Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Masalimo 107:1 - Buku Lopatulika

1 Yamikani Yehova pakuti Iye ndiye wabwino; pakuti chifundo chake nchosatha.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Yamikani Yehova pakuti Iye ndiye wabwino; pakuti chifundo chake nchosatha.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Thokozani Chauta chifukwa ngwabwino, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 107:1
15 Mawu Ofanana  

Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino; pakuti chifundo chake nchosatha.


ndi pamodzi nao Hemani, ndi Yedutuni, ndi osankhika otsalawo, otchulidwa maina, kuyamika Yehova; pakuti chifundo chake nchosatha;


Ndipo atafunsana ndi anthu, anaika oimbira Yehova, ndi kulemekeza chiyero chokometsetsa, pakutuluka iwo kutsogolera khamu la nkhondo, ndi kuti, Yamikani Yehova, pakuti chifundo chake chikhala chosatha.


Ndipo kunali, pakuchita limodzi amalipenga ndi oimba, kumveketsa mau amodzi akulemekeza ndi kuyamika Yehova, ndi pakukweza mau ao pamodzi ndi malipenga, ndi nsanje, ndi zoimbira zina, ndi kulemekeza Yehova, ndi kuti, Pakuti Iye ndiye wabwino, pakuti chifundo chake chikhala chikhalire; pamenepo mtambo unadzaza nyumbayi, ndiyo nyumba ya Yehova;


Ndi ana onse a Israele anapenyerera potsika motowo, ndi pokhala ulemerero wa Yehova pa nyumbayi; nawerama nkhope zao pansi poyalidwa miyala, nalambira, nayamika Yehova, nati, Pakuti Iye ndiye wabwino, pakuti chifundo chake chikhala chikhalire.


Naimirira ansembe mu udikiro wao; ndi Alevi omwe ndi zoimbira za Yehova, adazipanga Davide mfumu kuyamika nazo Yehova, pakuti chifundo chake chikhala chikhalire, polemekeza Davide mwa utumiki wao; ndi ansembe anaomba malipenga pamaso pao, nakhala chilili Israele yense.


Pakuti Yehova ndiye wabwino; chifundo chake chimanka muyaya; ndi chikhulupiriko chake ku mibadwomibadwo.


Koma chifundo cha Yehova ndicho choyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha kwa iwo akumuopa Iye, ndi chilungamo chake kufikira kwa ana a ana;


Yamikani Yehova, itanirani pa dzina lake; bukitsani mwa mitundu ya anthu zochita Iye.


Aleluya. Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino: Pakuti chifundo chake nchosatha.


Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino; pakuti chifundo chake nchosatha.


Inu ndinu wabwino, ndi wakuchita zabwino; mundiphunzitse malemba anu.


Ndipo Iye anati kwa iye, Undifunsiranji za chinthu chabwino? Alipo Mmodzi ndiye wabwino: koma ngati ufuna kulowa m'moyo, sunga malamulo.


Ndipo chifundo chake chifikira anthu a mibadwomibadwo pa iwo amene amuopa Iye.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa