Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


111 Mau a m'Baibulo Okhudza Kuba

111 Mau a m'Baibulo Okhudza Kuba

Mulungu amatiphunzitsa m’Mawu ake kuti kuba n’koletsedwa, ndi tchimo lolakwiridwa ndi malamulo a Mulungu komanso a dziko. Kuba sikuli koyenera ndipo sikubweretsa mphotho, koma chilango kwa ochita zimenezi. Choncho, konzani mitima yanu, musiye njira zoyipa zobweretsa imfa.

Kuba sikubweretsa phindu lililonse pa moyo wanu, koma kungofanana ndi kudzimangirira chingwe m’khosi. Kukula kwa chinthu chobedwacho sikofunika, chifukwa kungotenga chokhala cha wina kukupangitsani kukhala olakwa. Palibe chodzikhuza pamaso pa Mulungu, ngakhale muli pa umphawi.

Choncho, ndikukulangizani kuti: “Wakuba asabenso; koma agwire ntchito moona mtima ndi manja ake, kuti akhale ndi chofunikira chopatsa wosowa.” M’malo motengera ena, Yesu akufuna mukhale opatsa ndipo nthawi zonse mukhale ndi chogawana ndi ena. N’chifukwa chake muyenera kugwira ntchito ndipo musamaone ngati zinthu zopanda pake katundu wa anthu amene agwira ntchito molimbika kuti akapeze.

Ngakhale simunagwidwe mukuba koyamba, dziwani kuti zonse zidzadziwika ndipo mukhoza kukhala m’ndende zaka zambiri. Ganizirani zomwe zili zabwino pa moyo wanu, musatsatire zilakolako za kanthawi kochepa kapena kulola mavuto kukupusitsani. Fufuzani Mulungu, chifukwa m’chifundo chake chosatha adzakupatsani malinga ndi chuma ndi ulemerero wake.

Musagwere m’msampha wa mdani, funani thandizo, siyani zizolowezi zoipa zimenezo ndipo lolani Mzimu Woyera akutsogolereni. Musaswe malamulo, khalani olimba m’Mawu ake ndipo mudzaona momwe amakusamalirani tsiku lililonse.




Masalimo 62:10

Musakhulupirire kusautsa, ndipo musatama chifwamba; chikachuluka chuma musakhazikepo mitima yanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:2

Chuma cha uchimo sichithangata; koma chilungamo chipulumutsa kuimfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:6

Kupata chuma ndi lilime lonama ndiko nkhungu yoyendayenda, ngakhale misampha ya imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:21

Woipa akongola, wosabweza, koma wolungama achitira chifundo, napereka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 19:11

Musamaba, kapena kunyenga, kapena kunamizana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:22-23

Usalande za waumphawi chifukwa ali waumphawi, ngakhale kutsendereza wosauka kubwalo. Pakuti Yehova adzanenera mlandu wao; omwe akwatula zao Iye adzakwatula moyo wao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 5:3-4

Ndipo anati kwa ine, Ili ndi temberero lilikutulukira padziko lonse; pakuti aliyense wakuba adzapirikitsidwa kuno monga mwa ili; ndi aliyense wakulumbira zonama adzapirikitsidwa kuno monga mwa ili. Ndidzalitulutsa ili, ati Yehova wa makamu, ndipo lidzalowa m'nyumba ya wakuba, ndi m'nyumba ya iye wolumbira monama pa dzina langa; ndipo lidzakhala pakati pa nyumba yake, ndi kuitha pamodzi ndi mitengo yake ndi miyala yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 6:10

kapena ambala, kapena osirira, kapena oledzera, kapena olalatira, kapena olanda, sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 19:18

Iye ananena kwa Iye, Otani? Ndipo Yesu anati, Usaphe, Usachite chigololo, Usabe, Usachite umboni wonama,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 15:19

Pakuti mumtima muchokera maganizo oipa, zakupha, zachigololo, zachiwerewere, zakuba, za umboni wonama, zamwano;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 19:8

Ndipo Zakeyo anaimirira nati kwa Ambuye, Taonani, Ambuye, gawo limodzi la zanga zonse zogawika pakati ndipatsa osauka; ndipo ngati ndalanda kanthu kwa munthu monyenga, ndimbwezera kanai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:22

Usalande za waumphawi chifukwa ali waumphawi, ngakhale kutsendereza wosauka kubwalo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:70

Mtima wao unona ngati mafuta; koma ine ndikondwera nacho chilamulo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 2:21

ndiwe tsono wakuphunzitsa wina, kodi ulibe kudziphunzitsa mwini? Iwe wakulalikira kuti munthu asabe, kodi ulikuba mwini wekha?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Tito 2:10

osatapa pa zao, komatu aonetsere chikhulupiriko chonse chabwino; kuti akakometsere chiphunzitso cha Mpulumutsi wathu Mulungu m'zinthu zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:19-21

Ndipo ntchito za thupi zionekera, ndizo dama, chodetsa, kukhumba zonyansa, Taonani, ine Paulo ndinena ndi inu, kuti, ngati mulola akuduleni, Khristu simudzapindula naye kanthu. kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko, njiru, kuledzera, mchezo, ndi zina zotere; zimene ndikuchenjezani nazo, monga ndachita, kuti iwo akuchitachita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 4:6

asapitirireko munthu, nanyenge mbale wake m'menemo, chifukwa Ambuye ndiye wobwezera wa izi zonse, monganso tinakuuziranitu, ndipo tinachitapo umboni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 23:30

Chifukwa chake, taonani, Ine ndidana ndi aneneri, ati Yehova, amene amaba mau anga, yense kumbera mnansi wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:1

Muyeso wonyenga unyansa Yehova; koma mulingo wamphumphu umsekeretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 61:8

Pakuti Ine Yehova ndikonda chiweruziro, ndida chifwamba ndi choipa; ndipo ndidzawapatsa mphotho yao m'zoonadi; ndipo ndidzapangana nao pangano losatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 22:1-4

Munthu akaba ng'ombe, kapena nkhosa, nakaipha kapena kuigulitsa, azilipa ng'ombe zisanu pa ng'ombeyo, ndi nkhosa zinai pa nkhosayo. Munthu akaikiza bulu, kapena ng'ombe, kapena nkhosa, kapena choweta china kwa mnansi wake, ndipo chikafa, kapena chiphwetekwa, kapena wina achipirikitsa osachiona munthu; lumbiro la Yehova likhale pakati pa iwo awiri, kuti sanatulutse dzanja lake pa chuma cha mnansi wake; ndipo mwiniyo azivomereza, ndipo asalipe. Koma ngati chidabedwa kwaoko ndithu, alipe kwa mwiniyo. Ngati chajiwa ndithu, abwere nacho chikhale mboni; asalipe pa chojiwacho. Munthu akabwereka chinthu kwa mnansi wake, ndipo chiphwetekwa, kapena chifa, mwiniyo palibe, azilipa ndithu. Akakhalapo mwiniyo, asalipe; ngati chagwirira ntchito yakulipira, chadzera kulipira kwake. Munthu akanyenga namwali wosapalidwa ubwenzi, nakagona naye, alipetu kuti akhale mkazi wake. Atate wake akakana konse kumpatsa iye, alipe ndalama monga mwa cholipa cha anamwali. Wanyanga usamlola akhale ndi moyo. Aliyense agona ndi choweta aphedwe ndithu. Akampeza wakuba alimkuboola, nakamkantha kotero kuti wafa, palibe chamwazi. Wakuphera nsembe mulungu wina, wosati Yehova yekha, aonongeke konse. Ndipo usasautsa mlendo kapena kumpsinja; pakuti munali alendo m'dziko la Ejipito. Musazunza mkazi wamasiye, kapena mwana wamasiye aliyense. Ukawazunza ndi kakuti konse, nakandilirira pang'ono ponse iwowa, ndidzamvadi kulira kwao; ndi mkwiyo wanga udzayaka, ndipo ndidzapha inu ndi lupanga; ndipo akazi anu adzakhala amasiye, ndi ana anu omwe. Ukakongoletsa ndalama anthu anga osauka okhala nanu, usamkhalira ngati wangongole; usamuwerengera phindu. Ukati ulandire chikole kaya chovala cha mnansi wako, koma polowa dzuwa uchibwezere kwa iye; popeza chofunda chake ndi ichi chokha, ndicho chovala cha pathupi pake; azifundira chiyani pogona? Ndipo kudzakhala kuti akandifuulira Ine, ndidzamva; pakuti Ine ndine wachisomo. Usapeputsa oweruza, kapena kutemberera mkulu wa anthu a mtundu wako. Usachedwa kuperekako zipatso zako zochuluka, ndi zothira zako. Woyamba wa ana ako aamuna undipatse Ine. Litamtulukira dzuwa, pali chamwazi; wakubayo azilipa ndithu; ngati alibe kanthu, amgulitse pa umbala wake. Uzitero nazo ng'ombe zako, ndi nkhosa zako; masiku asanu ndi atatu akhale ndi amai wake; tsiku lachisanu ndi chitatu uzimpereka kwa Ine. Ndipo muzindikhalira Ine anthu opatulika; chifukwa chake musamadya nyama yojiwa kuthengo; itayireni agalu. Akachipeza chakubacho chili m'dzanja lake chamoyo, ngakhale ng'ombe, kapena bulu, kapena nkhosa, alipe mowirikiza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 24:1

Dziko lapansi nla Yehova ndi zodzala zake zomwe, dziko lokhalamo anthu ndi iwo okhala m'mwemo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:27

Wopindula monyenga avuta nyumba yake; koma wakuda mitulo adzakhala ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 146:7

ndiye wakuchitira chiweruzo osautsika; ndiye wakupatsa anjala chakudya; Yehova amasula akaidi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:19-21

Musadzikundikire nokha chuma padziko lapansi, pamene njenjete ndi dzimbiri ziononga; ndi pamene mbala ziboola ndi kuba: Chifukwa chake pamene paliponse upatsa mphatso zachifundo, usamaomba lipenga patsogolo pako, monga amachita onyenga m'masunagoge, ndi m'makwalala, kotero kuti atamandidwe ndi anthu. Indetu ndinena kwa inu, Iwo alandiriratu mphotho zao. koma mudzikundikire nokha chuma mu Mwamba, pamene njenjete kapena dzimbiri siziononga, ndipo mbala siziboola ndi kuba; pakuti kumene kuli chuma chako, komwe udzakhala mtima wakonso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 23:1

Usatola mbiri yopanda pake; usathandizana naye woipa ndi kukhala mboni yochititsa chiwawa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:61

Anandikulunga nazo zingwe za oipa; koma sindinaiwale chilamulo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 24:7

Akampeza munthu waba mbale wake wina wa ana a Israele, namuyesa kapolo, kapena wamgulitsa, afe wakubayo; potero muzichotsa choipacho pakati panu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 13:9

Pakuti ili, Usachite chigololo, Usaphe, Usabe, Usasirire, ndipo lingakhale lamulo lina lililonse, limangika pamodzi m'mau amenewa, kuti, Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe wekha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:24

Wobera atate wake, pena amake, nati, Palibe kulakwa; ndiye mnzake wa munthu wopasula.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 24:2

Alipo akusendeza malire; alanda gulu la zoweta, nazidyetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:12

Chifukwa chake zinthu zilizonse mukafuna kuti anthu achitire inu, inunso muwachitire iwo zotero; pakuti icho ndicho chilamulo ndi aneneri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 49:6-7

Iwo akutama kulemera kwao; nadzitamandira pa kuchuluka kwa chuma chao; kuombola mbale sangadzamuombole, kapena kumperekera dipo kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 9:11

Ngati takufeserani inu zauzimu, kodi nchachikulu ngati ife tituta za thupi lanu?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 10:2

Podzikuza woipa apsereza waumphawi; agwe m'chiwembu anapanganacho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 5:10

Wokonda siliva sadzakhuta siliva; ngakhale wokonda chuma sadzakhuta phindu; ichinso ndi chabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 50:18

Pakuona mbala, uvomerezana nayo, nuchita nao achigololo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 73:12

Tapenyani, oipa ndi awa; ndipo pokhazikika chikhazikikire aonjezerapo pa chuma chao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 24:43-44

Koma dziwani ichi, kuti mwini nyumba akadadziwa nthawi yiti mbala ikudza, iye akadadikira, ndipo sakadalola kuti nyumba yake ibooledwe. Chifukwa chake khalani inunso okonzekeratu; chifukwa munthawi m'mene simuganizira, Mwana wa Munthu adzadza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 1:23

Akulu ako apanduka, ali anzao a mbala; onse akonda mitulo, natsata zokometsera milandu; iwo saweruzira amasiye; ngakhale mlandu wa mkazi wamasiye suwafika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:7

Musanyengedwe; Mulungu sanyozeka; pakuti chimene munthu achifesa, chimenenso adzachituta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:23

M'ntchito zonse muli phindu; koma kulankhulalankhula kungopatsa umphawi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 26:10

amene m'manja mwao muli mphulupulu, ndi dzanja lao lamanja ladzala ndi zokometsera mlandu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:29-30

anadzala ndi zosalungama zonse, kuipa, kusirira, dumbo; odzala ndi kaduka, mbanda, ndeu, chinyengo, udani; wakunena za Mwana wake, amene anabadwa, wa mbeu ya Davide, monga mwa thupi, akazitape, osinjirira, akumuda Mulungu, achipongwe, odzitama, amatukutuku, oyamba zoipa, osamvera akulu ao,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:12

Woipa akhumba chokodwa ndi amphulupulu; koma muzu wa olungama umabala zipatso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:28

Pakuti Yehova akonda chiweruzo, ndipo sataya okondedwa ake. Asungika kosatha, koma adzadula mbumba za oipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 56:11

Inde agalu ali osusuka, sakhuta konse; amenewa ali abusa osazindikira; iwo onse atembenukira kunjira zao, yense kutsata phindu lake m'dera lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:11

Chuma cholandiridwa mokangaza chidzachepa; koma wokundika ndi dzanja adzaona zochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mika 2:1

Tsoka iwo akulingirira chinyengo, ndi kukonza choipa pakama pao! Kutacha m'mawa achichita, popeza chikhozeka m'manja mwao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 3:14

Ndipo asilikali omwe anamfunsa iye, nati, Nanga ife tizichita chiyani? Ndipo iye anati kwa iwo, Musaopse, musanamize munthu aliyense; khalani okhuta ndi kulipira kwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:17

Musabwezere munthu aliyense choipa chosinthana ndi choipa. Ganiziranitu zinthu za ulemu pamaso pa anthu onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 10:3

Pakuti woipa adzitamira chifuniro cha moyo wake, adalitsa wosirira, koma anyoza Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:40-42

Ndipo kwa iye wofuna kupita nawe kumlandu ndi kutenga malaya ako, umlolezenso chofunda chako. Ndipo amene akakukakamiza kumperekeza njira imodzi, upite naye ziwiri. Kwa iye wopempha iwe umpatse, ndipo kwa iye wofuna kukukongola usampotolokere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 6:10

Pakuti muzu wa zoipa zonse ndiwo chikondi cha pa ndalama; chimene ena pochikhumba, anasochera, nataya chikhulupiriro, nadzipyoza ndi zowawa zambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:119

Muchotsa oipa onse a padziko lapansi ngati mphala: Chifukwa chake ndikonda mboni zanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:8

Zapang'ono, pokhala chilungamo, ziposa phindu lalikulu lopanda chiweruzo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 49:16-17

Usaope polemezedwa munthu, pochuluka ulemu wa nyumba yake; pakuti pomwalira iye sadzamuka nako kanthu kalikonse; ulemu wake sutsika naye kumtsata m'mbuyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:17

Zakudya za chinyengo zikondweretsa munthu; koma pambuyo pake m'kamwa mwake mudzadzala tinsangalabwi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 78:70-72

Ndipo anasankha Davide mtumiki wake, namtenga kumakola a nkhosa. Anamtenga kuja anatsata zoyamwitsa, awete Yakobo, anthu ake, ndi Israele, cholowa chake. Potero anawaweta monga mwa mtima wake wangwiro; nawatsogolera ndi luso la manja ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 7:10

musazunza mkazi wamasiye, kapena ana amasiye, mlendo kapena waumphawi; ndipo nnena mmodzi wa inu alingirire m'mtima mwake kumchitira choipa munthu mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 5:19

Usabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:16-17

Zochepa zake za wolungama zikoma koposa kuchuluka kwao kwa oipa ambiri. Pakuti manja a oipa adzathyoledwa, koma Yehova achirikiza olungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 22:7

Munthu akaikiza ndalama kapena chuma kwa mnansi wake, ndipo zibedwa m'nyumba ya munthuyo; akapeza mbala, ilipe chowirikiza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 4:8

Pali mmodzi palibe wachiwiri; inde, alibe mwana ngakhale mbale; koma ntchito yake yonse ilibe chitsiriziro, ngakhale diso lake silikhuta chuma. Samati, Ndigwira ntchito ndi kumana moyo wanga zabwino chifukwa cha yani? Ichinso ndi chabe, inde, vuto lalikulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 23:28

Pakuti abisalira ngati wachifwamba, nachulukitsa anthu a chiwembu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:27

Wogawira aumphawi sadzasowa; koma wophimba maso ake adzatembereredwa kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 82:3

Weruzani osauka ndi amasiye; weruzani molungama ozunzika ndi osowa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 23:6

Usakhotetsa mlandu wa mnzako waumphawi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:19

Musabwezere choipa, okondedwa, koma patukani pamkwiyo; pakuti kwalembedwa, Kubwezera kuli kwanga, Ine ndidzabwezera, ati Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:94

Ine ndine wanu, ndipulumutseni pakuti ndinafuna malangizo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:24

Woyenda ndi mbala ada moyo wakewake; amva kulumbira, koma osawulula kanthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:19

Ndipo ntchito za thupi zionekera, ndizo dama, chodetsa, kukhumba zonyansa,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:10

Wosocheretsa oongoka mtima alowe m'njira yoipa, adzagwa mwini m'dzenje lake; koma angwiro adzalandira cholowa chabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 109:11

Wokongoletsa agwire zonse ali nazo; ndi alendo alande za ntchito yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 5:1-3

Nanga tsono achuma inu, lirani ndi kuchema chifukwa cha masautso anu akudza pa inu. Tengani, abale, chitsanzo cha kumva zowawa ndi kuleza mtima, aneneri amene analankhula m'dzina la Ambuye. Taonani tiwayesera odala opirirawo; mudamva za chipiriro cha Yobu, ndipo mwaona chitsiriziro cha Ambuye, kuti Ambuye ali wodzala chikondi, ndi wachifundo. Koma makamaka, abale anga, musalumbire, kungakhale kutchula kumwamba kapena dziko, kapena lumbiro lina lililonse; koma inde wanu akhale inde, ndi iai wanu akhale iai; kuti mungagwe m'chiweruziro. Kodi wina wa inu akumva zowawa? Apemphere. Kodi wina asekera? Aimbire. Pali wina kodi adwala mwa inu? Adziitanire akulu a Mpingo, ndipo apemphere pa iye, atamdzoza ndi mafuta m'dzina la Ambuye: ndipo pemphero la chikhulupiriro lidzapulumutsa wodwalayo, ndipo Ambuye adzamuukitsa; ndipo ngati adachita machimo adzakhululukidwa kwa iye. Chifukwa chake muvomerezane wina ndi mnzake machimo anu, ndipo mupempherere wina kwa mnzake kuti muchiritsidwe. Pemphero la munthu wolungama likhoza kwakukulu m'machitidwe ake. Eliya anali munthu wakumva zomwezi tizimva ife, ndipo anapemphera chipempherere kuti isavumbe mvula; ndipo siinagwe mvula padziko zaka zitatu kudza miyezi isanu ndi umodzi. Ndipo anapempheranso; ndipo m'mwamba munatsika mvula, ndi dziko lidabala zipatso zake. Abale anga, ngati wina wa inu asochera posiyana ndi choonadi, ndipo ambweza iye mnzake; Chuma chanu chaola ndi zovala zanu zajiwa ndi njenjete. azindikire, kuti iye amene abweza wochimwa kunjira yake yosochera adzapulumutsa munthu kwa imfa, ndipo adzavundikira machimo aunyinji. Golide wanu ndi siliva wanu zachita dzimbiri, ndipo dzimbiri lake lidzachita mboni zoneneza inu, ndipo zidzadya nyama yanu ngati moto. Mwadzikundikira chuma masiku otsiriza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 33:15

Iye amene ayenda molungama, nanena molunjika; iye amene anyoza phindu lonyenga, nasansa manja ake kusalandira zokometsera milandu, amene atseka makutu ake kusamva za mwazi, natsinzina maso ake kusayang'ana choipa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 3:13-14

M'mero mwao muli manda apululu; ndi lilime lao amanyenga; ululu wa mamba uli pansi pa milomo yao; m'kamwa mwao mudzala ndi zotemberera ndi zowawa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:155

Chipulumutso chitalikira oipa; popeza safuna malemba anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 21:13

nanena kwa iwo, Chalembedwa, Nyumba yanga idzanenedwa nyumba yakupemphera; koma inu mwaiyesa phanga la achifwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 12:5

Chifukwa cha kupasuka kwa ozunzika, chifukwa cha kuusa moyo kwa aumphawi, ndiuka tsopano, ati Yehova; ndidzamlonga mosungika muja alakalakamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:7

Chiwawa cha amphulupulu chidzawakokolola; chifukwa akana kuchita chiweruzo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 10:30-37

Ndipo Yesu anamlanda mau, nati, Munthu wina anatsika kuchokera ku Yerusalemu kunka ku Yeriko; ndipo anagwa m'manja a achifwamba amene anamvula zovala, namkwapula, nachoka atamsiya wofuna kufa. Ndipo kudangotero kuti wansembe wina anatsika njirayo, ndipo pakumuona iye anapita mbali ina. Momwemonso Mlevi, pofika pamenepo, ndi kumuona, anapita mbali ina. Koma Msamariya wina ali pa ulendo wake anadza pali iye; ndipo pakumuona, anagwidwa chifundo, nadza kwa iye, namanga mabala ake, nathirapo mafuta ndi vinyo; ndipo anamuika iye pa nyama yake ya iye yekha, nadza naye kunyumba ya alendo, namsungira. Ndipo m'mawa mwake anatulutsa marupiya atheka awiri napatsa mwini nyumba ya alendo, nati, Msungire iye, ndipo chilichonse umpatsa koposa, ine, pobwera, ndidzakubwezera iwe. Uti wa awa atatu, uyesa iwe, anakhala mnansi wa iye uja adagwa m'manja a achifwamba? Ndipo anati, Iye wakumchitira chifundo. Ndipo Yesu anati kwa iye, Pita nuchite iwe momwemo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:21-22

Woipa akongola, wosabweza, koma wolungama achitira chifundo, napereka. Pakuti iwo amene awadalitsa adzalandira dziko lapansi; koma iwo amene awatemberera adzadulidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 59:6

Maukonde ao sadzakhala zovala, sadzafunda ntchito zao; ntchito zao zili ntchito zoipa, ndi chiwawa chili m'manja mwao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:3

Kuongoka mtima kwa olungama kuwatsogolera; koma kukhota kwa achiwembu kudzawaononga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 18:30

Chifukwa chake ndidzakuweruzani inu, nyumba ya Israele, yense monga mwa njira zake, ati Ambuye Yehova. Bwererani, nimutembenukire kuleka zolakwa zanu zonse, ndipo simudzakhumudwa nazo, ndi kuonongeka nayo mphulupulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:118

Mupepula onse akusokera m'malemba anu; popeza chinyengo chao ndi bodza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:22

Chotikondetsa munthu ndicho kukoma mtima kwake; ndipo wosauka apambana munthu wonama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 79:12

Ndipo anansi athu amene anatonza Inu muwabwezere chotonza chao, kasanu ndi kawiri kumtima kwao, Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 56:2

Wodala munthu amene achita ichi, ndi mwana wa munthu amene agwira zolimba ichi, amene asunga Sabata osaliipitsa, nasunga dzanja lake osachita nalo choipa chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 52:1

Udzitamandiranji ndi choipa, chiphona iwe? Chifundo cha Mulungu chikhala tsiku lonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:17

Potero kwa iye amene adziwa kuchita bwino, ndipo sachita, kwa iye kuli tchimo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:25

Chifuniro cha waulesi chimupha; chifukwa manja ake akana kugwira ntchito.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:24

Palibe munthu angathe kukhala kapolo wa ambuye awiri: pakuti pena adzamuda mmodziyo, ndi kukonda winayo; pena adzakangamira kwa mmodzi, nadzanyoza wina. Simungathe kukhala kapolo wa Mulungu ndi wa Chuma.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 20:10

Miyeso yosiyana, ndi malichero osiyana, zonse ziwirizi zinyansa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:13

ndipo musapereke ziwalo zanu kuuchimo, zikhale zida za chosalungama; koma mudzipereke inu nokha kwa Mulungu, monga amoyo atatuluka mwa akufa, ndi ziwalo zanu kwa Mulungu zikhale zida za chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 53:4

Kodi ochita zopanda pake sadziwa? Pomadya anthu anga monga akudya mkate; ndipo saitana Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:21

njiru, kuledzera, mchezo, ndi zina zotere; zimene ndikuchenjezani nazo, monga ndachita, kuti iwo akuchitachita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:16

Wotsendereza waumphawi kuti achulukitse chuma chake, ndi wopatsa wolemera kanthu, angosauka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 84:11

Pakuti Yehova Mulungu ndiye dzuwa ndi chikopa; Yehova adzapatsa chifundo ndi ulemerero; sadzakaniza chokoma iwo akuyenda angwiro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 9:17

madzi akuba atsekemera, ndi chakudya chobisika chikoma.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Malaki 3:8

Kodi munthu adzalanda za Mulungu? Ndipo inu mundilanda Ine. Koma mukuti, Takulandani zotani? Limodzilimodzi la magawo khumi, ndi zopereka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 10:1

Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Iye wosalowa m'khola la nkhosa pakhomo, koma akwerera kwina, iyeyu ndiye wakuba ndi wolanda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 7:9

Kodi mudzapha, ndi kuba, ndi kuchita chigololo, ndi kulumbira zonama, ndi kupereka nsembe kwa Baala, ndi kutsata milungu ina imene simunaidziwa,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 6:30

Anthu sanyoza mbala ikaba, kuti ikhutitse mtima wake pomva njala;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 20:15

Usabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 22:1

Munthu akaba ng'ombe, kapena nkhosa, nakaipha kapena kuigulitsa, azilipa ng'ombe zisanu pa ng'ombeyo, ndi nkhosa zinai pa nkhosayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 2:26

Monga mbala ili ndi manyazi pamene igwidwa, chomwecho nyumba ya Israele ili ndi manyazi; iwo, mafumu ao, akulu ao, ansembe ao, ndi aneneri ao;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 10:19

Udziwa malamulo: Usaphe, Usachite chigololo, Usabe, Usachite umboni wakunama, Usanyenge, Lemekeza atate wako ndi amai ako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:28

Wakubayo asabenso; koma makamaka agwiritse ntchito, nagwire ntchito yokoma ndi manja ake, kuti akhale nacho chakuchereza wosowa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Mzimu Woyera wokondedwa wanga, Inu ndinu mtsogoleri wanga, chitonthozo changa, ndi amene amandisintha. Ndikukupemphani mundithandize ndi kundimasula ku chilichonse chomwe chimandimanga ku uchimo. Mawu anu amati: "Wakubayo asabenso, koma agwire ntchito, akuchita zabwino ndi manja ake, kuti akhale ndi chogawana ndi wosowa." Ambuye Yesu, ndikhululukireni munthu aliyense amene ndidamuwopseza ndi kumunyoza kuti ndimubwere, ndikhululukireni chilichonse chomwe ndidaba, kaya chifukwa cha kusowa kapena chifukwa cha ulesi, konzani ndi kulimbitsa munthu wamkati mwanga, ndithandizeni kuvua munthu wakale amene ali ndi zilakolako zonyenga kuti ndisapatse malo uchimo m'moyo mwanga. Ndikutsutsa chilakolako chilichonse ndi chilichonse chomwe chimandikakamiza kubera, chotsani Ambuye, anthu onse omwe amandilimbikitsa molakwika ndi omwe akufuna choipa changa achotsereni pa njira yanga. Mawu anu amati: "Indetu, indetu, ndikukuuzani, kuti aliyense wochita uchimo, ndi kapolo wa uchimo." Ambuye, ndithandizeni kupambana ndi kutseka zitseko za uchimo, kuti mtima wanga udane ndi kutaya kuba, kuba, dama, zolaula, bodza, chilakolako, umbombo, chigololo ndi chonyansa chilichonse. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa