Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yohane 3:20 - Buku Lopatulika

20 Pakuti yense wakuchita zoipa adana nako kuunika, ndipo sakudza kwa kuunika, kuti zingatsutsidwe ntchito zake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

20 Pakuti yense wakuchita zoipa adana nako kuunika, ndipo sakudza kwa kuunika, kuti zingatsutsidwe ntchito zake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

20 Aliyense wochita zoipa, amadana ndi kuŵala. Saonekera poyera, kuwopa kuti zochita zakezo zingaonekere.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

20 Aliyense wochita zoyipa amadana ndi kuwunika, ndipo sabwera poyera chifukwa cha mantha kuti ntchito zake zingaonekere.

Onani mutuwo Koperani




Yohane 3:20
18 Mawu Ofanana  

Ndipo anatenga chiwaya natitulutsa pamaso pake; koma anakana kudya. Ndipo Aminoni anati, Anthu onse atuluke kundisiya ine. Natuluka onse, kumsiya.


Ndipo mfumu ya Israele inati kwa Yehosafati, Alipo munthu wina kuti tifunsire kwa Yehova mwa iye; koma ndimuda, popeza samanenera za ine zabwino, koma zoipa; ndiye Mikaya mwana wake wa Imila. Nati Yehosafati, Isamatero mfumu.


Ndipo iye anauka pakati pa usiku, natenga mwana wanga kumimba kwanga, mdzakazi wanu ndili m'tulo, namuika m'mfukato mwake, naika mwana wake wakufa m'mfukato mwanga.


Popeza udana nacho chilangizo, nufulatira mau anga.


chifukwa anada nzeru, sanafune kuopa Yehova;


Wonyoza sakonda kudzudzulidwa, samapita kwa anzeru.


Wotsinzina ndiye aganizira zokhota; wosunama afikitsa zoipa.


akusiya mayendedwe olungama, akayende m'njira za mdima;


Koma mayendedwe a olungama akunga kuunika kwa mbandakucha, kunkabe kuwala kufikira usana woti mbee.


ndi kuti, Bwanji ndinada mwambo, mtima wanga ndi kunyoza chidzudzulo;


Ukhala pakati pa manyengo m'manyengo; akana kundidziwa, ati Yehova.


Ndipo mmodzi wa achilamulo anayankha, nanena kwa Iye, Mphunzitsi, ndi kunena izi, mutitonza ifenso.


Koma wochita choonadi adza kukuunika, kuti ntchito zake zionekere kuti zinachitidwa mwa Mulungu.


Dziko lapansi silingathe kudana ndi inu; koma Ine lindida popeza Ine ndilichitira umboni, kuti ntchito zake zili zoipa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa