Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mateyu 7:24 - Buku Lopatulika

24 Chifukwa chimenechi yense amene akamva mau anga amenewa, ndi kuwachita, ndidzamfanizira iye ndi munthu wochenjera, amene anamanga nyumba yake pathanthwe;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

24 Chifukwa chimenechi yense amene akamva mau anga amenewa, ndi kuwachita, ndidzamfanizira iye ndi munthu wochenjera, amene anamanga nyumba yake pathanthwe;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

24 “Munthu aliyense womva mau angaŵa nkumaŵagwiritsa ntchito, amafanafana ndi munthu wanzeru amene adaamanga nyumba yake pa thanthwe.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

24 “Nʼchifukwa chake aliyense amene amva mawu anga ndi kuwachita akufanana ndi munthu wanzeru amene anamanga nyumba yake pa thanthwe.

Onani mutuwo Koperani




Mateyu 7:24
41 Mawu Ofanana  

Koma kwa munthu anati, Taonani, kuopa Ambuye ndiko nzeru; ndi kupatukana nacho choipa ndiko luntha.


Kumuopa Yehova ndiko chiyambi cha nzeru; onse akuchita chotero ali nacho chidziwitso chokoma; chilemekezo chake chikhalitsa kosatha.


Potsegulira mau anu paunikira; kuzindikiritsa opusa.


Ndili nayo nzeru yakuposa aphunzitsi anga onse; pakuti ndilingalira mboni zanu.


Monga kavumvulu angopita, momwemo woipa kuli zii; koma olungama ndiwo maziko osatha.


Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo; koma chitsiru cholongolola chidzagwa.


Oipa amagwa kuli zii; koma banja la olungama limaimabe.


Nzeru ya wochenjera ndiyo yakuti azindikire njira yake; koma utsiru wa opusa ndiwo chinyengo.


Pakuti aliyense amene adzachita chifuniro cha Atate wanga wa Kumwamba, yemweyo ndiye mbale wanga, ndi mlongo wanga, ndi amai wanga.


Ndiponso Ine ndinena kwa iwe, kuti iwe ndiwe Petro, ndipo pa thanthwe ili ndidzakhazika Mpingo wanga; ndipo makomo a dziko la akufa sadzagonjetsa uwo.


Ndani kodi ali kapolo wokhulupirika ndi wanzeru, amene mbuye wake anamkhazika woyang'anira banja lake, kuwapatsa zakudya pa nthawi yake?


Ndipo asanu a iwo anali opusa, ndi asanu anali ochenjera.


koma anzeruwo anatenga mafuta m'nsupa zao, pamodzi ndi nyali zao.


Koma ochenjera anayankha nati, Kapena sangakwanire ife ndi inu; koma makamaka mukani kwa ogulitsa malonda, mukadzigulire inu nokha.


ndipo inagwa mvula, nidzala mitsinje, ndipo zinaomba mphepo, zinagunda pa nyumbayo; koma siinagwe; chifukwa inakhazikika pathanthwepo.


Ndipo yense akamva mau anga amenewa, ndi kusawachita, adzafanizidwa ndi munthu wopusa, yemwe anamanga nyumba yake pamchenga;


Koma Iye anati, Inde, koma odala iwo akumva mau a Mulungu, nawasunga.


Ngati mudziwa izi, odala inu ngati muzichita.


Ngati mukonda Ine, sungani malamulo anga.


Ngati musunga malamulo anga mudzakhala m'chikondi changa; monga Ine ndasunga malamulo a Atate wanga, ndipo ndikhala m'chikondi chake.


Muli abwenzi anga inu, ngati muzichita zimene ndikulamulani inu.


pakuti akumvaimva lamulo sakhala olungama pamaso pa Mulungu, koma akuchita lamulo adzayesedwa olungama.


Ndipo umo tizindikira kuti tamzindikira Iye, ngati tisunga malamulo ake.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa