Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


104 Mau a m'Baibulo Okhudza Kudzikuza

104 Mau a m'Baibulo Okhudza Kudzikuza

Baibulo limatiuza kuti Mulungu amaona kutali munthu wodzikuza. Kudzikuza ndi khalidwe lomwe silikondweretsa Mulungu, ndipo limapezeka mwa anthu ambiri, kumawapangitsa kudzidalira mopambanitsa ndikuganiza kuti angathe kulamulira chilichonse. Munthu wodzikuza sadziwa zolakwa zake, koma nthawi zonse amaona zolakwa za anzake, n’kunyalanyaza zake.

Njira yokha yothawa mtima umenewu womwe umawononga maganizo ndi mtima wanu, ndikuvomereza Mulungu pa chilichonse chimene muchita. Muziwerama pamaso pake ndi kuvomereza kuti mumadalira Iye, osati mphamvu kapena luso lanu. Koma chifukwa cha chikondi ndi chisomo chake. Ndikukutsimikizirani kuti mukachita izi, chikondi chake chochiritsa chidzakuphimbani, chidzasintha maganizo anu, ndi kukupangani munthu watsopano m’chifaniziro chake.

Dzipumbitsitseni pansi pa dzanja lamphamvu la Yehova, ndipo nthawi yake ikadzakwana adzakukwezani ndi kukuyikani pamalo amene anakukonzerani kuyambira kalekale.




Miyambo 16:5

Yense wonyada mtima anyansa Yehova; zoonadi sadzapulumuka chilango.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 23:12

Ndipo aliyense amene akadzikuza yekha adzachepetsedwa; koma amene adzichepetsa mwini yekha adzakulitsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 138:6

Angakhale Yehova ngwokwezeka, apenyanso wopepukayo; koma wodzikuza amdziwira kutali.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 10:4

Woipa, monga mwa kudzikuza kwa nkhope yake, akuti, Sadzafunsira. Malingaliro ake onse akuti, Palibe Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:12

Mtima wa munthu unyada asanaonongeke; koma chifatso chitsogolera ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:18

Kunyada kutsogolera kuonongeka; mtima wodzikuza ndi kutsogolera kuphunthwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:4

Maso akunyada, ndi mtima wodzikuza, ndi nyali ya oipa, zili tchimo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:23

Kudzikuza kwa munthu kudzamchepetsa; koma wokhala ndi mtima wodzichepetsa adzalemekezedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:7

Usadziyese wekha wanzeru; opa Yehova, nupatuke pazoipa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:1

Usanyadire zamawa, popeza sudziwa tsiku lina lidzabala chiyani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:2

Pakudza kudzikuza padzanso manyazi; koma nzeru ili ndi odzichepetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:2

Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi: Bwezerani odzikuza choyenera iwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:16

Mukhale ndi mtima umodzi wina ndi mnzake. Musasamalire zinthu zazikulu, koma phatikanani nao odzichepetsa. Musadziyesere anzeru mwa inu nokha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 2:11

Maso a munthu akuyang'anira kumwamba adzatsitsidwa, ndi kudzikweza kwa anthu kudzaweramitsidwa pansi; ndipo Yehova yekha adzakwezedwa tsiku limenelo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 131:1

Yehova, mtima wanga sunadzikuze ndi maso anga sanakwezeke; ndipo sindinatsate zazikulu, kapena zodabwitsa zondiposa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:3

Pakuti ngati wina ayesa ali kanthu pokhala ali chabe, adzinyenga yekha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:3

Pakuti ndi chisomo chapatsidwa kwa ine, ndiuza munthu aliyense wa inu, kuti asadziyese koposa kumene ayenera kudziyesa; koma aganize modziletsa yekha, monga Mulungu anagawira kwa munthu aliyense muyeso wa chikhulupiriro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:6

Koma apatsa chisomo choposa. Potero anena malembo, Mulungu akaniza odzikuza, koma apatsa chisomo odzichepetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:5

Momwemonso, anyamata inu, mverani akulu. Koma nonsenu muvale kudzichepetsa kuti mutumikirane; pakuti Mulungu akaniza odzikuza, koma apatsa chisomo kwa odzichepetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 10:17-18

Koma iye wodzitamandira adzitamandire mwa Ambuye; pakuti si iye amene adzitama yekha, koma iye amene Ambuye amtama ali wovomerezeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 73:6

Chifukwa chake kudzikuza kunga unyolo pakhosi pao; achivala chiwawa ngati malaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:16

Pakuti chilichonse cha m'dziko lapansi, chilakolako cha thupi ndi chilakolako cha maso, matamandidwe a moyo, sizichokera kwa Atate, koma kudziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:8-9

Chitsiriziro cha kanthu chiposa chiyambi chake; wofatsa mtima apambana wodzikuza mtima. Usakangaze mumtima mwako kukwiya; pakuti mkwiyo ugona m'chifuwa cha zitsiru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 1:43

Pamene ndinanena ndi inu simunamvere; koma munatsutsana nao mau a Yehova ndi kuchita modzikuza, nimunakwera kunka kumapiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mafumu 19:22

Ndiye yani wamtonza ndi kumchitira mwano? Ndiye yani wamkwezera mau ndi kumgadamira maso ako m'mwamba? Ndiye Woyerayo wa Israele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:10

Dzichepetseni pamaso pa Ambuye, ndipo adzakukwezani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:30

akazitape, osinjirira, akumuda Mulungu, achipongwe, odzitama, amatukutuku, oyamba zoipa, osamvera akulu ao,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 26:12

Kodi uona munthu wodziyesa wanzeru? Ngakhale chitsiru chidzachenjera koma ameneyo ai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:8

Chitsiriziro cha kanthu chiposa chiyambi chake; wofatsa mtima apambana wodzikuza mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 101:5

Wakuneneza mnzake m'tseri ndidzamdula; wa maso odzikuza ndi mtima wodzitama sindidzamlola.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:10

Kudzikuza kupikisanitsa; koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 10:12-13

Mau a m'kamwa mwa munthu wanzeru nga chisomo; koma milomo ya chitsiru idzachimeza. Chiyambi cha mau a m'kamwa mwake ndi utsiru; ndipo chimaliziro cha m'kamwa mwake ndi misala yoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:51

Odzikuza anandinyoza kwambiri: koma sindinapatukanso nacho chilamulo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:85

Odzikuza anandikumbira mbuna, ndiwo osasamalira chilamulo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 30:32

Ngati wapusa podzikweza, ngakhale kuganizira zoipa, tagwira pakamwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:12

Chifukwa chake iye wakuyesa kuti ali chilili, ayang'anire kuti angagwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 13:11

Ndipo ndidzalanga dziko lapansi, chifukwa cha kuipa kwao, ndi oipa chifukwa cha mphulupulu zao; ndipo ndidzaletsa kudzikuza kwa onyada, ndidzagwetsa kudzikweza kwa oopsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 50:31

Taonani, nditsutsana nawe, wonyada iwe, ati Ambuye, Yehova wa makamu; pakuti tsiku lako lafika, nthawi imene ndidzakulanga iwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 2:19

nulimbika mumtima kuti iwe wekha uli wotsogolera wa akhungu, nyali ya amene akhala mumdima,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:26

Tisakhale odzikuza, outsana, akuchitirana njiru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:19

Kufatsa mtima ndi osauka kuposa kugawana zofunkha ndi onyada.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 140:5

Odzikuza ananditchera msampha, nandibisira zingwe; anatcha ukonde m'mphepete mwa njira; ananditchera makwekwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:15

Njira ya chitsiru njolungama pamaso pakepake; koma wanzeru amamvera uphungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 35:12-13

Apo afuula, koma Iye sawayankha; chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oipa. Zedi Mulungu samvera zachabe, ndi Wamphamvuyonse sazisamalira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:25

Menya wonyoza, ndipo achibwana adzachenjera; nudzudzule wozindikira adzazindikira nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 59:12

Pakamwa pao achimwa ndi mau onse a pa milomo yao, potero akodwe m'kudzitamandira kwao, ndiponso chifukwa cha kutemberera ndi bodza azilankhula.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 14:13-14

Ndipo iwe unati mumtima mwako, Ndidzakwera kumwamba, ndidzakweza mpando wanga wachifumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pamwamba paphiri la khamu, m'malekezero a kumpoto; ndidzakwera pamwamba pa mitambo, ndidzafanana ndi Wam'mwambamwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:17-18

Usakondwere pakugwa mdani wako; mtima wako usasekere pokhumudwa iye; kuti Yehova angaone kukondwa kwako, ndi kukuyesa koipa, ndi kuleka kumkwiyira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 3:13

Ndani ali wanzeru, ndi waluso mwa inu? Aonetsere ndi mayendedwe ake abwino ntchito zake mu nzeru yofatsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:2

ndi kuonetsera kudzichepetsa konse, ndi chifatso, ndi kuonetsera chipiriro, ndi kulolerana wina ndi mnzake, mwa chikondi;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 75:4-5

Ndinati kwa odzitamandira, musamachita zodzitamandira; ndi kwa oipa, Musamakweza nyanga; musamakwezetsa nyanga yanu; musamalankhula ndi khosi louma.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:5

Odala ali akufatsa; chifukwa adzalandira dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:25

Wodukidwa mtima aputa makangano; koma wokhulupirira Yehova adzakula.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 66:7

Achita ufumu mwa mphamvu yake kosatha; maso ake ayang'anira amitundu; opikisana ndi Iye asadzikuze.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 4:7

Pakuti akusiyanitsa iwe ndani? Ndipo uli nacho chiyani chosati wachilandira? Koma ngati wachilandira udzitamanda bwanji, monga ngati sunachilandire?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 28:17

Unadzikuza mtima chifukwa cha kukongola kwako, waipsa nzeru zako; chifukwa cha kuwala kwako ndakugwetsa pansi, ndakuika pamaso pa mafumu, kuti akupenye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 2:12

Chifukwa padzakhala tsiku la Yehova wa makamu pa zonse zonyada ndi zakudzikuza, ndi pa zonse zotukulidwa; ndipo zidzatsitsidwa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 12:3

Yehova adzadula milomo yonse yothyasika, lilime lakudzitamandira;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 3:6

Asakhale wophunza, kuti podzitukumula ungamgwere mlandu wa mdierekezi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:25

Yehova adzapasula nyumba ya wonyada; koma adzalembera mkazi wamasiye malire ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:4

Ndani iwe wakuweruza mnyamata wa mwini wake? Iye aimirira kapena kugwa kwa mbuye wake wa mwini yekha. Ndipo adzaimiritsidwa; pakuti Ambuye ali wamphamvu kumuimiritsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:1

Yang'anirani kuti musachite zolungama zanu pamaso pa anthu kuti muonekere kwa iwo; pakuti ngati mutero mulibe mphotho ndi Atate wanu wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:26

Wokhulupirira mtima wakewake ali wopusa; koma woyenda mwanzeru adzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:119

Muchotsa oipa onse a padziko lapansi ngati mphala: Chifukwa chake ndikonda mboni zanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 40:4

Wodala munthuyo wakuyesa Yehova wokhulupirika; wosasamala odzikuza, ndi opatukira kubodza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:8

Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo; koma chitsiru cholongolola chidzagwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:4

Mphotho ya chifatso ndi kuopa Yehova ndiye chuma, ndi ulemu, ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 11:20

Chabwino; iwo anathyoledwa ndi kusakhulupirira kwao, ndipo iwe umaima ndi chikhulupiriro chako. Usamadzikuza mumtima, koma opatu:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:6

Potero dzichepetseni pansi padzanja la mphamvu la Mulungu, kuti panthawi yake akakukwezeni;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 23:4

Inde, amanga akatundu olemera ndi osautsa ponyamula, nawasenza pa mapewa a anthu; koma iwo eni okha safuna kuwasuntha amenewo ndi chala chao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:4-5

Anena mau, alankhula zowawa; adzitamandira onse ochita zopanda pake. Aphwanya anthu anu, Yehova, nazunza cholowa chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:33

Kuopa Yehova ndiko mwambo wanzeru; ndipo chifatso chitsogolera ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 131:1-2

Yehova, mtima wanga sunadzikuze ndi maso anga sanakwezeke; ndipo sindinatsate zazikulu, kapena zodabwitsa zondiposa. Indedi, ndinalinganiza ndi kutontholetsa moyo wanga; ngati mwana womletsa kuyamwa amake, moyo wanga ndili nao ngati mwana womletsa kuyamwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 5:21

Tsoka kwa iwo amene adziyesera anzeru ndi ochenjera!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:3

M'kamwa mwa chitsiru muli nthyole ya kudzikuza; koma milomo ya anzeru idzawasunga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:9

Maganizo opusa ndiwo tchimo; wonyoza anyansa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:11

Koma ofatsa adzalandira dziko lapansi; nadzakondwera nao mtendere wochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:16-17

Usapambanitse kukhala wolungama; usakhale wanzeru koposa; bwanji ufuna kudziononga wekha? Usapambanitse kuipa, ngakhale kupusa; uferenji nthawi yako isanafike?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 25:6-7

Usadzitame pamaso pa mfumu, ngakhale kuima m'malo mwa akulu. Pakuti kunena kwa iwe, Takwera kuno, kupambana ndi kuti utsitsidwe pamaso pa kalonga, amene maso ako anamuona.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:4

Koma yense ayesere ntchito yake ya iye yekha, ndipo pamenepo adzakhala nako kudzitamandira chifukwa cha iye yekha, si chifukwa cha wina.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 62:9

Indetu, anthu achabe ndi mpweya, ndipo anthu aakulu ndi bodza, pakuwayesa apepuka; onse pamodzi apepuka koposa mpweya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:20

Kodi uona munthu wansontho m'mau ake? Ngakhale chitsiru chidzachenjera, koma ameneyo ai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:12-13

Woipa apangira chiwembu wolungama, namkukutira mano. Ambuye adzamseka, popeza apenya kuti tsiku lake likudza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 8:13

Kuopa Yehova ndiko kuda zoipa; kunyada, ndi kudzikuza, ndi njira yoipa, ndi m'kamwa mokhota, ndizida.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 5:2

Ndipo mukhala odzitukumula, kosati makamaka mwachita chisoni, kuti achotsedwe pakati pa inu iye amene anachita ntchito iyi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:6

Chilungamo chitchinjiriza woongoka m'njira; koma udyo ugwetsa wochimwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 49:16-17

Usaope polemezedwa munthu, pochuluka ulemu wa nyumba yake; pakuti pomwalira iye sadzamuka nako kanthu kalikonse; ulemu wake sutsika naye kumtsata m'mbuyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:3-5

Pakuti ndi chisomo chapatsidwa kwa ine, ndiuza munthu aliyense wa inu, kuti asadziyese koposa kumene ayenera kudziyesa; koma aganize modziletsa yekha, monga Mulungu anagawira kwa munthu aliyense muyeso wa chikhulupiriro. Pakuti monga m'thupi limodzi tili nazo ziwalo zambiri, ndipo ziwalo zonsezo sizili nayo ntchito imodzimodzi; chomwecho ife, ndife ambiri, tili thupi limodzi mwa Khristu, ndi ziwalo zinzake, wina ndi wina.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:12

Kuchita mphulupulu kunyansa mafumu; pakuti mpando wao wakhazikika ndi chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 23:10-12

Ndipo musatchedwa atsogoleri, pakuti alipo mmodzi Mtsogoleri wanu, ndiye Khristu. Koma wamkulu wopambana wa inu adzakhala mtumiki wanu. Ndipo aliyense amene akadzikuza yekha adzachepetsedwa; koma amene adzichepetsa mwini yekha adzakulitsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:17

Wosunga mwambo ali m'njira ya moyo; koma wosiya chidzudzulo asochera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 36:11

Akamvera ndi kumtumikira, adzatsiriza masiku ao modala, ndi zaka zao mokondwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 76:4

Inu ndinu wakuunikira, ndi womveka wakuposa mapiri muli achifwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:19

Musabwezere choipa, okondedwa, koma patukani pamkwiyo; pakuti kwalembedwa, Kubwezera kuli kwanga, Ine ndidzabwezera, ati Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:24

Mau okoma ndiwo chisa cha uchi, otsekemera m'moyo ndi olamitsa mafupa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 109:28

Atemberere iwowa, koma mudalitse ndinu; pakuuka iwowa adzachita manyazi, koma mtumiki wanu adzakondwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:19-21

Ndipo ntchito za thupi zionekera, ndizo dama, chodetsa, kukhumba zonyansa, Taonani, ine Paulo ndinena ndi inu, kuti, ngati mulola akuduleni, Khristu simudzapindula naye kanthu. kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko, njiru, kuledzera, mchezo, ndi zina zotere; zimene ndikuchenjezani nazo, monga ndachita, kuti iwo akuchitachita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 26:26

Angakhale abisa udani wake pochenjera, koma udyo wake udzavumbulutsidwa posonkhana anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 57:15

Pakuti atero Iye amene ali wamtali wotukulidwa, amene akhala mwachikhalire, amene dzina lake ndiye Woyera, Ndikhala m'malo aatali ndi oyera, pamodzi ndi yense amene ali wa mzimu wosweka ndi wodzichepetsa, kutsitsimutsa mzimu wa odzichepetsa, ndi kutsitsimutsa mtima wa osweka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:18-19

Kunyada kutsogolera kuonongeka; mtima wodzikuza ndi kutsogolera kuphunthwa. Kufatsa mtima ndi osauka kuposa kugawana zofunkha ndi onyada.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 13:4-5

Chikondi chikhala chilezere, chili chokoma mtima; chikondi sichidukidwa; chikondi sichidziwa kudzitamanda, sichidzikuza, sichichita zosayenera, sichitsata za mwini yekha, sichipsa mtima, sichilingirira zoipa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:4

Akazi achigololo inu, kodi simudziwa kuti ubwenzi wa dziko lapansi uli udani ndi Mulungu? Potero, iye amene afuna kukhala bwenzi la dziko lapansi adziika mdani wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Yesu wanga wokondedwa, wodzala chifundo ndi wolekera kukwiya, ndikulambira dzina lanu ndi mtima wanga wonse, pakuti ndinu woyenera ulemerero ndi ulemu wonse. Ndikukutamandani Mulungu wanga wabwino, chifukwa cha chikondi chanu ndipo mwandiwombola moyo wanga ku imfa. Mwandipulumutsa ndi kundipatsa mwayi tsiku lililonse kuti ndikhale munthu wabwino. Mzimu Woyera, ndidzipereka pamaso panu podziwa kuti ndikukusowani. Sindikufuna kukhala moyo wodzikuza kapena kuchita chilichonse chomwe chingandisiyanitse ndi inu. Chonde munditsuke ku chilichonse chomwe chikudetsa mtima wanga ndi kundithandiza kukhala moyo woyera, kuti palibe choipa kapena chodzikweza chomwe chingakhale mkati mwanga. Ndikutsutsa kudzikuza konse lero ndipo ndikulengeza kuti ndine mfulu kwathunthu m'dzina la Yesu. Ndili m'manja mwanu, nditsogolereni nthawi zonse ndipo musalole kuti ndichoke pamaso panu. Mundilange ndi kundiphunzitsa njira yoyenera kuyenda. Zikomo chifukwa cha zonse Mulungu wanga wabwino, ndikukulambirani ndi kukukwezani kwamuyaya. M'dzina la Yesu, Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa