Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 82:3 - Buku Lopatulika

3 Weruzani osauka ndi amasiye; weruzani molungama ozunzika ndi osowa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

3 Weruzani osauka ndi amasiye; weruzani molungama ozunzika ndi osowa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

3 Inu tetezani anthu ofooka ndi amasiye mwachilungamo. Weruzani molungama ozunzika ndi amphaŵi.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 82:3
16 Mawu Ofanana  

Pakuti ndinapulumutsa wozunzika wakufuula; mwana wamasiye yemwe wosowa mthandizi.


ngati ndinasamulira ana amasiye dzanja langa, popeza ndinaona thandizo langa kuchipata;


kuti muweruze mlandu wa amasiye ndi wokhalira mphanthi, kuti munthu wa padziko lapansi angaonjeze kuopsa.


kapena usakometsera munthu wosauka pa mlandu wake.


Usakhotetsa mlandu wa mnzako waumphawi.


Tsegula pakamwa pako nuweruze molungama, nunenere osauka ndi aumphawi.


phunzirani kuchita zabwino; funani chiweruzo; thandizani osautsidwa, weruzirani ana amasiye, munenere akazi amasiye.


Akulu ako apanduka, ali anzao a mbala; onse akonda mitulo, natsata zokometsera milandu; iwo saweruzira amasiye; ngakhale mlandu wa mkazi wamasiye suwafika.


Nyumba ya Davide iwe, Yehova atero, Chita chiweruzo m'mawa, ndi kumlanditsa amene afunkhidwa m'dzanja la wosautsa, kungatuluke kupsa mtima kwanga ngati moto, ndi kutentha kosazimika, chifukwa cha ntchito zanu zoipa.


Iye anaweruza mlandu wa aumphawi ndi osowa; kumeneko kunali kwabwino. Kodi kumeneko si kundidziwa Ine? Ati Yehova.


Yehova atero: Chitani chiweruzo ndi chilungamo, landitsani ofunkhidwa m'dzanja la wosautsa; musachite choipa, musamchitire mlendo chiwawa, kapena ana amasiye, kapena akazi amasiye, musakhetse mwazi wosachimwa pamalo pano.


Anenepa, anyezimira; inde apitiriza kuchita zoipa; sanenera ana amasiye mlandu wao, kuti apindule; mlandu wa aumphawi saweruza.


Watero Yehova wa makamu, kuti, Weruzani chiweruzo choona, nimuchitire yense mnzake chifundo ndi ukoma mtima;


Aweruzira ana amasiye ndi mkazi wamasiye; ndipo akonda mlendo, ndi kumpatsa chakudya ndi chovala.


Musamaipsa mlandu wa mlendo, kapena wa ana amasiye; kapena kutenga chikole chovala cha mkazi wamasiye;


Mapembedzedwe oyera ndi osadetsa pamaso pa Mulungu ndi Atate ndiwo: kucheza ndi ana amasiye ndi akazi amasiye m'chisautso chao, ndi kudzisungira mwini wosachitidwa mawanga ndi dziko lapansi.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa