Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Eksodo 23:6 - Buku Lopatulika

6 Usakhotetsa mlandu wa mnzako waumphawi.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 Usakhotetsa mlandu wa mnzako waumphawi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 “Ngati mmodzi mwa anthu ako osauka aimbidwa mlandu, umuweruze molungama ndithu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 “Usakhotetse milandu ya anthu osauka.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 23:6
23 Mawu Ofanana  

Ndipo tsono, kuopa Yehova kukhale pa inu, musamalire ndi kuchita; pakuti palibe chosalungama kwa Yehova Mulungu wathu, kapena kusamalira monga mwa nkhope ya munthu, kapena kulandira mphatso.


Ngati ndapeputsa mlandu wa kapolo wanga, kapena wa mdzakazi wanga, potsutsana nane iwo,


Kukometsa mlandu wa wamphulupulu mwatsankho sikuli kwabwino, ngakhale kuchitira chetera wolungama.


Usalande za waumphawi chifukwa ali waumphawi, ngakhale kutsendereza wosauka kubwalo.


Kuti angamwe, naiwale malamulo, naweruze mokhota anthu onse osautsidwa.


Ukaona anthu alikutsendereza aumphawi, ndi kuchotsa chilungamo ndi chiweruzo mwachiwawa pa dera lina la dziko, usazizwepo; pakuti mkulu wopambana asamalira; ndipo alipo akulu ena oposa amenewo.


amene alungamitsa woipa pa chokometsera mlandu, nachotsera wolungama chilungamo chake!


Anenepa, anyezimira; inde apitiriza kuchita zoipa; sanenera ana amasiye mlandu wao, kuti apindule; mlandu wa aumphawi saweruza.


Onse ali opikisana ndithu, ayendayenda ndi maugogodi; ndiwo mkuwa ndi chitsulo; onsewa achita movunda;


ndi kuleka kutsendereza mlendo, ndi wamasiye, ndi mkazi wamasiye, osakhetsa mwazi wosachimwa m'malo muno, osatsata milungu ina ndi kudziipitsa nayo;


Musamachita chisalungamo pakuweruza mlandu; usamavomereza munthu wosauka, kapena kulemekeza munthu womveka; uweruze mlandu wa munthu mnzako molungama.


Ndipo ndidzayandikiza kwa inu kuti ndiweruze; ndipo ndidzakhala mboni yakufulumira kutsutsa obwebweta, ndi achigololo, ndi olumbira monama; ndi iwo akunyenga wolembedwa ntchito pa kulipira kwake, akazi amasiye, ndi ana amasiye, ndi wakuipsa mlandu wa mlendo, osandiopa Ine, ati Yehova wa makamu.


Musamapotoza chiweruzo, musamasamalira munthu, kapena kulandira chokometsera mlandu; popeza chokometsera mlandu chidetsa maso a anzeru, ndi kuipisa mau a olungama.


Wotembereredwa iye wakuipsa mlandu wa mlendo, mwana wamasiye, ndi mkazi wamasiye. Ndi anthu onse anene, Amen.


Ndipo ana ake sanatsanze makhalidwe ake, koma anapatukira ku chisiriro, nalandira chokometsera mlandu, naipitsa kuweruza.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa