Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo

- Zotsatsa -


113 Mau a m'Baibulo Okhudza Kusakhulupirira

113 Mau a m'Baibulo Okhudza Kusakhulupirira

Mulungu sakondwera ndi anthu osakhulupirira Iye. Amafuna kuti ana ake akhulupirire mwamphamvu mawu ake ndi malonjezo ake onse. Kusakhulupirira Mulungu kukuwonetsa kuti suli paubwenzi wolimba ndi Mzimu Woyera. Mzimu wa Mulungu, kudzera m'magazi a Yesu, nthawi zonse amakuwonetsa mphamvu za Mulungu Wamphamvuzonse, amene sadziwa cholephera.

Mukangowona mphamvu zake zodabwitsa, maganizo anu amasintha ndipo mtima wanu umakonzedwanso. Simudzalankhulanso chimodzimodzi, mudzakhala ndi chikhulupiriro choti ngakhale simukuona zomwe mukuyembekezera, zidzachitika nthawi iliyonse.

Mulungu safuna kuti anthu ake akhale osakhulupirira, amafuna kuti muyende m'chikhulupiriro, osati m'maganizo anu kapena m'zovuta zomwe mukukumanazo, koma muzimudyetsa mawu ake tsiku ndi tsiku. Kusakhulupirira kumakutsekerani zitseko za madalitso onse amene Mulungu akufuna kukupatsani, kumakulepheretsani kuchita chifuniro chake ndikukupangitsani kuchita zomwe inu mukuona kuti ndi zoyenera. Kumakupangitsani kuganiza kuti Mulungu sangakuthandizeni kapena kuti sasamala ndi zomwe mukukumanazo, kukubirani chiyembekezo ndikukhumudwitsa mtima wanu chifukwa cha zinthu zoipa zomwe zikukuzungulirani.

Mulungu akufuna kuti lero mukhale omasuka ku kusakhulupirira ndi kuti mumudziwe Iye bwino. Mulirire pamaso pake mpaka maso anu atatsegulidwa ndipo mumutha kuwona, mupemphe Mulungu kuti atsegule makutu anu ndi kukupangitsani kumvetsera malemba ake. Mukatero simudzakayikiranso mapulani ake pa inu ndi pa banja lanu.




Ahebri 11:6

koma wopanda chikhulupiriro sikutheka kumkondweretsa; pakuti iye wakudza kwa Mulungu ayenera kukhulupirira kuti alipo, ndi kuti ali wobwezera mphotho iwo akumfuna Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 10:17

Chomwecho chikhulupiriro chidza ndi mbiri, ndi mbiri idza mwa mau a Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 78:22

Popeza sanakhulupirire Mulungu, osatama chipulumutso chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 20:27

Pomwepo ananena kwa Tomasi, Bwera nacho chala chako kuno, nuone manja anga, ndipo bwera nalo dzanja lako, nuliike kunthiti yanga, ndipo usakhale wosakhulupirira, koma wokhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:6

Koma apemphe ndi chikhulupiriro, wosakayika konse; pakuti wokayikayo afanana ndi funde la nyanja lotengeka ndi mphepo ndi kuwinduka nayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 17:20

Ndipo Iye ananena kwa iwo, Chifukwa chikhulupiriro chanu nchaching'ono: pakuti indetu ndinena kwa inu, Mukakhala nacho chikhulupiriro monga kambeu kampiru, mudzati ndi phiri ili, Senderapo umuke kuja; ndipo lidzasendera; ndipo palibe kanthu kadzakukanikani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:23

Koma iye amene akayikakayika pakudya, atsutsika, chifukwa akudya wopanda chikhulupiriro; ndipo chinthu chilichonse chosatuluka m'chikhulupiriro, ndicho uchimo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:10

Iye amene amkhulupirira Mwana wa Mulungu ali nao umboni mwa iye; iye wosakhulupirira Mulungu anamuyesa Iye wonama; chifukwa sanakhulupirire umboni wa Mulungu anauchita wa Mwana wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 95:10

Zaka makumi anai mbadwo uwu unandimvetsa chisoni, ndipo ndinati, Iwo ndiwo anthu osokerera mtima, ndipo sadziwa njira zanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 10:26

Koma inu simukhulupirira, chifukwa simuli a mwa nkhosa zanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 4:1

Pakufuula ine mundiyankhe, Mulungu wa chilungamo changa; pondichepera mwandikulitsira malo. Ndichitireni chifundo, imvani pemphero langa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:38

Ndipo mulibe mau ake okhala mwa inu; chifukwa kuti amene Iyeyu anatuma, inu simumkhulupirira ameneyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 5:7

(Pakuti tiyendayenda mwa chikhulupiriro si mwa chionekedwe);

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 13:58

Ndipo Iye, chifukwa cha kusakhulupirira kwao, sanachite kumeneko zamphamvu zambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:19

Ndipo ndikudandaulirani koposa kuchita ichi, kuti kubwera kwanga kwa inu kufulumidwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 14:31

Ndipo pomwepo Yesu anatansa dzanja lake, namgwira iye, nanena naye, Iwe wokhulupirira pang'ono, wakayikiranji mtima?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 11:20

Chabwino; iwo anathyoledwa ndi kusakhulupirira kwao, ndipo iwe umaima ndi chikhulupiriro chako. Usamadzikuza mumtima, koma opatu:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 3:18

Wokhulupirira Iye saweruzidwa; wosakhulupirira waweruzidwa ngakhale tsopano, chifukwa sanakhulupirire dzina la Mwana wobadwa yekha wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 16:16

Amene akhulupirira nabatizidwa, adzapulumutsidwa; koma amene sakhulupirira adzalangidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:22-23

Koma chipatso cha Mzimu ndicho chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, chikhulupiriro, chifatso, chiletso; pokana zimenezi palibe lamulo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Atesalonika 2:12

kuti aweruzidwe onse amene sanakhulupirire choonadi, komatu anakondwera ndi chosalungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 9:24

Pomwepo atate wa mwana anafuula, nanena, Ndikhulupirira; thandizani kusakhulupirira kwanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 21:8

Koma amantha, ndi osakhulupirira, ndi onyansa, ndi ambanda, ndi achigololo, ndi olambira mafano, ndi onse a mabodza, cholandira chao chidzakhala m'nyanja yotentha ndi moto ndi sulufure; ndiyo imfa yachiwiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 3:3

Nanga bwanji ngati ena sanakhulupirire? Kodi kusakhulupirira kwao kuyesa chabe chikhulupiriko cha Mulungu?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:39

Koma ife si ndife a iwo akubwerera kulowa chitayiko; koma a iwo a chikhulupiriro cha ku chipulumutso cha moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 4:20

ndipo poyang'anira lonjezo la Mulungu sanagwedezeke chifukwa cha kusakhulupirira, koma analimbika m'chikhulupiriro, napatsa Mulungu ulemu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 10:4

Woipa, monga mwa kudzikuza kwa nkhope yake, akuti, Sadzafunsira. Malingaliro ake onse akuti, Palibe Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 11:23

Ndipo iwonso, ngati sakhala chikhalire mu kusakhulupirira, adzawalumikizanso, pakuti Mulungu ali wamphamvu yakutha kuwalumikizanso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:17

Pakuti m'menemo chaonetsedwa chilungamo cha Mulungu chakuchokera kuchikhulupiriro kuloza kuchikhulupiriro: monga kwalembedwa, Koma munthu wolungama adzakhala ndi moyo ndi chikhulupiriro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:37

Chifukwa palibe mau amodzi akuchokera kwa Mulungu adzakhala opanda mphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 1:13

ndingakhale kale ndinali wamwano, ndi wolondalonda, ndi wachipongwe; komatu anandichitira chifundo, popeza ndinazichita wosazindikira, wosakhulupirira;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 3:19

Si awo kodi osamverawo? Ndipo tiona kuti sanathe kulowa chifukwa cha kusakhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 21:21-22

Ndipo Yesu anayankha, nati kwa iwo, Indedi ndinena kwa inu, Ngati mukhala nacho chikhulupiriro, osakayikakayika, mudzachita si ichi cha pa mkuyu chokha, koma ngati mudzati ngakhale kuphiri ili, Tanyamulidwa, nuponyedwe m'nyanja, chidzachitidwa. Ndipo zinthu zilizonse mukazifunsa m'kupemphera ndi kukhulupirira, mudzazilandira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:8

Yandikirani kwa Mulungu, ndipo adzayandikira kwa inu. Sambani m'manja, ochimwa inu; yeretsani mitima, a mitima iwiri inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:66

Mundiphunzitse chisiyanitso ndi nzeru; pakuti ndinakhulupirira malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 11:1

Koma chikhulupiriro ndicho chikhazikitso cha zinthu zoyembekezeka, chiyesero cha zinthu zosapenyeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:1

Mtima wanu usavutike; mukhulupirira Mulungu, khulupirirani Inenso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 4:20-21

ndipo poyang'anira lonjezo la Mulungu sanagwedezeke chifukwa cha kusakhulupirira, koma analimbika m'chikhulupiriro, napatsa Mulungu ulemu, nakhazikikanso mumtima kuti, chimene Iye analonjeza, anali nayonso mphamvu yakuchichita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 146:6

Amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili m'mwemo. Ndiye wakusunga choonadi kosatha,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 11:23

Ndithu ndinena ndi inu, kuti, Munthu aliyense akanena ndi phiri ili, Tanyamulidwa, nuponyedwe m'nyanja; wosakayika mumtima mwake, koma adzakhulupirira kuti chimene achinena chichitidwa, adzakhala nacho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 2:13

ngati tikhala osakhulupirika, Iyeyu akhala wokhulupirika; pakuti sangathe kudzikana yekha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 27:13

Ndikadapanda kukhulupirira kuti ndikaone ubwino wa Yehova m'dziko la amoyo, ndikadatani!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 53:1

Ndani wamvera uthenga wathu? Ndi mkono wa Yehova wavumbulukira yani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 8:25

Ndipo Iye anati kwa iwo, Chikhulupiriro chanu chili kuti? Ndipo m'kuchita mantha anazizwa iwo, nanena wina ndi mnzake, Uyu ndani nanga, kuti angolamula mphepo ndi madzi, ndipo zimvera Iye?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 4:2

Pakuti kwa ifenso walalikidwa Uthenga Wabwino, monganso kwa iwo; koma iwowa sanapindule nao mau omvekawo, popeza sanasakanizike ndi chikhulupiriro mwa iwo amene adawamva.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 6:36

Koma ndinati kwa inu, kuti mungakhale mwandiona, simukhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 10:32-33

Chifukwa chake yense amene adzavomereza Ine pamaso pa anthu, Inenso ndidzamvomereza iye pamaso pa Atate wanga wa Kumwamba. Koma yense amene adzandikana Ine pamaso pa anthu, Inenso ndidzamkana iye pamaso pa Atate wanga wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 1:8

amene mungakhale simunamuone mumkonda; amene mungakhale simumpenya tsopano, pokhulupirira, mukondwera naye ndi chimwemwe chosaneneka, ndi cha ulemerero:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:24-25

Pakuti ife tinapulumutsidwa ndi chiyembekezo; koma chiyembekezo chimene chioneka si chili chiyembekezo ai; pakuti ayembekezera ndani chimene achipenya? Koma ngati tiyembekezera chimene sitichipenya, pomwepo tichilindirira ndi chipiriro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 28:17

Ndipo pamene anamuona Iye, anamlambira; koma ena anakayika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:5

Koma wina wa inu ikamsowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, amene apatsa kwa onse modzala manja, niwosatonza; ndipo adzampatsa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 14:1

Wauchitsiru amati mumtima mwake, Kulibe Mulungu. Achita zovunda, achita ntchito zonyansa; kulibe wakuchita bwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:5-6

Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako; umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 15:14

ndipo ngati Khristu sanaukitsidwe kulalikira kwathu kuli chabe, chikhulupiriro chanunso chili chabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 9:23-24

Ndipo Yesu polowa m'nyumba yake ya mkuluyo, ndi poona oimba zitoliro ndi khamu la anthu obuma, ananena, Tulukani, pakuti kabuthuko sikanafe koma kali m'tulo. Ndipo anamseka Iye pwepwete.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 73:22

ndinali wam'thengo, wosadziwa kanthu; ndinali ngati nyama pamaso panu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 100:5

Pakuti Yehova ndiye wabwino; chifundo chake chimanka muyaya; ndi chikhulupiriko chake ku mibadwomibadwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 6:64

Koma pali ena mwa inu amene sakhulupirira. Pakuti Yesu anadziwa poyamba amene ali osakhulupirira, ndi amene adzampereka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 12:28

Koma ngati Mulungu aveka kotere udzu wakuthengo ukhala lero, ndipo mawa uponyedwa pamoto; nanga inu sadzakuninkhani koposa, inu okhulupirira pang'ono?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:13

Ndipo Mulungu wa chiyembekezo adzaze inu ndi chimwemwe chonse ndi mtendere m'kukhulupirira, kuti mukachuluke ndi chiyembekezo, mu mphamvu ya Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:5

Pereka njira yako kwa Yehova; khulupiriranso Iye, adzachichita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 9:2

Ndipo onani, anabwera naye kwa Iye munthu wamanjenje, wakugona pamphasa: ndipo Yesu pakuona chikhulupiriro chao, anati kwa wodwalayo, Limba mtima, mwana, machimo ako akhululukidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:23

tigwiritse chivomerezo chosagwedera cha chiyembekezo chathu, pakuti wolonjezayo ali wokhulupirika;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 1:9

Ngati tivomereza machimo athu, ali wokhulupirika ndi wolungama Iye, kuti atikhululukire machimo athu, ndi kutisambitsa kutichotsera chosalungama chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 2:20

Ndinapachikidwa ndi Khristu; koma ndili ndi moyo; wosatinso ine ai, koma Khristu ali ndi moyo mwa ine; koma moyo umene ndili nao tsopano m'thupi, ndili nao m'chikhulupiriro cha Mwana wa Mulungu, amene anandikonda, nadzipereka yekha chifukwa cha ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:118

Mupepula onse akusokera m'malemba anu; popeza chinyengo chao ndi bodza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:14

Ndikuyamikani chifukwa kuti chipangidwe changa nchoopsa ndi chodabwitsa; ntchito zanu nzodabwitsa; moyo wanga uchidziwa ichi bwino ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:3

Pakuti ndi chisomo chapatsidwa kwa ine, ndiuza munthu aliyense wa inu, kuti asadziyese koposa kumene ayenera kudziyesa; koma aganize modziletsa yekha, monga Mulungu anagawira kwa munthu aliyense muyeso wa chikhulupiriro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 1:24

Si kuti tichita ufumu pa chikhulupiriro chanu, koma tikhala othandizana nacho chimwemwe chanu; pakuti ndi chikhulupiriro muimadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 12:38-39

Pomwepo alembi ndi Afarisi ena anayankha Iye nati, Mphunzitsi, tifuna kuona chizindikiro cha Inu. Koma Iye anayankha nati kwa iwo, Akubadwa oipa achigololo afunafuna chizindikiro; ndipo sichidzapatsidwa kwa iwo chizindikiro, komatu chizindikiro cha Yona mneneri;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:8

Kuthawira kwa Yehova nkokoma koposa kukhulupirira munthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 2:5

kuti chikhulupiriro chanu chisakhale m'nzeru ya anthu, koma mu mphamvu ya Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:2

Odala iwo akusunga mboni zake, akumfuna ndi mtima wonse;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 11:32-34

Ndipo ndinene chiyaninso? Pakuti idzandiperewera nthawi ndifotokozere za Gideoni, Baraki, Samisoni, Yefita; za Davide, ndi Samuele ndi aneneri; amene mwa chikhulupiriro anagonjetsa maufumu, anachita chilungamo, analandira malonjezano, anatseka pakamwa pa mikango, nazima mphamvu ya moto, napulumuka lupanga lakuthwa, analimbikitsidwa pokhala ofooka, anakula mphamvu kunkhondo, anapirikitsa magulu a nkhondo yachilendo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:21

chifukwa kuti, ngakhale anadziwa Mulungu, sanamchitire ulemu wakuyenera Mulungu, ndipo sanamyamike; koma anakhala opanda pake m'maganizo ao, ndipo unada mtima wao wopulukira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:7-8

Pemphani, ndipo chidzapatsidwa kwa inu; funani, ndipo mudzapeza; gogodani, ndipo chidzatsegulidwa kwa inu; pakuti yense wakupempha alandira; ndi wakufunayo apeza; ndi kwa wogogodayo chitsegulidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 8:24

Chifukwa chake ndinati kwa inu, kuti mudzafa m'machimo kwa inu, kuti mudzafa m'machimo anu, pakuti ngati simukhulupirira kuti Ine ndine, mudzafa m'machimo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 9:32

Chifukwa chanji? Chifukwa kuti sanachitsate ndi chikhulupiriro, koma monga ngati ndi ntchito. Anakhumudwa pamwala wokhumudwitsa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:7

Munathamanga bwino; anakuletsani ndani kuti musamvere choonadi?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:22

Khalani akuchita mau, osati akumva okha, ndi kudzinyenga nokha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:30

Ndinasankha njira yokhulupirika; ndinaika maweruzo anu pamaso panga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 1:12

Chifukwa cha ichicho ndinamva zowawa izi; komatu sindichita manyazi; pakuti ndimdziwa Iye amene ndamkhulupirira, ndipo ndikopeka mtima kuti ali wa mphamvu ya kudikira chosungitsa changacho kufikira tsiku lijalo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 18:8

Ndinena ndi inu, adzawachitira chilungamo posachedwa. Koma Mwana wa Munthu pakudza Iye, adzapeza chikhulupiriro padziko lapansi kodi?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:13

Ufumu wanu ndiwo ufumu womka muyaya, ndi kuweruza kwanu kufikira mibadwo yonseyonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:13

Ndikhoza zonse mwa Iye wondipatsa mphamvuyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 56:4

Mwa Mulungu ndidzalemekeza mau ake, ndakhulupirira Mulungu, sindidzaopa; anthu adzandichitanji?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 3:26

Pakuti inu nonse muli ana a Mulungu, mwa chikhulupiriro cha mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 23:4

Inde, ndingakhale ndiyenda m'chigwa cha mthunzi wa imfa, sindidzaopa choipa; pakuti Inu muli ndi ine; chibonga chanu ndi ndodo yanu, izi zindisangalatsa ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:7

ndi kutaya pa Iye nkhawa yanu yonse, pakuti Iye asamalira inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:34

Chifukwa chake musadere nkhawa za mawa; pakuti mawa adzadzidera nkhawa iwo okha. Zikwanire tsiku zovuta zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 4:18-20

Amene anakhulupirira nayembekeza zosayembekezeka, kuti iye akakhale kholo la mitundu yambiri ya anthu, monga mwa chonenedwachi, Mbeu yako idzakhala yotere. Ndipo iye osafooka m'chikhulupiriro sanalabadire thupi lake, ndilo longa ngati lakufa pamenepo, (pokhala iye ngati zaka makumi khumi), ndi mimba ya Sara idaumanso; Pakuti ngati Abrahamu anayesedwa wolungama chifukwa cha ntchito, iye akhala nacho chodzitamandira; koma kulinga kwa Mulungu ai. ndipo poyang'anira lonjezo la Mulungu sanagwedezeke chifukwa cha kusakhulupirira, koma analimbika m'chikhulupiriro, napatsa Mulungu ulemu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:13

Sichinakugwerani inu chiyeso koma cha umunthu; koma Mulungu ali wokhulupirika, amene sadzalola inu kuyesedwa koposa kumene mukhoza; koma pamodzi ndi chiyeso adzaikanso populumukirapo, kuti mudzakhoze kupirirako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 4:16

Potero tilimbike mtima poyandikira mpando wachifumu wachisomo, kuti tilandire chifundo ndi kupeza chisomo cha kutithandiza nthawi yakusowa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:16

Ndipo ife tazindikira, ndipo takhulupirira chikondicho Mulungu ali nacho pa ife. Mulungu ndiye chikondi, ndipo iye amene akhala m'chikondi akhala mwa Mulungu, ndipo Mulungu akhala mwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:119

Muchotsa oipa onse a padziko lapansi ngati mphala: Chifukwa chake ndikonda mboni zanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:25

Kuopa anthu kutchera msampha; koma wokhulupirira Yehova adzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 41:10

usaope, pakuti Ine ndili pamodzi ndi iwe; usaopsedwe, pakuti Ine ndine Mulungu wako; ndidzakulimbitsa; inde, ndidzakuthangata; inde, ndidzakuchirikiza ndi dzanja langa lamanja la chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 5:24

Wakuitana inu ali wokhulupirika, amenenso adzachichita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 14:27

Koma pomwepo Yesu analankhula nao, nati, Limbani mtima; ndine; musaope.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 3:20

Pakuti ufulu wathu uli Kumwamba; kuchokera komwenso tilindirira Mpulumutsi, Ambuye Yesu Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 31:14-15

Koma ine ndakhulupirira Inu, Yehova, ndinati, Inu ndinu Mulungu wanga. Nyengo zanga zili m'manja mwanu, mundilanditse m'manja a adani anga, ndi kwa iwo akundilondola ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:14-16

Inu ndinu kuunika kwa dziko lapansi. Mzinda wokhazikika pamwamba paphiri sungathe kubisika. Kapena sayatsa nyali, ndi kuivundikira m'mbiya, koma aiika iyo pa choikapo chake; ndipo iunikira onse ali m'nyumbamo. Chomwecho muwalitse inu kuunika kwanu pamaso pa anthu, kuti pakuona ntchito zanu zabwino, alemekeze Atate wanu wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 16:8-9

Ndipo atadza Iyeyo, adzatsutsa dziko lapansi za machimo, ndi za chilungamo, ndi za chiweruziro; za machimo, chifukwa sakhulupirira Ine;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Tito 1:15

Zonse ziyera kwa iwo amene ayera mtima; koma kwa iwo odetsedwa ndi osakhulupirira kulibe kanthu koyera; komatu zadetsedwa nzeru zao ndi chikumbumtima chao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 3:12

Tapenyani, abale, kuti kapena ukakhale mwa wina wa inu mtima woipa wosakhulupirira, wakulekana ndi Mulungu wamoyo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 24:25

Ndipo Iye anati kwa iwo, Opusa inu, ndi ozengereza mtima kusakhulupirira zonse adazilankhula aneneri!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 16:14

Ndipo chitatha icho anaonekera kwa khumi ndi mmodzi iwo okha, alikuseama pachakudya; ndipo anawadzudzula chifukwa cha kusavomereza kwao ndi kuuma mtima, popeza sanavomereze iwo amene adamuona, atauka Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 8:45-46

Koma Ine, chifukwa ndinena choonadi, simukhulupirira Ine. Ndani mwa inu anditsutsa Ine za tchimo? Ngati ndinena choonadi, simundikhulupirira Ine chifukwa ninji?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 4:4

mwa amene mulungu wa nthawi ino ya pansi pano anachititsa khungu maganizo ao a osakhulupirira, kuti chiwalitsiro cha Uthenga Wabwino wa ulemerero wa Khristu, amene ali chithunzithunzi cha Mulungu, chisawawalire.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 8:12

Ndipo za m'mbali mwa njira ndiwo anthu amene adamva; pamenepo akudza mdierekezi, nachotsa mau m'mitima yao, kuti angakhulupirire ndi kupulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 106:24

Anapeputsanso dziko lofunika, osavomereza mau ake;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 78:32

Chingakhale ichi chonse anachimwanso, osavomereza zodabwitsa zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Zikomo Ambuye, chifukwa ndinu thandizo langa ndi moyo wanga, chithandizo changa m'masautso ndi mtendere wanga m'mafunde. Zikomo chifukwa ndinu Mulungu wa chipulumutso changa, amene amandimasula ku mavuto anga onse. Ndikubwera kwa inu kudzera mwa Ambuye wanga Yesu Khristu, nthawi ino ya mantha ndi kukayika. Mzimu Woyera, ndikupemphani kuti mundipatse mphamvu, mundilenge mtima wokukondweretsani, mundikonzenso, musinthe maganizo anga, musinthe khalidwe langa. Ndithandizeni tsiku lililonse kuyenda m'chikhulupiriro osati m'kuwona, kumvetsa kuti ngakhale lero zinthu zikuoneka zoipa, mawa zidzakhala bwino, kuti ngakhale lero zinthu zikuoneka zakuda, mawa kuwala kudzabwera. Pa nthawi yovutayi ndithandizeni kuyang'ana kukula kwanu ndi mphamvu zanu osati pamavuto, ndipatseni chikhulupiriro chachikulu Ambuye, kuti ndisafooke poyembekezera, ndikudziwa amene ndakhulupirira, koma ndikuvomereza Mulungu wokondedwa kuti nthawi zina ndimakayikira mawu anu, kuti zimakhala zovuta kugwira inu. Mawu anu amati: "Onani abale, kuti pasakhale wina wa inu amene ali ndi mtima woipa wosakhulupirira kuti achoke kwa Mulungu wamoyo." Atate, ndithandizeni kuti ndisapatuke kutsata zilakolako ndi zokhumba za dziko lino kuti ndipambane kusakhulupirira kumeneku ndikumvetsa kuti palibe mvula yamkuntho yoopsa kuposa inu, sinthani maganizo anga ndipo yeretsani mtima wanga wachiwiri. Ndikulengeza kuti ndine womasuka ku kukayika, ku mantha, ku kusakhulupirira ndi chilichonse chomwe chikufuna kundilekanitsa ndi Mlengi wanga ndi Mulungu wanga. Ambuye, ulemerero ndi ulemu zonse zikhale zanu. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa