Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Mateyu 24:35 - Buku Lopatulika

35 Thambo ndi dziko lapansi zidzachoka, koma mau anga sadzachoka ai.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

35 Thambo ndi dziko lapansi zidzachoka, koma mau anga sadzachoka ai.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

35 Thambo ndi dziko lapansi zidzatha, koma mau anga sadzatha mphamvu konse.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

35 Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”

Onani mutuwo Koperani




Mateyu 24:35
23 Mawu Ofanana  

Zidzatha izi, koma Inu mukhala: Inde, zidzatha zonse ngati chovala; mudzazisintha ngati malaya, ndipo zidzasinthika:


Mau anu aikika kumwamba, kosatha, Yehova.


Malamulo a Yehova ali angwiro, akubwezera moyo; mboni za Yehova zili zokhazikika, zakuwapatsa opusa nzeru.


Sindidzaipsa chipangano changa, kapena kusintha mau otuluka m'milomo yanga.


Mau onse a Mulungu ali oyengeka; ndiye chikopa cha iwo amene amkhulupirira.


Ndipo makamu onse a kumwamba adzasungunuka, ndi miyamba idzapindika pamodzi ngati mpukutu; makamu ao onse adzafota monga tsamba limafota pampesa ndi kugwa, ndi monga tsamba lifota pamkuyu.


Udzu unyala, duwa lifota, koma mau a Mulungu wathu adzakhala nthawi zachikhalire.


Tukulani maso anu kumwamba, ndipo muyang'ane pansi padziko pakuti kumwamba kudzachoka ngati utsi, ndi dziko lidzatha ngati chofunda, ndipo iwo amene akhala m'menemo adzafa ngati njenjete; koma chipulumutso changa chidzakhala kunthawi zonse, ndi chilungamo changa sichidzachotsedwa.


Pakuti mapiri adzachoka, ndi zitunda zidzasunthika; koma kukoma mtima kwanga sikudzakuchokera iwe, kapena kusunthika chipangano changa cha mtendere, ati Yehova amene wakuchitira iwe chifundo.


momwemo adzakhala mau anga amene atuluka m'kamwa mwanga, sadzabwerera kwa Ine chabe, koma adzachita chimene ndifuna, ndipo adzakula m'mene ndinawatumizira.


Chonsechi chinagwera mfumu Nebukadinezara.


Mulungu sindiye munthu, kuti aname; kapena mwana wa munthu, kuti aleke; kodi anena, osachita?


Pakuti indetu ndinena kwa inu, Kufikira litapitirira thambo ndi dziko, kalemba kakang'ono kamodzi kapena kansonga kake kamodzi sikadzachokera kuchilamulo, kufikira zitachitidwa zonse.


Thambo ndi dziko lapansi zidzapita; koma mau anga sadzapita.


Thambo ndi dziko lapansi zidzapita; koma mau anga sadzapita.


m'chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu, wosanamayo, analonjeza zisanayambe nthawi zosayamba;


koma Mau a Ambuye akhala chikhalire. Ndipo mau olalikidwa kwa inu ndi awo.


Ndipo ndinaona, mpando wachifumu waukulu woyera, ndi Iye wakukhalapo, amene dziko ndi m'mwamba zinathawa pamaso pake, ndipo sanapezedwe malo ao.


Ndipo kwa mngelo wa Mpingo wa ku Laodikea lemba: Izi anena Ameni'yo, mboni yokhulupirika ndi yoona, woyamba wa chilengo cha Mulungu:


Ndipo kumwamba kudachoka monga ngati mpukutu wopindidwa; ndi mapiri onse ndi zisumbu zonse zinatunsidwa kuchoka m'malo mwao.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa