Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 118 - Buku Lopatulika


Wa Salimo alemekeza Mulungu womlanditsa m'manja mwa adani

1 Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino; pakuti chifundo chake nchosatha.

2 Anene tsono Israele, kuti chifundo chake nchosatha.

3 Anene tsono nyumba ya Aroni, kuti chifundo chake nchosatha.

4 Anene tsono iwo akuopa Yehova, kuti chifundo chake nchosatha.

5 M'mene ndinasautsika ndinaitanira pa Yehova; anandiyankha nandiika motakasuka Yehova.

6 Yehova ndi wanga; sindidzaopa; adzandichitanji munthu?

7 Yehova ndi wanga, mwa iwo akundithandiza; m'mwemo ndidzaona chofuna ine pa iwo akundida.

8 Kuthawira kwa Yehova nkokoma koposa kukhulupirira munthu.

9 Kuthawira kwa Yehova nkokoma koposa kukhulupirira akulu.

10 Amitundu onse adandizinga, zedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula.

11 Adandizinga, inde, adandizinga: Indedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula.

12 Adandizinga ngati njuchi; anazima ngati moto waminga; indedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula.

13 Kundikankha anandikankha ndikadagwa; koma Yehova anandithandiza.

14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; ndipo anakhala chipulumutso changa.

15 M'mahema a olungama muli liu lakufuula mokondwera Dzanja lamanja la Yehova ndi la chipulumutso:

16 Dzanja lamanja la Yehova likwezeka, Dzanja lamanja la Yehova lichita mwamphamvu.

17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo, ndipo ndidzafotokozera ntchito za Yehova.

18 Kulanga anandilangadi Yehova: koma sanandipereke kuimfa ai.

19 Nditsegulireni zipata za chilungamo; ndidzalowamo, ndidzayamika Yehova.

20 Chipata cha Yehova ndi ichi; olungama adzalowamo.

21 Ndidzakuyamikani, popeza munandiyankha, ndipo munakhala chipulumutso changa.

22 Mwala umene omangawo anaukana wakhala mutu wa pangodya.

23 Ichi chidzera kwa Yehova; nchodabwitsa ichi pamaso pathu.

24 Tsiku ili ndilo adaliika Yehova; tidzasekera ndi kukondwera m'mwemo.

25 Tikupemphani, Yehova, tipulumutseni tsopano; tikupemphani, Yehova, tipindulitseni tsopano.

26 Wodala wakudzayo m'dzina la Yehova; takudalitsani kochokera m'nyumba ya Yehova.

27 Yehova ndiye Mulungu, amene anatiunikira; mangani nsembe ndi zingwe, kunyanga za guwa la nsembe.

28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; ndinu Mulungu wanga, ndidzakukwezani.

29 Yamikani Yehova, pakuti Iye ndiye wabwino, pakuti chifundo chake nchosatha.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa