Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 26 - Buku Lopatulika


Davide popempha Mulungu amweruze, atchula zokoma zake
Salimo la Davide.

1 Mundiweruze, Yehova, pakuti ndayenda mu ungwiro wanga, ndipo ndakhulupirira Yehova, sindadzaterereka.

2 Mundiyesere, Yehova, ndipo mundisunthe; yeretsani impso zanga ndi mtima wanga.

3 Pakuti chifundo chanu chili pamaso panga; ndipo ndayenda m'choona chanu.

4 Sindinakhala pansi ndi anthu achabe; kapena kutsagana nao anthu othyasika.

5 Ndidana nao msonkhano wa ochimwa, ndipo sindidzakhala nao pansi ochita zoipa.

6 Ndidzasamba manja anga mosalakwa; kuti ndizungulire guwa la nsembe lanu, Yehova;

7 kuti ndimveketse mau a chiyamiko, ndi kulalikira ntchito zanu zonse zozizwa.

8 Yehova, ndikonda chikhalidwe cha nyumba yanu, ndi malo akukhalamo ulemerero wanu.

9 Musandichotsere mzimu wanga pamodzi ndi olakwa, kapena moyo wanga pamodzi ndi anthu okhetsa mwazi;

10 amene m'manja mwao muli mphulupulu, ndi dzanja lao lamanja ladzala ndi zokometsera mlandu.

11 Koma ine, ndidzayenda mu ungwiro wanga; mundiombole, ndipo ndichitireni chifundo.

12 Phazi langa liponda pachidikha, m'misonkhano ndidzalemekeza Yehova.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa