Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


NDIME ZA MULUNGU

NDIME ZA MULUNGU

Mulungu ndiye mlengi wako, mtetezi wako, wosamalira wako. Ndi wamphamvuzonse, wachifundo, wokhululuka, wabwino. Tingadziwe Mulungu kudzera m'mawu ake. Amakuikira mtima ndipo wakupangira dongosolo labwino pa moyo wako.

Amadziwa zonse zisanachitike. Ndi chikondi chosatha. Pakuti Ine Yehova ndine Mulungu wako, wakugwira dzanja lako lamanja, nanena ndi iwe, Usawopa; Ine ndikuthandiza. (Yesaya 41:13)

Choncho Mulungu nthawi zonse adzakhala nafe, timangofunika kumuyandikila. Iye ndiye mlengi ndi wosamalira zinthu zonse, amene anapulumutsa dziko kudzera mwa Mwana wake, Yesu Khristu.




Genesis 1:1

Pachiyambi Mulungu adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 42:2

Ndidziwa kuti mukhoza kuchita zonse, ndi kuti palibe choletsa cholingirira chanu chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 32:17

Ha! Yehova Mulungu, taonani, Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi ndi mphamvu yanu yaikulu ndi mkono wanu wotambasuka; palibe chokanika Inu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 19:26

Ndipo Yesu anawayang'ana, nati kwa iwo, Ichi sichitheka ndi anthu, koma zinthu zonse zitheka ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:37

Chifukwa palibe mau amodzi akuchokera kwa Mulungu adzakhala opanda mphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:28

Kodi iwe sunadziwe? Kodi sunamve? Mulungu wachikhalire, Yehova, Mlengi wa malekezero a dziko lapansi, salefuka konse, salema; nzeru zake sizisanthulika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 115:3

Koma Mulungu wathu ndiye ali m'mwamba; achita chilichonse chimkonda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 15:6

Dzanja lanu lamanja, Yehova, lalemekezedwa ndi mphamvu, dzanja lanu lamanja, Yehova, laphwanya mdani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 29:11-12

Ukulu, ndi mphamvu, ndi ulemerero, ndi chipambano, ndi chifumu ndi zanu, Yehova; pakuti zonse zam'mwamba ndi padziko lapansi ndi zanu; ufumu ndi wanu, Yehova; ndipo mwakwezeka mutu wa pa zonse. Zolemera ndi ulemu zifuma kwanu, ndipo muchita ufumu pa zonse, ndi m'dzanja mwanu muli mphamvu yaikulu; kukuza ndi kupatsa onse mphamvu kuli m'dzanja lanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 62:11

Mulungu ananena kamodzi, ndinachimva kawiri, kuti mphamvu ndi yake ya Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 32:27

Taona, Ine ndine Yehova, Mulungu wa anthu onse; kodi kuli kanthu kondikanika Ine?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 19:6

Ndipo ndinamva ngati mau a khamu lalikulu, ngati mkokomo wa madzi ambiri, ngati mau a mabingu olimba, ndi kunena, Aleluya; pakuti achita ufumu Ambuye Mulungu wathu, Wamphamvuyonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:5

Ambuye wathu ndi wamkulu ndi wa mphamvu zambiri; nzeru yake njosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:20

Pakuti chilengedwere dziko lapansi zaoneka bwino zosaoneka zake ndizo mphamvu yake yosatha ndi umulungu wake; popeza zazindikirika ndi zinthu zolengedwa, kuti iwo adzakhale opanda mau akuwiringula;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 14:14

Yehova adzakugwirirani nkhondo, ndipo inu mudzakhala chete.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 33:6

Zakumwamba zinalengedwa ndi mau a Yehova; ndipo ndi mpweya wa m'kamwa mwake khamu lao lonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 1:3

ameneyo, pokhala ali chinyezimiro cha ulemerero wake, ndi chizindikiro chenicheni cha chikhalidwe chake, nanyamula zonse ndi mau a mphamvu yake, m'mene adachita chiyeretso cha zoipa, anakhala padzanja lamanja la Ukulu mu Mwamba,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 26:14

Taonani, awa ndi malekezero a njira zake; ndi chimene tikumva za Iye ndi chinong'onezo chaching'ono; koma kugunda kwa mphamvu yake akuzindikiritsa ndani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Danieli 4:35

ndi okhala padziko lapansi onse ayesedwa achabe; ndipo Iye achita mwa chifuniro chake m'khamu la kumwamba ndi mwa okhala padziko lapansi; ndipo palibe woletsa dzanja lake, kapena wakunena naye, Muchitanji?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 45:7

Ine ndilenga kuyera ndi mdima, Ine ndilenga mtendere ndi choipa, Ine ndine Yehova wochita zinthu zonse zimenezi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 3:14

Ndipo Mulungu anati kwa Mose, INE NDINE YEMWE NDILI INE. Anatinso, Ukatero ndi ana a Israele, INE NDINE wandituma kwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 11:36

Chifukwa zinthu zonse zichokera kwa Iye, zichitika mwa Iye, ndi kufikira kwa Iye. Kwa Iyeyo ukhale ulemerero kunthawi zonse. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 6:14

koma Mulungu anaukitsa Ambuye, ndiponso adzaukitsa ife mwa mphamvu yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 46:10

Khalani chete, ndipo dziwani kuti Ine ndine Mulungu, Ndidzabuka mwa amitundu, ndidzabuka padziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:13

Ndikhoza zonse mwa Iye wondipatsa mphamvuyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 24:8

Mfumu imene ya ulemerero ndani? Yehova wamphamvu ndi wolimba, Yehova wolimba kunkhondo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 15:11

Afanana ndi Inu ndani mwa milungu, Yehova? Afanana ndi Inu ndani, wolemekezedwa, woyera, woopsa pomyamika, wakuchita zozizwa?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 77:14

Inu ndinu Mulungu wakuchita chodabwitsa; munazindikiritsa mphamvu yanu mwa mitundu ya anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:30

Kulibe nzeru ngakhale luntha ngakhale uphungu wotsutsana ndi Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 12:9

Ndipo ananena kwa ine, Chisomo changa chikukwanira; pakuti mphamvu yanga ithedwa mu ufooko. Chifukwa chake makamaka ndidzadzitamandira mokondweratu m'mafooko anga, kuti mphamvu ya Khristu ikhale pa ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 136:12

Ndi dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka; pakuti chifundo chake nchosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:4-5

Awerenga nyenyezi momwe zili; azitcha maina zonsezi. Ambuye wathu ndi wamkulu ndi wa mphamvu zambiri; nzeru yake njosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 44:24

Atero Yehova, Mombolo wako, ndi Iye amene anakuumba iwe m'mimba, Ine ndine Yehova, amene ndipanga zinthu zonse, ndi kufunyulula ndekha zakumwamba, ndi kuyala dziko lapansi; ndani ali ndi Ine?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 10:17

Popeza Yehova Mulungu wanu ndiye Mulungu wa milungu, ndi Mbuye wa ambuye; Mulungu wamkulu, wamphamvu, ndi woopsa, wosasamalira nkhope za anthu, kapena kulandira chokometsera mlandu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 6:15-16

limene adzalionetsa m'nyengo za Iye yekha, amene ali Mwini Mphamvu wodala ndi wayekha, ndiye Mfumu ya mafumu ndi Mbuye wa ambuye; amene Iye yekha ali nao moyo wosatha, wakukhala m'kuunika kosakhozeka kufikako; amene munthu sanamuone, kapena sangathe kumuona; kwa Iye kukhale ulemu ndi mphamvu yosatha. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 43:13

Inde chiyambire nthawi Ine ndine, ndipo palibe wina wopulumutsa m'dzanja langa; ndidzagwira ntchito, ndipo ndani adzaletsa?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Danieli 2:20-22

Daniele anayankha, nati, Lilemekezedwe dzina la Mulungu kunthawi za nthawi, pakuti nzeru ndi mphamvu zili zake; pakuti amasanduliza nthawi ndi nyengo, achotsa mafumu, nalonga mafumu, apatsa anzeru nzeru, ndi chidziwitso kwa iwo okhoza kuzindikira. Iye avumbulutsa zinthu zakuya ndi zinsinsi; adziwa zokhala mumdima, ndi kuunika kumakhala kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 9:4

Ndiye wa mtima wanzeru, ndi wa mphamvu yaikulu; ndaniyo anadziumitsa mtima pa Iye, nakhala nao mtendere?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 10:12

Iye analenga dziko lapansi ndi mphamvu yake, nakhazikitsa dziko lapansi ndi nzeru yake, nayala thambo ndi kuzindikira kwake;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 45:5-6

Ine ndili Yehova, ndipo palibe winanso; popanda Ine palibe Mulungu; ndidzakumanga m'chuuno, ngakhale sunandidziwe; kuti anthu akadziwe kuchokera kumatulukiro a dzuwa ndi kumadzulo, kuti palibe wina popanda Ine; Ine ndine Yehova, palibe winanso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 12:10

M'dzanja mwake muli mpweya wa zamoyo zonse, ndi mzimu wa munthu aliyense.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:31

Ndipo tidzatani ndi zinthu izi? Ngati Mulungu ali ndi ife, adzatikaniza ndani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:8

Yesu Khristu ali yemweyo dzulo, ndi lero, ndi kunthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 89:8

Yehova, Mulungu wa makamu, wamphamvu ndani wonga Inu, Yehova? Ndipo chikhulupiriko chanu chikuzingani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 1:3

Zonse zinalengedwa ndi Iye; ndipo kopanda Iye sikunalengedwe kanthu kalikonse kolengedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:16

pakuti mwa Iye, zinalengedwa zonse za m'mwamba, ndi za padziko, zooneka ndi zosaonekazo, kapena mipando yachifumu, kapena maufumu, kapena maukulu, kapena maulamuliro; zinthu zonse zinalengedwa mwa Iye ndi kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 46:1

Mulungu ndiye pothawirapo pathu ndi mphamvu yathu, thandizo lopezekeratu m'masautso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:22

Ndi Iye amene akhala pamwamba pa malekezero a dziko lapansi, ndipo okhalamo akunga ziwala; amene afutukula thambo ngati chinsalu, naliyala monga hema wakukhalamo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 18:2

Yehova ndiye thanthwe langa, ndi linga langa, ndi Mpulumutsi wanga; Mulungu wanga, ngaka yanga, ndidzakhulupirira Iye; chikopa changa, nyanga ya chipulumutso changa, msanje wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 66:7

Achita ufumu mwa mphamvu yake kosatha; maso ake ayang'anira amitundu; opikisana ndi Iye asadzikuze.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 37:23

Kunena za Wamphamvuyonse, sitingamsanthule; ndiye wa mphamvu yoposa; koma mwa chiweruzo ndi chilungamo chochuluka samasautsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nahumu 1:3

Yehova ndiye wolekerera mkwiyo, koma wa mphamvu yaikulu; ndi wosamasula ndithu wopalamula; njira ya Yehova ili m'kamvulumvulu ndi mumkuntho; ndipo mitambo ndiyo fumbi la mapazi ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 20:6

ndi kuwachitira chifundo anthu zikwizikwi a iwo amene akondana ndi Ine, nasunga malamulo anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 42:5

Atero Mulungu Yehova, Iye amene analenga thambo, nalifutukula, nayala ponse dziko lapansi, ndi chimene chituluka m'menemo, Iye amene amapatsa anthu a m'menemo mpweya, ndi mzimu kwa iwo amene ayenda m'menemo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 46:10

ndilalikira za chimaliziro kuyambira pachiyambi, ndi kuyambira nthawi zakale ndinena zinthu zimene zisanachitidwe; ndi kunena, Uphungu wanga udzakhala, ndipo ndidzachita zofuna zanga zonse;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 135:6

Chilichonse chimkonda Yehova achichita, kumwamba ndi padziko lapansi, m'nyanja ndi mozama monse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:6

Potero dzichepetseni pansi padzanja la mphamvu la Mulungu, kuti panthawi yake akakukwezeni;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 3:20

Ndipo kwa Iye amene angathe kuchita koposaposatu zonse zimene tizipempha, kapena tiziganiza, monga mwa mphamvu ya kuchita mwa ife,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 4:11

Muyenera inu, Ambuye wathu, ndi Mulungu wathu, kulandira ulemerero ndi ulemu ndi mphamvu; chifukwa mudalenga zonse, ndipo mwa chifuniro chanu zinakhala, ndipo zinalengedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 18:27

Koma Iye anati, Zinthu zosatheka ndi anthu zitheka ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 89:13

Muli nao mkono wanu wolimba; m'dzanja mwanu muli mphamvu, dzanja lamanja lanu nlokwezeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 9:6

Pakuti kwa ife mwana wakhanda wabadwa, kwa ife mwana wamwamuna wapatsidwa; ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake, ndipo adzamutcha dzina lake Wodabwitsa, Wauphungu, Mulungu wamphamvu, Atate Wosatha, Kalonga wa mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 4:6

Pamenepo anayankha, nanena kwa ine, ndi kuti, Awa ndi mau a Yehova kwa Zerubabele, Ndi khamu la nkhondo ai, ndi mphamvu ai, koma ndi Mzimu wanga, ati Yehova wa makamu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 93:1

Yehova achita ufumu; wadziveka ndi ukulu; wadziveka Yehova, wadzimangirira mphamvu m'chuuno; dziko lomwe lokhalamo anthu likhakizika, silidzagwedezeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 16:27

kwa Mulungu wanzeru yekhayo, mwa Yesu Khristu, kwa yemweyo ukhale ulemerero kunthawi zonse. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:24-25

Ntchito zanu zichulukadi, Yehova! Munazichita zonse mwanzeru; dziko lapansi lidzala nacho chuma chanu. Nyanja siyo, yaikulu ndi yachitando, m'mwemo muli zokwawa zosawerengeka; zamoyo zazing'ono ndi zazikulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 55:8-9

Pakuti maganizo anga sali maganizo anu, ngakhale njira zanu sizili njira zanga, ati Yehova. Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, momwemo njira zanga zili zazitali kupambana njira zanu, ndi maganizo anga kupambana maganizo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 28:18

Ndipo Yesu anadza nalankhula nao, nanena, Mphamvu zonse zapatsidwa kwa Ine Kumwamba ndi padziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Samueli 22:32-33

Pakuti Mulungu ndani, koma Yehova? Ndipo thanthwe ndani, koma Mulungu wathu? Mulungu ndiye linga langa lamphamvu; ndipo Iye ayendetsa angwiro mu njira yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 41:10

usaope, pakuti Ine ndili pamodzi ndi iwe; usaopsedwe, pakuti Ine ndine Mulungu wako; ndidzakulimbitsa; inde, ndidzakuthangata; inde, ndidzakuchirikiza ndi dzanja langa lamanja la chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 33:9

Pakuti ananena, ndipo chinachitidwa; analamulira, ndipo chinakhazikika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:15

Atumiza lamulo lake kudziko lapansi; mau ake athamanga liwiro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:10

Taonani, Ambuye Yehova adzadza ngati wamphamvu, ndipo mkono wake udzalamulira; taonani, mphotho yake ili ndi Iye, ndipo chobwezera chake chili patsogolo pa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 6:3

ndipo ndinaonekera Abrahamu, Isaki ndi Yakobo, Mulungu Wamphamvuyonse; koma sindinadziwike kwa iwo ndi dzina langa YEHOVA.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 7:21

Musamaopa pamaso pao; popeza Yehova Mulungu wanu ali pakati pa inu, Mulungu wamkulu ndi woopsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Oweruza 6:12

Ndipo mthenga wa Yehova anamuonekera, nati kwa iye, Yehova ali nawe, ngwazi iwe, wamphamvu iwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 106:8

Koma anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti adziwitse chimphamvu chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:17

Koma Yesu anayankha iwo, Atate wanga amagwira ntchito kufikira tsopano, Inenso ndigwira ntchito.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 12:29

Pakuti Mulungu wathu ndiye moto wonyeketsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 18:14

Kodi chilipo chinthu chomkanika Yehova? Pa nthawi yoikidwa ndidzabwera kwa iwe, pakufika nyengo yake, ndipo Sara adzakhala ndi mwana wamwamuna.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 8:3-4

Pakuona ine thambo la kumwamba lanu, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene munazikhazika, munthu ndani kuti mumkumbukira? Ndi mwana wa munthu kuti mucheza naye?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 9:16

Koma ndithu chifukwa chake ndakuimika kuti ndikuonetse mphamvu yanga, ndi kuti alalikire dzina langa padziko lonse lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 29:4

Liu la Yehova ndi lamphamvu; liu la Yehova ndi lalikulukulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:8

Udzu unyala, duwa lifota, koma mau a Mulungu wathu adzakhala nthawi zachikhalire.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 4:35

Inu munachiona ichi, kuti mudziwe kuti Yehova ndiye Mulungu; palibe wina wopanda Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 51:9

Galamuka, galamuka, khala ndi mphamvu, mkono wa Yehova; galamuka monga masiku akale, mibadwo ya nthawi zakale. Kodi si ndiwe amene unadula Rahabu zipinjirizipinjiri; amene unapyoza chinjoka chamnyanja chija?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 93:4

Yehova Wam'mwamba ndiye wamphamvu, wakuposa mkokomo wa madzi ambiri, ndi mafunde olimba a nyanja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 51:15

Iye analenga dziko lapansi ndi mphamvu yake, wakhazika dziko lapansi ndi nzeru yake, ndi luso anayala thambo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 5:24

Koma kuti mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali nayo mphamvu padziko lapansi yakukhululukira machimo, (anati Iye kwa wamanjenjeyo), Ndinena kwa iwe, Tauka, nusenze kama wako, numuke kunyumba kwako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 29:10

Yehova anakhala pa chigumula, inde Yehova akhala mfumu kunthawi yonka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 55:11

momwemo adzakhala mau anga amene atuluka m'kamwa mwanga, sadzabwerera kwa Ine chabe, koma adzachita chimene ndifuna, ndipo adzakula m'mene ndinawatumizira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 21:6

Ndipo anati kwa ine, Zatha. Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza. Kwa iye wakumva ludzu ndidzampatsa amwe kukasupe wa madzi a moyo kwaulere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 9:21

Kodi kapena woumba mbiya sakutha kuchita zake padothi, kuumba ndi nchinchi yomweyo chotengera chimodzi chaulemu ndi china chamanyazi?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 1:10-12

Ndipo, Inu, Ambuye, pachiyambipo munaika maziko ake a dziko, ndipo miyamba ili ntchito ya manja anu. Iyo idzataika; komatu mukhalitsa; ndipo iyo yonse idzasuka monga malaya; ndi monga chofunda mudzaipinda monga malaya, ndipo idzasanduka; koma Inu ndinu yemweyo, ndipo zaka zanu sizidzatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:1-2

Lemekeza Yehova, moyo wanga; Yehova, Mulungu wanga, Inu ndinu wamkulukulu; Atumiza akasupe alowe m'makwawa; ayenda pakati pa mapiri: Zimamwamo nyama zonse zakuthengo; mbidzi zipherako ludzu lao. Mbalame za mlengalenga zifatsa pamenepo, zimaimba pakati pa mitawi. Iye amwetsa mapiri mochokera m'zipinda zake: Dziko lakhuta zipatso za ntchito zanu. Ameretsa msipu ziudye ng'ombe, ndi zitsamba achite nazo munthu; natulutse chakudya chochokera m'nthaka; ndi vinyo wokondweretsa mtima wa munthu, ndi mafuta akunyezimiritsa nkhope yake, ndi mkate wakulimbitsa mtima wa munthu. Mitengo ya Yehova yadzala ndi madzi; mikungudza ya ku Lebanoni imene anaioka; m'mwemo mbalame zimanga zisa zao; pokhala chumba mpa mitengo ya mikungudza. Mapiri aatali ndiwo ayenera zinkhoma; pamatanthwe mpothawirapo mbira. Anaika mwezi nyengo zake; dzuwa lidziwa polowera pake. muvala ulemu ndi chifumu. Amene mudzikuta nako kuunika monga ndi chovala; ndi kuyala thambo ngati nsalu yotchinga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:17

Ndipo Iye ali woyamba wa zonse, ndipo zonse zigwirizana pamodzi mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 33:11

Chiweruzo cha Yehova chikhazikika chikhazikikire, zolingirira za m'mtima mwake ku mibadwomibadwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 1:11

Mwa Iye tinayesedwa akeake olandira cholowa, popeza tinakonzekeratu monga mwa chitsimikizo mtima cha Iye wakuchita zonse monga mwa uphungu wa chifuniro chake;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:17

Amitundu onse ali chabe pamaso pa Iye; awayesa ngati chinthu chachabe, ndi chopanda pake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Samueli 22:33

Mulungu ndiye linga langa lamphamvu; ndipo Iye ayendetsa angwiro mu njira yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:5-6

Ndidzalingalira ulemerero waukulu wa ulemu wanu, ndi ntchito zanu zodabwitsa. Ndipo adzanenera mphamvu za ntchito zanu zoopsa; ndi ukulu wanu ndidzaufotokozera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 50:1

Mulungu wa milungu, Yehova, wanena, aitana dziko lapansi kuyambira kutuluka kwa dzuwa kufikira kulowa kwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 43:16-17

Atero Yehova, amene akonza njira panyanja, ndi popita m'madzi amphamvu; amene atulutsa galeta ndi kavalo, nkhondo ndi mphamvu; iwo agona pansi pamodzi sadzaukai; iwo atha, azimidwa ngati lawi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:28

Ndipo tidziwa kuti amene akonda Mulungu zinthu zonse zithandizana kuwachitira ubwino, ndiwo amene aitanidwa monga mwa kutsimikiza kwa mtima wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 51:19

Gawo la Yakobo silifanafana ndi izo; pakuti Iye ndiye analenga zonse; Israele ndi mtundu wa cholowa chake, dzina lake ndi Yehova wa makamu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 66:5-6

Idzani, muone ntchito za Mulungu; zochitira Iye ana a anthu nzoopsa. Anasanduliza nyanja ikhale mtunda. Anaoloka mtsinje choponda pansi, apo tinakondwera mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:16

Dzanja lamanja la Yehova likwezeka, Dzanja lamanja la Yehova lichita mwamphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 45:12

Ine ndalenga dziko lapansi, ndalengamo munthu; Ine, ngakhale manja anga, ndafunyulula kumwamba, ndi zonse za m'menemo, ndinazilamulira ndine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 1:8

Ine ndine Alefa ndi Omega, ati Ambuye Mulungu, amene ali, amene adali, ndi amene alinkudza, Wamphamvuyonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:11-12

Adzanenera ulemerero wa ufumu wanu, adzalankhulira mphamvu yanu. Kudziwitsa ana a anthu zamphamvu zake, ndi ulemerero waukulu wa ufumu wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 46:4

ngakhale mpaka mudzakalamba Ine ndine, ndipo ngakhale mpaka tsitsi laimvi, Ine ndidzakusenzani inu; ndalenga, ndipo ndidzanyamula; inde, ndidzasenza, ndipo ndidzapulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:49

Chifukwa Iye Wamphamvuyo anandichitira ine zazikulu; ndipo dzina lake lili loyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 9:29

Ndipo Mose ananena naye, Potuluka m'mzinda ine, ndidzakweza manja anga kwa Yehova; mabingu adzaleka, ndi matalala sadzakhalaponso; kuti mudziwe kuti dziko lapansi nla Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:13

Sichinakugwerani inu chiyeso koma cha umunthu; koma Mulungu ali wokhulupirika, amene sadzalola inu kuyesedwa koposa kumene mukhoza; koma pamodzi ndi chiyeso adzaikanso populumukirapo, kuti mudzakhoze kupirirako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 1:7

Pakuti Mulungu sanatipatse mzimu wa mantha; komatu wa mphamvu ndi chikondi ndi chidziletso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 68:35

Inu Mulungu, ndinu woopsa m'malo oyera anu; Mulungu wa Israele ndiye amene apatsa anthu ake mphamvu ndi chilimbiko. Alemekezeke Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:13-14

Ndani anapangira mzimu wa Yehova, kapena kukhala phungu lake, ndi kumphunzitsa Iye? Iye anakhala upo ndi yani, ndipo ndani analangiza Iye ndi kumphunzitsa m'njira ya chiweruzo, ndi kumphunzitsa nzeru ndi kumuonetsa njira ya luntha?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 26:12

Mwa mphamvu yake agwetsa nyanja bata; ndipo mwa luntha lake akantha kudzikuza kwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 32:18-19

amene muchitira chifundo anthu zikwi; nimubwezera mphulupulu ya atate m'chifukwa cha ana ao a pambuyo pao, dzina lake ndi Mulungu wamkulu, wamphamvu, Yehova wa makamu; wamkulu mu upo, wamphamvu m'ntchito; maso anu ali otsegukira njira zonse za ana a anthu; kuti mupatse yense monga mwa chipatso cha machitidwe ake;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 95:3-5

Pakuti Yehova ndiye Mulungu wamkulu; ndi mfumu yaikulu yoposa milungu yonse. Malo ozama a dziko lapansi ali m'dzanja lake; chuma cha m'mapiri chomwe ndi chake. Nyanja ndi yake, anailenga; ndipo manja ake anaumba dziko louma.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:33-34

Ndidzaimbira Yehova m'moyo mwanga: ndidzaimbira Mulungu wanga zomlemekeza pokhala ndilipo. Pomlingirira Iye pandikonde; ndidzakondwera mwa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Danieli 3:17-18

Taonani, Mulungu wathu amene timtumikira akhoza kutilanditsa m'ng'anjo yotentha yamoto, nadzatilanditsa m'dzanja lanu, mfumu. Koma akapanda kutero, dziwani, mfumu, kuti sitidzatumikira milungu yanu, kapena kulambira fano lagolide mudaliimikalo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 13:3

Ndipo Mose ananena ndi anthu, Kumbukirani tsiku lino limene munatuluka mu Ejipito, m'nyumba ya ukapolo; pakuti Yehova anakutulutsani muno ndi dzanja lamphamvu; ndipo asadye kanthu ka chotupitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 45:18

Pakuti atero Yehova amene analenga kumwamba, Iye ndiye Mulungu amene anaumba dziko lapansi, nalipanga; Iye analikhazikitsa, sanalilenge mwachabe; Iye analiumba akhalemo anthu; Ine ndine Yehova; ndipo palibenso wina.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:12-13

Yerusalemu, lemekezani Yehova; Ziyoni, lemekezani Mulungu wanu. Popeza analimbitsa mipiringidzo ya zitseko zanu: Anadalitsa ana anu m'kati mwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 4:21

nakhazikikanso mumtima kuti, chimene Iye analonjeza, anali nayonso mphamvu yakuchichita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 28:29

Ichinso chifumira kwa Yehova wa makamu, uphungu wake uzizwitsa ndi nzeru yake impambana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 15:3

Yehova ndiye wankhondo; dzina lake ndiye Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 49:15-16

Kodi mkazi angaiwale mwana wake wa pabere, kuti iye sangachitire chifundo mwana wombala iye? Inde awa angaiwale, koma Ine sindingaiwale iwe. Taona ndakulembera iwe pa zikhato za manja anga; makoma ako alipo masiku onse pamaso panga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nehemiya 9:6

Inu ndinu Yehova, nokhanu; mwalenga thambo, kumwambamwamba, ndi khamu lao lonse, dziko lapansi, ndi zonse zili pomwepo, nyanja ndi zonse zili m'mwemo, ndi Inu muzisunga zamoyo zonsezi, ndi khamu lakumwamba lilambira Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:14-16

Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; ndipo anakhala chipulumutso changa. M'mahema a olungama muli liu lakufuula mokondwera Dzanja lamanja la Yehova ndi la chipulumutso: Dzanja lamanja la Yehova likwezeka, Dzanja lamanja la Yehova lichita mwamphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 64:8

Koma tsopano, Yehova, Inu ndinu Atate wathu; ife tili dongo, ndipo Inu ndinu Muumbi wathu; ndipo ife tonse tili ntchito ya dzanja lanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 71:18

Poteronso pokalamba ine ndi kukhala nazo imvi musandisiye, Mulungu; kufikira nditalalikira mbadwo uwu za dzanja lanu, mphamvu yanu kwa onse akudza m'mbuyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 105:4

Funani Yehova, ndi mphamvu yake; funsirani nkhope yake nthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 6:7

m'mau a choonadi, mu mphamvu ya Mulungu; mwa zida za chilungamo kulamanja ndi kulamanzere,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:3

Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu; ndi ukulu wake ngwosasanthulika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 63:1

Ndani uyu alikudza kuchokera ku Edomu, ndi zovala zonyika zochokera ku Bozira? Uyu wolemekezeka m'chovala chake, nayenda mu ukulu wa mphamvu zake? Ndine amene ndilankhula m'cholungama, wa mphamvu yakupulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 34:10

Ndipo Iye anati, Taona, Ine ndichita pangano; ndidzachita zozizwa pamaso pa anthu ako onse, sizinachitike zotere ku dziko lonse lapansi, kapena ku mtundu uliwonse wa anthu; ndipo anthu onse amene uli pakati pao adzaona ntchito ya Yehova, pakuti chinthu ndikuchitirachi nchoopsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:13-14

Pakuti Inu munalenga impso zanga; munandiumba ndisanabadwe ine. Ndikuyamikani chifukwa kuti chipangidwe changa nchoopsa ndi chodabwitsa; ntchito zanu nzodabwitsa; moyo wanga uchidziwa ichi bwino ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 33:27

Mulungu wamuyaya ndiye mokhaliramo mwako; ndi pansipo pali manja osatha. Ndipo aingitsa mdani pamaso pako, nati, Ononga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 10:6

Chifukwa palibe akunga Inu, Yehova; muli wamkulu, ndipo dzina lanu lili lalikulu ndi lamphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 20:6

nati, Yehova Mulungu wa makolo athu, Inu sindinu Mulungu wa mu Mwamba kodi? Sindinu woweruza maufumu onse a amitundu kodi? Ndi m'dzanja mwanu muli mphamvu yolimba; palibe wina wakulimbana ndi Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 5:9

amene achita zazikulu ndi zosalondoleka, zinthu zodabwitsa zosawerengeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 72:18

Wolemekezeka Yehova Mulungu, Mulungu wa Israele, amene achita zodabwitsa yekhayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 26:4

Khulupirirani Yehova nthawi zamuyaya, pakuti mwa Ambuye Yehova muli thanthwe lachikhalire.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Danieli 2:21

pakuti amasanduliza nthawi ndi nyengo, achotsa mafumu, nalonga mafumu, apatsa anzeru nzeru, ndi chidziwitso kwa iwo okhoza kuzindikira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 50:2

Chifukwa chanji ndinafika osapeza munthu? Ndi kuitana koma panalibe wina woyankha? Kodi dzanja langa lafupika konse, kuti silingathe kuombola? Pena Ine kodi ndilibe mphamvu zakupulumutsa? Taona pa kudzudzula kwanga ndiumitsa nyanja, ndi kusandutsa mitsinje chipululu; nsomba zake zinunkha chifukwa mulibe madzi, ndipo zifa ndi ludzu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 36:22

Taonani, Mulungu achita mokwezeka mu mphamvu yake, mphunzitsi wakunga Iye ndani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 15:3-4

Ndipo aimba nyimbo ya Mose kapolo wa Mulungu, ndi nyimbo ya Mwanawankhosa, nanena, Ntchito zanu nzazikulu ndi zozizwitsa, Ambuye Mulungu, Wamphamvuyonse; njira zanu nzolungama ndi zoona, Mfumu Inu ya nthawi zosatha. Ndani adzakhala wosaopa ndi wosalemekeza dzina lanu Ambuye? Chifukwa Inu nokha muli woyera; chifukwa mitundu yonse idzadza nidzalambira pamaso panu, popeza zolungama zanu zidaonetsedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Zikomo Ambuye, inu ndinu wochiritsa wanga, wopereka wanga, ndi mlonda wanga. Inu ndinu amene mumalowerera nkhondo zanga, ndi kunditsogolera kuchoka pa ulemerero kupita pa ulemerero. M'dzina lamphamvu la Yesu, ndimabwera kwa inu kukulambirani ndi kukudalitsani chifukwa cha chikondi chanu chachikulu ndi chifundo chanu chosatha. Mfumu yanga, ndikudalitsani ndi kukukwezani chifukwa mwandikhululukira, mwandipulumutsa, mwandiyang'ana ndi chisomo Mulungu. Inu mumachita zizindikiro kumwamba ndi pano padziko lapansi, munatsegula nyanja pakati. Aa wodalitsidwa, Woyera wa Israeli! Aa Mulungu wodalitsidwa pakati pa mitundu yonse, iwo akukutamandani ndi kudalitsa dzina lanu, lomwe lili pamwamba pa dzina lililonse ndi kulengeza kuti ndinu Mfumu yayikulu. Mulungu ndikupemphani kuti nthawi zonse chiyamiko chanu chikhale mkamwa mwanga nthawi zonse. Mawu anu amati: "Wodalitsika Mulungu ndi Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu, amene anatidalitsa ndi madalitso onse auzimu m'malo akumwamba mwa Khristu." Zikomo chifukwa chifundo chanu ndi cha mibadwo ndi mibadwo, inu ndinu Mulungu wanga, Mfumu yanga ndipo palibe chabwino kunja kwa inu. Inu ndinu mlengi wa kumwamba ndi dziko lapansi, dzina lanu lokha ndilo lokwezeka, onse oyera mtima anu atamande ndi kuimba ndi chimwemwe chifukwa ntchito zanu ndi zodabwitsa ndi zosawerengeka monga mchenga wa m'nyanja. M'dzina la Yesu. Ameni!
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa