Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 147 - Buku Lopatulika


Alemekeze dzina la Mulungu chifukwa cha zokoma amachitira anthu ake

1 Aleluya; Pakuti kuimbira zomlemekeza Mulungu wathu nkokoma; pakuti chikondweretsa ichi, chilemekezo chiyenera.

2 Yehova amanga Yerusalemu; asokolotsa otayika a Israele.

3 Achiritsa osweka mtima, namanga mabala ao.

4 Awerenga nyenyezi momwe zili; azitcha maina zonsezi.

5 Ambuye wathu ndi wamkulu ndi wa mphamvu zambiri; nzeru yake njosatha.

6 Yehova agwiriziza ofatsa; atsitsira oipa pansi.

7 Yamikani Yehova ndi kuthira mang'ombe; muimbireni Mulungu wathu zomlemekeza pazeze:

8 Amene aphimba thambo ndi mitambo, amene akonzera mvula nthaka, amene aphukitsa msipu pamapiri.

9 Amene apatsa zoweta chakudya chao, ana a khwangwala alikulira.

10 Mphamvu ya kavalo siimkonda: Sakondwera nayo miyendo ya munthu.

11 Yehova akondwera nao akumuopa Iye, iwo akuyembekeza chifundo chake.

12 Yerusalemu, lemekezani Yehova; Ziyoni, lemekezani Mulungu wanu.

13 Popeza analimbitsa mipiringidzo ya zitseko zanu: Anadalitsa ana anu m'kati mwanu.

14 Ndiye amene akhalitsa malire anu mumtendere; akukhutitsani ndi tirigu wakucha bwino.

15 Atumiza lamulo lake kudziko lapansi; mau ake athamanga liwiro.

16 Apatsa chipale chofewa ngati ubweya; awaza chisanu ngati phulusa.

17 Aponya matalala ake ngati zidutsu: Adzaima ndani pa kuzizira kwake?

18 Atumiza mau ake nazisungunula; aombetsa mphepo yake, ayenda madzi ake.

19 Aonetsa mau ake kwa Yakobo; malemba ake, ndi maweruzo ake kwa Israele.

20 Sanatero nao anthu a mtundu wina; ndipo za maweruzo ake, sanawadziwe. Aleluya.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa