Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 82 - Buku Lopatulika


Oweruza aweruza bwino
Salimo la Asafu.

1 Mulungu aima mu msonkhano wa Mulungu, aweruza pakati pa milungu.

2 Mudzaweruza mosalunjika kufikira liti, ndi kusamalira nkhope ya oipa?

3 Weruzani osauka ndi amasiye; weruzani molungama ozunzika ndi osowa.

4 Pulumutsani osauka ndi aumphawi; alanditseni m'dzanja la oipa.

5 Sadziwa, ndipo sazindikira; amayendayenda mumdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

6 Ndinati Ine, Inu ndinu milungu, ndi ana a Wam'mwambamwamba nonsenu.

7 Komatu mudzafa monga anthu, ndipo mudzagwa monga wina wa akulu.

8 Ukani, Mulungu, weruzani dziko lapansi; pakuti Inu mudzalandira amitundu onse.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa