Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


68 Mau a Mulungu: Malemba Opatulika

68 Mau a Mulungu: Malemba Opatulika

Mawu a Mulungu ndi amoyo ndi amphamvu. Amandiwongolera pa zochitika zonse za moyo wanga, akundionetsa njira ndikakadzuka, ndi kundipatsa mayankho pamavuto anga. Ndikofunikira osati kungokhulupirira Mawu a Mulungu ngati choonadi chokha, komanso kuwatsatira pa moyo wanga.

Monga mmene Salmo 119:105 imanenera, Mawu ake ndi nyali ya kumapazi anga, ndi kuunika pa njira yanga. Mawu a Mulungu saunikira kokha ulendo wanga, komanso amandidziwitsa chikondi chimene Mulungu ali nacho pa ine.

Ndikofunikira kukumbukira kuti si chinthu cha kanthawi kochepa, koma monga taonera kale, Mawu a Mulungu amakhala kosatha.




Yohane 8:31-32

Chifukwa chake Yesu ananena kwa Ayuda aja adakhulupirira Iye, Ngati mukhala inu m'mau anga, muli ophunzira anga ndithu; ndipo mudzazindikira choonadi, ndipo choonadi chidzakumasulani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:20-21

Mwananga, tamvera mau anga; tcherera makutu ku zonena zanga. Asachoke kumaso ako; uwasunge m'kati mwa mtima wako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:16

Mau a Khristu akhalitse mwa inu chichulukire mu nzeru yonse, ndi kuphunzitsa ndi kuyambirirana eni okha ndi masalimo, ndi mayamiko ndi nyimbo zauzimu, ndi kuimbira Mulungu ndi chisomo mumtima mwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:160

Chiwerengero cha mau anu ndicho choonadi; ndi maweruzo anu olungama onse akhala kosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:11

Ndinawabisa mau anu mumtima mwanga, kuti ndisalakwire Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 130:5

Ndilindira Yehova, moyo wanga ulindira, ndiyembekeza mau ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Samueli 22:31

Kunena za Mulungu, njira yake ili yangwiro; mau a Yehova anayesedwa; Iye ndiye chikopa kwa onse akukhulupirira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 1:23

inu amene mudabadwanso, osati ndi mbeu yofeka, komatu yosaola, mwa mau a Mulungu amoyo ndi okhalitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 19:7

Malamulo a Yehova ali angwiro, akubwezera moyo; mboni za Yehova zili zokhazikika, zakuwapatsa opusa nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 12:28

Chifukwa chake uziti nao, Atero Ambuye Yehova, Palibe amodzi a mau anga adzazengerezekanso; koma mau ndidzanenawo adzachitika, ati Ambuye Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:5

Tenga nzeru, tenga luntha; usaiwale, usapatuke pa mau a m'kamwa mwanga;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 15:3

Mwakhala okonzeka tsopano inu chifukwa cha mau amene ndalankhula ndi inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:18

Pakuti indetu ndinena kwa inu, Kufikira litapitirira thambo ndi dziko, kalemba kakang'ono kamodzi kapena kansonga kake kamodzi sikadzachokera kuchilamulo, kufikira zitachitidwa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yoswa 1:8

Buku ili la chilamulo lisachoke pakamwa pako; koma ulingiriremo usana ndi usiku, kuti usamalire kuchita monga mwa zonse zolembedwamo; popeza ukatero udzakometsa njira yako, nudzachita mwanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 4:2

Musamaonjeza pa mau amene ndikuuzani, kapena kuchotsapo, kuti musunge malamulo a Yehova Mulungu wanu, amene ndikuuzani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:103

Mau anu azunadi powalawa ine! Koposa uchi m'kamwa mwanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 12:6

Mau a Yehova ndi mau oona; ngati siliva woyenga m'ng'anjo yadothi, yoiyeretsa kasanu ndi kawiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 15:7

Ngati mukhala mwa Ine, ndi mau anga akhala mwa inu, pemphani chilichonse chimene muchifuna ndipo chidzachitika kwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 55:11

momwemo adzakhala mau anga amene atuluka m'kamwa mwanga, sadzabwerera kwa Ine chabe, koma adzachita chimene ndifuna, ndipo adzakula m'mene ndinawatumizira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 15:16

Mau anu anapezeka, ndipo ndinawadya; mau anu anakhala kwa ine chikondwero ndi chisangalalo cha mtima wanga; pakuti ndatchedwa dzina lanu, Yehova Mulungu wa makamu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:140-144

Mau anu ngoyera ndithu; ndi mtumiki wanu awakonda. Wamng'ono ine, ndi wopepulidwa; koma sindiiwala malemba anu. Chilungamo chanu ndicho chilungamo chosatha; ndi chilamulo chanu ndicho choonadi. Kusautsika ndi kupsinjika kwandigwera; koma malamulo anu ndiwo ondikondweretsa ine. Mboni zanu ndizo zolungama kosatha; mundizindikiritse izi, ndipo ndidzakhala ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 4:12

Pakuti mau a Mulungu ali amoyo, ndi ochitachita, ndi akuthwa koposa lupanga lakuthwa konsekonse, napyoza kufikira kugawira moyo ndi mzimu, ndi zimfundo ndi mafuta a m'mafupa, nazindikiritsa zolingirira ndi zitsimikizo za mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 3:16-17

Lemba lililonse adaliuzira Mulungu, ndipo lipindulitsa pa chiphunzitso, chitsutsano, chikonzero, chilangizo cha m'chilungamo: kuti munthu wa Mulungu akhale woyenera, wokonzeka kuchita ntchito iliyonse yabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:105

Mau anu ndiwo nyali ya ku mapazi anga, ndi kuunika kwa panjira panga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:22

Khalani akuchita mau, osati akumva okha, ndi kudzinyenga nokha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 6:17

Mutengenso chisoti cha chipulumutso, ndi lupanga la Mzimu, ndilo Mau a Mulungu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 11:28

Koma Iye anati, Inde, koma odala iwo akumva mau a Mulungu, nawasunga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 11:18

Chifukwa chake muzisunga mau anga awa mumtima mwanu ndi m'moyo mwanu; ndi kuwamanga ngati chizindikiro pamanja panu; ndipo zikhale zapamphumi pakati pamaso anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 18:30

Mulungu ndiye wangwiro m'njira zake; mau a Yehova ngoyengeka; ndiye chikopa cha onse okhulupirira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:24

Chifukwa chimenechi yense amene akamva mau anga amenewa, ndi kuwachita, ndidzamfanizira iye ndi munthu wochenjera, amene anamanga nyumba yake pathanthwe;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 24:35

Thambo ndi dziko lapansi zidzachoka, koma mau anga sadzachoka ai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:130

Potsegulira mau anu paunikira; kuzindikiritsa opusa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 4:4

Koma Iye anayankha nati, Kwalembedwa, Munthu sadzakhala ndi moyo ndi mkate wokha, koma ndi mau onse akutuluka m'kamwa mwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:24

Indetu, indetu, ndinena kwa inu, kuti iye wakumva mau anga, ndi kukhulupirira Iye amene anandituma Ine, ali nao moyo wosatha, ndipo salowa m'kuweruza, koma wachokera kuimfa, nalowa m'moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 33:4

Pakuti mau a Yehova ali olunjika; ndi ntchito zake zonse zikhulupirika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 21:33

Thambo ndi dziko lapansi zidzapita; koma mau anga sadzapita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 19:8

Malangizo a Yehova ali olungama, akukondweretsa mtima; malamulo a Yehova ali oyera, akupenyetsa maso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:8

Udzu unyala, duwa lifota, koma mau a Mulungu wathu adzakhala nthawi zachikhalire.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:9

Mnyamata adzayeretsa mayendedwe ake bwanji? Akawasamalira monga mwa mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:114

Inu ndinu pobisalapo panga, ndi chikopa changa; ndiyembekezera mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:1

Pachiyambi panali Mau, ndipo Mau anali kwa Mulungu, ndipo Mau ndiye Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 30:5

Mau onse a Mulungu ali oyengeka; ndiye chikopa cha iwo amene amkhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 1:3

ameneyo, pokhala ali chinyezimiro cha ulemerero wake, ndi chizindikiro chenicheni cha chikhalidwe chake, nanyamula zonse ndi mau a mphamvu yake, m'mene adachita chiyeretso cha zoipa, anakhala padzanja lamanja la Ukulu mu Mwamba,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 23:12

Sindinabwerera kusiya malamulo a pa milomo yake; ndasungitsa mau a pakamwa pake koposa lamulo langalanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:97

Ha! Ndikondadi chilamulo chanu; ndilingiriramo ine tsiku lonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:165

Akukonda chilamulo chanu ali nao mtendere wambiri; ndipo alibe chokhumudwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 1:25

koma Mau a Ambuye akhala chikhalire. Ndipo mau olalikidwa kwa inu ndi awo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 17:17

Patulani iwo m'choonadi; mau anu ndi choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 10:17

Chomwecho chikhulupiriro chidza ndi mbiri, ndi mbiri idza mwa mau a Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 1:8-9

Koma ngakhale ife, kapena mngelo wochokera Kumwamba, ngati akakulalikireni Uthenga Wabwino wosati umene tidakulalikirani ife, akhale wotembereredwa. Monga tinanena kale, ndipo ndinenanso tsopano apa, ngati wina akulalikirani Uthenga Wabwino wosati umene mudaulandira, akhale wotembereredwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 19:7-8

Malamulo a Yehova ali angwiro, akubwezera moyo; mboni za Yehova zili zokhazikika, zakuwapatsa opusa nzeru. Malangizo a Yehova ali olungama, akukondweretsa mtima; malamulo a Yehova ali oyera, akupenyetsa maso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 138:2

Ndidzagwadira kuloza ku Kachisi wanu woyera, ndi kuyamika dzina lanu, chifukwa cha chifundo chanu ndi choonadi chanu; popeza munakuzitsa mau anu koposa dzina lanu lonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 2:13

Ndipo mwa ichinso ife tiyamika Mulungu kosalekeza, kuti, pakulandira mau a Uthenga wa Mulungu, simunawalandire monga mau a anthu, komatu monga momwe ali ndithu, mau a Mulungu, amenenso achita mwa inu okhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:14

Ndakulemberani, atate, popeza mwamzindikira Iye amene ali kuyambira pachiyambi. Ndakulemberani, anyamata, popeza muli amphamvu, ndi mau a Mulungu akhala mwa inu, ndipo mwamgonjetsa woipayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 1:1-3

Wodala munthuyo wosayenda mu uphungu wa oipa, kapena wosaimirira m'njira ya ochimwa, kapena wosakhala pansi pa bwalo la onyoza. Komatu m'chilamulo cha Yehova muli chikondwerero chake; ndipo m'chilamulo chake amalingirira usana ndi usiku. Ndiye akunga mtengo wooka pa mitsinje ya madzi; wakupatsa chipatso chake pa nyengo yake, tsamba lake lomwe losafota; ndipo zonse azichita apindula nazo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 6:6-7

Ndipo mau awa ndikuuzani lero, azikhala pamtima panu; ndipo muziwaphunzitsa mwachangu kwa ana anu, ndi kuwalankhula awa pokhala pansi m'nyumba zanu, ndi poyenda inu panjira, ndi pogona inu pansi, ndi pouka inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:8-9

Kuthawira kwa Yehova nkokoma koposa kukhulupirira munthu. Kuthawira kwa Yehova nkokoma koposa kukhulupirira akulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 2:6

Pakuti Yehova apatsa nzeru; kudziwa ndi kuzindikira kutuluka m'kamwa mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:5

koma iye amene akasunga mau ake, mwa iyeyu zedi chikondi cha Mulungu chathedwa. M'menemo tizindikira kuti tili mwa Iye;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:4

Pakuti zonse zinalembedwa kale zinalembedwa kutilangiza, kuti mwa chipiriro ndi chitonthozo cha malembo, tikhale ndi chiyembekezo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:26

kuti akampatule, atamyeretsa ndi kumsambitsa madzi ndi mau;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:18

Munditsegulire maso, kuti ndipenye zodabwitsa za m'chilamulo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 6:18

kuti mwa zinthu ziwiri zosasinthika, m'mene Mulungu sangathe kunama, tikakhale nacho chotichenjeza cholimba, ife amene tidathawira kuchigwira chiyembekezo choikika pamaso pathu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 3:10

Ananenanso nane, Wobadwa ndi munthu iwe, mau anga onse ndidzawanena ndi iwe uwalandire m'mtima mwako, utawamva m'makutu mwako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:24

Mboni zanu zomwe ndizo zondikondweretsa, ndizo zondipangira nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:14

Ndinakondwera m'njira ya mboni zanu, koposa ndi chuma chonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:148

Maso anga anakumana ndi maulonda a usiku, kuti ndilingirire mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 8:3

Ndipo anakuchepetsani, nakumvetsani njala, nakudyetsani ndi mana, amene simunawadziwe, angakhale makolo anu sanawadziwe; kuti akudziwitseni kuti munthu sakhala wamoyo ndi mkate wokha, koma munthu akhala wamoyo ndi zonse zakutuluka m'kamwa mwa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Mulungu wanga, wamkulu ndi wokhulupirika! Ndikukuyamikani chifukwa cha mawu anu, chifukwa kudzera mwa iwo ndimalandira chitsogozo chanu ndi chilango chanu. Mawu anu ndi amoyo, ndi amphamvu, akuthwa kuposa lupanga lakuthwa konsekonse, ndiwo anditsutsa, andiphunzitsa, ndi kundilangiza. Ndikupempha kuti mawu anu awululidwe mwa ine. Zikomo chifukwa ndi chakudya changa chabwino koposa ndipo mmenemo muli kukula kwanga kwauzimu. Ndiwo andisintha ndi kundipatsa moyo, akuulula zobisika zomwe zili mkati mwanga, akuzindikira zolinga za mtima wanga. Ambuye, mawu anu amati: "Wokhulupirira iwe, mitsinje ya madzi amoyo idzatuluka m'mimba mwake." Ndiwo amaunikira njira yanga ndi kunditeteza kuti ndisagwe. Ndipatseni nzeru zanu kuti ndikudziweni ndi kukumvetsani kudzera mwa iwo. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa