Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Masalimo 116:1 - Buku Lopatulika

1 Ndimkonda, popeza Yehova amamva mau anga ndi kupemba kwanga.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Ndimkonda, popeza Yehova amamva mau anga ndi kupemba kwanga.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Ndimakonda Chauta chifukwa amamva mau anga omupemba.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 116:1
20 Mawu Ofanana  

Ndipo Yakobo anati kwa a banja lake, ndi kwa onse amene anali ndi iye, Chotsani milungu yachilendo ili mwa inu, mudziyeretse, ndi kupindula zovala zanu:


Ndipo Yehova anati kwa iye, Ndamva pemphero lako ndi pembedzero lako wandipembedza nalo; ndapatula nyumba imene waimangayi kuikamo dzina langa nthawi zosatha, ndipo maso anga ndi mtima wanga zidzakhala kumeneko masiku onse.


Munditembenukire, ndi kundichitira chifundo, monga mumatero nao akukonda dzina lanu.


Wodalitsika Yehova, Pakuti adamva mau a kupemba kwanga.


Kuyembekeza ndayembekeza Yehova; ndipo anandilola, namva kufuula kwanga.


Pakuti Yehova amvera aumphawi, ndipo sapeputsa am'ndende ake.


Kodi ndidzanena chiyani? Iye wanena kwa ine, ndiponso Iye mwini wachita ichi; Ine ndidzayenda chete zaka zanga zonse, chifukwa cha zowawa za moyo wanga.


munamva mau anga; musabise khutu lanu popuma ndi pofuula ine.


Pakuti munandiponya mwakuya m'kati mwa nyanja, ndipo madzi anandizinga; mafunde anu onse a nyondonyondo anandimiza.


Ndipo Yehova anamvera mau a Israele, napereka Akanani; ndipo anawaononga konse ndi mizinda yao yomwe; natcha dzina lake la malowo Horoma.


ndipo, kumkonda Iye ndi mtima wonse, ndi nzeru yonse, ndi mphamvu yonse, ndi kukonda mnzake monga adzikonda mwini, ndiko kuposa nsembe zopsereza zamphumphu zonse, ndi nsembe zophedwa.


Kufikira tsopano simunapemphe kanthu m'dzina langa; pemphani, ndipo mudzalandira, kuti chimwemwe chanu chikwaniridwe.


Ananena naye kachitatu, Simoni mwana wa Yona, kodi undikonda Ine? Petro anamva chisoni kuti anati kwa iye kachitatu, Kodi undikonda Ine? Ndipo anati kwa iye, Ambuye, mudziwa Inu zonse; muzindikira kuti ndikukondani Inu. Yesu ananena naye, Dyetsa nkhosa zanga.


Tikonda ife, chifukwa anayamba Iye kutikonda.


Ndipo mkaziyo ananena, Mbuye wanga, pali moyo wanu, zoonadi ine ndine mkazi uja ndidaima pano ndi inu, ndi kupemphera kwa Yehova.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa