Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

103 Mau a m'Baibulo Okhudza Chidani

Ndikufuna ndikuuzeni anzanga, nkhani ya kaduka ndi yowopsa kwambiri. Mawu a Mulungu amatichenjeza za kuipa kwake.

M’mawu a Ambuye Yesu pa phiri, Iye anati, “Koma Ine ndinena kwa inu, kuti aliyense wakwiyira m’bale wake popanda chifukwa adzayankha mlandu kwa oweruza; ndipo aliyense wonenera m’bale wake, ‘Wopusa iwe,’ adzayankha mlandu ku bwalo lalikulu; ndipo aliyense wonenera, ‘Chitsiru,’ adzakhala woyenera moto wa gehena” (Mateyu 5:22).

Pamene tikumuyandikila Ambuye ndikukhala naye paubwenzi, timazindikira machimo athu, mkati ndi kunja. Tiyenera kusiya chinyengo ndi mkwiyo, chifukwa nthawi zina tingakhale ndi kaduka koma tioneka ngati tilibe.

Tiyenera kuchotsa mzimu wa kaduka mwa ife ndikupempha chikhululukiro kwa Mulungu, kudzipereka kwa Yesu. Kaduka kangawononge mitima yathu, maganizo athu, komanso matupi athu.


Levitiko 19:17

Usamamuda mbale wako mumtima mwako; umdzudzule munthu mnzako ndithu, usadzitengera uchimo chifukwa cha iye.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:9

Iye amene anena kuti ali m'kuunika, namuda mbale wake, ali mumdima kufikira tsopano lino.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:11

Koma iye wakumuda mbale wake ali mumdima, nayenda mumdima, ndipo sadziwa kumene amukako, pakuti mdima wamdetsa maso ake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:20

Munthu akati, kuti, Ndikonda Mulungu, nadana naye mbale wake, ali wabodza: pakuti iye wosakonda mbale wake amene wamuona, sangathe kukonda Mulungu amene sanamuone.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:15

Yense wakudana ndi mbale wake ali wakupha munthu; ndipo mudziwa kuti wakupha munthu aliyense alibe moyo wosatha wakukhala mwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 6:27-28

Koma ndinena kwa inu akumva, Kondanani nao adani anu; chitirani zabwino iwo akuda inu,

dalitsani iwo akutemberera inu, pemphererani iwo akuchitira inu chipongwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 7:15

Ndipo Yehova adzakuchotserani nthenda zonse; sadzakuikirani nthenda zoipa zilizonse za Aejipito muzidziwa zija; koma adzaziika pa onse akudana ndi inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:12

Udani upikisanitsa; koma chikondi chikwirira zolakwa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 32:41

ndikanola lupanga langa lonyezimira, ndi dzanja langa likagwira chiweruzo; ndidzabwezera chilango ondiukira, ndi kulanga ondida.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:104

Malangizo anu andizindikiritsa; chifukwa chake ndidana nao mayendedwe onse achinyengo.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 10:22

Ndipo adzada inu anthu onse chifukwa cha dzina langa; koma iye wakupirira kufikira chimaliziro, iyeyu adzapulumutsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 3:8

mphindi yakukonda ndi mphindi yakudana; mphindi ya nkhondo ndi mphindi ya mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 5:5

Opusa sadzakhazikika pamaso panu, mudana nao onse akuchita zopanda pake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 11:5

Yehova ayesa wolungama mtima, koma moyo wake umuda woipa ndi iye wakukonda chiwawa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 26:5

Ndidana nao msonkhano wa ochimwa, ndipo sindidzakhala nao pansi ochita zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 31:6

Ndikwiya nao iwo akusamala zachabe zonama, koma ndikhulupirira Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:21

Mphulupulu idzamupha woipa; ndipo adzawatsutsa kumlandu iwo akudana naye wolungama.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 36:2

Pakuti adzidyoletsa yekha m'kuona kwake, kuti anthu sadzachipeza choipa chake ndi kukwiya nacho.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 3:20

Pakuti yense wakuchita zoipa adana nako kuunika, ndipo sakudza kwa kuunika, kuti zingatsutsidwe ntchito zake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 45:7

Mukonda chilungamo, ndipo mudana nacho choipa, chifukwa chake Mulungu, ndiye Mulungu wanu, wadzoza inu ndi mafuta a chikondwerero koposa anzanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:18

Ngati dziko lapansi lida inu, mudziwa kuti lidada Ine lisanayambe kuda inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 50:17

Popeza udana nacho chilangizo, nufulatira mau anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 55:12-14

Pakuti si mdani amene ananditonzayo; pakadatero ndikadachilola, amene anadzikuza pa ine sindiye munthu wondida; pakadatero ndikadambisalira:

Koma ameneyo ndiwe, munthu woyenerana nane, tsamwali wanga, wodziwana nane.

Tinapangirana upo wokoma, tinaperekeza khamu la anthu popita kunyumba ya Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:31-32

Chiwawo chonse, ndi kupsa mtima, ndi mkwiyo, ndi chiwawa, ndi mwano zichotsedwe kwa inu, ndiponso choipa chonse.

Koma mukhalirane okoma wina ndi mnzake, a mtima wachifundo, akukhululukirana nokha, monganso Mulungu mwa Khristu anakhululukira inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 68:1

Auke Mulungu, abalalike adani ake; iwonso akumuda athawe pamaso pake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 69:4

Ondida kopanda chifukwa achuluka koposa tsitsi la pamutu panga; ofuna kunditha, ndiwo adani anga monama, ali ndi mphamvu. Pamenepo andibwezetsa chosafunkha ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 97:10

Inu okonda Yehova, danani nacho choipa: Iye asunga moyo wa okondedwa ake; awalanditsa m'manja mwa oipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 101:3

Sindidzaika chinthu choipa pamaso panga; chochita iwo akupatuka padera chindiipira; sichidzandimamatira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 109:3-5

Ndipo anandizinga ndi mau a udani, nalimbana nane kopanda chifukwa.

Ndidzayamika Yehova kwakukulu pakamwa panga; ndi pakati pa anthu aunyinji ndidzamlemekeza.

Popeza adzaima padzanja lamanja la waumphawi, kumpulumutsa kwa iwo akuweruza koipa moyo wake.

M'malo mwa chikondi changa andibwezera udani; koma ine, kupemphera ndiko.

Ndipo anandisenza choipa m'malo mwa chokoma, ndi udani m'malo mwa chikondi changa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:113

Ndidana nao a mitima iwiri; koma ndikonda chilamulo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:163

Ndidana nalo bodza ndi kunyansidwa nalo; koma ndikonda chilamulo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 6:16-19

Zilipo zinthu zisanu ndi chimodzi Yehova azida; ngakhale zisanu ndi ziwiri zimnyansa:

Maso akunyada, lilime lonama, ndi manja akupha anthu osachimwa;

mtima woganizira ziwembu zoipa, mapazi akuthamangira mphulupulu m'mangum'mangu;

mboni yonama yonong'ona mabodza, ndi wopikisanitsa abale.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:13

Kuopa Yehova ndiko kuda zoipa; kunyada, ndi kudzikuza, ndi njira yoipa, ndi m'kamwa mokhota, ndizida.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 11:17

Wachifundo achitira moyo wake zokoma; koma wankhanza avuta nyama yake.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 11:20

Okhota mtima anyansa Yehova; koma angwiro m'njira zao amsekeretsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:17

Kudya masamba, pali chikondano, kuposa ng'ombe yonenepa pali udani.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:26

Ziwembu zoipa zinyansa Yehova; koma oyera mtima alankhula mau okondweretsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 26:24-26

Wakuda mnzake amanyenga ndi milomo yake; koma akundika chinyengo m'kati mwake.

Pamene akometsa mau ake usamkhulupirire; pakuti m'mtima mwake muli zonyansa zisanu ndi ziwiri.

Angakhale abisa udani wake pochenjera, koma udyo wake udzavumbulutsidwa posonkhana anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 26:28

Lilime lonama lida omwewo linawasautsa; ndipo m'kamwa mosyasyalika mungoononga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 1:14

Masiku anu okhala mwezi ndi nthawi ya zikondwerero zanu mtima wanga uzida; zindivuta Ine; ndalema ndi kupirira nazo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 61:8

Pakuti Ine Yehova ndikonda chiweruziro, ndida chifwamba ndi choipa; ndipo ndidzawapatsa mphotho yao m'zoonadi; ndipo ndidzapangana nao pangano losatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 66:5

Imvani mau a Yehova, inu amene munthunthumira ndi mau ake; abale anu amene akudani inu, amene anaponya inu kunja chifukwa cha dzina langa, iwo anati, Yehova alemekezedwe, kuti ife tione kusangalala kwanu; koma iwo adzakhala ndi manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 12:8

Cholowa changa chandisandukira mkango wa m'nkhalango; anatsutsana nane ndi mau ake; chifukwa chake ndinamuda.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 44:4

Koma ndinatuma kwa inu atumiki anga onse aneneri, ndinauka mamawa ndi kuwatuma, ndi kuti, Musachitetu chonyansa ichi ndidana nacho.

Mutu    |  Mabaibulo
Hoseya 9:15

Choipa chao chonse chili mu Giligala; pakuti pamenepo ndinawada, chifukwa cha kuipa kwa machitidwe ao ndidzawainga kuwachotsa m'nyumba mwanga; sindidzawakondanso; akalonga ao onse ndiwo opanduka.

Mutu    |  Mabaibulo
Amosi 5:10

Iwo adana naye wodzudzula kuchipata, nanyansidwa naye wolunjikitsa mau.

Mutu    |  Mabaibulo
Amosi 5:15

Danani nacho choipa, nimukonde chokoma; nimukhazikitse chiweruzo kuchipata; kapena Yehova Mulungu wa makamu adzachitira chifundo otsala a Yosefe.

Mutu    |  Mabaibulo
Mika 3:2

Inu amene mudana nacho chokoma ndi kukondana nacho choipa; inu akumyula khungu lao pathupi pao, ndi mnofu wao pa mafupa ao;

Mutu    |  Mabaibulo
Zekariya 8:17

ndipo musalingirira choipa m'mtima mwanu yense pa mnzake; nimusakonde lumbiro lonama; pakuti izi zonse ndidana nazo, ati Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Malaki 1:2-3

Ndakukondani, ati Yehova; koma inu mukuti, Mwatikonda motani? Esau si mkulu wake wa Yakobo kodi? Ati Yehova; ndipo ndinakonda Yakobo;

koma Esau ndinamuda, ndinasanduliza mapiri ake abwinja, ndi kupereka cholowa chake kwa ankhandwe a m'chipululu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:43-44

Munamva kuti kunanenedwa, Uzikondana ndi mnansi wako, ndi kumuda mdani wako:

koma Ine ndinena kwa inu, Kondanani nao adani anu, ndi kupempherera iwo akuzunza inu;

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 6:24

Palibe munthu angathe kukhala kapolo wa ambuye awiri: pakuti pena adzamuda mmodziyo, ndi kukonda winayo; pena adzakangamira kwa mmodzi, nadzanyoza wina. Simungathe kukhala kapolo wa Mulungu ndi wa Chuma.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 13:13

Ndipo adzada inu anthu onse chifukwa cha dzina langa: koma iye wakupirira kufikira chimaliziro, yemweyo adzapulumutsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 1:71

chipulumutso cha adani athu, ndi padzanja la anthu onse amene atida ife.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 6:22

Odala inu, pamene anthu adzada inu, nadzapatula inu, nadzatonza inu, nadzalitaya dzina lanu monga loipa, chifukwa cha Mwana wa Munthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 21:17

Ndipo anthu onse adzadana ndi inu chifukwa cha dzina langa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 7:7

Dziko lapansi silingathe kudana ndi inu; koma Ine lindida popeza Ine ndilichitira umboni, kuti ntchito zake zili zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 8:44

Inu muli ochokera mwa atate wanu mdierekezi, ndipo zolakalaka zake za atate wanu mufuna kuchita. Iyeyu anali wambanda kuyambira pachiyambi, ndipo sanaime m'choonadi, pakuti mwa iye mulibe choonadi. Pamene alankhula bodza, alankhula za mwini wake; pakuti ali wabodza, ndi atate wake wa bodza.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:18-19

Ngati dziko lapansi lida inu, mudziwa kuti lidada Ine lisanayambe kuda inu.

Mukadakhala a dziko lapansi, dziko lapansi likadakonda zake za lokha; koma popeza simuli a dziko lapansi, koma Ine ndinakusankhani inu mwa dziko lapansi, chifukwa cha ichi likudani inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:23-25

Iye wondida Ine, adanso Atate wanga.

Sindikadachita mwa iwo ntchito zosachita wina, sakadakhala nalo tchimo; koma tsopano anaona, nada Ine ndi Atate wanganso.

Koma chitero, kuti mau olembedwa m'chilamulo chao akwaniridwe, kuti, Anandida Ine kopanda chifukwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 17:14

Ine ndawapatsa iwo mau anu; ndipo dziko lapansi, linadana nao, chifukwa sakhala a dziko lapansi, monga Ine sindikhala wa dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:30

akazitape, osinjirira, akumuda Mulungu, achipongwe, odzitama, amatukutuku, oyamba zoipa, osamvera akulu ao,

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:7

Chifukwa chisamaliro cha thupi chidana ndi Mulungu; pakuti sichigonja ku chilamulo cha Mulungu, pakuti sichikhoza kutero.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:9

Chikondano chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choipa; gwirizana nacho chabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:17-19

Musabwezere munthu aliyense choipa chosinthana ndi choipa. Ganiziranitu zinthu za ulemu pamaso pa anthu onse.

Ngati nkutheka, monga momwe mukhoza, khalani ndi mtendere ndi anthu onse.

Musabwezere choipa, okondedwa, koma patukani pamkwiyo; pakuti kwalembedwa, Kubwezera kuli kwanga, Ine ndidzabwezera, ati Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 13:10

Chikondano sichichitira mnzake choipa; chotero chikondanocho chili chokwanitsa lamulo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 13:4-5

Chikondi chikhala chilezere, chili chokoma mtima; chikondi sichidukidwa; chikondi sichidziwa kudzitamanda, sichidzikuza,

sichichita zosayenera, sichitsata za mwini yekha, sichipsa mtima, sichilingirira zoipa;

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 4:16

Kotero kodi ndasanduka mdani wanu, pakukunenerani zoona?

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:19-21

Ndipo ntchito za thupi zionekera, ndizo dama, chodetsa, kukhumba zonyansa,

Taonani, ine Paulo ndinena ndi inu, kuti, ngati mulola akuduleni, Khristu simudzapindula naye kanthu.

kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko,

njiru, kuledzera, mchezo, ndi zina zotere; zimene ndikuchenjezani nazo, monga ndachita, kuti iwo akuchitachita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:26-27

Kwiyani, koma musachimwe; dzuwa lisalowe muli chikwiyire,

ndiponso musampatse malo mdierekezi.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:31

Chiwawo chonse, ndi kupsa mtima, ndi mkwiyo, ndi chiwawa, ndi mwano zichotsedwe kwa inu, ndiponso choipa chonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:11

ndipo musayanjane nazo ntchito za mdima zosabala kanthu, koma makamakanso muzitsutse;

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:15

Enatu alalikiranso Khristu chifukwa cha kaduka ndi ndeu; koma enanso chifukwa cha kukoma mtima;

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 2:3

musachite kanthu monga mwa chotetana, kapena monga mwa ulemerero wopanda pake, komatu ndi kudzichepetsa mtima, yense ayese anzake omposa iye mwini;

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:8

Koma tsopano tayani inunso zonsezi: mkwiyo, kupsa mtima, dumbo, mwano, zonyansa zotuluka m'kamwa mwanu:

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:15

Penyani kuti wina asabwezere choipa womchitira choipa; komatu nthawi zonse mutsatire chokoma, kwa anzanu, ndi kwa onse.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Atesalonika 1:6-8

popeza nkolungama kwa Mulungu kubwezera chisautso kwa iwo akuchitira inu chisautso,

ndi kwa inu akumva chisautso mpumulo pamodzi ndi ife, pa vumbulutso la Ambuye Yesu wochokera Kumwamba pamodzi ndi angelo a mphamvu yake,

m'lawi lamoto, ndi kubwezera chilango kwa iwo osamdziwa Mulungu, ndi iwo osamvera Uthenga Wabwino wa Ambuye wathu Yesu;

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 3:3

osayera mtima, opanda chikondi chachibadwidwe, osayanjanitsika, akudierekeza, osakhoza kudziletsa, aukali, osakonda abwino,

Mutu    |  Mabaibulo
Tito 3:3

Pakuti kale ifenso tinali opusa, osamvera, onyengeka, akuchitira ukapolo zilakolako ndi zokondweretsa za mitundumitundu, okhala m'dumbo ndi njiru, odanidwa, odana wina ndi mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 1:9

Mwakonda chilungamo, ndi kudana nacho choipa; mwa ichi Mulungu, ndiye Mulungu wanu, wakudzozani ndi mafuta a chikondwerero chenicheni koposa anzanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:26-27

Pakuti tikachimwa ife eni ake, titatha kulandira chidziwitso cha choonadi, siitsalanso nsembe ya kwa machimo,

koma kulindira kwina koopsa kwa chiweruziro, ndi kutentha kwake kwa moto wakuononga otsutsana nao.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 12:14-15

Londolani mtendere ndi anthu onse, ndi chiyeretso chimene, akapanda ichi, palibe mmodzi adzaona Ambuye:

ndi kuyang'anira kuti pangakhale wina wakuperewera chisomo cha Mulungu, kuti ungapuke muzu wina wa kuwawa mtima ungavute inu, ndipo aunyinji angadetsedwe nao;

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:19-20

Mudziwa, abale anga okondedwa, kuti munthu aliyense akhale wotchera khutu, wodekha polankhula, wodekha pakupsa mtima.

Muchiyese chimwemwe chokha, abale anga, m'mene mukugwa m'mayesero a mitundumitundu;

Pakuti mkwiyo wa munthu suchita chilungamo cha Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:1-2

Zichokera kuti nkhondo, zichokera kuti zolimbana mwa inu? Kodi sizichokera kuzikhumbitso zanu zochita nkhondo m'ziwalo zanu?

Dzichepetseni pamaso pa Ambuye, ndipo adzakukwezani.

Musamanenerana, abale. Wonenera mbale, kapena woweruza mbale wake, anenera lamulo, naweruza lamulo: koma ngati uweruza lamulo, suli wochita lamulo, komatu woweruza.

Woika lamulo ndi woweruza ndiye mmodzi, ndiye amene akhoza kupulumutsa ndi kuononga; koma iwe woweruza mnzako ndiwe yani?

Nanga tsono, inu akunena, Lero kapena mawa tidzapita kulowa kumudzi wakutiwakuti, ndipo tidzagonerako ndi kutsatsa malonda, ndi kupindula nao;

inu amene simudziwa chimene chidzagwa mawa. Moyo wanu uli wotani? Pakuti muli utsi, wakuonekera kanthawi, ndi pamenepo ukanganuka.

Mukadanena inu, Akalola Ambuye, ndipo tikakhala ndi moyo, tidzachita kakutikakuti.

Koma tsopano mudzitamandira m'kudzikuza kwanu; kudzitamandira kulikonse kotero nkoipa.

Potero kwa iye amene adziwa kuchita bwino, ndipo sachita, kwa iye kuli tchimo.

Mulakalaka, ndipo zikusowani; mukupha, nimuchita kaduka, ndipo simungathe kupeza; mulimbana, nimuchita nkhondo; mulibe kanthu, chifukwa simupempha.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:4

Akazi achigololo inu, kodi simudziwa kuti ubwenzi wa dziko lapansi uli udani ndi Mulungu? Potero, iye amene afuna kukhala bwenzi la dziko lapansi adziika mdani wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:1

Momwemo pakutaya choipa chonse, ndi chinyengo chonse, ndi maonekedwe onyenga, ndi kaduka, ndi masinjiriro onse,

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 3:9

osabwezera choipa ndi choipa, kapena chipongwe ndi chipongwe, koma penatu madalitso; pakuti kudzatsata ichi mwaitanidwa, kuti mukalandire dalitso.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 4:8

koposa zonse mukhale nacho chikondano chenicheni mwa inu nokha; pakuti chikondano chikwiriritsa unyinji wa machimo;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:13

Musazizwe, abale, likadana nanu dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:7-8

Okondedwa, tikondane wina ndi mnzake: chifukwa kuti chikondi chichokera kwa Mulungu, ndipo yense amene akonda, abadwa kuchokera kwa Mulungu, namzindikira Mulungu.

Iye wosakonda sazindikira Mulungu; chifukwa Mulungu ndiye chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:20-21

Munthu akati, kuti, Ndikonda Mulungu, nadana naye mbale wake, ali wabodza: pakuti iye wosakonda mbale wake amene wamuona, sangathe kukonda Mulungu amene sanamuone.

Ndipo lamulo ili tili nalo lochokera kwa Iye, kuti iye amene akonda Mulungu akondenso mbale wake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 5:3

Pakuti ichi ndi chikondi cha Mulungu, kuti tisunge malamulo ake: ndipo malamulo ake sali olemetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Yohane 1:6

Ndipo chikondi ndi ichi, kuti tiyende monga mwa malamulo ake. Ili ndi lamulolo, monga mudalimva kuyambira pachiyambi, kuti mukayende momwemo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yuda 1:10

Koma iwowa zimene sazidziwa azichitira mwano; ndipo zimene azizindikira chibadwire, monga zamoyo zopanda nzeru, mu izi atayika.

Mutu    |  Mabaibulo
Yuda 1:17-19

Koma inu, abale, mukumbukire mau onenedwa kale ndi atumwi a Ambuye wathu Yesu Khristu;

kuti ananena nanu, Pa nthawi yotsiriza padzakhala otonza, akuyenda monga mwa zilakolako zosapembedza za iwo okha.

Iwo ndiwo opatukitsa, anthu a makhalidwe achibadwidwe, osakhala naye Mzimu.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 2:6

Koma ichi uli nacho, kuti udana nazo ntchito za Anikolai, zimene Inenso ndidana nazo.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 2:15

Kotero uli nao akugwira chiphunzitso cha Anikolai momwemonso.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 12:11

Ndipo iwo anampambana iye chifukwa cha mwazi wa Mwanawankhosa, ndi chifukwa cha mau a umboni wao; ndipo sanakonde moyo wao kungakhale kufikira imfa.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 12:17

Ndipo chinjoka chinakwiya ndi mkazi, ndipo chinachoka kunka kuchita nkhondo ndi otsala a mbeu yake, amene asunga malamulo a Mulungu, nakhala nao umboni wa Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 17:16

Ndipo nyanga khumi udaziona, ndi chilombo, izi zidzadana ndi mkazi wachigololoyo, ndipo zidzamkhalitsa wabwinja wausiwa, ndi kudya nyama yake, ndipo zidzampsereza ndi moto.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 18:2

Ndipo anafuula ndi mau olimba, nanena, Wagwa, wagwa, Babiloni waukulu, nusandulika mokhalamo ziwanda, ndi mosungiramo mizimu yonse yonyansa, ndi mosungiramo mbalame zonse zonyansa ndi zodanidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 22:15

Kunja kuli agalu ndi anyanga, ndi achigololo, ndi ambanda, ndi opembedza mafano, ndi yense wakukonda bodza ndi kulichita.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga wachilungamo, ndinu thandizo langa ndi moyo wanga, amene amasunga moyo wanga, amatsitsimutsa mzimu wanga ndi kuchiritsa mtima wanga. Atate Woyera, ndinu nokha amene muli ndi mphamvu yomasula ine ku chidani ndi mkwiyo, chifukwa ndikudziwa kuti mkumbukidwe ndi kuwawa zikundidyetsa pang'onopang'ono. Ndithandizeni kudula maunyolo ndi zomangira za kale, kundilekanitsa ndi maganizo onse a chidani omwe amangobweretsa poizoni wakufa mwa ine kuti ndidziwononge ndekha. Ndikupemphani kuti Mzimu wanu Woyera undipatse mphamvu yosiya chilichonse chomwe chikundilepheretsa kupita patsogolo, kuti ndikhoze kukonzanso ndi kuchiritsa mtima wanga, kuti ndikhulitsa aliyense amene mwanjira ina wandipweteka. Chomwe ndapeza nthawi yonseyi ndi khalidwe loipa, ndikuchotsa anthu omwe amandizungulira. Tsegulani nzeru zanga, ndimvetse choonadi chanu ndi kundiphunzitsa kuyenda molingana ndi mawu anu. Chifukwa zoonadi: "Iye amene akunena kuti ali mumdima, ndipo amadana ndi m'bale wake, ali mumdimabe." Ambuye, kuyambira pano, ndikusiya chidani, mkwiyo, mkumbukidwe ndi kusakhululuka. M'dzina la Yesu. Amen!