Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 118:6 - Buku Lopatulika

6 Yehova ndi wanga; sindidzaopa; adzandichitanji munthu?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 Yehova ndi wanga; sindidzaopa; adzandichitanji munthu?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 Chauta akakhala pa mbali yanga, sindichita mantha. Munthu angandichite chiyani?

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 118:6
20 Mawu Ofanana  

Mtima wake ngwochirikizika, sadzachita mantha, kufikira ataona chofuna iye pa iwo omsautsa.


Wodala munthu amene akhala naye Mulungu wa Yakobo kuti amthandize, chiyembekezo chake chili pa Yehova, Mulungu wake.


Inde, ndingakhale ndiyenda m'chigwa cha mthunzi wa imfa, sindidzaopa choipa; pakuti Inu muli ndi ine; chibonga chanu ndi ndodo yanu, izi zindisangalatsa ine.


Mulungu ndiye pothawirapo pathu ndi mphamvu yathu, thandizo lopezekeratu m'masautso.


Yehova wa makamu ali ndi ife, Mulungu wa Yakobo ndiye pamsanje pathu.


Mwa Mulungu ndidzalemekeza mau ake, mwa Yehova ndidzalemekeza mau ake.


Pa Mulungu ndakhulupirira, sindidzaopa; munthu adzandichitanji?


Zowindira Inu Mulungu, zili pa ine, ndidzakuchitirani zoyamika.


Mwa Mulungu ndidzalemekeza mau ake, ndakhulupirira Mulungu, sindidzaopa; anthu adzandichitanji?


Tsiku lonse atenderuza mau anga, zolingirira zao zonse zili pa ine kundichitira choipa.


Pamenepo adani anga adzabwerera m'mbuyo tsiku lakuitana ine. Ichi ndidziwa, kuti Mulungu avomerezana nane.


Adzandiukira ndani kutsutsana nao ochita zoipa? Adzandilimbikira ndani kutsutsana nao ochita zopanda pake?


Ine, Inedi, ndine amene nditonthoza mtima wako; kodi iwe ndani, kuti uopa munthu amene adzafa, ndi mwana wa munthu amene adzakhala ngati udzu;


Koma Yehova ali ndi ine ngati wamphamvu ndi woopsa; chifukwa chake ondisautsa adzaphunthwa, sadzandilala; adzakhala ndi manyazi ambiri, chifukwa sanachite chanzeru, ngakhale ndi kunyazitsa kwamuyaya kumene sikudzaiwalika.


Ndipo tidzatani ndi zinthu izi? Ngati Mulungu ali ndi ife, adzatikaniza ndani?


Kotero kuti tinena molimbika mtima, Mthandizi wanga ndiye Ambuye; sindidzaopa; adzandichitira chiyani munthu?


Ndipo pamene Saulo ndi Aisraele onse anamva mau ao a Mfilistiyo, anadodoma, naopa kwambiri.


Nati Davide, Yehova wakundipulumutsa pa mphamvu ya mkango, ndi mphamvu ya chimbalangondo, Iyeyu adzandipulumutsa m'dzanja la Mfilisti uyu. Ndipo Saulo anati kwa Davide, Muka, Yehova akhale nawe.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa