Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yakobo 4:10 - Buku Lopatulika

10 Dzichepetseni pamaso pa Ambuye, ndipo adzakukwezani.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

10 Dzichepetseni pamaso pa Ambuye, ndipo adzakukwezani.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

10 Mudzichepetse pamaso pa Ambuye, ndipo adzakukwezani.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

10 Dzichepetseni pamaso pa Ambuye ndipo Iye adzakukwezani.

Onani mutuwo Koperani




Yakobo 4:10
19 Mawu Ofanana  

ndipo anthu anga otchedwa dzina langa akadzichepetsa, nakapemphera, nakafuna nkhope yanga, nakatembenuka kuleka njira zao zoipa; pamenepo ndidzamvera mu Mwamba, ndi kukhululukira choipa chao, ndi kuchiritsa dziko lao.


Anthu akakugwetsa pansi, udzati, Adzandikweza; ndipo adzapulumutsa wodzichepetsayo.


kuika opeputsidwa pamalo ponyamuka, kuti iwo a maliro akwezedwe kosatekeseka.


Amene autsa wosauka kumchotsa kufumbi, nakweza waumphawi kumchotsa kudzala.


Yehova agwiriziza ofatsa; atsitsira oipa pansi.


Ndipo tsopano mutu wanga udzakwezeka pamwamba pa adani anga akundizinga; ndipo ndidzapereka m'chihema mwake nsembe za kufuula mokondwera; ndidzaimba, inde, ndidzaimbira Yehova zomlemekeza.


Pulumutsani anthu anu, ndi kudalitsa cholowa chanu; muwawetenso, ndi kuwanyamula nthawi zonse.


Ndidzakukwezani, Yehova; pakuti mwandinyamutsa, ndipo simunandikondwetsere adani anga.


Ndipo Mose ndi Aroni analowa kwa Farao nanena naye, Atero Yehova, Mulungu wa Ahebri, Ukana kudzichepetsa pamaso panga kufikira liti? Lola anthu anga amuke, akanditumikire;


Kudzikuza kwa munthu kudzamchepetsa; koma wokhala ndi mtima wodzichepetsa adzalemekezedwa.


atero Ambuye Yehova, Chotsa chilemba, vula korona, ufumu sudzakhalanso momwemo, kweza chopepuka, chepsa chokwezeka.


Ndipo aliyense amene akadzikuza yekha adzachepetsedwa; koma amene adzichepetsa mwini yekha adzakulitsidwa.


Iye anatsitsa mafumu pa mipando yao yachifumu, ndipo anakweza aumphawi.


Chifukwa munthu aliyense wakudzikuza adzachepetsedwa; ndipo wakudzichepetsa adzakulitsidwa.


Ndinena ndi inu, anatsikira kunyumba kwake woyesedwa wolungama uyutu, wosati uja ai; pakuti yense wakudzikuza yekha adzachepetsedwa; koma wodzichepetsa yekha adzakulitsidwa.


Potero dzichepetseni pansi padzanja la mphamvu la Mulungu, kuti panthawi yake akakukwezeni;


Yehova asaukitsa, nalemeretsa; achepetsa, nakuzanso.


Adzasunga mapazi a okondedwa ake, koma oipawo adzawakhalitsa chete mumdima; pakuti palibe munthu adzapambana ndi mphamvu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa