Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Masalimo 119:142 - Buku Lopatulika

142 Chilungamo chanu ndicho chilungamo chosatha; ndi chilamulo chanu ndicho choonadi.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

142 Chilungamo chanu ndicho chilungamo chosatha; ndi chilamulo chanu ndicho choonadi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

142 Kulungama kwanu nkwamuyaya, ndipo malamulo anu ndi oona.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 119:142
11 Mawu Ofanana  

Mboni zanu ndizo zolungama kosatha; mundizindikiritse izi, ndipo ndidzakhala ndi moyo.


Inu muli pafupi, Yehova; ndipo malamulo anu onse ndiwo choonadi.


Chiwerengero cha mau anu ndicho choonadi; ndi maweruzo anu olungama onse akhala kosatha.


Kuopa Yehova kuli mbee, kwakukhalabe nthawi zonse; maweruzo a Yehova ali oona, alungama konsekonse.


Chilungamo chanu chikunga mapiri a Mulungu; maweruzo anu akunga chozama chachikulu, Yehova, musunga munthu ndi nyama.


Tukulani maso anu kumwamba, ndipo muyang'ane pansi padziko pakuti kumwamba kudzachoka ngati utsi, ndi dziko lidzatha ngati chofunda, ndipo iwo amene akhala m'menemo adzafa ngati njenjete; koma chipulumutso changa chidzakhala kunthawi zonse, ndi chilungamo changa sichidzachotsedwa.


Pakuti njenjete idzawadya ngati chofunda, ndi mbozi zidzawadya ngati ubweya; koma chilungamo changa chidzakhala kunthawi zonse, ndi chipulumutso changa kumibadwo yonse.


Masabata makumi asanu ndi awiri alamulidwira anthu a mtundu wako ndi mzinda wako wopatulika, kumaliza cholakwacho, ndi kutsiriza machimo, ndi kutetezera mphulupulu, ndi kufikitsa chilungamo chosalekeza, ndi kukhomera chizindikiro masomphenya ndi zonenera, ndi kudzoza malo opatulika kwambiri.


Patulani iwo m'choonadi; mau anu ndi choonadi.


ngatitu mudamva Iye, ndipo munaphunzitsidwa mwa Iye, monga choonadi chili mwa Yesu;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa