Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 136 - Buku Lopatulika


Mulungu alemekezedwe pa chifundo chake

1 Yamikani Yehova pakuti ndiye wabwino; pakuti chifundo chake nchosatha.

2 Yamikani Mulungu wa milungu; pakuti chifundo chake nchosatha.

3 Yamikani Mbuye wa ambuye; pakuti chifundo chake nchosatha.

4 Amene yekha achita zodabwitsa zazikulu; pakuti chifundo chake nchosatha.

5 Amene analenga zakumwamba mwanzeru; pakuti chifundo chake nchosatha.

6 Amene anayala dziko lapansi pamwamba pamadzi; pakuti chifundo chake nchosatha.

7 Amene analenga miuni yaikulu; pakuti chifundo chake nchosatha.

8 Dzuwa liweruze usana; pakuti chifundo chake nchosatha.

9 Mwezi ndi nyenyezi ziweruze usiku; pakuti chifundo chake nchosatha.

10 Iye amene anapandira Aejipito ana ao oyamba; pakuti chifundo chake nchosatha.

11 Natulutsa Israele pakati pao; pakuti chifundo chake nchosatha.

12 Ndi dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka; pakuti chifundo chake nchosatha.

13 Amene anagawa magawo Nyanja Yofiira; pakuti chifundo chake nchosatha.

14 Napititsa Israele pakati pake; pakuti chifundo chake nchosatha.

15 Nakhuthula Farao ndi khamu lake mu Nyanja Yofiira: pakuti chifundo chake nchosatha.

16 Amene anatsogolera anthu ake m'chipululu; pakuti chifundo chake nchosatha.

17 Amene anapanda mafumu aakulu; pakuti chifundo chake nchosatha.

18 Ndipo anawapha mafumu omveka; pakuti chifundo chake nchosatha.

19 Sihoni mfumu ya Aamori; pakuti chifundo chake nchosatha.

20 Ndi Ogi mfumu ya Basani; pakuti chifundo chake nchosatha.

21 Ndipo anapereka dziko lao likhale cholowa; pakuti chifundo chake nchosatha.

22 Cholowa cha kwa Israele mtumiki wake; pakuti chifundo chake nchosatha.

23 Amene anatikumbukira popepuka ife; pakuti chifundo chake nchosatha.

24 Natikwatula kwa otisautsa; pakuti chifundo chake nchosatha.

25 Ndiye wakupatsa nyama zonse chakudya; pakuti chifundo chake nchosatha.

26 Yamikani Mulungu wa Kumwamba, pakuti chifundo chake nchosatha.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa