Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 26:1 - Buku Lopatulika

1 Mundiweruze, Yehova, pakuti ndayenda mu ungwiro wanga, ndipo ndakhulupirira Yehova, sindadzaterereka.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

1 Mundiweruze, Yehova, pakuti ndayenda m'ungwiro wanga, ndipo ndakhulupirira Yehova, sindadzaterereka.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

1 Inu Chauta, onetsani kuti ine ndine wosalakwa, pakuti ndimachita zolungama, ndipo ndakhulupirira Inu mosakayika konse.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Weruzeni Inu Yehova pakuti ndakhala moyo wosalakwa. Ndadalira Yehova popanda kugwedezeka.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 26:1
30 Mawu Ofanana  

Mukumbukire Yehova kuti ndinayendabe pamaso panu m'choonadi, ndi mtima wangwiro, ndi kuchita zokoma m'kuona kwanu. Nalira Hezekiya kulira kwakukulu.


Ndipo Yehova anati kwa Satana, Kodi waonerera mtumiki wanga Yobu? Pakuti palibe wina wonga iye m'dzikomo, munthu wangwiro ndi woongoka, wakuopa Mulungu, ndi kupewa zoipa; naumirirabe kukhala wangwiro, chinkana undisonkhezera ndimuononge kopanda chifukwa.


Kodi kulimbika mtima kwako si ndiko kuti uopa Mulungu, ndi chiyembekezo chako si ndiwo ungwiro wa njira zako?


Sadzalola phazi lako literereke: Iye amene akusunga sadzaodzera.


Iye wakuyendayo mokwanira, nachita chilungamo, nanena zoonadi mumtima mwake.


Pakuti mfumu akhulupirira Yehova, ndipo mwa chifundo cha Wam'mwambamwamba sadzagwedezeka iye.


Mulungu wanga, ndakhulupirira Inu, ndisachite manyazi; adani anga asandiseke ine.


Ungwiro ndi kuongoka mtima zindisunge, pakuti ndayembekezera Inu.


Koma ine, ndidzayenda mu ungwiro wanga; mundiombole, ndipo ndichitireni chifundo.


Yehova ndiye mphamvu yanga, ndi chikopa changa; mtima wanga wakhulupirira Iye, ndipo anandithandiza, chifukwa chake mtima wanga ukondwera kwakukulu; ndipo ndidzamyamika nayo nyimbo yanga.


Koma ine ndakhulupirira Inu, Yehova, ndinati, Inu ndinu Mulungu wanga.


Mundiweruze monga mwa chilungamo chanu, Yehova Mulungu wanga; ndipo asandisekerere ine.


Malamulo a Mulungu wake ali mumtima mwake; pakuyenda pake sadzaterereka.


Iphani nsembe za chilungamo, ndipo mumkhulupirire Yehova.


Mundiweruzire, Mulungu, ndipo mundinenere mlandu kwa anthu opanda chifundo. Mundilanditse kwa munthu wonyenga ndi wosalungama.


Ndipulumutseni, Mulungu, mwa dzina lanu, ndipo mundiweruze ndi mphamvu yanu.


Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; msanje wanga, sindidzagwedezeka kwakukulu.


Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa, msanje wanga, sindidzagwedezeka.


Yehova aweruza anthu mlandu; mundiweruze, Yehova, monga mwa chilungamo changa, ndi ungwiro wanga uli mwa ine.


Pamene ndinati, Literereka phazi langa, chifundo chanu, Yehova, chinandichirikiza.


Wolungama woyenda mwangwiro, anake adala pambuyo pake.


Kuopa anthu kutchera msampha; koma wokhulupirira Yehova adzapulumuka.


Pakuti kudzitamandira kwathu ndiko umboni wa chikumbumtima chathu, kuti m'chiyero ndi kuona mtima kwa Mulungu, si m'nzeru ya thupi, koma m'chisomo cha Mulungu tinadzisunga m'dziko lapansi, koma koposa kwa inu.


tigwiritse chivomerezo chosagwedera cha chiyembekezo chathu, pakuti wolonjezayo ali wokhulupirika;


amene musungidwa ndi mphamvu ya Mulungu mwa chikhulupiriro, kufikira chipulumutso chokonzeka kukavumbulutsidwa nthawi yotsiriza.


Momwemo abale, onjezani kuchita changu kukhazikitsa maitanidwe ndi masankhulidwe anu; pakuti mukachita izi, simudzakhumudwa nthawi zonse;


Adzasunga mapazi a okondedwa ake, koma oipawo adzawakhalitsa chete mumdima; pakuti palibe munthu adzapambana ndi mphamvu.


Chifukwa chake Yehova akhale woweruza, naweruze pakati pa ine ndi inu, nayang'anire, nandigwirire moyo, nandipulumutse m'dzanja lanu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa