Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


103 Mau a m'Baibulo Okhudza Mkwiyo

103 Mau a m'Baibulo Okhudza Mkwiyo

Ndikufuna ndikuuzeni nkhani ya mkwiyo. Mkwiyo ndi chida cha mdani wathu kuti atichititse tichinjirize Mulungu. Tikalola mkwiyo kutilamulire, sitidzathawa mavuto ake. Ngakhale Mulungu wakwiya kale ndi anthu, nthawi zonse amatipatsa mwayi woti tiyanjane naye.

Mkwiyo umatibweretsera mavuto ambiri, osati kungotaya madalitso a Mulungu okha, koma umatibweretseranso chisoni chamumtima. Kaya tikwiya pa zifukwa zomveka kapena ayi, lemba la Efeso 4:26-27 limatiuza kuti, “Kwiyani, koma musachimwe; dzuwa lisalowe muli chikwiyo, ndipo musampatse mmalo Mdyerekezi.”

N’zomveka kukwiya ngati tawona zosalungama kapena zamwano zokhudza Mulungu, koma Ambuye amatiuza mu Aroma 12 kuti, “Kubwezera ndi kwanga; Ine ndidzabwezera.”

Kukhala paubwenzi ndi Mzimu Woyera n’kofunika kwambiri kuti tizitha kulamulira maganizo athu. Tiyeni tipemphe Mzimu Woyera kuti zipatso zake zilamule mitima yathu, kutilimbitsa mkati mwathu.




Masalimo 37:8

Leka kupsa mtima, nutaye mkwiyo; usavutike mtima ungachite choipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:19

Mudziwa, abale anga okondedwa, kuti munthu aliyense akhale wotchera khutu, wodekha polankhula, wodekha pakupsa mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:26

Kwiyani, koma musachimwe; dzuwa lisalowe muli chikwiyire,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:32

Wosakwiya msanga aposa wamphamvu; wolamulira mtima wake naposa wolanda mzinda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:8

Koma tsopano tayani inunso zonsezi: mkwiyo, kupsa mtima, dumbo, mwano, zonyansa zotuluka m'kamwa mwanu:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:9

Usakangaze mumtima mwako kukwiya; pakuti mkwiyo ugona m'chifuwa cha zitsiru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:8

Yehova ndiye wachisomo, ndi wachifundo; osakwiya msanga, ndi wa chifundo chachikulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:18

Munthu wozaza aputa makani; koma wosakwiya msanga atonthoza makangano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:1

Mayankhidwe ofatsa abweza mkwiyo; koma mau owawitsa aputa msunamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 4:6-7

Ndipo Yehova anati kwa Kaini, Ukwiyiranji? Yagweranji nkhope yako? Ukachita zabwino, sudzalandiridwa kodi? Ukaleka kuchita zabwino, uchimo ubwatama pakhomo: kwa iwe kudzakhala kulakalaka kwake, ndipo iwe udzamlamulira iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:24

Usayanjane ndi munthu wokwiya msanga; ngakhale kupita ndi mwamuna waukali;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:19

Musabwezere choipa, okondedwa, koma patukani pamkwiyo; pakuti kwalembedwa, Kubwezera kuli kwanga, Ine ndidzabwezera, ati Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 34:6

Ndipo Yehova anapita pamaso pake, nafuula, Yehova, Yehova, Mulungu wachifundo ndi wachisomo, wolekereza, ndi wa ukoma mtima wochuluka, ndi wachoonadi;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:11

Kulingalira kwa munthu kuchedwetsa mkwiyo; ulemerero wake uli wakuti akhululukire cholakwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:11

Chitsiru chivumbulutsa mkwiyo wake wonse; koma wanzeru auletsa nautontholetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:31

Chiwawo chonse, ndi kupsa mtima, ndi mkwiyo, ndi chiwawa, ndi mwano zichotsedwe kwa inu, ndiponso choipa chonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:22

koma Ine ndinena kwa inu, kuti yense wokwiyira mbale wake wopanda chifukwa adzakhala wopalamula mlandu; ndipo amene adzanena ndi mbale wake, Wopanda pake iwe, adzakhala wopalamula mlandu wa akulu: koma amene adzati, Chitsiru iwe: adzakhala wopalamula Gehena wamoto.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 7:11

Mulungu ndiye Woweruza wolungama, ndiye Mulungu wakukwiya masiku onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 14:18

Yehova ndiye wolekereza, ndi wa chifundo chochuluka, wokhululukira mphulupulu ndi kulakwa, koma wosamasula wopalamula; wakuwalanga ana chifukwa cha mphulupulu ya atate ao, kufikira mbadwo wachitatu ndi wachinai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 9:8

Mu Horebu momwe munautsa mkwiyo wa Yehova; ndipo Yehova anakwiya nanu kukuonongani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 32:35

Kubwezera chilango nkwanga, kubwezera komwe, pa nyengo ya kuterereka phazi lao; pakuti tsiku la tsoka lao layandika, ndi zinthu zowakonzeratu zifulumira kudza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 32:41

ndikanola lupanga langa lonyezimira, ndi dzanja langa likagwira chiweruzo; ndidzabwezera chilango ondiukira, ndi kulanga ondida.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 78:38

Koma Iye pokhala ngwa chifundo, anakhululukira choipa, osawaononga; nabweza mkwiyo wake kawirikawiri, sanautse ukali wake wonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 85:3

Munabweza kuzaza kwanu konse; munabwerera kumkwiyo wanu wotentha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 103:8

Yehova ndiye wa nsoni zokoma ndi wachisomo, wosakwiya msanga, ndi wa chifundo chochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:29

Wosakwiya msanga apambana kumvetsa; koma wansontho akuza utsiru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:19

Munthu waukali alipire mwini; pakuti ukampulumutsa udzateronso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:3

Kuli ulemu kwa mwamuna kupewa ndeu; koma zitsiru zonse zimangokangana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:19

Kukhala m'chipululu kufunika kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wong'ung'udza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:24-25

Usayanjane ndi munthu wokwiya msanga; ngakhale kupita ndi mwamuna waukali; kuti ungaphunzire mayendedwe ake, ndi kutengera moyo wako msampha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:4

Kupweteka mtima nkwa nkhanza, mkwiyo usefuka; koma ndani angalakike ndi nsanje?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:22

Mwamuna wamkwiyo aputa makangano; waukali achuluka zolakwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 13:13

Chifukwa chake ndidzanthunthumiritsa miyamba, ndipo dziko lapansi lidzagwedezeka kuchokera m'malo ake, m'mkwiyo wa Yehova wa makamu, tsiku la mkwiyo wake waukali.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 34:2

Pakuti Yehova akwiyira amitundu onse, nachitira ukali khamu lao lonse; Iye wawaononga psiti, wawapereka kukaphedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 48:9

Chifukwa cha dzina langa ndidzachedwetsa mkwiyo wanga, ndi chifukwa cha kutamanda kwanga ndidzakulekerera, kuti ndisakuchotse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 54:8

M'kukwiya kwa kusefukira ndinakubisira nkhope yanga kamphindi; koma ndi kukoma mtima kwa chikhalire ndidzakuchitira chifundo, ati Yehova Mombolo wako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 57:16

Pakuti sindidzatsutsana kunthawi zonse, sindidzakwiya masiku onse; pakuti mzimu udzalefuka pamaso pa Ine, ndi miyoyo imene ndinailenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 63:3

Ndaponda ndekha mopondera mphesa, ndipo panalibe nane mmodzi wa mitundu ya anthu; inde ndinawaponda m'kukwiya kwanga, ndi kuwapondereza mu ukali wanga; ndi mwazi wa moyo wao unawazidwa pa zovala zanga; ndipo ndadetsa chofunda changa chonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 3:12

Pita; nulalikire mau awa kuyang'ana kumpoto, ndi kuti, Bwera iwe Israele wobwerera, ati Yehova; sindidzakuyang'anira iwe ndi kukwiya; pakuti Ine ndili wachifundo, ati Yehova, sindidzakhala nako kukwiya kunthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 10:24

Yehova, mundilangize, koma ndi chiweruzo; si m'mkwiyo wanu, mungandithe psiti.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 30:24

Mkwiyo waukali wa Yehova sudzabwerera, mpaka wachita, mpaka watha zomwe afuna kuchita m'mtima mwake: masiku akumaliza mudzachizindikira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 51:45

Anthu anga, tulukani pakati pake, mudzipulumutse munthu yense ku mkwiyo waukali wa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Maliro 3:66

mudzawalondola mokwiya ndi kuwaononga pansi pa thambo la Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 7:8

Katsala kamphindi, ndipo ndidzakutsanulira ukali wanga, ndi kukukwaniritsira mkwiyo wanga, ndi kukuweruza monga mwa njira zako, ndipo ndidzakubwezera zonyansa zako zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 16:42

M'mwemo ukali wanga udzakhuta nawe, ndi nsanje yanga idzakuchokera, ndipo ndidzakhala chete wosakwiyanso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 25:17

Ndipo ndidzawabwezera chilango chachikulu, ndi malango ankharwe; motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pakuwabwezera chilango Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 38:18-19

Ndipo kudzachitika tsiku ilo, tsiku loti Gogi adzadza kulimbana ndi dziko la Israele, ati Ambuye Yehova, ukali wanga udzakwera m'mphuno mwanga. Pakuti ndanena mu nsanje yanga, ndi m'moto wa kuzaza kwanga, Zoonadi tsiku ilo kudzakhala kugwedezeka kwakukulu m'dziko la Israele;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Hoseya 11:9

Sindidzachita mkwiyo wanga waukali, sindidzabwerera kuononga Efuremu; pakuti Ine ndine Mulungu, si munthu ai; Woyera wa pakati pako; ndipo sindidzalowa m'mzinda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yoweli 2:13

ndipo ng'ambani mitima yanu, si zovala zanu ai; ndi kutembenukira kwa Yehova Mulungu wanu; pakuti Iye ndiye wachisomo, ndi wodzala chifundo, wosapsa mtima msanga, ndi wochuluka kukoma mtima, ndi woleka choipacho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yona 4:2

Ndipo anapemphera kwa Yehova, nati, Ha, Yehova! Si ndiwo mau anga ndikali m'dziko langa? Chifukwa chake ndinafulumira kuthawira ku Tarisisi, pakuti ndinadziwa kuti Inu ndinu Mulungu wachisomo ndi wodzala chifundo, wolekerera ndi wokoma mtima mochuluka, ndi woleka choipacho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nahumu 1:2-3

Yehova ndiye Mulungu wansanje, nabwezera chilango; Yehova ndiye wobwezera chilango, ndi waukali ndithu; Yehova ndiye wobwezera chilango oyambana naye, nasungira mkwiyo pa adani ake. Yehova ndiye wolekerera mkwiyo, koma wa mphamvu yaikulu; ndi wosamasula ndithu wopalamula; njira ya Yehova ili m'kamvulumvulu ndi mumkuntho; ndipo mitambo ndiyo fumbi la mapazi ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zefaniya 2:3

Funani Yehova, ofatsa inu nonse a m'dziko, amene munachita chiweruzo chake; funani chilungamo, funani chifatso; kapena mudzabisika tsiku la mkwiyo wa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zefaniya 3:8

Chifukwa chake, mundilindire, ati Yehova, kufikira tsiku loukira Ine zofunkha; pakuti ndatsimikiza mtima Ine kusonkhanitsa amitundu, kuti ndimemeze maufumu kuwatsanulira kulunda kwanga, ndilo mkwiyo wanga wonse waukali; pakuti dziko lonse lapansi lidzathedwa ndi moto wa nsanje yanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 1:15

Ndipo ndikwiya nao amitundu okhala osatekeseka ndi mkwiyo waukulu; pakuti ndinakwiya pang'ono, ndipo anathandizira choipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:44

koma Ine ndinena kwa inu, Kondanani nao adani anu, ndi kupempherera iwo akuzunza inu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 21:12-13

Ndipo Yesu analowa ku Kachisi wa Mulungu natulutsira kunja onse akugulitsa ndi kugula malonda, nagubuduza magome a osintha ndalama, ndi mipando ya ogulitsa nkhunda; nanena kwa iwo, Chalembedwa, Nyumba yanga idzanenedwa nyumba yakupemphera; koma inu mwaiyesa phanga la achifwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 23:33

Njoka inu, obadwa inu a mamba, mudzatha bwanji kuthawa kulanga kwake kwa Gehena?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 3:5

Ndipo m'mene anawaunguza ndi mkwiyo, ndi kumva chisoni chifukwa cha kuuma kwa mitima yao, ananena kwa munthuyo, Tambasula dzanja lako. Ndipo analitambasula; ndipo linachira dzanja lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 6:28-29

dalitsani iwo akutemberera inu, pemphererani iwo akuchitira inu chipongwe. Iye amene akupanda iwe pa tsaya limodzi umpatsenso linzake; ndi iye amene alanda chofunda chako, usamkanize malaya ako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 9:54-55

Ndipo pamene ophunzira ake Yakobo ndi Yohane anaona, anati, Ambuye, Kodi mufuna kuti ife tiuze moto utsike kumwamba ndi kuwanyeketsa iwo? Koma Iye anapotoloka nawadzudzula.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 2:15-16

Ndipo pamene adapanga mkwapulo wazingwe, anatulutsa onse mu Kachisimo, ndi nkhosa ndi ng'ombe; nakhuthula ndalama za osinthanawo, nagubuduza magome; nati kwa iwo akugulitsa nkhunda, Chotsani izi muno; musamayesa nyumba ya Atate wanga nyumba ya malonda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:18

Pakuti mkwiyo wa Mulungu, wochokera Kumwamba, uonekera pa chisapembedzo chonse ndi chosalungama cha anthu, amene akanikiza pansi choonadi m'chosalungama chao;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 2:5

Koma kolingana ndi kuuma kwako, ndi mtima wako wosalapa, ulikudziunjikira wekha mkwiyo pa tsiku la mkwiyo ndi la kuvumbulutsa kuweruza kolungama kwa Mulungu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:9

Ndipo tsono popeza tinayesedwa olungama ndi mwazi wake, makamaka ndithu tidzapulumuka mkwiyo wa Mulungu mwa Iyeyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:21

Musagonje kwa choipa, koma ndi chabwino gonjetsani choipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 13:4

pakuti ndiye mtumiki wa Mulungu, kuchitira iwe zabwino. Koma ngati uchita choipa, opatu, pakuti iye sagwira lupanga kwachabe; pakuti ndiye mtumiki wa Mulungu wakukwiyira ndi kubwezera chilango wochita zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 13:5

sichichita zosayenera, sichitsata za mwini yekha, sichipsa mtima, sichilingirira zoipa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 12:20

Pakuti ndiopa, kuti kaya, pakudza ine, sindidzakupezani inu otere onga ndifuna, ndipo ine ndidzapezedwa ndi inu wotere wonga simufuna; kuti kaya pangakhale chotetana, kaduka, mikwiyo, zilekanitso, maugogodi, ukazitape, zodzikuza, mapokoso;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:19-21

Ndipo ntchito za thupi zionekera, ndizo dama, chodetsa, kukhumba zonyansa, Taonani, ine Paulo ndinena ndi inu, kuti, ngati mulola akuduleni, Khristu simudzapindula naye kanthu. kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko, njiru, kuledzera, mchezo, ndi zina zotere; zimene ndikuchenjezani nazo, monga ndachita, kuti iwo akuchitachita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:6

Asakunyengeni inu munthu ndi mau opanda pake, pakuti chifukwa cha izi umadza mkwiyo wa Mulungu pa ana a kusamvera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:6-8

chifukwa cha izi zomwe ukudza mkwiyo wa Mulungu pa ana a kusamvera; zimene munayendamo inunso kale, pamene munakhala ndi moyo wanu m'menemo. Koma tsopano tayani inunso zonsezi: mkwiyo, kupsa mtima, dumbo, mwano, zonyansa zotuluka m'kamwa mwanu:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 5:9

Pakuti Mulungu sanatiike ife tilawe mkwiyo, komatu kuti tilandire chipulumutso mwa Ambuye wathu Yesu Khristu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 2:8

Chifukwa chake ndifuna kuti amunawo apemphere pamalo ponse, ndi kukweza manja oyera, opanda mkwiyo ndi makani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 2:24

Ndipo kapolo wa Ambuye sayenera kuchita ndeu, komatu akhale woyenera, waulere pa onse, wodziwa kuphunzitsa, woleza,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Tito 1:7

Pakuti woyang'anira ayenera kukhala wopanda chilema, ngati mdindo wa Mulungu; wosati waliuma, wosapsa mtima msanga, wosati wachiwawa, wopanda ndeu, wosati wa chisiriro chonyansa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 3:10-11

Momwemo ndinakwiya nao mbadwo uwu, ndipo ndinati, Nthawi zonse amasochera mumtima; koma sanazindikire njira zanga iwowa; Monga ndinalumbira mu ukali wanga: Ngati adzalowa mpumulo wanga!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 4:7

alangizanso tsiku lina, ndi kunena mu Davide, itapita nthawi yaikulu yakuti, Lero, monga kwanenedwa kale, Lero ngati mudzamva mau ake, musaumitse mitima yanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:30-31

pakuti timdziwa Iye amene anati, Kubwezera chilango nkwanga, Ine ndidzabwezera. Ndiponso, Ambuye adzaweruza anthu ake. Kugwa m'manja a Mulungu wamoyo nkoopsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 12:29

Pakuti Mulungu wathu ndiye moto wonyeketsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:19-20

Mudziwa, abale anga okondedwa, kuti munthu aliyense akhale wotchera khutu, wodekha polankhula, wodekha pakupsa mtima. Muchiyese chimwemwe chokha, abale anga, m'mene mukugwa m'mayesero a mitundumitundu; Pakuti mkwiyo wa munthu suchita chilungamo cha Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:1-2

Zichokera kuti nkhondo, zichokera kuti zolimbana mwa inu? Kodi sizichokera kuzikhumbitso zanu zochita nkhondo m'ziwalo zanu? Dzichepetseni pamaso pa Ambuye, ndipo adzakukwezani. Musamanenerana, abale. Wonenera mbale, kapena woweruza mbale wake, anenera lamulo, naweruza lamulo: koma ngati uweruza lamulo, suli wochita lamulo, komatu woweruza. Woika lamulo ndi woweruza ndiye mmodzi, ndiye amene akhoza kupulumutsa ndi kuononga; koma iwe woweruza mnzako ndiwe yani? Nanga tsono, inu akunena, Lero kapena mawa tidzapita kulowa kumudzi wakutiwakuti, ndipo tidzagonerako ndi kutsatsa malonda, ndi kupindula nao; inu amene simudziwa chimene chidzagwa mawa. Moyo wanu uli wotani? Pakuti muli utsi, wakuonekera kanthawi, ndi pamenepo ukanganuka. Mukadanena inu, Akalola Ambuye, ndipo tikakhala ndi moyo, tidzachita kakutikakuti. Koma tsopano mudzitamandira m'kudzikuza kwanu; kudzitamandira kulikonse kotero nkoipa. Potero kwa iye amene adziwa kuchita bwino, ndipo sachita, kwa iye kuli tchimo. Mulakalaka, ndipo zikusowani; mukupha, nimuchita kaduka, ndipo simungathe kupeza; mulimbana, nimuchita nkhondo; mulibe kanthu, chifukwa simupempha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:1

Momwemo pakutaya choipa chonse, ndi chinyengo chonse, ndi maonekedwe onyenga, ndi kaduka, ndi masinjiriro onse,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:23

amene pochitidwa chipongwe sanabwezere chipongwe, pakumva zowawa, sanaopse, koma anapereka mlandu kwa Iye woweruza kolungama;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 3:9

osabwezera choipa ndi choipa, kapena chipongwe ndi chipongwe, koma penatu madalitso; pakuti kudzatsata ichi mwaitanidwa, kuti mukalandire dalitso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 4:8

koposa zonse mukhale nacho chikondano chenicheni mwa inu nokha; pakuti chikondano chikwiriritsa unyinji wa machimo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:8

Khalani odzisungira, dikirani; mdani wanu mdierekezi, monga mkango wobuma, ayendayenda ndi kufunafuna wina akamlikwire:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Petro 2:9

Ambuye adziwa kupulumutsa opembedza poyesedwa iwo, ndi kusunga osalungama kufikira tsiku loweruza akalangidwe;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Petro 3:9

Ambuye sazengereza nalo lonjezano, monga ena achiyesa chizengerezo; komatu aleza mtima kwa inu, wosafuna kuti ena aonongeke, koma kuti onse afike kukulapa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:15

Yense wakudana ndi mbale wake ali wakupha munthu; ndipo mudziwa kuti wakupha munthu aliyense alibe moyo wosatha wakukhala mwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 4:18

Mulibe mantha m'chikondi; koma chikondi changwiro chitaya kunja mantha, popeza mantha ali nacho chilango, ndipo wamanthayo sakhala wangwiro m'chikondi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:16

Wina akaona mbale wake alikuchimwa tchimo losati la kuimfa, apemphere Mulungu, ndipo Iye adzampatsira moyo wa iwo akuchita machimo osati a kuimfa. Pali tchimo la kuimfa: za ililo sindinena kuti mupemphere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 6:16-17

nanena kwa mapiri ndi matanthwe, Igwani pa ife, ndipo tibiseni ife kunkhope ya Iye amene akhala pa mpando wachifumu, ndi kumkwiyo wa Mwanawankhosa; chifukwa lafika tsiku lalikulu la mkwiyo wao, ndipo akhoza kuima ndani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 11:18

Ndipo amitundu anakwiya, ndipo unadza mkwiyo wanu, ndi nthawi ya akufa yakuti aweruzidwe, ndi yakupereka mphotho akapolo anu aneneriwo, ndi oyera mtima, ndi iwo akuopa dzina lanu, ang'ono ndi akulu; ndi kuononga iwo akuononga dziko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 14:10

iyenso adzamwako kuvinyo wa mkwiyo wa Mulungu, wokonzeka wosasakaniza m'chikho cha mkwiyo wake; ndipo adzazunzika ndi moto ndi sulufure pamaso pa angelo oyera mtima ndi pamaso pa Mwanawankhosa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 14:19

Ndipo mngelo anaponya chisenga chake kudziko nadula mphesa za m'munda wa m'dziko, naziponya moponderamo mphesa mwamukulu mwa mkwiyo wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 15:1

Ndipo ndinaona chizindikiro china m'mwamba, chachikulu ndi chozizwitsa, angelo asanu ndi awiri akukhala nayo miliri isanu ndi iwiri, ndiyo yotsiriza, kuti mwa iyo watsirizika mkwiyo wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 15:7

Ndipo chimodzi cha zamoyo zinai chinapatsa angelo asanu ndi awiri mbale zisanu ndi ziwiri zagolide zodzala ndi mkwiyo wa Mulungu wakukhala ndi moyo ku nthawi za nthawi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 16:1

Ndipo ndinamva mau aakulu ochokera ku Kachisi, akunena kwa angelo asanu ndi awiri, Mukani, ndipo tsanulirani kudziko mbale zisanu ndi ziwiri za mkwiyo wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 16:19

Ndipo chimzinda chachikulucho chidagawika patatu, ndi mizinda ya amitundu inagwa; ndipo Babiloni waukulu unakumbukika pamaso pa Mulungu, kuti aupatse chikho cha vinyo waukali wa mkwiyo wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 19:15

Ndipo m'kamwa mwake mutuluka lupanga lakuthwa, kuti akanthe nalo mitundu ya anthu; ndipo Iye adzawalamulira ndi ndodo yachitsulo: ndipo aponda Iye moponderamo mphesa mwa vinyo waukali wa mkwiyo wa Mulungu Wamphamvuyonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 20:15

Ndipo ngati munthu sanapezedwe wolembedwa m'buku la moyo, anaponyedwa m'nyanja yamoto.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 21:8

Koma amantha, ndi osakhulupirira, ndi onyansa, ndi ambanda, ndi achigololo, ndi olambira mafano, ndi onse a mabodza, cholandira chao chidzakhala m'nyanja yotentha ndi moto ndi sulufure; ndiyo imfa yachiwiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 22:12

Taonani, ndidza msanga; ndipo mphotho yanga ndili nayo yakupatsa yense monga mwa ntchito yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Mulungu Wamphamvuyonse, ulemerero ndi ulemu zikhale zanu! Mulungu wanga wakumwamba, ndikubwerera kwa Inu chifukwa ndikudziwa kuti ndikufunika kukhalapo kwanu kulamulira moyo wanga kuti mtima wanga udzazidwe ndi kubwezeretsedwa ndi kumasulidwa. M'dzina la Yesu, ndikupemphani kuti mundithandize kuganiza ndi kuzindikira mwanzeru zinthu, osachita zinthu mopupuluma ndi mosasamala, koma kudzera mu mpanda wa Mzimu Woyera wanu ndiphunzire kulamulira maganizo ndi malingaliro anga. Mundidziwitse tanthauzo la mawu anu akuti: "Mayankho ofatsa amathetsa mkwiyo; koma mawu okalipa amayatsa ukali." Ndikudziwa kuti ndawaletsa anthu ondizungulira powamenya ndi mawu anga, ndikuwapweteka, ndipo zotsatira zake ndikuwononga moyo wanga ndi wa banja langa. Ndidziwitseni kuyenda mogwirizana ndi zomwe zili m'mawu mwanu kuti kukhalapo kwanu kukhale patsogolo pa chilichonse. Ndithandizeni kudikira ndi kutseka mipata yonse ya mdani, mundidziwitse kuti mkwiyo umangondipangitsa kukhala ndi khoma lolekanitsa ndi anthu ondizungulira komanso kufesa mkwiyo, ukali ndi chisoni. Ndikutsutsa mkwiyo, ukali ndi kupsa mtima. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa