Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 147:6 - Buku Lopatulika

6 Yehova agwiriziza ofatsa; atsitsira oipa pansi.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 Yehova agwiriziza ofatsa; atsitsira oipa pansi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 Amakweza oponderezedwa, koma amagwetsa pansi anthu oipa.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 147:6
16 Mawu Ofanana  

Yehova agwiriziza onse akugwa, naongoletsa onse owerama.


Popeza Yehova akondwera nao anthu ake; adzakometsa ofatsa ndi chipulumutso.


Adzawatsogolera ofatsa m'chiweruzo; ndipo adzaphunzitsa ofatsa njira yake.


Koma ofatsa adzalandira dziko lapansi; nadzakondwera nao mtendere wochuluka.


Wodalitsika Yehova, Mulungu wa Israele, kuchokera nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha. Amen, ndi Amen.


Koma Inu, Mulungu, mudzawatsitsira kudzenje la chionongeko. Anthu okhetsa mwazi ndi achinyengo masiku ao sadzafikira nusu; koma ine ndidzakhulupirira Inu.


Funani Yehova, ofatsa inu nonse a m'dziko, amene munachita chiweruzo chake; funani chilungamo, funani chifatso; kapena mudzabisika tsiku la mkwiyo wa Yehova.


Ndipo mudzapondereza oipa; pakuti adzakhala ngati mapulusa kumapazi anu, tsiku ndidzaikalo, ati Yehova wa makamu.


Odala ali akufatsa; chifukwa adzalandira dziko lapansi.


Dzichepetseni pamaso pa Ambuye, ndipo adzakukwezani.


koma kukhale munthu wobisika wamtima, m'chovala chosaola cha mzimu wofatsa ndi wachete, ndiwo wa mtengo wake wapatali pamaso pa Mulungu.


Potero dzichepetseni pansi padzanja la mphamvu la Mulungu, kuti panthawi yake akakukwezeni;


Amuutsa waumphawi m'fumbi, nanyamula wosowa padzala, kukamkhalitsa kwa akalonga; ndi kuti akhale nacho cholowa cha chimpando cha ulemerero. Chifukwa nsanamira za dziko lapansi nza Yehova, ndipo Iye anakhazika dziko pa izo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa