Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 128 - Buku Lopatulika


Wakuopa Yehova adalitsidwa m'banja mwake
Nyimbo yokwerera.

1 Wodala yense wakuopa Yehova, wakuyenda m'njira zake.

2 Pakuti udzadya za ntchito ya manja ako; wodala iwe, ndipo kudzakukomera.

3 Mkazi wako adzanga mpesa wopatsa m'mbali za nyumba yako; ana ako adzanga timitengo ta azitona pozinga podyera pako.

4 Taonani, m'mwemo adzadalitsika munthu wakuopa Yehova.

5 Yehova adzakudalitsa ali mu Ziyoni; ndipo udzaona zokoma za Yerusalemu masiku onse a moyo wako.

6 Inde, udzaona zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israele.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa