Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 36 - Buku Lopatulika


Kuipitsitsa kwa anthu, kukometsetsa kwa Mulungu
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide, mtumiki wa Yehova.

1 Cholakwa cha woipayo chimati m'kati mwa mtima wanga, palibe kuopa Mulungu pamaso pake.

2 Pakuti adzidyoletsa yekha m'kuona kwake, kuti anthu sadzachipeza choipa chake ndi kukwiya nacho.

3 Mau a pakamwa pake ndiwo opanda pake ndi onyenga, waleka kuzindikira ndi kuchita bwino.

4 Alingirira zopanda pake pakama pake; adziika panjira posati pabwino; choipa saipidwa nacho.

5 Yehova, m'mwamba muli chifundo chanu; choonadi chanu chifikira kuthambo.

6 Chilungamo chanu chikunga mapiri a Mulungu; maweruzo anu akunga chozama chachikulu, Yehova, musunga munthu ndi nyama.

7 Ha! Chifundo chanu, Mulungu, nchokondedwadi! Ndipo ana a anthu athawira kumthunzi wa mapiko anu.

8 Adzakhuta kwambiri ndi zonona za m'nyumba mwanu, ndipo mudzawamwetsa mu mtsinje wa zokondweretsa zanu.

9 Pakuti chitsime cha moyo chili ndi Inu, M'kuunika kwanu tidzaona kuunika.

10 Tanimphitsani chifundo chanu pa iwo akudziwa Inu; ndi chilungamo chanu pa oongoka mtima.

11 Phazi la akudzikuza lisandifikire ine, ndi dzanja la oipa lisandichotse.

12 Pomwepo padagwera ochita zopanda pake. Anawalikha, ndipo sadzatha kuukanso.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa