Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 101 - Buku Lopatulika


Davide akuti adzasamala okhulupirika nadzachotsa oipa
Salimo la Davide.

1 Ndidzaimba zachifundo ndi chiweruzo; ndidzaimba zakukulemekezani Inu, Yehova.

2 Ndidzachita mwanzeru m'njira yangwiro; mudzandidzera liti? Ndidzayenda m'nyumba mwanu ndi mtima wangwiro.

3 Sindidzaika chinthu choipa pamaso panga; chochita iwo akupatuka padera chindiipira; sichidzandimamatira.

4 Mtima wopulukira udzandichokera; sindidzadziwana naye woipa.

5 Wakuneneza mnzake m'tseri ndidzamdula; wa maso odzikuza ndi mtima wodzitama sindidzamlola.

6 Maso anga ayang'ana okhulupirika m'dziko, kuti akhale ndi Ine; iye amene ayenda m'njira yangwiro, iyeyu adzanditumikira Ine.

7 Wakuchita chinyengo sadzakhala m'kati mwa nyumba yanga; wakunena mabodza sadzakhazikika pamaso panga.

8 Mamawa onse ndidzadula oipa onse a m'dziko; kuduliratu onse akuchita zopanda pake kumzinda wa Yehova.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa