, natulutsa mthunzi wa imfa ukhale poyera;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 2:16

tsiku limene Mulungu adzaweruza ndi Khristu Yesu zinsinsi za anthu, monga mwa Uthenga wanga Wabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 11:27

Zinthu zonse zinaperekedwa kwa Ine ndi Atate wanga; ndipo palibe munthu adziwa Mwana, koma Atate yekha, ndi palibe wina adziwa Atate, koma Mwana yekha, ndi iye amene Mwana afuna kumuululira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 28:12

Koma nzeru, idzapezeka kuti? Ndi luntha, malo ake ali kuti?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:7

Usadziyese wekha wanzeru; opa Yehova, nupatuke pazoipa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Danieli 5:21

ndipo anamuinga kumchotsa kwa ana a anthu, ndi mtima wake unasandulika ngati wa nyama zakuthengo, ndi pokhala pake mpa mbidzi, anamdyetsa udzu ngati ng'ombe, ndi thupi lake linakhathamira ndi mame a kumwamba; mpaka anadziwa kuti Wam'mwambamwamba alamulira mu ufumu wa anthu, nauikira aliyense Iye afuna mwini.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 25:14

Chinsinsi cha Yehova chili kwa iwo akumuopa Iye; ndipo adzawadziwitsa pangano lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 12:6-7

Kodi mpheta zisanu sizigulidwa timakobiri tiwiri? Ndipo palibe imodzi ya izo iiwalika pamaso pa Mulungu; komatu ngakhale matsitsi onse a pamutu panu awerengedwa. Musaopa, muposa mtengo wake wa mpheta zambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:30

Kulibe nzeru ngakhale luntha ngakhale uphungu wotsutsana ndi Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 9:11

pakuti anawo asanabadwe, kapena asanachite kanthu kabwino kapena koipa, kuti kutsimikiza mtima kwa Mulungu monga mwa kusankha kukhale, si chifukwa cha ntchito ai, koma chifukwa cha wakuitanayo,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 36:9

Pakuti chitsime cha moyo chili ndi Inu, M'kuunika kwanu tidzaona kuunika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 8:4

munthu ndani kuti mumkumbukira? Ndi mwana wa munthu kuti mucheza naye?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 14:24

Yehova wa makamu walumbira, nati, Ndithu monga ndaganiza, chotero chidzachitidwa; ndipo monga ndapanga uphungu, chotero chidzakhala;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Petro 3:8

Koma ichi chimodzi musaiwale, okondedwa inu, kuti tsiku limodzi likhala kwa Ambuye ngati zaka chikwi, ndi zaka chikwi ngati tsiku limodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 4:5

Chifukwa chake musaweruze kanthu isanadze nthawi yake, kufikira akadze Ambuye, amenenso adzaonetsera zobisika za mdima, nadzasonyeza zitsimikizo za mtima; ndipo pamenepo yense adzakhala nao uyamiko wake wa kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa