Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


117 Mau a Mulungu Ponena za Kuddzitama

117 Mau a Mulungu Ponena za Kuddzitama

Ndikufuna ndikuuzeni anzanga, Mulungu amasankha zinthu zofooka ndi zonyozeka padziko lapansi, zinthu zomwe anthu amaziona ngati zopanda pake, kuti azitsitse zamphamvu. Izi zimachitika kuti pasakhale munthu wodzitamandira pamaso pa Mulungu.

Tsiku lililonse tiyenera kuzindikira kuti timafunikira Mulungu ndipo timadalira chikondi chake chosatha. Munthu wodzitamandira ndi amene amaganiza kuti angathe kuchita chilichonse yekha, akudalira luso lake ndi mphamvu zake.

Mulungu amafuna kuti ana ake akhale opanda kudzitamandira chifukwa iye amatsutsa odzikuza, koma amapereka chisomo kwa odzichepetsa. Akamadza mtima wakudzitamandira, kumbukira momwe unalili poyamba, Mulungu asanalowe m'moyo mwako. Uone zabwino zonse zomwe wakuchitira.

Perekani ulemerero wonse kwa Yehova, chifukwa poyamba munali mumdima, koma tsopano kuwala kwakukulu kwawala m'moyo mwanu. Choncho, musadzitamandire pa chilichonse chifukwa zonse zomwe muli nazo ndi zomwe muli, ndi chifukwa cha chisomo chachikulu chomwe Mulungu wakupatsani.




1 Samueli 2:3

Musalankhulenso modzikuza kwambiri motero; m'kamwa mwanu musatuluke zolulutsa; chifukwa Yehova ndi Mulungu wanzeru, ndipo Iye ayesa zochita anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 1:31

kuti monga mwalembedwa, Iye amene adzitamanda, adzitamande mwa Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:1

Usanyadire zamawa, popeza sudziwa tsiku lina lidzabala chiyani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:18

Kunyada kutsogolera kuonongeka; mtima wodzikuza ndi kutsogolera kuphunthwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:3

Pakuti ngati wina ayesa ali kanthu pokhala ali chabe, adzinyenga yekha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 9:24

koma wakudzitamandira adzitamandire adzikweze umo, kuti ali wakuzindikira, ndi kundidziwa Ine, kuti ndine Yehova wakuchita zokoma mtima, chiweruziro, ndi chilungamo m'dziko lapansi, pakuti m'menemo ndikondwerera, ati Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 3:27

Pamenepo kudzitama kuli kuti? Kwaletsedwa. Ndi lamulo lotani? La ntchito kodi? Iai; koma ndi lamulo la chikhulupiriro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 7:14

Pakuti ngati ndadzitamandira nako kanthu kwa iye chifukwa cha inu, sindinamvetsedwe manyazi; koma monga tinalankhula zonse ndi inu m'choonadi, koteronso kudzitamandira kwathu kumene kwa Tito, kunakhala choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 1:28-29

ndipo zopanda pake za dziko lapansi, ndi zonyozeka, anazisankhula Mulungu, ndi zinthu zoti kulibe; kuti akathere zinthu zoti ziliko; kuti thupi lililonse lisadzitamande pamaso pa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:3

Pakuti ndi chisomo chapatsidwa kwa ine, ndiuza munthu aliyense wa inu, kuti asadziyese koposa kumene ayenera kudziyesa; koma aganize modziletsa yekha, monga Mulungu anagawira kwa munthu aliyense muyeso wa chikhulupiriro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:16

Koma tsopano mudzitamandira m'kudzikuza kwanu; kudzitamandira kulikonse kotero nkoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 10:17

Koma iye wodzitamandira adzitamandire mwa Ambuye;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 3:21

Chifukwa chake palibe mmodzi adzitamande mwa anthu. Pakuti zinthu zonse nzanu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:2

Wina akutume, si m'kamwa mwako ai; mlendo, si milomo ya iwe wekha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:14

Koma kudzitamandira ine konsekonse, iai, koma mu mtanda wa Ambuye wathu Yesu Khristu, amene mwa Iye dziko lapansi lapachikidwira ine, ndi ine ndapachikidwira dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 10:15

osadzitamandira popitirira muyeso mwa machititso a ena; koma tili nacho chiyembekezo kuti pakukula chikhulupiriro chanu, tidzakulitsidwa mwa inu monga mwa chilekezero chathu kwa kuchulukira,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 10:3

Pakuti woipa adzitamira chifuniro cha moyo wake, adalitsa wosirira, koma anyoza Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 25:14

Monga mitambo ndi mphepo popanda mvula, momwemo ndiye wodzikweza ndi zipatso zake monyenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 2:9

chosachokera kuntchito, kuti asadzitamandire munthu aliyense.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 2:23

Iwe wakudzitamandira pachilamulo, kodi uchitira Mulungu mwano ndi kulakwa kwako m'chilamulo?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 5:2

Usalankhule mwanthuku mtima wako, usafulumire kunena kanthu pamaso pa Mulungu; pakuti Mulungu ali kumwamba, iwe uli pansi; chifukwa chake mau ako akhale owerengeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:16

Pakuti chilichonse cha m'dziko lapansi, chilakolako cha thupi ndi chilakolako cha maso, matamandidwe a moyo, sizichokera kwa Atate, koma kudziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 9:23

Atero Yehova, wanzeru asadzitamandire m'nzeru zake, wamphamvu asadzitamandire m'mphamvu yake, wachuma asadzitamandire m'chuma chake;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:4

Maso akunyada, ndi mtima wodzikuza, ndi nyali ya oipa, zili tchimo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 12:9

Ndipo ananena kwa ine, Chisomo changa chikukwanira; pakuti mphamvu yanga ithedwa mu ufooko. Chifukwa chake makamaka ndidzadzitamandira mokondweratu m'mafooko anga, kuti mphamvu ya Khristu ikhale pa ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:30

akazitape, osinjirira, akumuda Mulungu, achipongwe, odzitama, amatukutuku, oyamba zoipa, osamvera akulu ao,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 4:2

Pakuti ngati Abrahamu anayesedwa wolungama chifukwa cha ntchito, iye akhala nacho chodzitamandira; koma kulinga kwa Mulungu ai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 73:6

Chifukwa chake kudzikuza kunga unyolo pakhosi pao; achivala chiwawa ngati malaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:26

Wokhulupirira mtima wakewake ali wopusa; koma woyenda mwanzeru adzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:4

Koma yense ayesere ntchito yake ya iye yekha, ndipo pamenepo adzakhala nako kudzitamandira chifukwa cha iye yekha, si chifukwa cha wina.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mafumu 20:11

Ndipo mfumu ya Israele anayankha, nati, Kamuuzeni, Wakumanga zida asadzikuze ngati wakuvulayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 75:4

Ndinati kwa odzitamandira, musamachita zodzitamandira; ndi kwa oipa, Musamakweza nyanga;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 2:11

Maso a munthu akuyang'anira kumwamba adzatsitsidwa, ndi kudzikweza kwa anthu kudzaweramitsidwa pansi; ndipo Yehova yekha adzakwezedwa tsiku limenelo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:5

Yense wonyada mtima anyansa Yehova; zoonadi sadzapulumuka chilango.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 3:5-6

Kotero lilimenso lili chiwalo chaching'ono, ndipo lidzikuzira zazikulu. Taonani, kamoto kakang'ono kayatsa nkhuni zambiri! Ndipo lilime ndilo moto; ngati dziko la chosalungama mwa ziwalo zathu laikika lilime, ndili lodetsa thupi lonse, niliyatsa mayendedwe a chibadwidwe, ndipo liyatsidwa ndi Gehena.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:5

Momwemonso, anyamata inu, mverani akulu. Koma nonsenu muvale kudzichepetsa kuti mutumikirane; pakuti Mulungu akaniza odzikuza, koma apatsa chisomo kwa odzichepetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 49:16-17

Usaope polemezedwa munthu, pochuluka ulemu wa nyumba yake; pakuti pomwalira iye sadzamuka nako kanthu kalikonse; ulemu wake sutsika naye kumtsata m'mbuyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:3

M'kamwa mwa chitsiru muli nthyole ya kudzikuza; koma milomo ya anzeru idzawasunga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 13:4

Chikondi chikhala chilezere, chili chokoma mtima; chikondi sichidukidwa; chikondi sichidziwa kudzitamanda, sichidzikuza,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 2:8-9

Pakuti muli opulumutsidwa ndi chisomo chakuchita mwa chikhulupiriro, ndipo ichi chosachokera kwa inu: chili mphatso ya Mulungu; chosachokera kuntchito, kuti asadzitamandire munthu aliyense.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:4

Anena mau, alankhula zowawa; adzitamandira onse ochita zopanda pake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 10:12

Pakuti sitilimba mtima kudziwerenga, kapena kudzilinganiza tokha ndi ena a iwo amene adzivomeretsa okha; koma iwowa, podziyesera okha ndi iwo okha, ndi kudzilinganiza okha ndi iwo okha, alibe nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:26

Tisakhale odzikuza, outsana, akuchitirana njiru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:12

Mtima wa munthu unyada asanaonongeke; koma chifatso chitsogolera ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:21

Muli zolingalira zambiri m'mtima mwa munthu; koma uphungu wa Yehova ndiwo udzaimika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:3

musachite kanthu monga mwa chotetana, kapena monga mwa ulemerero wopanda pake, komatu ndi kudzichepetsa mtima, yense ayese anzake omposa iye mwini;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 23:12

Ndipo aliyense amene akadzikuza yekha adzachepetsedwa; koma amene adzichepetsa mwini yekha adzakulitsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:1

Ndipo ife amene tili olimba tiyenera kunyamula zofooka za opanda mphamvu, ndi kusadzikondweretsa tokha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 101:5

Wakuneneza mnzake m'tseri ndidzamdula; wa maso odzikuza ndi mtima wodzitama sindidzamlola.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:10

Kudzikuza kupikisanitsa; koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:23

Kudzikuza kwa munthu kudzamchepetsa; koma wokhala ndi mtima wodzichepetsa adzalemekezedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 23:9

Yehova wa makamu wapanga uphungu uwu, kuipitsa kunyada kwa ulemerero wonse, kupepula onse olemekezeka a m'dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:16

Chomwecho muwalitse inu kuunika kwanu pamaso pa anthu, kuti pakuona ntchito zanu zabwino, alemekeze Atate wanu wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 4:7

Pakuti akusiyanitsa iwe ndani? Ndipo uli nacho chiyani chosati wachilandira? Koma ngati wachilandira udzitamanda bwanji, monga ngati sunachilandire?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 31:18

Ikhale yosalankhula milomo ya mabodza, imene imalankhula mwachipongwe pa olungama mtima, ndi kudzikuza ndi kunyoza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:15

Njira ya chitsiru njolungama pamaso pakepake; koma wanzeru amamvera uphungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 14:11

Chifukwa munthu aliyense wakudzikuza adzachepetsedwa; ndipo wakudzichepetsa adzakulitsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 3:2

Pakuti anthu adzakhala odzikonda okha, okonda ndalama, odzitamandira, odzikuza, amwano, osamvera akuwabala, osayamika,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:1-2

Usavutike mtima chifukwa cha ochita zoipa, usachite nsanje chifukwa cha ochita chosalungama. Katsala kanthawi ndipo woipa adzatha psiti; inde, udzayang'anira mbuto yake, nudzapeza palibe. Koma ofatsa adzalandira dziko lapansi; nadzakondwera nao mtendere wochuluka. Woipa apangira chiwembu wolungama, namkukutira mano. Ambuye adzamseka, popeza apenya kuti tsiku lake likudza. Oipa anasolola lupanga, nakoka uta wao; alikhe ozunzika ndi aumphawi, aphe amene ali oongoka m'njira. Lupanga lao lidzalowa m'mtima mwao momwe, ndipo mauta ao adzathyoledwa. Zochepa zake za wolungama zikoma koposa kuchuluka kwao kwa oipa ambiri. Pakuti manja a oipa adzathyoledwa, koma Yehova achirikiza olungama. Yehova adziwa masiku a anthu angwiro; ndipo cholowa chao chidzakhala chosatha. Sadzachita manyazi m'nyengo yoipa, ndipo m'masiku a njala adzakhuta. Pakuti adzawamweta msanga monga udzu, ndipo adzafota monga msipu wauwisi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 30:32

Ngati wapusa podzikweza, ngakhale kuganizira zoipa, tagwira pakamwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:10

Dzichepetseni pamaso pa Ambuye, ndipo adzakukwezani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:1

Yang'anirani kuti musachite zolungama zanu pamaso pa anthu kuti muonekere kwa iwo; pakuti ngati mutero mulibe mphotho ndi Atate wanu wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:2

Pakudza kudzikuza padzanso manyazi; koma nzeru ili ndi odzichepetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:51

Odzikuza anandinyoza kwambiri: koma sindinapatukanso nacho chilamulo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:16

Mukhale ndi mtima umodzi wina ndi mnzake. Musasamalire zinthu zazikulu, koma phatikanani nao odzichepetsa. Musadziyesere anzeru mwa inu nokha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 8:13

Kuopa Yehova ndiko kuda zoipa; kunyada, ndi kudzikuza, ndi njira yoipa, ndi m'kamwa mokhota, ndizida.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 5:6

Kudzitamanda kwanu sikuli bwino. Kodi simudziwa kuti chotupitsa pang'ono chitupitsa mtanda wonse?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Petro 2:18

Pakuti polankhula mau otukumuka opanda pake, anyengerera pa zilakolako za thupi, ndi zonyansa, anthu amene adayamba kupulumuka kwa iwo a mayendedwe olakwa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 6:4

iyeyo watukumuka, wosadziwa kanthu, koma ayalukira pa mafunso ndi makani a mau, kumene zichokerako njiru, ndeu, zamwano, mayerekezo oipa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:2

Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi: Bwezerani odzikuza choyenera iwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:17-18

Usakondwere pakugwa mdani wako; mtima wako usasekere pokhumudwa iye; kuti Yehova angaone kukondwa kwako, ndi kukuyesa koipa, ndi kuleka kumkwiyira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 5:21

Tsoka kwa iwo amene adziyesera anzeru ndi ochenjera!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 23:7

Pakuti monga asinkha m'kati mwake, ali wotere; ati kwa iwe, Idya numwe; koma mtima wake suli pa iwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 138:6

Angakhale Yehova ngwokwezeka, apenyanso wopepukayo; koma wodzikuza amdziwira kutali.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:17

Musabwezere munthu aliyense choipa chosinthana ndi choipa. Ganiziranitu zinthu za ulemu pamaso pa anthu onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:1-2

Musaweruze, kuti mungaweruzidwe. Kapena pompempha nsomba, adzampatsa iye njoka kodi? Chomwecho, ngati inu, muli oipa, mudziwa kupatsa ana anu mphatso zabwino, kopambana kotani nanga Atate wanu wa Kumwamba adzapatsa zinthu zabwino kwa iwo akumpempha Iye? Chifukwa chake zinthu zilizonse mukafuna kuti anthu achitire inu, inunso muwachitire iwo zotero; pakuti icho ndicho chilamulo ndi aneneri. Lowani pa chipata chopapatiza; chifukwa chipata chili chachikulu, ndi njira yakumuka nayo kukuonongeka ili yotakata; ndipo ali ambiri amene alowa pa icho. Pakuti chipata chili chopapatiza, ndi ichepetsa njirayo yakumuka nayo kumoyo, ndimo akuchipeza chimenecho ali owerengeka. Yang'anirani mupewe aneneri onyenga, amene adza kwa inu ndi zovala zankhosa, koma m'kati mwao ali mimbulu yolusa. Mudzawazindikira ndi zipatso zao. Kodi atchera mphesa paminga, kapena nkhuyu pamtula? Chomwecho mtengo wabwino uliwonse upatsa zipatso zokoma; koma mtengo wamphuchi upatsa zipatso zoipa. Sungathe mtengo wabwino kupatsa zipatso zoipa, kapena mtengo wamphuchi kupatsa zipatso zokoma. Mtengo uliwonse wosapatsa chipatso chokoma, audula, nautaya kumoto. Pakuti ndi kuweruza kumene muweruza nako, inunso mudzaweruzidwa; ndipo ndi muyeso umene muyesa nao, kudzayesedwa kwa inunso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:15

Koma ngati mulumana ndi kudyana, chenjerani mungaonongane.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:1

Momwemo pakutaya choipa chonse, ndi chinyengo chonse, ndi maonekedwe onyenga, ndi kaduka, ndi masinjiriro onse,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:20

Kodi uona munthu wansontho m'mau ake? Ngakhale chitsiru chidzachenjera, koma ameneyo ai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 56:5

Tsiku lonse atenderuza mau anga, zolingirira zao zonse zili pa ine kundichitira choipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 73:12

Tapenyani, oipa ndi awa; ndipo pokhazikika chikhazikikire aonjezerapo pa chuma chao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:12

Udani upikisanitsa; koma chikondi chikwirira zolakwa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:7-8

Ndipo amati, Yehova sachipenya, ndi Mulungu wa Yakobo sachisamalira. Zindikirani, opulukira inu mwa anthu; ndipo opusa inu, mudzachita mwanzeru liti?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 18:3-4

nati, Indetu ndinena kwa inu, Ngati simutembenuka, nimukhala monga tianato, simudzalowa konse mu Ufumu wa Kumwamba. Ndipo iye sanafune; koma anamuka, namponya iye m'nyumba yandende, kufikira abwezere ngongole. Chifukwa chake m'mene akapolo anzake anaona zochitidwazo, anagwidwa chisoni chachikulu, nadza, nalongosolera mbuye wao zonse zimene zinachitidwa. Pomwepo mbuye wake anamuitana iye, nanena naye, Kapolo iwe woipa, ndinakukhululukira iwe mangawa onse aja momwe muja unandipempha ine; kodi iwenso sukadamchitira kapolo mnzako chisoni, monga inenso ndinakuchitira iwe chisoni? Ndipo mbuye wake anakwiya, nampereka kwa azunzi, kufikira akambwezere iye mangawa onse. Chomwechonso Atate wanga a Kumwamba adzachitira inu, ngati inu simukhululukira yense mbale wake ndi mitima yanu. Chifukwa chake yense amene adzichepetsa yekha monga kamwana aka, yemweyo ali wopambana mu Ufumu wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 1:8

Tikati kuti tilibe uchimo, tidzinyenga tokha, ndipo mwa ife mulibe choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:19

Kufatsa mtima ndi osauka kuposa kugawana zofunkha ndi onyada.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:4

Ndani iwe wakuweruza mnyamata wa mwini wake? Iye aimirira kapena kugwa kwa mbuye wake wa mwini yekha. Ndipo adzaimiritsidwa; pakuti Ambuye ali wamphamvu kumuimiritsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:25

Yehova adzapasula nyumba ya wonyada; koma adzalembera mkazi wamasiye malire ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:12-13

Chifukwa chake valani, monga osankhika a Mulungu, oyera mtima ndi okondedwa, mtima wachifundo, kukoma mtima, kudzichepetsa, chifatso, kuleza mtima; kulolerana wina ndi mnzake, ndi kukhululukirana eni okha, ngati wina ali nacho chifukwa pa mnzake; monganso Ambuye anakhululukira inu, teroni inunso;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:24

Mau okoma ndiwo chisa cha uchi, otsekemera m'moyo ndi olamitsa mafupa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:69

Odzikuza anandipangira bodza: Ndidzasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:3-4

musachite kanthu monga mwa chotetana, kapena monga mwa ulemerero wopanda pake, komatu ndi kudzichepetsa mtima, yense ayese anzake omposa iye mwini; pakuti chifukwa cha ntchito ya Khristu anafikira pafupi imfa, wosasamalira moyo wake, kuti akakwaniritse chiperewero cha utumiki wanu wa kwa ine. munthu yense asapenyerere zake za iye yekha, koma yense apenyererenso za mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 66:2

Pakuti zonsezi mkono wanga wazilenga, momwemo zonsezi zinaoneka, ati Yehova; koma ndidzayang'anira munthu uyu amene ali waumphawi, ndi wa mzimu wosweka, nanthunthumira ndi mau anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:31

Chifukwa chake mungakhale mudya, mungakhale mumwa, mungakhale muchita kanthu kena, chitani zonse ku ulemerero wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:19

Mudziwa, abale anga okondedwa, kuti munthu aliyense akhale wotchera khutu, wodekha polankhula, wodekha pakupsa mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:1-2

Abale, ngatinso munthu agwidwa nako kulakwa kwakuti, inu auzimu, mubweze wotereyo mu mzimu wa chifatso; ndi kudzipenyerera wekha, ungayesedwe nawenso. Chifukwa chake, monga tili nayo nyengo, tichitire onse chokoma, koma makamaka iwo a pa banja la chikhulupiriro. Taonani, malembedwe aakuluwo ndakulemberani inu ndi dzanja langa la ine mwini. Onse amene afuna kuonekera okoma m'thupi, iwowa akukakamizani inu mudulidwe; chokhacho, chakuti angazunzike chifukwa cha mtanda wa Khristu. Pakuti angakhale iwo omwe odulidwa sasunga lamulo; komatu afuna inu mudulidwe, kuti akadzitamandire m'thupi lanu. Koma kudzitamandira ine konsekonse, iai, koma mu mtanda wa Ambuye wathu Yesu Khristu, amene mwa Iye dziko lapansi lapachikidwira ine, ndi ine ndapachikidwira dziko lapansi. Pakuti mdulidwe ulibe kanthu, kusadulidwa kulibe kanthunso, komatu wolengedwa watsopano. Ndipo onse amene atsata chilangizo ichi, mtendere ndi chifundo zikhale pa iwo, ndi pa Israele wa Mulungu. Kuyambira tsopano palibe munthu andivute, pakuti ndili nayo ine m'thupi mwanga mikwingwirima ya Yesu. Chisomo cha Ambuye wathu Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wanu, abale. Amen. Nyamuliranani zothodwetsa, ndipo kotero mufitse chilamulo cha Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 25:6-7

Usadzitame pamaso pa mfumu, ngakhale kuima m'malo mwa akulu. Pakuti kunena kwa iwe, Takwera kuno, kupambana ndi kuti utsitsidwe pamaso pa kalonga, amene maso ako anamuona.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:23-24

Mundisanthule, Mulungu, nimudziwe mtima wanga; mundiyese nimudziwe zolingalira zanga. Ndipo mupenye ngati ndili nao mayendedwe oipa, nimunditsogolere panjira yosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:11

Wolemera adziyesa wanzeru; koma wosauka wozindikira aululitsa zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:25

Mtima wa mataya udzalemera; wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 2:23-24

Iwe wakudzitamandira pachilamulo, kodi uchitira Mulungu mwano ndi kulakwa kwako m'chilamulo? Pakuti dzina la Mulungu lichitidwa mwano chifukwa cha inu, pakati pa anthu a mitundu, monga mwalembedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 23:5-7

Koma amachita ntchito zao zonse kuti aonekere kwa anthu; pakuti akulitsa chitando chake cha njirisi zao, nakulitsa mphonje, nakonda malo a ulemu pamaphwando, ndi mipando ya ulemu m'masunagoge, ndi kulonjeredwa m'misika, ndi kutchedwa ndi anthu, Rabi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 52:1-3

Udzitamandiranji ndi choipa, chiphona iwe? Chifundo cha Mulungu chikhala tsiku lonse. Lilime lako likupanga zoipa; likunga lumo lakuthwa, lakuchita monyenga. Ukonda choipa koposa chokoma; ndi bodza koposa kunena chilungamo,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:16

Mkwiyo wa chitsiru udziwika posachedwa; koma wanzeru amabisa manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 3:13

komatu dandaulirananani nokha tsiku ndi tsiku, pamene patchedwa, Lero; kuti angaumitsidwe wina wa inu ndi chenjerero la uchimo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:3-5

Ndipo upenya bwanji kachitsotso kali m'diso la mbale wako, koma mtanda uli m'diso la iwe mwini suuganizira? Kapena udzati bwanji kwa mbale wako, Tandilola ndichotse kachitsotso m'diso lako; ndipo ona, mtandawo ulimo m'diso lakoli. Wonyenga iwe! Tayamba kuchotsa m'diso lako mtandawo, ndipo pomwepo udzapenyetsa kuchotsa kachitsotso m'diso la mbale wako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 4:23

Chinjiriza mtima wako koposa zonse uzisunga; pakuti magwero a moyo atulukamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:10

Koma iwe uweruziranji mbale wako? Kapena iwenso upeputsiranji mbale wako? Pakuti ife tonse tidzaimirira kumpando wakuweruza wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:6

Koma apatsa chisomo choposa. Potero anena malembo, Mulungu akaniza odzikuza, koma apatsa chisomo odzichepetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 10:4

Woipa, monga mwa kudzikuza kwa nkhope yake, akuti, Sadzafunsira. Malingaliro ake onse akuti, Palibe Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 15:33-34

Musanyengedwe; mayanjano oipa aipsa makhalidwe okoma. Ukani molungama, ndipo musachimwe; pakuti ena alibe chidziwitso cha Mulungu. Ndilankhula kunyaza inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:21-22

Mau onsetu onenedwa usawalabadire; kuti usamve kapolo wako alikukutemberera; pakuti kawirikawiritu mtima wako udziwa kuti nawenso unatemberera ena.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:29

Wosakwiya msanga apambana kumvetsa; koma wansontho akuza utsiru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:14

Ndikuyamikani chifukwa kuti chipangidwe changa nchoopsa ndi chodabwitsa; ntchito zanu nzodabwitsa; moyo wanga uchidziwa ichi bwino ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:25

Wodukidwa mtima aputa makangano; koma wokhulupirira Yehova adzakula.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga wokondedwa, ndikufuna kukuthokozani chifukwa cha zonse zomwe mwandipangira. Zikomo chifukwa cha chikondi chanu chosatha chomwe chaphimba moyo wanga ndi kundidzaza ndi chisomo ndi chiphaso chanu. Zikomo chifukwa simunandisiyepo ndi dzanja lanu lamphamvu, nthawi zonse mwandilimbitsa. Ambuye Yesu, tsiku lililonse ndikufuna kukhala chithunzi cha chikondi chanu, ndikufuna kufanana nanu ndikukuzindikirani m'njira zanga zonse, chifukwa ndinu chifukwa chomwe ndilipo ndipo ndimakhala padziko lapansi. Ndikukupemphani kuti tsiku lililonse mundipatse mtima watsopano ndipo musandilole kudzitamandira pa chilichonse chomwe ndingachite kapena kukhala nacho, kuti Mzimu wanu woyera anditsogolere ku choonadi chonse ndi kundiveka ndi kudzichepetsa nthawi zonse. Mundipatse mtima wosalira zambiri pamaso panu m'mawa uliwonse, chifukwa ndikufuna kukusangalatsani nthawi zonse. Ndimakukondani Mulungu wanga, zikomo chifukwa cha zinthu zonse. M'dzina la Yesu, Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa