Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 5:5 - Buku Lopatulika

5 Opusa sadzakhazikika pamaso panu, mudana nao onse akuchita zopanda pake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

5 Opusa sadzakhazikika pamaso panu, mudana nao onse akuchita zopanda pake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

5 Anthu onyada sangathe kuwonekera pamaso panu. Inu mumadana ndi anthu onse ochita zoipa.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

5 Onyada sangathe kuyima pamaso panu; Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 5:5
21 Mawu Ofanana  

Chifukwa chake oipa sadzaimirira pa mlanduwo, kapena ochimwa mu msonkhano wa olungama.


Pakuti woipa adzitamira chifuniro cha moyo wake, adalitsa wosirira, koma anyoza Yehova.


Yehova ayesa wolungama mtima, koma moyo wake umuda woipa ndi iye wakukonda chiwawa.


Mukasunga mphulupulu, Yehova, adzakhala chilili ndani, Ambuye?


Wauchitsiru amati mumtima mwake, Kulibe Mulungu. Achita zovunda, achita ntchito zonyansa; kulibe wakuchita bwino.


Pakuti ndinachitira nsanje odzitamandira, pakuona mtendere wa oipa.


Ndinati kwa odzitamandira, musamachita zodzitamandira; ndi kwa oipa, Musamakweza nyanga;


Munthu wopulukira sachidziwa; ndi munthu wopusa sachizindikira ichi;


Zindikirani, opulukira inu mwa anthu; ndipo opusa inu, mudzachita mwanzeru liti?


Kodi mudzakonda zazibwana kufikira liti, achibwana inu? Onyoza ndi kukonda kunyoza, opusa ndi kuda nzeru?


Kuopa Yehova ndiko chiyambi cha kudziwa; opusa anyoza nzeru ndi mwambo.


Njira ya oipa inyansa Yehova; koma akonda wolondola chilungamo.


Achibwana inu, chenjerani, opusa inu, khalani ndi mtima wozindikira;


Utawinda chiwindo kwa Mulungu, usachedwe kuchichita; pakuti sakondwera ndi zitsiru; chita chomwe unachiwindacho.


Choipa chao chonse chili mu Giligala; pakuti pamenepo ndinawada, chifukwa cha kuipa kwa machitidwe ao ndidzawainga kuwachotsa m'nyumba mwanga; sindidzawakondanso; akalonga ao onse ndiwo opanduka.


Musamatsata miyambo ya mtundu umene ndiuchotsa pamaso panu; popeza anachita izi zonse, ndinalema nao.


Inu wa maso osalakwa, osapenya choipa, osakhoza kupenyerera chovuta, mupenyereranji iwo akuchita mochenjerera, ndi kukhala chete pamene woipa ammeza munthu wolungama woposa iye mwini;


Ndipo ndinatha abusa atatuwo mwezi umodzi; pakuti mtima wanga unalema nao, ndi mtima waonso unaipidwa nane.


Pomwepo Iye adzanena kwa iwo a kudzanja lamanzere, Chokani kwa Ine otembereredwa inu, kumoto wa nthawi zonse wokolezedwera mdierekezi ndi angelo ake:


Ndipo pamenepo ndidzafukulira iwo, Sindinakudziweni inu nthawi zonse; chokani kwa Ine, inu akuchita kusaweruzika.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa