Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




1 Yohane 3:13 - Buku Lopatulika

13 Musazizwe, abale, likadana nanu dziko lapansi.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

13 Musazizwe, abale, likadana nanu dziko lapansi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

13 Motero musadabwe abale, anthu odalira zapansipano akamadana nanu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

13 Abale anga, musadabwe ngati dziko lapansi lidana nanu.

Onani mutuwo Koperani




1 Yohane 3:13
18 Mawu Ofanana  

Munthu woipa anyansa olungama; ndipo woongoka m'njira anyansa wochimwa.


Ukaona anthu alikutsendereza aumphawi, ndi kuchotsa chilungamo ndi chiweruzo mwachiwawa pa dera lina la dziko, usazizwepo; pakuti mkulu wopambana asamalira; ndipo alipo akulu ena oposa amenewo.


Ndipo adzada inu anthu onse chifukwa cha dzina langa; koma iye wakupirira kufikira chimaliziro, iyeyu adzapulumutsidwa.


Pamenepo adzakuperekani kunsautso, nadzakuphani; ndipo anthu a mitundu yonse adzadana nanu, chifukwa cha dzina langa.


Ndipo adzada inu anthu onse chifukwa cha dzina langa: koma iye wakupirira kufikira chimaliziro, yemweyo adzapulumutsidwa.


Ndipo anthu onse adzadana ndi inu chifukwa cha dzina langa.


Odala inu, pamene anthu adzada inu, nadzapatula inu, nadzatonza inu, nadzalitaya dzina lanu monga loipa, chifukwa cha Mwana wa Munthu.


Adzakutulutsani m'masunagoge, koma ikudza nthawi imene yense wakupha inu adzayesa kuti atumikira Mulungu.


Zinthu izi ndalankhula ndi inu, kuti mwa Ine mukakhale nao mtendere. M'dziko lapansi mudzakhala nacho chivuto, koma limbikani mtima; ndalingonjetsa dziko lapansi Ine.


Ine ndawapatsa iwo mau anu; ndipo dziko lapansi, linadana nao, chifukwa sakhala a dziko lapansi, monga Ine sindikhala wa dziko lapansi.


Usadabwe chifukwa ndinati kwa iwe, Uyenera kubadwa mwatsopano.


Dziko lapansi silingathe kudana ndi inu; koma Ine lindida popeza Ine ndilichitira umboni, kuti ntchito zake zili zoipa.


Koma m'mene Petro anachiona, anayankha kwa anthu, Amuna inu a Israele, muzizwa naye bwanji ameneyo? Kapena mutipenyetsetsa ife bwanji, monga ngati tamyendetsa iye ndi mphamvu ya ife eni, kapena ndi chipembedzo chathu?


Chifukwa chisamaliro cha thupi chidana ndi Mulungu; pakuti sichigonja ku chilamulo cha Mulungu, pakuti sichikhoza kutero.


Ndipo onse akufuna kukhala opembedza m'moyo mwa Khristu Yesu, adzamva mazunzo.


Akazi achigololo inu, kodi simudziwa kuti ubwenzi wa dziko lapansi uli udani ndi Mulungu? Potero, iye amene afuna kukhala bwenzi la dziko lapansi adziika mdani wa Mulungu.


Ndipo mngelo anati kwa ine, Uzizwa chifukwa ninji? Ine ndidzakuuza iwe chinsinsi cha mkazi, ndi cha chilombo chakumbereka iye, chokhala nayo mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa