Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


128 Mau a m'Baibulo Okhudza Kulambira Mafano

128 Mau a m'Baibulo Okhudza Kulambira Mafano

Mverani ine, ndikufuna kukuuzani nkhani yofunika kwambiri. Baibulo, m’buku la Ekisodo 20:4-5, limatiuza kuti tisapange fano lililonse la chinthu chilichonse chimene chili kumwamba, pansi pa nthaka, kapena m’madzi. Tisazipembedzere kapena kuzigwadira, chifukwa ine ndine Yehova Mulungu wanu, Mulungu wansanje komanso wamphamvu. Ndimalanga ana chifukwa cha machimo a makolo awo mpaka mbadwo wachitatu ndi wachinayi wa ondiipira.

Kupembedza mafano ndi kupembedza milungu yonyenga yopangidwa ndi manja a anthu. Kuyambira kalekale, mdierekezi wakhala akuyesera kutenga malo a Mulungu, akukopa anthu kupembedza mafano. Amene amapembedza mafano ayenera kudziwa kuti sapemphera oyera mtima kapena anamwali, koma akupembedza mwachindunji Satana. Ndi tchimo lalikulu, ndipo ngati mutalapa, lingakupangitseni kukhala ku gehena kwamuyaya.

Dziwani kuti ndi Mulungu yekha amene tiyenera kuwagwadira ndi kuwapembedza. Iye ndiye Wamphamvuyonse, mlengi wa thambo, dziko lapansi, ndi zonse zili mmenemo. Musamadalire mafano opangidwa ndi dothi, matabwa, kapena zitsulo, chifukwa sangakuthandizeni kapena kukutetezani.

Pempherani kuti Yesu akuvumbulutseni zomwe simukumvetsa ndi kukumasulani kupembedza mafano, kuti mupembedze dzina la Mulungu yekha. Zinthu izi ndizofunika kwambiri pa moyo wanu.




Levitiko 26:1

Musamadzipangira mafano, kapena kudziutsira mafano osema, kapena choimiritsa, kapena kuika mwala wozokota m'dziko mwanu kuugwadira umenewo; popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 20:4

Usadzipangire iwe wekha fano losema, kapena chifaniziro chilichonse cha zinthu za m'thambo la kumwamba, kapena za m'dziko lapansi, kapena za m'madzi a pansi padziko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:14

Chifukwa chake, okondedwa anga, thawani kupembedza mafano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 20:3-6

Usakhale nayo milungu ina koma Ine ndekha. Usadzipangire iwe wekha fano losema, kapena chifaniziro chilichonse cha zinthu za m'thambo la kumwamba, kapena za m'dziko lapansi, kapena za m'madzi a pansi padziko. Usazipembedzere izo, usazitumikire izo; chifukwa Ine Yehova Mulungu wako ndili Mulungu wansanje, wakulanga ana chifukwa cha atate ao, kufikira mbadwo wachitatu ndi wachinai wa iwo amene akudana ndi Ine; ndi kuwachitira chifundo anthu zikwizikwi a iwo amene akondana ndi Ine, nasunga malamulo anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 19:4

Musamatembenukira mafano, kapena kudzipangira mulungu woyenga; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 16:4

Zidzachuluka zisoni zao za iwo otsata Mulungu wina. Sindidzathira nsembe zao zamwazi, ndipo sindidzatchula maina ao pakamwa panga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 20:3-5

Usakhale nayo milungu ina koma Ine ndekha. Usadzipangire iwe wekha fano losema, kapena chifaniziro chilichonse cha zinthu za m'thambo la kumwamba, kapena za m'dziko lapansi, kapena za m'madzi a pansi padziko. Usazipembedzere izo, usazitumikire izo; chifukwa Ine Yehova Mulungu wako ndili Mulungu wansanje, wakulanga ana chifukwa cha atate ao, kufikira mbadwo wachitatu ndi wachinai wa iwo amene akudana ndi Ine;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 5:7-9

Usakhale nayo milungu ina koma Ine ndekha. Usadzipangire iwe wekha fano losema, kapena chifaniziro chilichonse cha zinthu za m'thambo la kumwamba, kapena za m'dziko lapansi, kapena za m'madzi a pansi padziko; usazipembedzere izo, usazitumikire izo; chifukwa Ine Yehova Mulungu wako ndine Mulungu wansanje, wakulanga ana chifukwa cha atate wao, kufikira mbadwo wachitatu ndi wachinai wa iwo amene akudana ndi Ine;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:7

Kapena musakhale opembedza mafano, monga ena a iwo, monga kwalembedwa, Anthu anakhala pansi kudya ndi kumwa, nanyamuka kusewera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 115:4-8

Mafano ao ndiwo a siliva ndi golide, ntchito za manja a anthu. Pakamwa ali napo, koma osalankhula; maso ali nao, koma osapenya; makutu ali nao, koma osamva; mphuno ali nazo, koma osanunkhiza; manja ali nao, koma osagwira; mapazi ali nao, koma osayenda; kapena sanena pammero pao. Adzafanana nao iwo akuwapanga; ndi onse akuwakhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Hoseya 11:2

Monga anawaitana, momwemo anawachokera; anaphera nsembe Abaala, nafukizira mafano osema.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 135:15

Mafano a amitundu ndiwo siliva ndi golide, ntchito ya manja a anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:20

kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 45:20

Sonkhanani nokha, mudze; yandikirani chifupi pamodzi, inu amene mwapulumuka amitundu; iwo alibe nzeru, amene anyamula mtengo wa fano lao losema, ndi kupemphera mulungu wosakhoza kupulumutsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:21

Tiana, dzisungireni nokha kupewa mafano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:5

Chifukwa chake fetsani ziwalozo zili padziko; dama, chidetso, chifunitso chamanyazi, chilakolako choipa, ndi chisiriro, chimene chili kupembedza mafano;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 23:13

Ndipo samalirani zonse ndanena ndi inu; nimusatchule dzina la milungu ina; lisamveke pakamwa pako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 20:23

Musapange milungu yasiliva ikhale pamodzi ndi Ine; musadzipangire milungu yagolide.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 6:14-15

Musamatsate milungu ina, milungu ina ya mitundu ya anthu akuzinga inu; pakuti Yehova Mulungu wanu ali pakati panu, ndiye Mulungu wansanje; kuti ungapse mtima wa Yehova Mulungu wanu, ndi kukuonongani, kukuchotsani pankhope padziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 15:23

Pakuti kupanduka kuli ngati choipa cha kuchita nyanga, ndi mtima waliuma uli ngati kupembedza milungu yachabe ndi maula. Popeza inu munakaniza mau a Yehova, Iyenso anakaniza inu, kuti simudzakhalanso mfumu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 31:6

Ndikwiya nao iwo akusamala zachabe zonama, koma ndikhulupirira Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:23

nasandutsa ulemerero wa Mulungu wosaonongeka, naufanizitsa ndi chifaniziro cha munthu woonongeka ndi cha mbalame, ndi cha nyama zoyendayenda, ndi cha zokwawa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mika 5:13

ndidzaononganso mafano ako osema, ndi zoimiritsa zako pakati pako; ndipo sudzalambiranso ntchito za manja ako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 42:8

Ine ndine Yehova; dzina langa ndi lomweli; ndipo ulemerero wanga Ine sindidzapereka kwa wina, ngakhale kunditamanda kwa mafano osemedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 46:7

Iwo amanyamula mlunguwu paphewa, nausenza, naukhazika m'malo mwake, nukhala chilili; pamalo pakepo sudzasunthika; inde, wina adzaufuulira, koma sungathe kuyankha, kapena kumpulumutsa m'zovuta zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:24

Palibe munthu angathe kukhala kapolo wa ambuye awiri: pakuti pena adzamuda mmodziyo, ndi kukonda winayo; pena adzakangamira kwa mmodzi, nadzanyoza wina. Simungathe kukhala kapolo wa Mulungu ndi wa Chuma.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 6:9

Kapena simudziwa kuti osalungama sadzalandira ufumu wa Mulungu? Musasocheretsedwe; adama, kapena opembedza mafano, kapena achigololo, kapena olobodoka ndi zoipa, kapena akudziipsa ndi amuna,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 1:16

Ndipo ndidzanena nao za maweruzo anga akuweruzira zoipa zao zonse; popeza anandisiya Ine, nafukizira milungu ina, nagwadira ntchito za manja ao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:21-23

chifukwa kuti, ngakhale anadziwa Mulungu, sanamchitire ulemu wakuyenera Mulungu, ndipo sanamyamike; koma anakhala opanda pake m'maganizo ao, ndipo unada mtima wao wopulukira. Pakunena kuti ali anzeru, anapusa; nasandutsa ulemerero wa Mulungu wosaonongeka, naufanizitsa ndi chifaniziro cha munthu woonongeka ndi cha mbalame, ndi cha nyama zoyendayenda, ndi cha zokwawa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Habakuku 2:18

Apindulanji nalo fano losema, kuti wakulipanga analisema; fano loyenga ndi mphunzitsi wamabodza, kuti wakulipanga alikhulupirira, atapanga mafano osanena mau?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 65:3

anthu amene andiputa Ine kumaso kwanga nthawi zonse, apereka nsembe m'minda, nafukizira zonunkhira panjerwa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 32:1-6

Koma pamene anaona kuti Mose anachedwa kutsika m'phiri, anthuwo anasonkhana kwa Aroni, nanena naye, Ukani, tipangireni milungu yakutitsogolera; pakuti Mose uyu, munthuyu anatikweza kuchokera m'dziko la Ejipito, sitidziwa chomwe chamgwera. ndipo tsopano ndileke, kuti ndipse mtima pa awo ndi kuwatha, ndi kukuza iwe ukhale mtundu waukulu. Ndipo Mose anapemba kwa Yehova Mulungu wake, nati, Yehova, mtima wanu upserenji pa anthu anu, amene munawatulutsa m'dziko la Ejipito ndi mphamvu yaikulu, ndi dzanja lolimba? Akaneneranji Aejipito, ndi kuti, Anawatulutsa ndi cholinga choipa, kuti awaphe m'mapiri, ndi kuwatha pankhope padziko lapansi? Pepani, lekani choipacho cha pa anthu anu. Kumbukirani Abrahamu, Isaki ndi Israele, atumiki anu, amene munawalumbirira ndi kudzitchula nokha, amene munanena nao, Ndidzachulukitsa mbeu zanu ngati nyenyezi za kuthambo, ndi dziko ili lonse ndanenali ndidzapatsa mbeu zanu, likhale cholowa chao nthawi zonse. Ndipo Yehova analeka choipa adanenachi, kuwachitira anthu ake. Ndipo Mose anatembenuka, natsika m'phirimo, magome awiri a mboni ali m'dzanja lake; magome olembedwa kwina ndi kwina; analembedwa mbali ina ndi inzake yomwe. Ndipo magomewo ndiwo ntchito ya Mulungu, kulembaku ndiko kulemba kwa Mulungu, kozokoteka pa magomewo. Ndipo pamene Yoswa anamva phokoso la kufuula kwa anthu, anati kwa Mose, Kuli phokoso la nkhondo kuchigono. Koma iye anati, Phokosoli sindilo la kufuula kwa ogonjetsa, kapena la kufuula kwa opasuka; koma phokoso ndikumvali ndilo la othirirana mang'ombe. Ndipo kunali, pamene anayandikiza chigono, anaona mwanawang'ombeyo ndi kuvinako; ndipo Mose anapsa mtima, nataya magome ali m'manja mwake, nawaswa m'tsinde mwa phiri. Ndipo Aroni ananena nao, Thyolani mphete zagolide zili m'makutu a akazi anu, a ana anu aamuna ndi aakazi, ndi kubwera nazo kwa ine. Ndipo anatenga mwanawang'ombe anampangayo, namtentha ndi moto, nampera asalale, namwaza pamadzi, namwetsako ana a Israele. Ndipo Mose anati kwa Aroni, Anthu awa anakuchitiranji, kuti iwe watengera iwo kulakwa kwakukulu kotere? Ndipo Aroni anati, Asapse mtima mbuye wanga; udziwa anthuwa kuti akhumba choipa. Pakuti ananena nane, Tipangireni milungu yakutitsogolera; popeza Mose uyu, munthuyu anatikweza kuchokera m'dziko la Ejipito, sitidziwa chomwe chamgwera. Ndipo ndinanena nao, Aliyense ali naye golide amthyole; ndipo anandipatsa; ndipo ndinachiponya m'moto, ndimo anatulukamo mwanawang'ombe uyu. Ndipo pamene Mose anaona kuti anthu anamasuka, popeza Aroni adawamasula kuti awatonze adani ao, Mose anaima pa chipata cha chigono, nati, Onse akuvomereza Yehova, adze kwa ine. Pamenepo ana aamuna onse a Levi anasonkhana kwa iye. Ndipo ananena nao, Atero Yehova Mulungu wa Israele, Yense amange lupanga lake m'chuuno mwake, napite, nabwerere kuyambira chipata kufikira chipata, pakati pa chigono, naphe yense mbale wake, ndi yense bwenzi lake, ndi yense mnansi wake. Ndipo ana a Levi anachita monga mwa mau a Mose; ndipo adagwa tsiku lija anthu ngati zikwi zitatu. Popeza Mose adati, Mdzazireni Yehova manja anu lero, pakuti yense akhale mdani wa mwana wake wamwamuna, ndi mdani wa mbale wake; kuti akudalitseni lero lino. Ndipo anthu onse anathyola mphete zagolide zinali m'makutu mwao, nabwera nazo kwa Aroni Ndipo kunali m'mawa mwake, kuti Mose anati kwa anthu, Mwachimwa kuchimwa kwakukulu; koma ndikwera kwa Yehova tsopano, kapena ndidzachita chotetezera uchimo wanu. Ndipo Mose anabwerera kunka kwa Yehova, nati, Ha! Pepani, anthu awa anachimwa kuchimwa kwakukulu, nadzipangira milungu yagolide. Koma tsopano, kapena mudzakhululukira kuchimwa kwao; koma ngati mukana, mundifafanizetu, kundichotsa m'buku lanu limene munalembera, Ndipo Yehova anati kwa Mose, Iye amene wandichimwira, ndifafaniza yemweyo kumchotsa m'buku langa. Ndipo tsopano, muka, tsogolera anthu kunka nao kumene ndinakuuza; taona, mthenga wanga akutsogolera; koma tsiku lakuwazonda Ine ndidzawalanga chifukwa cha kuchimwa kwao. Ndipo Yehova anakantha anthu, chifukwa anapanga mwanawang'ombe amene Aroni anapanga. Ndipo anazilandira ku manja ao, nachikonza ndi chozokotera, nachiyenga mwanawang'ombe; ndipo anati, Siyi milungu yako, Israele, imene inakukweza kuchokera m'dziko la Ejipito. Pakuchiona Aroni, anamanga guwa la nsembe patsogolo pake; ndipo Aroni anafuula nati, Mawa aliko madyerero a Yehova. Ndipo m'mawa mwake anauka mamawa, nafukiza nsembe zopsereza, nabwera nazo nsembe zamtendere; ndi anthu anakhala pansi kudya ndi kumwa, nauka kusewera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 17:16

Pamene Paulo analindira iwo pa Atene, anavutidwa mtima pamene anaona mzinda wonse wadzala ndi mafano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 9:16-17

Ndipo ndinapenya, taonani, mudachimwira Yehova Mulungu wanu; mudadzipangira mwanawang'ombe woyenga; mudapatuka msanga m'njira imene Yehova adalamulira inu. Pamenepo ndinagwira magome awiriwo, ndi kuwataya achoke m'manja anga awiri, ndi kuwaswa pamaso panu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 46:5

Kodi mudzandifanizira ndi yani, ndi kundilinganiza ndi kundiyerekeza, kuti ife tifanane?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 18:21

Ndipo usamapereka a mbumba yako kuwapitiriza kumoto chifukwa cha Moleki; usamaipsa dzina la Mulungu wako; Ine ndine Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 97:7

Onse akutumikira fano losema, akudzitamandira nao mafano, achite manyazi: Mgwadireni Iye, milungu yonse inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 135:15-18

Mafano a amitundu ndiwo siliva ndi golide, ntchito ya manja a anthu. Pakamwa ali napo koma osalankhula; maso ali nao, koma osapenya; makutu ali nao, koma osamva; inde, pakamwa pao palibe mpweya. Akuwapanga adzafanana nao; inde, onse akuwakhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 12:29-31

Pamene Yehova Mulungu wanu akadzadulatu amitundu pamaso panu, kumene mulowako kuwalandira, ndipo mutawalandira, ndi kukhala m'dziko lao, nimugumule maguwa ao a nsembe, ndi kuphwanya zoimiritsa zao, ndi kutentha zifanizo zao, ndi kulikha mafano osema a milungu yao; ndipo muononge dzina lao lichoke m'malomo. dzichenjerani nokha mungakodwe ndi kuwatsata, ataonongeka pamaso panu; ndi kuti mungafunsire milungu yao, ndi kuti, Amitundu awa atumikira milungu yao bwanji? Ndichite momwemo inenso. Musamatero ndi Yehova Mulungu wanu; pakuti zilizonse zinyansira Yehova, zimene azida Iye, iwowa anazichitira milungu yao; pakuti angakhale ana ao aamuna ndi ana ao aakazi awatentha m'moto, nsembe ya milungu yao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 10:3-5

Pakuti miyambo ya anthu ili yachabe, pakuti wina adula mtengo m'nkhalango, ntchito ya manja a mmisiri ndi nkhwangwa. Aukometsa ndi siliva ndi golide; auchirikiza ndi misomali ndi nyundo, kuti usasunthike. Mafanowa akunga mtengo wakanjedza, wosemasema, koma osalankhula; ayenera awanyamule, pakuti sangathe kuyenda. Musawaope; pakuti sangathe kuchita choipa, mulibenso mwa iwo kuchita chabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 11:11

Chifukwa chake atero Yehova, Taonani, ndidzatengera pa iwo choipa, chimene sangathe kuchipulumuka; ndipo adzandifuulira Ine, koma sindidzamvera iwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 14:3-5

Wobadwa ndi munthu iwe, anthu awa anautsa mafano ao mumtima mwao, naimika chokhumudwitsa cha mphulupulu yao pamaso pao; ndifunsidwe nao konse kodi? Chifukwa chake ulankhule nao, nunene nao, Atero Ambuye Yehova, Aliyense wa nyumba ya Israele wakuutsa mafano ake mumtima mwake, naimika chokhumudwitsa cha mphulupulu yake pamaso pake, nadza kwa mneneri, Ine Yehova ndidzamyankhapo monga mwa mafano ake aunyinji; kuti ndigwire nyumba ya Israele mumtima mwao; popeza onsewo asanduka alendo ndi Ine mwa mafano ao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Oweruza 10:14

Mukani ndi kufuulira kwa milungu munaisankha, ikupulumutseni nyengo ya kusauka kwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 27:15

Wotembereredwa munthu wakupanga fano losema kapena loyenga, lonyansidwa nalo Yehova, ntchito ya manja a mmisiri, ndi kuliika m'malo a m'tseri. Ndipo anthu onse ayankhe ndi kuti, Amen.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 17:29

Popeza tsono tili mbadwa za Mulungu, sitiyenera kulingalira kuti umulungu uli wofanafana ndi golide, kapena siliva, kapena mwala, wolocha ndi luso ndi zolingalira za anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 7:25

Mafano osema a milungu yao muwatenthe ndi moto; musamasirira siliva ndi golide zili pa iwo, kapena kudzitengera izi; mungakodwe nazo; pakuti izi zinyansira Yehova Mulungu wanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 2:8

Dziko lao ladzalanso mafano; iwo apembedza ntchito ya manja aoao, imene zala zaozao zinaipanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 16:1

Ndipo Yehova ananena ndi Mose, atamwalira ana aamuna awiri a Aroni, muja anasendera pamaso pa Yehova, namwalira;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 16:30

popeza tsikuli adzachitira inu chotetezera, kukuyeretsani; adzakuyeretsani, kukuchotserani zoipa zanu zonse pamaso pa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 2:22

Iwe wakunena kuti munthu asachite chigololo, kodi umachita chigololo mwini wekha? Iwe wakudana nao mafano, umafunkha za mu Kachisi kodi?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:37

Muchititse mlubza maso anga ndisapenye zachabe, mundipatse moyo mu njira yanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 33:51-52

Nena ndi ana a Israele, nuti nao, Mutaoloka Yordani kulowa m'dziko la Kanani, mupirikitse onse okhala m'dziko pamaso panu, ndi kuononga mafano ao onse a miyala, ndi kuononga mafano ao onse oyenga, ndi kupasula misanje yao yonse;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 4:10

Pomwepo Yesu ananena kwa iye, Choka Satana, pakuti kwalembedwa, Ambuye Mulungu wako udzamgwadira, ndipo Iye yekhayekha udzamlambira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 32:21

Anautsa nsanje yanga ndi chinthu chosati Mulungu; anautsa mkwiyo wanga ndi zopanda pake zao. Ndidzautsa nsanje yao ndi iwo osakhala mtundu wa anthu; ndidzautsa mkwiyo wao ndi mtundu wa anthu opusa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mafumu 17:12

natumikira mafano amene Yehova anawanena nao, Musachita ichi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 78:58

Ndipo anautsa mtima wake ndi malo amsanje ao, namchititsa nsanje ndi mafano osema.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 16:26

Pakuti milungu ya mitundu ya anthu ndiyo mafano; koma Yehova analenga zakumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 20:7

ndipo ndinanena nao, Aliyense ataye zonyansa za pamaso pake, nimusadzidetsa ndi mafano a Ejipito; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 106:36

Ndipo anatumikira mafano ao, amene anawakhalira msampha:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 10:2

Pakuti aterafi anena zopanda pake, ndi aula aona bodza; nafotokoza maloto achabe, asangalatsa nazo zopanda pake; chifukwa chake ayendayenda ngati nkhosa, azunzika popeza palibe mbusa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 81:9

Kwanu kusakhale mulungu wofuma kwina; nusagwadire mulungu wachilendo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 115:4

Mafano ao ndiwo a siliva ndi golide, ntchito za manja a anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 2:17-18

Ndipo kudzikweza kwa munthu kudzaweramitsidwa pansi, kudzikuza kwa munthu kudzatsitsidwa; ndipo Yehova yekha adzakwezedwa tsiku limenelo. Ndimo mafano adzapita psiti.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 57:13

Pamene pakufuula iwe akupulumutse amene unawasonkhanitsa; koma mphepo idzawatenga, mpweya udzachotsa onse; koma iye amene andikhulupirira Ine adzakhala ndi dziko, nadzakhala nacho cholowa m'phiri langa lopatulika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 51:17-18

Anthu onse ali opulukira ndi opanda nzeru; wakusula golide achitidwa manyazi ndi fanizo lake losema; pakuti fanizo lake loyenga lili bodza, mulibe mpweya m'menemo. Ngwachabe, chiphamaso; nthawi ya kulangidwa kwao adzatayika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 36:18

M'mwemo ndinawatsanulira ukali wanga, chifukwa cha mwazi anautsanulira padziko, ndi chifukwa cha mafano analidetsa nalo dziko;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 115:2-3

Aneneranji amitundu, Ali kuti Mulungu wao? Koma Mulungu wathu ndiye ali m'mwamba; achita chilichonse chimkonda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 36:25

Ndipo ndidzakuwazani madzi oyera, ndipo mudzakhala oyera; ndidzakuyeretsani kukuchotserani zodetsa zanu zonse, ndi mafano anu nonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 44:10

Koma Aleviwo anandichokera kunka kutaliwo, posokera Israele, amene anandisokerera ndi kutsata mafano ao, iwowa adzasenza mphulupulu yao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 4:8-9

Komatu pajapo, posadziwa Mulungu inu, munachitira ukapolo iyo yosakhala milungu m'chibadwidwe chao; koma tsopano, podziwa Mulungu inu, koma makamaka podziwika ndi Mulungu, mubwereranso bwanji kutsata miyambo yofooka ndi yaumphawi, imene mufuna kubwerezanso kuichitira ukapolo?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 8:7

Komatu chidziwitso sichili mwa onse; koma ena, ozolowera fano kufikira tsopano, adyako monga yoperekedwa nsembe kwa fano; ndipo chikumbumtima chao, popeza nchofooka, chidetsedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 2:18

Munthu aliyense asakunyengeni ndi kulanda mphotho yanu ndi kudzichepetsa mwini wake, ndi kugwadira kwa angelo, ndi kukhalira mu izi adaziona, wodzitukumula chabe ndi zolingalira za thupi lake, wosagwiritsa mutuwo,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 6:16

Ndipo chiphatikizo chake nchanji ndi Kachisi wa Mulungu ndi wa mafano? Pakuti ife ndife Kachisi wa Mulungu wamoyo; monga Mulungu anati, Ndidzakhalitsa mwa iwo, ndipo ndidzayendayenda mwa iwo; ndipo ndidzakhala Mulungu wao, ndi iwo adzakhala anthu anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 106:36-39

Ndipo anatumikira mafano ao, amene anawakhalira msampha: Ndipo anapereka ana ao aamuna ndi aakazi nsembe ya kwa ziwanda, nakhetsa mwazi wosachimwa, ndiwo mwazi wa ana ao aamuna ndi aakazi, amene anawaperekera nsembe mafano a Kanani; m'mwemo analidetsa dziko ndi mwaziwo. Ndipo anadziipsa nazo ntchito zao, nachita chigololo nao machitidwe ao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 7:18

Ana atola nkhuni, atate akoleza moto, akazi akanyanga ufa, kuti aumbe mikate ya mfumu yaikazi ya kumwamba, athirire milungu ina nsembe yothira, kuti autse mkwiyo wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:18-20

Mudzafanizira Mulungu ndi yani tsopano, kapena kumyerekeza ndi chithunzithunzi chotani? Fano losema mmisiri analisungunula, ndipo wosula golide analikuta ndi golide, naliyengera maunyolo asiliva. Munene inu zotonthoza mtima kwa Yerusalemu, nimufuulire kwa iye, kuti nkhondo yake yatha, kuti kuipa kwake kwakhululukidwa; kuti iye walandira mowirikiza m'dzanja la Yehova, chifukwa cha machimo ake onse. Wosowa nsembe yoteroyo asankha mtengo umene sungavunde, iye adzisankhira yekha munthu mmisiri waluso, akonze fano losema, limene silisunthika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 23:24

Usagwadira milungu yao, kapena kuwatumikira, kapena kuchita monga mwa ntchito zao; koma uwapasule konse, ndi kugamulatu zoimiritsa zao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:19-21

Musadzikundikire nokha chuma padziko lapansi, pamene njenjete ndi dzimbiri ziononga; ndi pamene mbala ziboola ndi kuba: Chifukwa chake pamene paliponse upatsa mphatso zachifundo, usamaomba lipenga patsogolo pako, monga amachita onyenga m'masunagoge, ndi m'makwalala, kotero kuti atamandidwe ndi anthu. Indetu ndinena kwa inu, Iwo alandiriratu mphotho zao. koma mudzikundikire nokha chuma mu Mwamba, pamene njenjete kapena dzimbiri siziononga, ndipo mbala siziboola ndi kuba; pakuti kumene kuli chuma chako, komwe udzakhala mtima wakonso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:20

Popeza anena za Inu moipa, ndi adani anu atchula dzina lanu mwachabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 8:4-6

Tsono kunena za kudya zoperekedwa nsembe kwa mafano, tidziwa kuti fano silili kanthu padziko lapansi, ndi kuti palibe Mulungu koma mmodzi. Pakuti ngakhalenso iliko yoti yonenedwa milungu, kapena m'mwamba, kapena padziko lapansi, monga iliko milungu yambiri, ndi ambuye ambiri; koma kwa ife kuli Mulungu mmodzi, Atate amene zinthu zonse zichokera kwa Iye, ndi ife kufikira kwa Iye; ndi Ambuye mmodzi Yesu Khristu, amene zinthu zonse zili mwa Iye, ndi ife mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:17

Akadapanda kukhala thandizo langa Yehova, moyo wanga ukadakhala kuli chete.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 44:18

Iwo sadziwa, kapena kuzindikira, chifukwa pamaso mwao papakidwa thope, kuti sangaone, ndi m'mitima mwako kuti sangadziwitse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:16

Kodi simudziwa kuti kwa iye amene mudzipereka eni nokha kukhala akapolo ake akumvera iye, mukhalatu akapolo ake a yemweyo mulikumvera iye; kapena a uchimo kulinga kuimfa, kapena a umvero kulinga kuchilungamo?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 4:3

Pakuti nthawi yapitayi idakufikirani kuchita chifuniro cha amitundu, poyendayenda inu m'kukhumba zonyansa, zilakolako, maledzero, madyerero, maimwaimwa, ndi kupembedza mafano kosaloleka;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 5:4

Pakuti Inu sindinu Mulungu wakukondwera nacho choipa mphulupulu siikhala ndi Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 34:17

Usadzipangire milungu yoyenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 32:16-17

Anamchititsa nsanje ndi milungu yachilendo, anautsa mkwiyo wake ndi zonyansa. Anaziphera nsembe ziwanda, si ndizo Mulungu ai; milungu yosadziwa iwo, yatsopano yofuma pafupi, imene makolo anu sanaiope.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 8:10-12

M'mwemo ndinalowa ndi kupenya, ndipo taonani, maonekedwe ali onse a zokwawa, ndi zilombo zonyansa, ndi mafano onse a nyumba ya Israele, zolembedwa pakhoma pozungulira ponse. Ndipo pamaso pao panaima amuna makumi asanu ndi awiri a akulu a nyumba ya Israele, ndi pakati pao panaima Yazaniya mwana wa Safani, munthu aliyense ndi mbale yake ya zofukiza m'dzanja lake; ndi fungo lake la mtambo wa zonunkhira linakwera. Pamenepo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, wapenya kodi chochita akulu a nyumba ya Israele mumdima, aliyense m'chipinda chake cha zifanizo? Pakuti ati, Yehova satipenya, Yehova wataya dziko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 19:26-27

Ndipo muona ndi kumva, kuti si pa Efeso pokha, koma monga pa Asiya ponse, Paulo uyu akopa ndi kutembenutsa anthu ambiri, ndi kuti, Si milungu iyi imene ipangidwa ndi manja: ndipo tiopa ife kuti ntchito yathuyi idzayamba kunyonyosoka; komanso kuti Kachisi wa mulungu wamkazi Aritemi adzayamba kuyesedwa wachabe; ndiponso kuti iye adzayamba kutsitsidwa ku ukulu wake, iye amene a mu Asiya onse, ndi onse a m'dziko lokhalamo anthu, ampembedza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 16:3

Za oyera mtima okhala padziko lapansi, iwo ndiwo omveka mbiri, mwa iwowo muli chikondwero changa chonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 130:4

Koma kwa Inu kuli chikhululukiro, kuti akuopeni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 1:29

Chifukwa adzakhala ndi manyazi, chifukwa cha mitengo yathundu munaikhumba, ndipo inu mudzagwa nkhope, chifukwa cha minda imene mwaisankha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 18:30

Chifukwa chake ndidzakuweruzani inu, nyumba ya Israele, yense monga mwa njira zake, ati Ambuye Yehova. Bwererani, nimutembenukire kuleka zolakwa zanu zonse, ndipo simudzakhumudwa nazo, ndi kuonongeka nayo mphulupulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 146:3-4

Musamakhulupirira zinduna, kapena mwana wa munthu, amene mulibe chipulumutso mwa iye. Mpweya wake uchoka, abwerera kunka kunthaka yake; tsiku lomwelo zotsimikiza mtima zake zitayika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 12:30

Iye wosakhala pamodzi ndi Ine akana Ine, ndi iye wosasonkhanitsa pamodzi ndi Ine amwazamwaza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 6:13

Muziopa Yehova Mulungu wanu; ndi kutumikira Iyeyu; ndipo polumbira muzitchula dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 12:2

Amanena za bodza munthu yense ndi mnansi wake, amanena ndi mlomo wothyasika, ndi mitima iwiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:17

Pakuti thupi lilakalaka potsutsana naye Mzimu, ndi Mzimu potsutsana nalo thupi; pakuti izi sizilingana; kuti zimene muzifuna musazichite.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 34:14

pakuti musalambira mulungu wina; popeza Yehova dzina lake ndiye Wansanje, ali Mulungu wansanje;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:9

Maganizo opusa ndiwo tchimo; wonyoza anyansa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 66:3

Wakupha ng'ombe alingana ndi wakupha munthu; iye wapereka nsembe ya mwanawankhosa alingana ndi wothyola khosi la galu; wothira nsembe yaufa akunga wothira mwazi wa nkhumba; wofukiza lubani akunga wodalitsa fano; inde iwo asankha njira zaozao, ndipo moyo wao ukondwerera m'zonyansa zao;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 14:6

Chifukwa chake uziti kwa nyumba ya Israele, Atero Ambuye Yehova, Bwerani, lekani mafano anu, tembenuzani nkhope zanu kuzisiya zonyansa zanu zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 31:7

Ndidzakondwera ndi kusangalala m'chifundo chanu, pakuti mudapenya zunzo langa; ndipo mudadziwa mzimu wanga mu nsautso yanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:9

Wopewetsa khutu lake kuti asamve chilamulo, ngakhale pemphero lake linyansa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 4:15-16

Potero dzichenjerani nao moyo wanu ndithu; popeza simunapenye mafanidwe konse tsikuli Yehova ananena ndi inu mu Horebu, ali pakati pa moto; kuti mungadziipse, ndi kudzipangira fano losema, lakunga chifaniziro chilichonse, mafanidwe a mwamuna kapena mkazi;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 30:22

Ndipo mudzaipitsa chokuta cha mafano ako, osema asiliva, ndi chomata cha mafano ako osungunula agolide; udzawataya ngati kanthu konyansa, udzati kwa iwo, Chokani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 14:15

nafuula nati, Anthuni, bwanji muchita zimenezi? Ifenso tili anthu a mkhalidwe wathu umodzimodzi ndi wanu, akulalikira kwa inu Uthenga Wabwino, wakuti musiye zinthu zachabe izi, nimutembenukire kwa Mulungu wamoyo, amene analenga zakumwamba ndi zapansi, ndi nyanja, ndi zonse zili momwemo:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:25

amenewo anasandutsa choonadi cha Mulungu chabodza napembedza, natumikira cholengedwa, ndi kusiya Wolengayo, ndiye wolemekezeka nthawi yosatha. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 97:9

Pakuti Inu, Yehova, ndinu Wam'mwambamwamba padziko lonse lapansi, ndinu wokwezeka kwakukulu pamwamba pa milungu ina yonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 41:24

Taonani, inu muli achabe, ndi ntchito yanu yachabe; wonyansa ali iye amene asankha inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 21:11

Pakuti anakupangirani choipa, anapangana chiwembu, osakhoza kuchichita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 6:10

Pakuti muzu wa zoipa zonse ndiwo chikondi cha pa ndalama; chimene ena pochikhumba, anasochera, nataya chikhulupiriro, nadzipyoza ndi zowawa zambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 115:1

Kwa ife ai, Yehova, kwa ife ai, koma kwa dzina lanu patsani ulemerero, chifukwa cha chifundo chanu, ndi choonadi chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 44:2-5

Atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israele: Mwaona choipa chonse chimene ndatengera pa Yerusalemu, ndi pa mizinda yonse ya Yuda; ndipo, taonani, lero lomwe ili bwinja, palibe munthu wokhalamo; Ndipo Yeremiya anati kwa anthu onse, kwa amuna, ndi kwa akazi, kwa anthu onse amene anambwezera mau amenewa, ndi kuti, Zofukizira zanu m'mizinda ya Yuda, ndi m'miseu ya Yerusalemu, za inu ndi atate anu, mafumu anu ndi akulu anu, ndi anthu a m'dziko, kodi Yehova sanazikumbukire, kodi sizinalowe m'mtima mwake? Ndipo Yehova sanathe kupirirabe, chifukwa cha machitidwe anu oipa, ndi chifukwa cha zonyansa zimene munazichita; chifukwa chake dziko lanu likhala bwinja, ndi chizizwitso, ndi chitemberero, lopanda wokhalamo, monga lero lomwe. Chifukwa mwafukiza, ndi chifukwa mwachimwira Yehova, osamvera mau a Yehova, osayenda m'chilamulo chake, ndi m'malemba ake, ndi m'mboni zake, chifukwa chake choipachi chakugwerani, monga lero lomwe. Ndiponso Yeremiya anati kwa anthu onse, ndi kwa akazi onse, Tamvani mau a Yehova, nonse Ayuda amene muli m'dziko la Ejipito. Atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israele, Inu ndi akazi anu mwanena ndi m'kamwa mwanu, ndi kukwaniritsa ndi manja anu kuti, Tidzachita ndithu zowinda zathu taziwindira, kufukizira mfumu yaikazi ya kumwamba, ndi kumthirira iye nsembe zothira; khazikitsanitu zowinda zanu, chitani zowinda zanu. Chifukwa chake tamvani mau a Yehova, nonse Ayuda okhala m'dziko la Ejipito: Taonani, ndalumbira, Pali dzina langa lalikulu, ati Yehova, kuti dzina langa silidzatchulidwanso m'kamwa mwa munthu aliyense wa Yuda m'dziko la Ejipito, ndi kuti, Pali Yehova Mulungu. Taonani, ndiwayang'anira kuwachitira zoipa, si zabwino; ndipo amuna onse a Yuda okhala m'dziko la Ejipito adzathedwa ndi lupanga ndi njala, mpaka kutha kwao. Ndipo iwo amene adzapulumuka kulupanga adzabwera kutuluka kudziko la Ejipito kulowa m'dziko la Yuda, owerengeka; ndipo otsala onse a Yuda, amene analowa m'dziko la Ejipito kuti akhale m'menemo, adzadziwa ngati adzatsimikizidwa mau a yani, kapena anga, kapena ao. Ndipo ichi chidzakhala chizindikiro cha kwa inu, ati Yehova, chakuti Ine ndidzakulangani m'malo muno, kuti mudziwe kuti mau anga adzatsimikizidwatu akuchitireni inu zoipa. chifukwa cha choipa chao anachichita kuutsa nacho mkwiyo wanga; pakuti anapita kukafukizira, ndi kutumikira milungu ina, imene sanaidziwe, ngakhale iwo, ngakhale inu, ngakhale makolo anu. Yehova atero: Taonani, ndidzapereka Farao Hofira mfumu ya Aejipito m'manja a adani ake, ndi m'manja a iwo akufuna moyo wake; monga ndinapereka Zedekiya mfumu ya Yuda m'manja a Nebukadinezara mfumu ya ku Babiloni mdani wake, amene anafuna moyo wake. Koma ndinatuma kwa inu atumiki anga onse aneneri, ndinauka mamawa ndi kuwatuma, ndi kuti, Musachitetu chonyansa ichi ndidana nacho. Koma sanamvere, sanatchere khutu lao kuti atembenuke asiye choipa chao, osafukizira milungu ina.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 8:3

Ndipo anatambasula chonga dzanja, nandigwira tsitsi la pamutu panga; ndipo mzimu unandilengetsa pakati padziko ndi thambo, numuka nane m'masomphenya a Mulungu ku Yerusalemu, ku chitseko cha chipata cha bwalo la m'katimo loloza kumpoto, kumene kunali mpando wa fano la nsanje lochititsa nsanje.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 44:9

Omwe apanga fano losema onsewo asokonezeka; ndipo zokondweretsa zao sadzapindula nazo kanthu; ndipo mboni zao siziona, kapena kudziwa; kuti akhale ndi manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:25

Ilipo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka, koma matsiriziro ake ndi njira za imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mafumu 18:21

Ndipo Eliya anayandikira kwa anthu onse, nati, Mukayikakayika kufikira liti? Ngati Yehova ndiye Mulungu, mtsateni Iye; ngati Baala, mumtsate iyeyo. Ndipo panalibe ndi mmodzi yemwe anamuyankha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 106:20-21

M'mwemo anasintha ulemerero wao ndi fanizo la ng'ombe yakudya msipu. Anaiwala Mulungu Mpulumutsi wao, amene anachita zazikulu mu Ejipito;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:115

Mundichokere ochita zoipa inu; kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 36:2

Pakuti adzidyoletsa yekha m'kuona kwake, kuti anthu sadzachipeza choipa chake ndi kukwiya nacho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:2

Ndipo musafanizidwe ndi makhalidwe a pansi pano: koma mukhale osandulika, mwa kukonzanso kwa mtima wanu, kuti mukazindikire chimene chili chifuniro cha Mulungu, chabwino, ndi chokondweretsa, ndi changwiro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:19-20

Ndinena chiyani tsono? Kuti choperekedwa nsembe kwa mafano chili kanthu? Kapena kuti fano lili kanthu kodi? nabatizidwa onse kwa Mose, mumtambo, ndi m'nyanja, Koma nditi kuti zimene amitundu apereka nsembe azipereka kwa ziwanda osati kwa Mulungu; ndipo sindifuna kuti inu muyanjane ndi ziwanda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 44:15-17

Ndipo udzakhala kuti munthu autenthe; iye natengako, nauotha moto; inde auyatsa, naotcha mkate; inde, apanga mulungu, naulambira, naupanga fano losema, naligwadira. Iye atenthako mbali ina pamoto; ndi mbali yinayo adya nyama; akazinga zokazinga nakhuta, inde, aotha moto, nati, Ha, ndakongonoka, ndauona moto. Ndipo chotsalacho apanga mulungu, ngakhale fano lake losema; iye aligwadira, nalipembedza, nalipemphera nati, Ndipulumutse ine, chifukwa kuti ndinu mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:20-21

kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko, njiru, kuledzera, mchezo, ndi zina zotere; zimene ndikuchenjezani nazo, monga ndachita, kuti iwo akuchitachita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Mulungu woona ndi wokhulupirika, Wamkulukulu! Ndikukutamandani chifukwa ndinu Wolungama, Woyera, ndi Woyenera kutamandidwa ndi kupembedzedwa konse. Atate wakumwamba, m'dzina la Yesu ndikuvomereza kuti ndine wochimwa, ndipo uchimo umandilekanitsa ndi inu. Lero pamaso pa mpando wanu wachifumu ndikutsutsa mphamvu zonse za mdierekezi zomwe zikufuna kundimanga ku mafano ndi zonyansa. Ndikukhulupirira kuti Yesu anafera machimo anga ndipo modzifunira ndikulapa machimo anga onse, ndikukuululani Yesu, Ambuye ndi Mpulumutsi wa moyo wanga. Mulungu wokondedwa, ndikulakalaka ndi mtima wanga wonse kukutumikirani ndi kukukondweretsani, chifukwa ndazindikira kuti ndinu nokha amene muli ndi mphamvu zokhululukira machimo ndi kuchiritsa wolumidwa, pakuti mkhalapakati pakati pa Mulungu ndi anthu ndi Yesu yekha. Ndikukhulupirira ndi mtima wanga wonse kuti Mulungu anamuukitsa kwa akufa ndipo kudzera mu nsembe yake ndamasulidwa ku imfa, chinyengo ndi mabodza a satana. M'dzina la Yesu ndine cholengedwa chatsopano, ndine woyera, watsopano ndipo ndili ndi chigonjetso. M'dzina la Yesu, Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa